1 Petro 1 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 1:1-25

1Ndine Petro, mtumwi wa Yesu Khristu.

Ndikulemba kalatayi kwa onse osankhidwa ndi Mulungu, alendo mʼdziko lapansi, obalalikira ku Ponto, Galatiya, Kapadokiya, Asiya ndi Bituniya. 2Mulungu Atate anakusankhani, atakudziwani kuyambira pachiyambi, ndipo Mzimu Woyera wakuyeretsani kuti mumvere Yesu Khristu ndikutsukidwa ndi magazi ake.

Chisomo ndi mtendere zikhale ndi inu mochuluka.

Kuyamika Mulungu Chifukwa cha Chiyembekezo Chamoyo

3Alemekezedwe Mulungu, Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu. Mwachifundo chake chachikulu anatibadwitsa kwatsopano, mʼchiyembekezo chamoyo pomuukitsa Yesu Khristu kwa akufa, 4kuti tidzalandire chuma chomwe sichingawonongeke, kuyipitsidwa kapena kufota. Chuma chimenechi akukusungirani kumwamba. 5Mwachikhulupiriro, mukusungidwa ndi mphamvu ya Mulungu mpaka chipulumutso chitafika chimene chinakonzedwa kuti adzachionetse nthawi yotsiriza. 6Zimenezi zikukondweretseni kwambiri, ngakhale tsopano, kwa kanthawi kochepa, mukumva zowawa mʼmayesero osiyanasiyana. 7Mayeserowa abwera nʼcholinga chakuti chikhulupiriro chanu, chimene ndi chamtengo woposa wa golide, amene amawonongeka ngakhale amayengedwa ndi moto, chitsimikizike kuti ndi chenicheni. Pamenepo ndiye mudzalandire mayamiko, ulemerero ndi ulemu pamene Yesu Khristu adzaoneka. 8Ngakhale kuti simunamuone, mumamukonda; ndipo ngakhale kuti simukumuona tsopano, mumamukhulupirira ndipo mumakondwera ndi chimwemwe chachikulu ndi chosaneneka. 9Motero mukulandira mphotho ya chikhulupiriro chanu, ndiyo chipulumutso cha moyo wanu.

10Kunena za chipulumutso chimenechi, aneneri amene ananeneratu za chisomo chimene chimabwera kwa inu, anafunafuna mofufuzafufuza za chipulumutsochi, 11kufuna kudziwa nthawi ndi momwe zidzachitikire zinthu zimene Mzimu wa Khristu amene ali mwa iwo ankanenera za kuvutika kwa Khristu, ndi ulemerero umene adzakhale nawo pambuyo pake. 12Mulungu anawawululira kuti ntchito yawoyo sankayigwira chifukwa cha iwo eni, koma chifukwa inu, pamene iwo ankayankhula zinthu zimene mwamva tsopano kuchokera kwa amene amalalikira Uthenga Wabwino mwamphamvu ya Mzimu Woyera wotumidwa kuchokera kumwamba. Ngakhale angelo amalakalaka kuona nawo zinthuzi.

Khalani Oyera Mtima

13Choncho konzani mtima wanu, khalani odziretsa; khazikitsani chiyembekezo chanu kotheratu pa chisomo chimene mudzapatsidwe pamene Yesu Khristu adzaonekera. 14Monga ana omvera, musatsatenso zilakolako zoyipa zomwe munali nazo pamene munali osadziwa. 15Koma monga amene anakuyitanani ndi woyera, inunso khalani oyera mtima mʼmakhalidwe anu wonse. 16Pakuti, kwalembedwa kuti, “Khalani oyera mtima, chifukwa Ine ndine Woyera.”

17Popeza mumapemphera kwa Atate amene amaweruza munthu aliyense mopanda tsankho molingana ndi zochita zake, pa nthawi imene muli alendo pa dziko lapansi khalani moopa Mulungu. 18Pakuti mukudziwa kuti simunawomboledwe ndi zinthu zimene zimawonongeka monga siliva kapena golide, kuchoka ku khalidwe lanu lachabe limene munalandira kwa makolo anu. 19Koma munawomboledwa ndi magazi a mtengowapatali a Khristu, Mwana Wankhosa wopanda banga kapena chilema. 20Iye anasankhidwa lisanalengedwe dziko lapansi, koma waonetsedwa chifukwa cha inu pa nthawi ino yotsiriza. 21Kudzera mwa Iye mumakhulupirira Mulungu, amene anamuukitsa kwa akufa namupatsa ulemerero. Nʼchifukwa chake chikhulupiriro ndi chiyembekezo chanu chili mwa Mulungu.

22Tsopano mwayeretsa mitima yanu pomvera choonadi, kuti muzikondana ndi abale anu, kukondana kwenikweni kochokera pansi pa mtima. 23Popeza mwabadwanso, osati ndi mbewu imene imawonongeka, koma imene siwonongeka, ndiye kuti ndi Mawu a Mulungu amoyo ndi okhalitsa. 24Pakuti,

“Anthu onse ali ngati udzu,

ndipo ulemerero wawo uli ngati duwa la kuthengo.

Udzu umafota ndipo duwa limathothoka,

25koma mawu a Ambuye adzakhala mpaka muyaya.”

Ndipo awa ndi mawu amene tinalalikira kwa inu.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרתו הראשונה של פטרוס השליח 1:1-25

1מאת פטרוס, שליחו של ישוע המשיח.

אל המאמינים הפזורים בפנטוס, גלטיא, קפדוקיא, אסיה וביתיניא. 2אחים יקרים, האלוהים אבינו בחר בכם עוד לפני זמן רב וקידש אתכם על־ידי רוחו, כדי שתצייתו למשיח וכדי שדם המשיח יטהר אתכם. יהי רצון שאלוהים יברך אתכם בברכה גדולה של חסד ושלום.

3השבח לאלוהים, אבי אדוננו ישוע המשיח, על אשר ברחמיו הרבים ובזכות תקומתו של ישוע המשיח מן המתים, העניק לנו חיים חדשים מלאי תקווה. 4אלוהים גם הועיד לכם נחלה נצחית בשמים – נחלה מושלמת שלא תירקב או תשתנה. 5בזכות אמונתכם שומר אתכם אלוהים בגבורה, עד שתתגלה ישועתו בשלמותה ביום האחרון. 6משום כך עליכם לשמוח – גם אם עתה, לזמן קצר, סובלים אתם מצרות שונות. 7הסבל והצרות האלה אינם מקריים; מטרתם לבחון את אמונתכם היקרה יותר מזהב, לצרפה ולטהרה.

אם תישאר אמונתכם איתנה וטהורה למרות הצרות והקשיים, היא תביא לכם שבח, כבוד והדר רב ביום שובו של ישוע המשיח.

8אתם אוהבים את המשיח למרות שמעולם לא ראיתם אותו; אתם מאמינים ובוטחים בו למרות שאינכם רואים אותו, ואתם מלאים שמחה שאין מילים לתארה. 9בזכות אמונתכם מעניק לכם אלוהים לא רק שמחה גדולה, כי אם גם מושיע את נפשותיכם.

10אף כי נביאי התנ״ך ניבאו וכתבו על ישועה זאת שמיועדת לכם, הם לא הבינו את מלוא משמעותה. 11הנביאים השתדלו לגלות את המועד ואת הנסיבות שעליהם הצביע רוח הקודש, אשר פעל בקרבם וסיפר להם מראש על סבלו של המשיח וייסוריו, ועל הכבוד שיבוא בעקבותיהם. 12לבסוף נאמר להם שנבואות אלה לא תתקיימנה בימי חייהם, כי אם שנים רבות לאחר מותם – בימי חייכם! נבואות אלה הן הבשורה שבישרו לכם שליחי המשיח בהשראת רוח הקודש. אפילו מלאכי אלוהים השתוקקו לדעת יותר על דברים אלה. 13לפיכך, התכוננו וצפו בפיכחות וערנות לחסד שיעניק לכם אלוהים ביום שובו של ישוע המשיח.

14הואיל ועתה בני־אלוהים אתם, עליכם לציית לו. אל תשובו למעשיכם הרעים ולדרך החיים שניהלתם לפני שהאמנתם במשיח. 15היו קדושים בכל מעשיכם, כשם שהאלוהים אשר אימץ אתכם לבניו קדוש הוא. 16הלא אלוהים אומר לנו בכתובים:1‏.16 א 16 ויקרא יט 2 ”קדושים תהיו כי קדוש אני“.

17זכרו כי אביכם שבשמים, שאליו אתם מתפללים, אינו שופט במשוא־פנים; הוא ישפוט את כל מעשיכם בצדק מוחלט! משום כך עליכם להתייחס אליו בכבוד וביראה כל ימי חייכם עלי־אדמות. 18אלוהים פדה וגאל אתכם מאמונות־שווא ומעשי־הבל שנחלתם מאבותיכם, אך הוא פדה אתכם לא בזהב, בכסף או בצורת תשלום אחרת שמקובלת בעולם הזה, 19כי אם בדמו היקר של המשיח – השה התמים והטהור של האלוהים. 20עוד לפני בריאת העולם יעד אלוהים את המשיח להיות קורבן בעד בני־האדם, אולם תוכניתו זאת נודעה ברבים רק בימים אחרונים אלה. 21על־ידי המשיח אתם מאמינים באלוהים אשר הקימו מן המתים והעניק לו כבוד רב, כך שאמונתכם ותקוותכם מבוססות באלוהים.

22היות שטוהרתם מאנוכיות ומשנאה כשהאמנתם במשיח ובבשורתו, אהבו איש את רעהו אהבה כנה ועזה. 23שהרי עתה נולדתם מחדש, לא מזרע שנשחת אלא מזרע בלתי נשחת, באמצעות דבר ה׳ החי וקיים. 24אכן, חיינו הנוכחיים יגיעו לקיצם; הם יבלו כעשב שמתייבש ומצהיב. כל דבר שהתפארנו בו יבול כפרח, 25אולם דבר ה׳ יעמוד לעולם!1‏.25 א 24‏-25 ראה ישעיהו מ 6‏-8 והבשורה אשר שמעתם היא דבר ה׳.