1 Mbiri 29 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 29:1-30

Zopereka Zomangira Nyumba ya Mulungu

1Kenaka, mfumu Davide inati kwa gulu lonse: “Mwana wanga Solomoni amene Mulungu wamusankha ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Ntchitoyi ndi yayikulu chifukwa nyumba yaufumuyi si ya munthu, koma ndi ya Yehova Mulungu. 2Ine ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu zinthu zanga zonse, golide wopangira zinthu zagolide, siliva wopangira zinthu zasiliva ndi zitsulo zopangira zinthu zazitsulo, mkuwa wopangira zinthu zamkuwa ndi matabwa opangira zinthu zamatabwa komanso miyala yokongola ya onikisi yokongoletsera, miyala ya maonekedwe osiyanasiyana, ndi miyala yonse yosalala ndi miyala ya marabulo, zonsezi ndapereka zochuluka. 3Kupatulapo izi, ine modzipereka ku Nyumba ya Mulungu wanga, tsopano ndikupereka chuma changachanga cha golide ndi siliva ku Nyumba ya Mulungu wanga, kuwonjezera pa zimene ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu woyerayu: 4Matani 100 agolide (golide wa ku Ofiri) ndi matani 240 a siliva woyengeka bwino wokutira makoma a nyumba, 5zinthu zagolide ndi zinthu zasiliva, ndiponso zinthu zonse zimene anthu aluso adzagwiritse ntchito. Tsopano ndani amene akufuna kudzipatulira yekha kwa Yehova lero?”

6Tsono atsogoleri a mabanja, akuluakulu a mafuko a Israeli, olamulira asilikali 1,000, ndi olamulira asilikali 100, ndiponso akuluakulu onse amene amayangʼanira ntchito ya mfumu anapereka mwaufulu. 7Iwo anapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu matani 170 a golide, matani 340 a siliva, matani 620 a mkuwa ndi matani 3,400 a chitsulo. 8Aliyense amene anali ndi miyala yokongola anayipereka ku nyumba yosungiramo chuma cha Nyumba ya Yehova ndipo amene ankayangʼanira anali Yehieli Mgeresoni. 9Anthu anakondwa chifukwa cha kupereka mwaufulu kwa atsogoleri awo, pakuti anapereka kwa Yehova mwaufulu ndiponso ndi mtima wonse. Nayenso mfumu Davide anakondwera kwambiri.

Pemphero la Davide

10Davide anatamanda Yehova pamaso pa gulu lonse, ponena kuti,

“Mutamandidwe Inu Yehova

Mulungu wa kholo lathu Israeli

kuchokera muyaya mpaka muyaya.

11Wanu, Inu Yehova ndi ukulu ndi mphamvu,

ulemerero ndiponso ufumu ndi kukongola.

Pakuti zinthu zonse zakumwamba ndi pa dziko lapansi ndi zanu.

Wanu, Inu Yehova ndi ufumu;

Inu ndinu wokwezeka ndipo ndinu mtsogoleri wa zonse.

12Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu;

Inu ndinu wolamulira zinthu zonse.

Mʼdzanja lanu muli nyonga ndi mphamvu,

kukweza ndi kupereka nyonga kwa onse.

13Tsopano Mulungu wathu, ife tikukuthokozani

ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.

14“Koma ine ndine yani, ndipo anthu anga ndani, kuti tikupatsani mowolowamanja motere? Zinthu zonse zimachokera kwa Inu, ndipo ife takupatsani zomwe zimachokera mʼdzanja lanu. 15Ife ndife anthu osadziwika ndiponso alendo pamaso panu, monga analili makolo athu. Masiku anthu pa dziko lapansi ali ngati chithunzithunzi, wopanda chiyembekezo. 16Inu Yehova Mulungu wathu, zinthu zonse zimene tapereka kumangira Nyumba yanu zachokera mʼdzanja lanu ndipo zonsezi ndi zanu. 17Mulungu wanga, ine ndikudziwa kuti mumayesa mtima ndipo mumakondwera ndi anthu angwiro. Zinthu zonsezi ndapereka mwaufulu ndi cholinga chabwino. Ndipo tsopano ndaona ndi chimwemwe momwe anthu anu amene ali pano akuperekera mwaufulu kwa Inu. 18Inu Yehova Mulungu wa makolo athu Abrahamu, Isake ndi Israeli, mukhazikitse chofuna ichi mʼmitima ya anthu anu kwamuyaya, ndipo mukhazikitse mtima wokhulupirika kwa Inu. 19Ndipo mumupatse mwana wanga Solomoni mtima wodzipereka kwathunthu kwa Inu kuti asunge malamulo anu, zofuna ndi malangizo anu. Achite chilichonse pomanga nyumba yaufumu imene ine ndayipezera zofunika zonse.”

20Kenaka mfumu Davide inati kwa gulu lonse, “Tamandani Yehova Mulungu wanu.” Kotero onse anatamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anawerama pansi ndi kugona chafufumimba pamaso pa Yehova ndi mfumu.

Solomoni Avomerezedwa Monga Mfumu

21Mmawa mwake anthu anapereka nsembe zosiyanasiyana ndi nsembe zopsereza kwa Yehova; ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa zamphongo 1,000 ndi ana ankhosa 1,000, pamodzi ndi nsembe yachakumwa ndi nsembe zina zambiri zoperekera Aisraeli onse. 22Tsiku limeneli, iwo anadya ndi kumwa mosangalala pamaso pa Yehova ndipo anavomereza Solomoni mwana wa Davide kukhala mfumu yawo kachiwiri.

Anamudzoza pamaso pa Yehova kukhala wolamulira wawo ndipo Zadoki anadzozedwa kukhala wansembe. 23Ndipo Solomoni ankakhala pa mpando waufumu wa Yehova monga mfumu mʼmalo mwa Davide abambo ake. Iye analemera ndipo Aisraeli onse ankamumvera. 24Akuluakulu onse a ankhondo ndi anthu amphamvu, pamodzinso ndi ana onse aamuna a mfumu Davide, analonjeza kumvera mfumu Solomoni.

25Yehova anamukweza kwambiri Solomoni pamaso pa Aisraeli onse ndi kumupatsa ulemerero waufumu umene sunapatsidwepo kwa mfumu ina iliyonse ya Israeli.

Imfa ya Davide

26Davide mwana wa Yese anali mfumu ya Aisraeli onse. 27Iye analamulira Israeli kwa zaka makumi anayi; zaka zisanu ndi ziwiri ali ku Hebroni ndi zaka 33 ali ku Yerusalemu. 28Iye anamwalira atakalamba kwambiri, atakhala ndi moyo wautali, chuma ndi ulemu. Solomoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

29Tsono zonse zimene mfumu Davide anachita, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mneneri Samueli, mʼbuku la mneneri Natani ndi mʼbuku la mneneri Gadi, 30pamodzi ndi tsatanetsatane wa mbiri ya ulamuliro wake ndi mphamvu zake, ndi zonse zomwe zinamuzungulira iye ndi Israeli ndiponso mafumu a mayiko ena onse.

New International Version

1 Chronicles 29:1-30

Gifts for Building the Temple

1Then King David said to the whole assembly: “My son Solomon, the one whom God has chosen, is young and inexperienced. The task is great, because this palatial structure is not for man but for the Lord God. 2With all my resources I have provided for the temple of my God—gold for the gold work, silver for the silver, bronze for the bronze, iron for the iron and wood for the wood, as well as onyx for the settings, turquoise,29:2 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain. stones of various colors, and all kinds of fine stone and marble—all of these in large quantities. 3Besides, in my devotion to the temple of my God I now give my personal treasures of gold and silver for the temple of my God, over and above everything I have provided for this holy temple: 4three thousand talents29:4 That is, about 110 tons or about 100 metric tons of gold (gold of Ophir) and seven thousand talents29:4 That is, about 260 tons or about 235 metric tons of refined silver, for the overlaying of the walls of the buildings, 5for the gold work and the silver work, and for all the work to be done by the craftsmen. Now, who is willing to consecrate themselves to the Lord today?”

6Then the leaders of families, the officers of the tribes of Israel, the commanders of thousands and commanders of hundreds, and the officials in charge of the king’s work gave willingly. 7They gave toward the work on the temple of God five thousand talents29:7 That is, about 190 tons or about 170 metric tons and ten thousand darics29:7 That is, about 185 pounds or about 84 kilograms of gold, ten thousand talents29:7 That is, about 380 tons or about 340 metric tons of silver, eighteen thousand talents29:7 That is, about 675 tons or about 610 metric tons of bronze and a hundred thousand talents29:7 That is, about 3,800 tons or about 3,400 metric tons of iron. 8Anyone who had precious stones gave them to the treasury of the temple of the Lord in the custody of Jehiel the Gershonite. 9The people rejoiced at the willing response of their leaders, for they had given freely and wholeheartedly to the Lord. David the king also rejoiced greatly.

David’s Prayer

10David praised the Lord in the presence of the whole assembly, saying,

“Praise be to you, Lord,

the God of our father Israel,

from everlasting to everlasting.

11Yours, Lord, is the greatness and the power

and the glory and the majesty and the splendor,

for everything in heaven and earth is yours.

Yours, Lord, is the kingdom;

you are exalted as head over all.

12Wealth and honor come from you;

you are the ruler of all things.

In your hands are strength and power

to exalt and give strength to all.

13Now, our God, we give you thanks,

and praise your glorious name.

14“But who am I, and who are my people, that we should be able to give as generously as this? Everything comes from you, and we have given you only what comes from your hand. 15We are foreigners and strangers in your sight, as were all our ancestors. Our days on earth are like a shadow, without hope. 16Lord our God, all this abundance that we have provided for building you a temple for your Holy Name comes from your hand, and all of it belongs to you. 17I know, my God, that you test the heart and are pleased with integrity. All these things I have given willingly and with honest intent. And now I have seen with joy how willingly your people who are here have given to you. 18Lord, the God of our fathers Abraham, Isaac and Israel, keep these desires and thoughts in the hearts of your people forever, and keep their hearts loyal to you. 19And give my son Solomon the wholehearted devotion to keep your commands, statutes and decrees and to do everything to build the palatial structure for which I have provided.”

20Then David said to the whole assembly, “Praise the Lord your God.” So they all praised the Lord, the God of their fathers; they bowed down, prostrating themselves before the Lord and the king.

Solomon Acknowledged as King

21The next day they made sacrifices to the Lord and presented burnt offerings to him: a thousand bulls, a thousand rams and a thousand male lambs, together with their drink offerings, and other sacrifices in abundance for all Israel. 22They ate and drank with great joy in the presence of the Lord that day.

Then they acknowledged Solomon son of David as king a second time, anointing him before the Lord to be ruler and Zadok to be priest. 23So Solomon sat on the throne of the Lord as king in place of his father David. He prospered and all Israel obeyed him. 24All the officers and warriors, as well as all of King David’s sons, pledged their submission to King Solomon.

25The Lord highly exalted Solomon in the sight of all Israel and bestowed on him royal splendor such as no king over Israel ever had before.

The Death of David

26David son of Jesse was king over all Israel. 27He ruled over Israel forty years—seven in Hebron and thirty-three in Jerusalem. 28He died at a good old age, having enjoyed long life, wealth and honor. His son Solomon succeeded him as king.

29As for the events of King David’s reign, from beginning to end, they are written in the records of Samuel the seer, the records of Nathan the prophet and the records of Gad the seer, 30together with the details of his reign and power, and the circumstances that surrounded him and Israel and the kingdoms of all the other lands.