1 Mbiri 24 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 24:1-31

Magulu a Ansembe

1Magulu a ana a Aaroni anali awa:

Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara. 2Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe. 3Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira. 4Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara. 5Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.

6Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.

7Maere woyamba anagwera Yehoyaribu,

achiwiri anagwera Yedaya,

8achitatu anagwera Harimu,

achinayi anagwera Seorimu,

9achisanu anagwera Malikiya,

achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,

10achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi,

achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,

11achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa,

a khumi anagwera Sekaniya,

12a 11 anagwera Eliyasibu,

a 12 anagwera Yakimu,

13a 13 anagwera Hupa,

a 14 anagwera Yesebeabu,

14a 15 anagwera Biliga,

a 16 anagwera Imeri,

15a 17 anagwera Heziri,

a 18 anagwera Hapizezi,

16a 19 anagwera Petahiya,

a 20 anagwera Ezekieli,

17a 21 anagwera Yakini,

a 22 anagwera Gamuli,

18a 23 anagwera Delaya,

ndipo a 24 anagwera Maaziya.

19Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.

Alevi Ena Onse

20Za zidzukulu zina zonse za Levi:

Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli;

kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.

21Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake:

Mtsogoleri anali Isiya.

22Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti;

kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.

23Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.

24Mwana wa Uzieli: Mika;

kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.

25Mʼbale wa Mika: Isiya;

kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.

26Ana a Merari: Mahili ndi Musi.

Mwana wa Yaaziya: Beno.

27Ana a Merari:

Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.

28Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.

29Kuchokera kwa Kisi:

Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.

30Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti.

Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo. 31Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

Hoffnung für Alle

1. Chronik 24:1-31

Die Dienstgruppen der Priester

1Auch die Nachkommen von Aaron wurden in verschiedene Gruppen aufgeteilt. Aarons Söhne hießen Nadab, Abihu, Eleasar und Itamar. 2Nadab und Abihu starben noch vor ihrem Vater und hinterließen keine männlichen Nachkommen. Eleasar und Itamar wurden Priester. 3David teilte die Priester in Dienstgruppen ein. Zadok, ein Nachkomme von Eleasar, und Ahimelech, ein Nachkomme von Itamar, halfen ihm dabei: 4Eleasar hatte mehr männliche Nachkommen als Itamar. Darum wurde die Sippe Eleasar in sechzehn Dienstgruppen eingeteilt, die Sippe Itamar in acht. Jede Gruppe wurde von einem Sippenoberhaupt geleitet. 5Die Diensteinteilung wurde durch das Los bestimmt, denn die Priester, die im Heiligtum vor Gott den höchsten Dienst versahen, sollten aus beiden Sippen stammen.

6Bei der Auslosung waren die Nachkommen von Eleasar und Itamar abwechselnd an der Reihe. Dabei waren anwesend: der König, die führenden Männer Israels, der Priester Zadok, Ahimelech, der Sohn von Abjatar, und die Sippenoberhäupter der Priester und Leviten. Der Schreiber Schemaja, ein Sohn von Netanel aus dem Stamm Levi, schrieb die Dienstgruppen in der Reihenfolge auf, in der sie ausgelost wurden:

7-181. Jojarib; 2. Jedaja; 3. Harim; 4. Seorim; 5. Malkija; 6. Mijamin; 7. Hakkoz; 8. Abija; 9. Jeschua; 10. Schechanja; 11. Eljaschib; 12. Jakim; 13. Huppa; 14. Jeschebab; 15. Bilga; 16. Immer; 17. Hesir; 18. Pizez; 19. Petachja; 20. Jeheskel; 21. Jachin; 22. Gamul; 23. Delaja; 24. Maasja.

19Dieser Einteilung entsprechend mussten die Priester in den Tempel des Herrn kommen und ihren Dienst versehen, so wie es der Herr, der Gott Israels, durch ihren Stammvater Aaron befohlen hatte.

Weitere Dienstgruppen der Leviten

20Weitere Sippenoberhäupter der Leviten waren:

Jechdeja, der über Schubaël von Amram abstammte;

21Jischija, ein Nachkomme von Rehabja;

22Jahat, der über Schelomit von Jizhar abstammte;

23Hebrons Söhne in der Reihenfolge ihres Alters: Jerija, Amarja, Jahasiël und Jekamam;

24Schamir, der über Micha von Usiël abstammte;

25Secharja, ein Nachkomme von Michas Bruder Jischija.

26Die Söhne von Merari hießen Machli, Muschi und Jaasija.24,26 Der hebräische Text ist nicht sicher zu deuten.

27Die Söhne von Jaasija, Meraris Sohn, waren Schoham, Sakkur und Ibri. 28-29Machlis Söhne hießen Eleasar und Kisch. Eleasar hatte keine Söhne, Kischs Sohn war Jerachmeel.

30Die Söhne von Muschi hießen Machli, Eder und Jeremot.

Dies waren weitere Sippen der Leviten.

31Wie für die Priester, so wurde auch für sie die Diensteinteilung durch das Los bestimmt. Dabei wurde die Familie eines Sippenoberhaupts genauso behandelt wie die seines jüngsten Bruders. Wieder waren König David, Zadok, Ahimelech und die Sippenoberhäupter der Priester und Leviten anwesend.