1 Mbiri 29 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 29:1-30

Zopereka Zomangira Nyumba ya Mulungu

1Kenaka, mfumu Davide inati kwa gulu lonse: “Mwana wanga Solomoni amene Mulungu wamusankha ndi wamngʼono ndipo sadziwa zambiri. Ntchitoyi ndi yayikulu chifukwa nyumba yaufumuyi si ya munthu, koma ndi ya Yehova Mulungu. 2Ine ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu zinthu zanga zonse, golide wopangira zinthu zagolide, siliva wopangira zinthu zasiliva ndi zitsulo zopangira zinthu zazitsulo, mkuwa wopangira zinthu zamkuwa ndi matabwa opangira zinthu zamatabwa komanso miyala yokongola ya onikisi yokongoletsera, miyala ya maonekedwe osiyanasiyana, ndi miyala yonse yosalala ndi miyala ya marabulo, zonsezi ndapereka zochuluka. 3Kupatulapo izi, ine modzipereka ku Nyumba ya Mulungu wanga, tsopano ndikupereka chuma changachanga cha golide ndi siliva ku Nyumba ya Mulungu wanga, kuwonjezera pa zimene ndapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu woyerayu: 4Matani 100 agolide (golide wa ku Ofiri) ndi matani 240 a siliva woyengeka bwino wokutira makoma a nyumba, 5zinthu zagolide ndi zinthu zasiliva, ndiponso zinthu zonse zimene anthu aluso adzagwiritse ntchito. Tsopano ndani amene akufuna kudzipatulira yekha kwa Yehova lero?”

6Tsono atsogoleri a mabanja, akuluakulu a mafuko a Israeli, olamulira asilikali 1,000, ndi olamulira asilikali 100, ndiponso akuluakulu onse amene amayangʼanira ntchito ya mfumu anapereka mwaufulu. 7Iwo anapereka ku ntchito ya Nyumba ya Mulungu matani 170 a golide, matani 340 a siliva, matani 620 a mkuwa ndi matani 3,400 a chitsulo. 8Aliyense amene anali ndi miyala yokongola anayipereka ku nyumba yosungiramo chuma cha Nyumba ya Yehova ndipo amene ankayangʼanira anali Yehieli Mgeresoni. 9Anthu anakondwa chifukwa cha kupereka mwaufulu kwa atsogoleri awo, pakuti anapereka kwa Yehova mwaufulu ndiponso ndi mtima wonse. Nayenso mfumu Davide anakondwera kwambiri.

Pemphero la Davide

10Davide anatamanda Yehova pamaso pa gulu lonse, ponena kuti,

“Mutamandidwe Inu Yehova

Mulungu wa kholo lathu Israeli

kuchokera muyaya mpaka muyaya.

11Wanu, Inu Yehova ndi ukulu ndi mphamvu,

ulemerero ndiponso ufumu ndi kukongola.

Pakuti zinthu zonse zakumwamba ndi pa dziko lapansi ndi zanu.

Wanu, Inu Yehova ndi ufumu;

Inu ndinu wokwezeka ndipo ndinu mtsogoleri wa zonse.

12Chuma ndi ulemu zimachokera kwa Inu;

Inu ndinu wolamulira zinthu zonse.

Mʼdzanja lanu muli nyonga ndi mphamvu,

kukweza ndi kupereka nyonga kwa onse.

13Tsopano Mulungu wathu, ife tikukuthokozani

ndi kutamanda dzina lanu laulemerero.

14“Koma ine ndine yani, ndipo anthu anga ndani, kuti tikupatsani mowolowamanja motere? Zinthu zonse zimachokera kwa Inu, ndipo ife takupatsani zomwe zimachokera mʼdzanja lanu. 15Ife ndife anthu osadziwika ndiponso alendo pamaso panu, monga analili makolo athu. Masiku anthu pa dziko lapansi ali ngati chithunzithunzi, wopanda chiyembekezo. 16Inu Yehova Mulungu wathu, zinthu zonse zimene tapereka kumangira Nyumba yanu zachokera mʼdzanja lanu ndipo zonsezi ndi zanu. 17Mulungu wanga, ine ndikudziwa kuti mumayesa mtima ndipo mumakondwera ndi anthu angwiro. Zinthu zonsezi ndapereka mwaufulu ndi cholinga chabwino. Ndipo tsopano ndaona ndi chimwemwe momwe anthu anu amene ali pano akuperekera mwaufulu kwa Inu. 18Inu Yehova Mulungu wa makolo athu Abrahamu, Isake ndi Israeli, mukhazikitse chofuna ichi mʼmitima ya anthu anu kwamuyaya, ndipo mukhazikitse mtima wokhulupirika kwa Inu. 19Ndipo mumupatse mwana wanga Solomoni mtima wodzipereka kwathunthu kwa Inu kuti asunge malamulo anu, zofuna ndi malangizo anu. Achite chilichonse pomanga nyumba yaufumu imene ine ndayipezera zofunika zonse.”

20Kenaka mfumu Davide inati kwa gulu lonse, “Tamandani Yehova Mulungu wanu.” Kotero onse anatamanda Yehova, Mulungu wa makolo awo ndipo anawerama pansi ndi kugona chafufumimba pamaso pa Yehova ndi mfumu.

Solomoni Avomerezedwa Monga Mfumu

21Mmawa mwake anthu anapereka nsembe zosiyanasiyana ndi nsembe zopsereza kwa Yehova; ngʼombe zamphongo 1,000, nkhosa zamphongo 1,000 ndi ana ankhosa 1,000, pamodzi ndi nsembe yachakumwa ndi nsembe zina zambiri zoperekera Aisraeli onse. 22Tsiku limeneli, iwo anadya ndi kumwa mosangalala pamaso pa Yehova ndipo anavomereza Solomoni mwana wa Davide kukhala mfumu yawo kachiwiri.

Anamudzoza pamaso pa Yehova kukhala wolamulira wawo ndipo Zadoki anadzozedwa kukhala wansembe. 23Ndipo Solomoni ankakhala pa mpando waufumu wa Yehova monga mfumu mʼmalo mwa Davide abambo ake. Iye analemera ndipo Aisraeli onse ankamumvera. 24Akuluakulu onse a ankhondo ndi anthu amphamvu, pamodzinso ndi ana onse aamuna a mfumu Davide, analonjeza kumvera mfumu Solomoni.

25Yehova anamukweza kwambiri Solomoni pamaso pa Aisraeli onse ndi kumupatsa ulemerero waufumu umene sunapatsidwepo kwa mfumu ina iliyonse ya Israeli.

Imfa ya Davide

26Davide mwana wa Yese anali mfumu ya Aisraeli onse. 27Iye analamulira Israeli kwa zaka makumi anayi; zaka zisanu ndi ziwiri ali ku Hebroni ndi zaka 33 ali ku Yerusalemu. 28Iye anamwalira atakalamba kwambiri, atakhala ndi moyo wautali, chuma ndi ulemu. Solomoni mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

29Tsono zonse zimene mfumu Davide anachita, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zalembedwa mʼbuku la mneneri Samueli, mʼbuku la mneneri Natani ndi mʼbuku la mneneri Gadi, 30pamodzi ndi tsatanetsatane wa mbiri ya ulamuliro wake ndi mphamvu zake, ndi zonse zomwe zinamuzungulira iye ndi Israeli ndiponso mafumu a mayiko ena onse.

La Bible du Semeur

1 Chroniques 29:1-30

Les dons du roi pour la construction du Temple

1Puis le roi David dit à toute l’assemblée : Mon fils Salomon, le seul que Dieu ait choisi, est jeune et inexpérimenté, alors que l’ouvrage est immense, car ce n’est pas pour un homme qu’il s’agit de construire un palais, mais bien pour l’Eternel Dieu. 2Quant à moi, j’ai consacré tous mes efforts à préparer pour le temple de mon Dieu de l’or, de l’argent, du bronze, du fer et du bois pour tout ce qui est à fabriquer avec ces divers matériaux. J’ai préparé aussi des pierres d’onyx et des pierres à enchâsser, des pierres brillantes et de diverses couleurs, toutes sortes de pierres précieuses et des blocs de marbre blanc en abondance29.2 Voir 22.5.. 3De plus, par amour pour le temple de Dieu, je donne pour sa construction des biens précieux en or et en argent que je possède personnellement, en plus de tout ce que j’ai préparé pour le sanctuaire. 4Il y a dans mes réserves cent tonnes d’or pur d’Ophir29.4 Région souvent mentionnée (1 R 10.11 ; Jb 28.16) comme lieu de provenance de l’or le plus pur (voir note 1 R 9.28). et deux cent cinquante tonnes d’argent affiné pour recouvrir les parois des bâtiments. 5Cet or et cet argent sont destinés à la confection de tout ce qui doit être en or et en argent, ainsi qu’à tous les travaux que les artisans auront à exécuter. A présent, qui d’entre vous est prêt à donner volontairement et de façon généreuse pour l’Eternel ?

Les dons du peuple pour la construction du Temple

6Alors les chefs des groupes familiaux et des tribus d’Israël, les chefs des « milliers » et des « centaines » et les responsables des affaires du roi offrirent des dons volontaires. 7Ils remirent spontanément pour le temple de Dieu cent soixante-dix tonnes d’or, dix mille pièces d’or, plus de trois cents tonnes d’argent, quelque six cents tonnes de bronze et plus de trois mille tonnes de fer. 8Ceux qui possédaient des pierres précieuses les confièrent à Yehiel le Guershonite pour le trésor du temple de l’Eternel. 9Le peuple se réjouit de ses dons volontaires, car c’était d’un cœur sans partage qu’ils les avaient faits à l’Eternel. Le roi David en éprouva lui aussi une très grande joie.

Prière de reconnaissance

10David bénit l’Eternel devant toute l’assemblée en disant :

Béni sois-tu à tout jamais, ╵ô Eternel,

Dieu de notre ancêtre Israël !

11A toi, Eternel, appartiennent ╵la grandeur, la puissance ╵et la magnificence,

et la gloire et la majesté.

Car tout ce qui est dans le ciel ╵et sur la terre ╵est à toi, Eternel.

C’est à toi qu’appartient le règne,

tu es le souverain ╵au-dessus de tout être29.11 Cf. Mt 6.13..

12Et c’est de toi que viennent ╵la richesse et la gloire.

Tu domines sur tout

et dans ta main résident ╵la force et la puissance,

tu détiens le pouvoir ╵d’élever qui tu veux ╵et de le rendre fort.

13C’est pourquoi, notre Dieu, ╵nous te louons,

nous célébrons ta gloire.

14Car, qui donc suis-je,

et qui donc est mon peuple

pour avoir les moyens ╵de t’offrir de tels dons ?

Tout cela vient de toi,

et c’est de ta main même ╵que nous avons reçu ╵ce que nous te donnons.

15Nous sommes devant toi ╵comme des étrangers, des hôtes, ╵tout comme nos ancêtres.

Notre vie sur la terre ╵est aussi éphémère ╵qu’une ombre passagère, ╵qui passe sans espoir.

16Eternel, notre Dieu, ╵c’est de ta main que vient ╵toute cette fortune

que nous venons de réunir ╵pour te bâtir un temple ╵qui portera ton nom, ╵toi qui es saint.

Tout cela t’appartient.

17Je le sais, ô mon Dieu, ╵tu sondes notre cœur

et tu as du plaisir ╵lorsque quelqu’un est droit.

Eh bien, c’est d’un cœur droit ╵que je t’ai apporté ╵tous ces dons volontaires,

et j’ai vu avec joie ╵ton peuple ici présent ╵t’apporter ses dons volontaires.

18O Eternel, Dieu d’Abraham, ╵d’Isaac et d’Israël, nos pères,

conserve pour toujours ╵dans le cœur de ton peuple ╵ces dispositions, ces pensées,

et maintiens fermement ╵leur cœur tourné vers toi !

19A mon fils Salomon ╵donne un cœur sans partage

afin qu’il obéisse ╵à tes commandements,

tes ordonnances et tes lois, ╵et les applique tous,

et qu’il bâtisse le palais29.19 Autre traduction : qu’il exécute tout pour bâtir le palais. ╵en vue duquel j’ai fait ╵tous ces préparatifs.

L’onction royale de Salomon

20Là-dessus, David dit à toute l’assemblée : Bénissez l’Eternel, votre Dieu !

Alors toute l’assemblée loua l’Eternel, le Dieu de ses ancêtres. Ils s’inclinèrent et se prosternèrent devant l’Eternel et devant le roi. 21Le lendemain, ils offrirent des sacrifices et des holocaustes à l’Eternel : mille taureaux, mille béliers et mille agneaux, accompagnés des offrandes de vin requises29.21 Les libations accompagnent obligatoirement les sacrifices (voir Ex 29.40-41 ; Nb 15.1-16). ; et ils offrirent un grand nombre de sacrifices pour tout Israël. 22Ils mangèrent et burent ce jour-là devant l’Eternel dans de grandes réjouissances. Pour la seconde fois29.22 Voir 1 R 1 ; 1 Ch 23.1., ils proclamèrent roi Salomon, fils de David, et lui conférèrent l’onction au nom de l’Eternel pour être leur chef. Ils établirent aussi par l’onction Tsadoq comme prêtre. 23Salomon prit place sur le trône de l’Eternel, pour régner à la place de son père David. Il l’occupa avec succès et tout Israël lui obéit. 24Tous les chefs, et les soldats, et même tous les fils du roi David se soumirent à lui. 25L’Eternel éleva au plus haut point le prestige de Salomon aux yeux de tout Israël, et il rendit son règne plus éclatant que celui de tous ses prédécesseurs, comme roi sur Israël.

La mort de David

(1 R 2.10-12)

26David, fils d’Isaï, avait régné sur tout Israël. 27Il avait régné quarante ans sur Israël, sept ans à Hébron29.27 De 1010 à 1003 av. J.-C. et trente-trois ans à Jérusalem29.27 De 1003 à 970 av. J.-C..

28Et il mourut au terme d’une heureuse vieillesse, rassasié de jours, de richesses et de gloire. Son fils Salomon lui succéda sur le trône.

29Les faits et gestes du roi David, des premiers aux derniers, sont cités dans les Annales du prophète Samuel, dans les Annales du prophète Nathan, et dans les Annales du prophète Gad. 30On y raconte tout son règne, sa puissance, et tout ce qui lui est arrivé, ainsi qu’à Israël, et à tous les royaumes de la région.