1 Petro 1 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Petro 1:1-25

1Ndine Petro, mtumwi wa Yesu Khristu.

Ndikulemba kalatayi kwa onse osankhidwa ndi Mulungu, alendo mʼdziko lapansi, obalalikira ku Ponto, Galatiya, Kapadokiya, Asiya ndi Bituniya. 2Mulungu Atate anakusankhani, atakudziwani kuyambira pachiyambi, ndipo Mzimu Woyera wakuyeretsani kuti mumvere Yesu Khristu ndikutsukidwa ndi magazi ake.

Chisomo ndi mtendere zikhale ndi inu mochuluka.

Kuyamika Mulungu Chifukwa cha Chiyembekezo Chamoyo

3Alemekezedwe Mulungu, Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu. Mwachifundo chake chachikulu anatibadwitsa kwatsopano, mʼchiyembekezo chamoyo pomuukitsa Yesu Khristu kwa akufa, 4kuti tidzalandire chuma chomwe sichingawonongeke, kuyipitsidwa kapena kufota. Chuma chimenechi akukusungirani kumwamba. 5Mwachikhulupiriro, mukusungidwa ndi mphamvu ya Mulungu mpaka chipulumutso chitafika chimene chinakonzedwa kuti adzachionetse nthawi yotsiriza. 6Zimenezi zikukondweretseni kwambiri, ngakhale tsopano, kwa kanthawi kochepa, mukumva zowawa mʼmayesero osiyanasiyana. 7Mayeserowa abwera nʼcholinga chakuti chikhulupiriro chanu, chimene ndi chamtengo woposa wa golide, amene amawonongeka ngakhale amayengedwa ndi moto, chitsimikizike kuti ndi chenicheni. Pamenepo ndiye mudzalandire mayamiko, ulemerero ndi ulemu pamene Yesu Khristu adzaoneka. 8Ngakhale kuti simunamuone, mumamukonda; ndipo ngakhale kuti simukumuona tsopano, mumamukhulupirira ndipo mumakondwera ndi chimwemwe chachikulu ndi chosaneneka. 9Motero mukulandira mphotho ya chikhulupiriro chanu, ndiyo chipulumutso cha moyo wanu.

10Kunena za chipulumutso chimenechi, aneneri amene ananeneratu za chisomo chimene chimabwera kwa inu, anafunafuna mofufuzafufuza za chipulumutsochi, 11kufuna kudziwa nthawi ndi momwe zidzachitikire zinthu zimene Mzimu wa Khristu amene ali mwa iwo ankanenera za kuvutika kwa Khristu, ndi ulemerero umene adzakhale nawo pambuyo pake. 12Mulungu anawawululira kuti ntchito yawoyo sankayigwira chifukwa cha iwo eni, koma chifukwa inu, pamene iwo ankayankhula zinthu zimene mwamva tsopano kuchokera kwa amene amalalikira Uthenga Wabwino mwamphamvu ya Mzimu Woyera wotumidwa kuchokera kumwamba. Ngakhale angelo amalakalaka kuona nawo zinthuzi.

Khalani Oyera Mtima

13Choncho konzani mtima wanu, khalani odziretsa; khazikitsani chiyembekezo chanu kotheratu pa chisomo chimene mudzapatsidwe pamene Yesu Khristu adzaonekera. 14Monga ana omvera, musatsatenso zilakolako zoyipa zomwe munali nazo pamene munali osadziwa. 15Koma monga amene anakuyitanani ndi woyera, inunso khalani oyera mtima mʼmakhalidwe anu wonse. 16Pakuti, kwalembedwa kuti, “Khalani oyera mtima, chifukwa Ine ndine Woyera.”

17Popeza mumapemphera kwa Atate amene amaweruza munthu aliyense mopanda tsankho molingana ndi zochita zake, pa nthawi imene muli alendo pa dziko lapansi khalani moopa Mulungu. 18Pakuti mukudziwa kuti simunawomboledwe ndi zinthu zimene zimawonongeka monga siliva kapena golide, kuchoka ku khalidwe lanu lachabe limene munalandira kwa makolo anu. 19Koma munawomboledwa ndi magazi a mtengowapatali a Khristu, Mwana Wankhosa wopanda banga kapena chilema. 20Iye anasankhidwa lisanalengedwe dziko lapansi, koma waonetsedwa chifukwa cha inu pa nthawi ino yotsiriza. 21Kudzera mwa Iye mumakhulupirira Mulungu, amene anamuukitsa kwa akufa namupatsa ulemerero. Nʼchifukwa chake chikhulupiriro ndi chiyembekezo chanu chili mwa Mulungu.

22Tsopano mwayeretsa mitima yanu pomvera choonadi, kuti muzikondana ndi abale anu, kukondana kwenikweni kochokera pansi pa mtima. 23Popeza mwabadwanso, osati ndi mbewu imene imawonongeka, koma imene siwonongeka, ndiye kuti ndi Mawu a Mulungu amoyo ndi okhalitsa. 24Pakuti,

“Anthu onse ali ngati udzu,

ndipo ulemerero wawo uli ngati duwa la kuthengo.

Udzu umafota ndipo duwa limathothoka,

25koma mawu a Ambuye adzakhala mpaka muyaya.”

Ndipo awa ndi mawu amene tinalalikira kwa inu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

彼得前書 1:1-25

1我是耶穌基督的使徒彼得,寫信給蒙上帝揀選,寄居在本都加拉太加帕多迦亞細亞庇推尼各地的人。 2你們蒙揀選是按照父上帝預先定好的旨意,藉著聖靈得以聖潔,好順服耶穌基督,並靠祂的血得到潔淨。

願上帝賜給你們豐豐富富的恩典和平安!

活潑的盼望

3願頌讚歸於我們主耶穌基督的父上帝!祂有無窮的憐憫,藉著耶穌基督從死裡復活使我們獲得重生,有活潑的盼望, 4可以承受那不會朽壞、沒有污點、不會衰殘、為你們存留在天上的產業。 5你們這些因信而蒙上帝用大能保守的人,必能得到那已經預備好、在末世要顯明的救恩。

6為此,即使現今你們必須暫時在百般試煉中忍受痛苦,也要滿懷喜樂。 7這樣,你們的信心經過試驗便顯明是真實的,比那經過火煉仍會壞掉的金子更加寶貴,使你們可以在耶穌基督顯現時得到稱讚、榮耀和尊貴。 8你們雖然沒有見過基督,卻愛祂;雖然現在看不見祂,卻信祂,並且有無法形容、充滿榮耀的喜樂。 9因為你們得到了信心帶來的果效,就是你們的靈魂得救。

10有關這救恩,那些預言恩典要臨到你們的眾先知早已詳細尋求查考了。 11基督的靈曾在他們心中指示他們,預言基督要受苦,然後得榮耀。他們便詳細查考這些事會在什麼時候、什麼情況下發生。 12他們得到啟示,知道他們傳講這些事不是為了自己,而是為了你們。現在,那些靠著從天上差來的聖靈向你們傳福音的人,已經將這些事傳給你們了。連天使也想把這些事看個明白。

要聖潔像主

13所以,要預備好你們的心,謹慎自律,專心盼望耶穌基督顯現時要帶給你們的恩典。 14你們既是順服的兒女,就不要再像從前無知的時候那樣放縱私慾。 15那呼召你們的是聖潔的,你們在一切事上也要聖潔。 16因為聖經上說:「你們要聖潔,因為我是聖潔的。」

17既然你們稱呼那位按各人的行為公正無私地審判人的上帝為父,就應該存著敬畏的心過你們在世上寄居的日子。 18要知道,你們從傳統的、沒有意義的生活中被救贖出來,不是靠金銀等會朽壞的東西, 19而是靠無瑕無疵的代罪羔羊——基督的寶血。 20基督是上帝在創世以前預先揀選的,卻在這末世為你們顯現。 21你們藉著基督信了使祂從死裡復活、賜祂榮耀的上帝,所以,你們的信心和盼望都在於上帝。

22你們既因順服真理,潔淨了自己的心,能夠真誠地愛弟兄姊妹,就當以清潔的心彼此切實相愛。 23你們獲得重生,不是藉著會腐爛的種子,而是藉著不會腐爛的種子——上帝活潑永存的道。 24因為

「芸芸眾生盡如草,

榮華不過草上花;

草必枯乾花必殘,

25唯有主道永長存。」

這道就是傳給你們的福音。