1 Mbiri 4 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 4:1-43

Mabanja Ena a Yuda

1Ana a Yuda anali awa:

Perezi, Hezironi, Karimi, Huri ndi Sobali.

2Reaya mwana wa Sobala anabereka Yahati, ndipo Yahati anabereka Ahumai ndi Lahadi. Awa anali mabanja a Azorati.

3Ana a Etamu anali awa:

Yezireeli, Isima ndi Idibasi. Dzina la mlongo wawo linali Hazeleliponi. 4Penueli anabereka Gedori, ndipo Ezeri anabereka Husa.

Awa anali ana a Huri, mwana wachisamba wa Efurata ndi abambo a Betelehemu.

5Asihuri abambo a Tekowa anali ndi akazi awiri, Hela ndi Naara.

6Naara anamuberekera Ahuzamu, Heferi, Temani ndi Haahasitari. Awa ndiwo anali ana a Naara.

7Ana a Hela:

Zereti, Zohari, Etinani, 8ndi Kozi, amene anali abambo ake a Anubi ndi Hazo-Beba ndi mabanja a Ahariheli mwana wa Harumi.

9Yabesi anali munthu wolemekezeka kwambiri kuposa abale ake. Amayi ake anamutcha Yabesi kutanthauza kuti, “Chifukwa ndinamubala ndi ululu wambiri.” 10Yabesi analira kwa Mulungu wa Israeli kuti, “Mundidalitse ndipo mukulitse dziko langa! Dzanja lanu likhale pa ine ndipo mundisunge kuti choyipa chisandigwere ndi kundisautsa.” Ndipo Mulungu anamupatsa chopempha chakecho.

11Kelubi, mʼbale wa Suha, anabereka Mehiri, amene anabereka Esitoni. 12Esitoni anabereka Beti-Rafa, Paseya ndi Tehina amene anabereka Iri Nahasi. Amenewa ndiwo anthu a ku Reka.

13Ana a Kenazi anali awa:

Otanieli ndi Seraya.

Ana a Otanieli anali awa:

Hatati ndi Meonotai. 14Meonotai anabereka Ofura.

Seraya anabereka Yowabu,

amene anabereka Ge-Harasimu. Anawatcha dzina ili chifukwa anthu ake anali amisiri.

15Ana a Kalebe mwana wa Yefune anali awa:

Iru, Ela ndi Naama.

Mwana wa Ela anali

Kenazi.

16Ana a Yehaleleli anali awa:

Zifi, Zifa, Tiriya ndi Asareli.

17Ana a Ezara anali awa:

Yeteri, Meredi, Eferi ndi Yaloni. Mmodzi mwa akazi a Meredi anabereka Miriamu, Samai ndi Isiba abambo ake a Esitemowa. 18(Mkazi wake wa Chiyuda anabereka Yaredi abambo ake a Gedori, Heberi abambo ake a Soko ndi Yekutieli abambo a Zanowa). Awa anali ana a mwana wamkazi wa Farao, Bitia, amene Meredi anakwatira.

19Ana a mkazi wa Hodiya, mlongo wa Nahamu anali awa:

abambo ake a Keila wa ku Garimi ndi Esitemowa wa ku Maaka.

20Ana a Simeoni anali awa:

Amnoni, Rina, Beni-Hanani ndi Tiloni.

Ana a Isi anali awa:

Zoheti ndi Beni-Zoheti.

21Ana a Sela mwana wa Yuda anali awa:

Eri amene anabereka Leka, Laada amene anabereka Maresa ndi mabanja a anthu owomba nsalu zofewa ndi zosalala a ku Beti-Asibeya, 22Yokimu, anthu a ku Kozeba, ndiponso Yowasi ndi Sarafi, amene ankalamulira Mowabu ndi Yasibu-Lehemu. (Nkhani zimenezi ndi zakalekale). 23Iwo anali owumba mbiya amene ankakhala ku Netaimu ndi Gederi. Ankakhala kumeneko ndi kumatumikira mfumu.

Simeoni

24Ana a Simeoni anali awa:

Nemueli, Yamini, Yaribu, Zera ndi Sauli;

25Salumu anali mwana wa Sauli, Mibisamu anali mwana wa Salumu ndipo Misima anali mwana wa Mibisamu.

26Zidzukulu za Misima zinali izi:

Hamueli, Zakuri ndi Simei.

27Simei anali ndi ana aamuna 16 ndi ana aakazi 6, koma abale ake sanabereke ana ambiri; kotero banja lawo silinakule ngati anthu ena a ku Yuda. 28Iwo amakhala ku Beeriseba, Molada, Hazari-Suwali, 29Biliha, Ezemu, Toladi, 30Betueli, Horima, Zikilagi, 31Beti-Marikaboti, Hazari-Susimu, Beti-Biri ndi Saaraimu. Iyi inali mizinda yawo mpaka pa nthawi ya ulamuliro wa Davide. 32Midzi yowazungulira inali Etamu, Aini, Rimoni, Tokeni ndi Asani, midzi isanu 33ndi midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baala. Awa anali malo awo okhalapo. Ndipo anasunga mbiri ya makolo awo.

34Mesobabu, Yamuleki, Yosa mwana wa Amaziya, 35Yoweli, Yehu mwana wa Yosibiya, mwana wa Seraya, mwana wa Asieli, 36komanso Eliyoenai, Yaakoba, Yesohaya, Asaya, Adieli, Yesimieli, Benaya, 37ndiponso Ziza mwana wa Sifi, mwana wa Aloni, mwana wa Yedaya, mwana wa Simiri, mwana wa Semaya.

38Anthu amene atchulidwawa anali atsogoleri a mabanja awo. Mabanja awo anakula kwambiri 39ndipo anakafika ku malire a Gedori ku chigwa cha kummawa kufuna msipu wodyetsa ziweto zawo. 40Anapeza msipu wobiriwira ndi wabwino ndipo dziko linali lalikulu, la mtendere ndi bata. Kumeneko kunkakhala fuko la Hamu poyamba.

41Anthu amene mayina awowa alembedwa, anabwera pa nthawi ya Hezekiya mfumu ya Yuda. Iwo anathira nkhondo fuko la Hamu mʼmalo awo amene amakhala komanso Ameuni amene anali kumeneko ndipo anawononga onsewo kotero kuti mbiri yawo simvekanso mpaka lero lino. Kotero iwo anakhala mʼmalo awo chifukwa kunali msipu wa ziweto zawo. 42Ndipo anthu 500 a fuko la Simeoni, motsogozedwa ndi Pelatiya, Neariya, Refaya ndi Uzieli, ana a Isi, analanda dziko lamapiri la Seiri. 43Iwo anapha Aamaleki otsala amene anali atapulumuka ndipo akukhala kumeneko mpaka lero lino.