1 Mbiri 26 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 26:1-32

Alonda a pa Zipata

1Magulu a alonda a pa zipata:

Kuchokera ku banja la Kora: Meselemiya mwana wa Kore, mmodzi mwa ana a Asafu.

2Meselemiya anali ndi ana awa:

woyamba Zekariya,

wachiwiri Yediaeli,

wachitatu Zebadiya,

wachinayi Yatinieli,

3wachisanu Elamu,

wachisanu ndi chimodzi Yehohanani,

ndipo wachisanu ndi chiwiri Elihunai.

4Obedi-Edomu analinso ndi ana awa:

woyamba Semaya,

wachiwiri Yehozabadi,

wachitatu Yowa,

wachinayi Sakara,

wachisanu Netaneli,

5wachisanu ndi chimodzi Amieli,

wachisanu ndi chiwiri Isakara

ndipo wachisanu ndi chitatu Peuletayi.

(Pakuti Mulungu anadalitsa Obedi-Edomu).

6Mwana wake Semaya analinso ndi ana amene anali atsogoleri mʼbanja la abambo awo chifukwa anali anthu amphamvu. 7Ana a Semaya anali: Otini, Refaeli, Obedi ndi Elizabadi; abale ake, Elihu ndi Semakiya, analinso anthu amphamvu. 8Onsewa anali adzukulu a Obedi-Edomu. Iwo ndi ana awo ndiponso abale awo anali anthu aluso ndi amphamvu pogwira ntchito. Zidzukulu zonse za Obedi-Edomu zinalipo 62.

9Meselemiya anali ndi ana ndi abale ake amene anali aluso ndipo onse analipo 18.

10Hosa Mmerari anali ndi ana awa: woyamba anali Simiri (ngakhale kuti iye sanali woyamba kubadwa, abambo ake anamusankha kuti akhale mtsogoleri), 11wachiwiri Hilikiya, wachitatu Tebaliya ndipo wachinayi Zekariya. Ana ndi abale onse a Hosa analipo 13.

12Magulu amenewa a alonda a pa zipata, motsogozedwa ndi atsogoleri awo, anali ndi ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova, monga momwe amachitira abale awo. 13Iwo anachita maere mwa mabanja awo aangʼono ndi aakulu omwe kuti apeze mlonda pa chipata chilichonse.

14Maere a chipata chakummwa anagwera Selemiya. Maere anachitikanso chifukwa cha mwana wake Zekariya, phungu wanzeru ndipo maere a chipata chakumpoto anagwera iye. 15Maere a chipata chakummwera anagwera Obedi-Edomu, ndipo maere a nyumba yosungiramo katundu anagwera ana ake. 16Maere a chipata chakumadzulo ndi chipata cha Saleketi ku msewu wa ku mtunda anagwera Supimu ndi Hosa.

Mlonda ankayangʼanana ndi mlonda mnzake: 17Mbali ya kummawa kunkakhala Alevi 6 pa tsiku, kumpoto anayi pa tsiku, kummwera anayi pa tsiku ndipo awiri ankakhala pa nyumba yosungiramo katundu. 18Ndipo ku bwalo cha kumadzulo, anayi amakhala mu msewu ndi awiri pabwalo penipeni.

19Awa anali magulu a alonda a pa zipata amene anali zidzukulu za Kora ndi Merari.

Asungichuma ndi Akuluakulu Ena

20Abale awo Alevi, motsogozedwa ndi Ahiya, anali oyangʼanira chuma cha nyumba ya Mulungu ndi zinthu zoperekedwa kwa Mulungu.

21Adzukulu a Ladani, mmodzi mwa ana a Geresoni, amene anali atsogoleri a mabanja a Ageresoni, anali awa: Yehieli, 22ana a Yehieli, Zetamu ndi mʼbale wake Yoweli. Iwo amayangʼanira chuma cha ku Nyumba ya Mulungu wa Yehova.

23Kuchokera ku banja la Amramu, banja la Aizihara, banja la Ahebroni ndi banja la Auzieli:

24Subaeli, chidzukulu cha Geresomu, mwana wa Mose, anali mkulu woyangʼanira chuma. 25Abale ake obadwa mwa Eliezara, anali Rekabiya mwana wake, Yesaya mwana wake, Yoramu mwana wake, Zikiri mwana wake ndi Selomiti mwana wake. 26Selomiti ndi abale ake amayangʼanira zinthu zonse zoperekedwa kwa Mulungu ndi mfumu Davide, atsogoleri a mabanja amene anali olamulira ankhondo 1,000, olamulira ankhondo 100, ndi olamulira ankhondo ena. 27Zina zofunkha ku nkhondo anazipereka kuti zikhale zokonzera Nyumba ya Yehova. 28Ndipo zonse zimene zinaperekedwa ndi Mlosi Samueli, Sauli mwana wa Kisi, Abineri mwana wa Neri ndiponso Yowabu mwana wa Zeruya ndi zinthu zonse zimene zinkaperekedwa zimasungidwa ndi Selomiti ndi abale ake.

29Kuchokera ku banja la Izihari: Kenaniya ndi ana ake anapatsidwa ntchito kutali ndi Nyumba ya Mulungu ngati akuluakulu ndi oweruza Israeli.

30Kuchokera ku banja la Ahebroni: Hasabiya ndi abale ake, anthu anzeru 1,700. Iwo ankayangʼanira ntchito zonse za Yehova ndi ntchito yonse ya mfumu cha kumadzulo kwa Yorodani. 31Pa banja la Ahebroni, Yeriya anali mtsogoleri monga mwa mbiri ya mibado ya mabanja awo. Mʼchaka cha 40 cha ufumu wa Davide, panachitika kafukufuku ndipo ena mwa anthu aluso a banja la Hebroni anapezeka kuti anali ku Yazeri ku Giliyadi. 32Yeriya anali ndi abale 2,700 amene anali aluso ndiponso atsogoleri a mabanja. Mfumu Davide anawayika iwowa kuti aziyangʼanira fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase pa zinthu zonse za Mulungu ndi za mfumu.

New Russian Translation

1 Паралипоменон 26:1-32

Распределение привратников

1Вот распределение привратников:

из корахитов: Мешелемия, сын Коре, один из сыновей Асафа.

2У Мешелемии были сыновья:

первенец Захария,

второй сын – Иедиаил,

третий – Зевадия,

четвертый – Иафниил,

3пятый – Елам,

шестой – Иоханан

и седьмой – Элиегоэнай.

4У Овид-Эдома тоже были сыновья:

первенец Шемая,

второй сын – Иегозавад,

третий – Иоах,

четвертый – Сахар,

пятый – Нафанаил,

5шестой – Аммиил,

седьмой – Иссахар

и восьмой – Пеульфай.

(Ведь Бог благословил Овид-Эдома).

6У его сына Шемаи тоже родились сыновья, которые были вождями своего клана, потому что были очень способными людьми. 7Сыновья Шемаи: Офни, Рефаил, Овид и Элзавад; его родственники Элигу и Семахия тоже были очень способными людьми. 8Все они были потомками Овид-Эдома. Они сами, их сыновья и родственники были очень способными людьми, прилежными в работе. – Всего их было у Овид-Эдома шестьдесят два человека.

9У Мешелемии было восемнадцать сыновей и родственников, которые также были способными людьми.

10У мераритянина Хосы были сыновья: первый Шимрий (хотя он и не был первенцем, его отец сделал его главным), 11второй Хелкия, третий Тевалия и четвертый Захария. Сыновей и родственников Хосы было тринадцать человек.

12Эти отделения привратников – согласно тому, кто был их начальником, – имели обязанности в служении в доме Господа, как и их родственники. 13Они бросали жребии по своим кланам на каждые ворота – молодой наравне со старым.

14Восточные ворота выпали по жребию Шелемии26:14 Вариант имени Мешелемия; см. 26:2. Затем был брошен жребий для его сына Захарии, мудрого советчика, и ему выпали Северные ворота. 15Южные ворота выпали по жребию Овид-Эдому, а кладовые – его сыновьям. 16Западные ворота и ворота Шаллехет на верхней дороге выпали по жребию Шупиму и Хосе.

Одна стража стояла напротив другой: 17шестеро левитов каждый день стояли на восточной стороне, четверо на северной, четверо на южной и по двое у кладовых. 18Что же до западной колоннады, то четверо стояли там у дороги и двое – внутри самой колоннады.

19Так были распределены привратники, потомки Кораха и Мерари.

Распределение хранителей сокровищницы

20Их собратьям-левитам были вверены сокровищницы Божьего дома и сокровищницы для посвященных вещей.

21Потомки Лаедана, которые были гершонитами по линии Лаедана и главами семейств, происходивших от гершонита Лаедана: Иехиил. 22Сыновья Иехиила: Зетам и его брат Иоиль. Им были вверены сокровищницы Господнего дома.

23Из амрамитов, ицгаритов, хевронитов и узиилитов:

24Шевуил, потомок сына Моисея Гершома, был главным смотрителем за сокровищницами. 25Его родственники через Элиезера: сын Элиезера Рехавия, отец Иешаии, отца Иорама, отца Зихрия, отца Шеломита. 26Шеломиту и его родственникам были вверены все сокровищницы для вещей, посвященных царем Давидом, главами семейств, которые были тысячниками, сотниками и военачальниками. 27Часть добычи, взятой в сражении, они посвящали на поддержание Господнего дома. 28Все, что было посвящено провидцем Самуилом, Саулом, сыном Киша, Авнером, сыном Нира, и Иоавом, сыном Саруи, и все прочие посвященные вещи были доверены Шеломиту и его родственникам.

29Из ицгаритов: Хенании и его сыновьям были определены обязанности за пределами дома – они были сановниками и судьями над Израилем.

30Из хевронитов: Хашавия и его родственники – тысяча семьсот способных людей – отвечали в Израиле к западу от Иордана за всю работу в служении Господу и на царской службе. 31Вождем у хевронитов был Иерия. (В сороковой год правления Давида родословные записи хевронитян были исследованы и в Иазере Галаадском нашлись очень способные люди из хевронитов.) 32У Иерии было две тысячи семьсот родственников, очень способных людей, глав семейств, и царь Давид поставил их над родами Рувима, Гада и половиной рода Манассии во всяком Божьем деле и во всех делах царя.