1 Mbiri 23 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 23:1-32

Fuko la Levi

1Davide atakalamba, ali ndi zaka zambiri, anayika Solomoni mwana wake kukhala mfumu ya Israeli.

2Iye anasonkhanitsanso pamodzi atsogoleri onse a Israeli, pamodzi ndi ansembe ndi Alevi. 3Anawerenga Alevi kuyambira a zaka makumi atatu ndi kupitirirapo, ndipo chiwerengero cha amuna onse chinali 38,000. 4Davide anati, “Mwa amenewa, amuna 24,000 aziyangʼanira ntchito za mʼNyumba ya Mulungu ndipo 6,000 akhale akuluakulu ndi oweruza. 5Amuna 4,000 akhale alonda a pa zipata ndipo 4,000 azitamanda Yehova ndi zipangizo zoyimbira zimene ndazipereka ndi cholinga chimenecho.”

6Davide anagawa Aleviwo mʼmagulumagulu motsatira ana a Levi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.

Banja la Geresoni

7Ana a Geresoni:

Ladani ndi Simei.

8Ana a Ladani:

Mtsogoleri Yehieli, Zetamu ndi Yoweli. Onse analipo atatu.

9Ana a Simei:

Selomoti, Haziyeli ndi Harani. Onse analipo atatu.

Awa anali atsogoleri a mabanja a Ladani.

10Ndipo ana a Simei anali:

Yahati, Zina, Yeusi ndi Beriya.

Awa anali ana a Semei. Onse analipo anayi.

11Mtsogoleri anali Yahati, ndipo Ziza anali wachiwiri, koma Yeusi ndi Beriya analibe ana aamuna ambiri. Kotero iwo anawerengedwa ngati banja limodzi ndipo anapatsidwa ntchito imodzinso yofanana.

Banja la Kohati

12Ana a Kohati:

Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli. Onse analipo anayi.

13Ana a Amramu:

Aaroni ndi Mose.

Aaroni ndi zidzukulu zake anapatulidwa kwamuyaya kuti azipereka zinthu zopatulika kwambiri monga nsembe pamaso pa Yehova, komanso kuti azitumikira pamaso pake ndi kumadalitsa anthu mʼdzina lake kwamuyaya. 14Ana a Mose munthu wa Mulungu anawerengedwa ngati gawo la fuko la Levi.

15Ana a Mose:

Geresomu ndi Eliezara.

16Zidzukulu za Geresomu:

Mtsogoleri anali Subaeli.

17Zidzukulu za Eliezara:

Mtsogoleri anali Rehabiya.

Eliezara analibe ana ena aamuna, koma ana a Rehabiya anali ochuluka kwambiri.

18Ana a Izihari:

Mtsogoleri anali Selomiti.

19Ana a Hebroni:

Mtsogoleri anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, Yahazieli anali wachitatu ndipo Yekameamu anali wachinayi.

20Ana a Uzieli:

Mtsogoleri anali Mika ndipo wachiwiri anali Isiya.

Banja la Merari

21Ana a Merari:

Mahili ndi Musi.

Ana a Mahili:

Eliezara ndi Kisi.

22Eliezara anamwalira wopanda ana aamuna. Iye anali ndi ana aakazi okhaokha. Abale awo, ana a Kisi, ndiwo amene anawakwatira.

23Ana a Musi:

Mahili, Ederi ndi Yeremoti. Onse analipo atatu.

24Izi zinali zidzukulu za Levi mwa mabanja awo, atsogoleri a mabanja monga momwe analembedwera mayina awo ndi monga momwenso anawerengedwera, banja lililonse pa lokha. Awa ndi anthu ogwira ntchito oyambira zaka makumi awiri zobadwa kapena kupitirirapo, amene amatumikira mʼNyumba ya Yehova. 25Popeza Davide anati, “Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli, wapereka mpumulo kwa anthu ake ndipo wabwera kudzakhala mu Yerusalemu kwamuyaya, 26sikofunikiranso kuti Alevi azinyamula tenti kapena zipangizo za chipembedzo.” 27Potsata malangizo otsiriza a Davide, Alevi anawerengedwa kuyambira amuna a zaka makumi awiri zakubadwa kapena kupitirirapo.

28Ntchito ya Alevi inali kuthandiza zidzukulu za Aaroni pa ntchito yotumikira mʼNyumba ya Yehova monga kuyangʼanira mabwalo, zipinda zamʼmbali, kuyeretsa zinthu zonse zachipembedzo, ndiponso kuchita ntchito zina za mʼnyumba ya Mulungu. 29Iwo amayangʼanira buledi amene amayikidwa pa tebulo, ufa wa nsembe yachakudya, timitanda ta buledi wopanda yisiti: kuphika ndi kusakaniza, ndiponso miyeso yonse ndi kukula kwake. 30Iwo amayimiriranso mmawa uliwonse kuthokoza ndi kutamanda Yehova. Amachitanso chomwecho madzulo, 31ndiponso popereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa Sabata ndi pa chikondwerero cha Mwezi Watsopano, ndi pa nthawi yosankhidwa ya Chikondwerero. Iwo amatumikira pamaso pa Yehova nthawi zonse mwa chiwerengero chawo ndi momwe analangizidwira.

32Ndipo kotero Alevi anachita ntchito yawo ya ku tenti ya msonkhano ya ku Malo Opatulika ndiponso molamulidwa ndi abale awo, zidzukulu za Aaroni, pa ntchito ya mʼNyumba ya Yehova.

King James Version

1 Chronicles 23:1-32

1So when David was old and full of days, he made Solomon his son king over Israel.

2¶ And he gathered together all the princes of Israel, with the priests and the Levites. 3Now the Levites were numbered from the age of thirty years and upward: and their number by their polls, man by man, was thirty and eight thousand. 4Of which, twenty and four thousand were to set forward the work of the house of the LORD; and six thousand were officers and judges:23.4 set…: or, oversee 5Moreover four thousand were porters; and four thousand praised the LORD with the instruments which I made, said David, to praise therewith. 6And David divided them into courses among the sons of Levi, namely, Gershon, Kohath, and Merari.23.6 courses: Heb. divisions

7¶ Of the Gershonites were, Laadan, and Shimei.23.7 Laadan: or, Libni 8The sons of Laadan; the chief was Jehiel, and Zetham, and Joel, three. 9The sons of Shimei; Shelomith, and Haziel, and Haran, three. These were the chief of the fathers of Laadan. 10And the sons of Shimei were, Jahath, Zina, and Jeush, and Beriah. These four were the sons of Shimei.23.10 Zina: or, Zizah 11And Jahath was the chief, and Zizah the second: but Jeush and Beriah had not many sons; therefore they were in one reckoning, according to their father’s house.23.11 had…: Heb. did not multiply sons

12¶ The sons of Kohath; Amram, Izhar, Hebron, and Uzziel, four. 13The sons of Amram; Aaron and Moses: and Aaron was separated, that he should sanctify the most holy things, he and his sons for ever, to burn incense before the LORD, to minister unto him, and to bless in his name for ever. 14Now concerning Moses the man of God, his sons were named of the tribe of Levi. 15The sons of Moses were, Gershom, and Eliezer. 16Of the sons of Gershom, Shebuel was the chief.23.16 Shebuel: also called, Shubael 17And the sons of Eliezer were, Rehabiah the chief. And Eliezer had none other sons; but the sons of Rehabiah were very many.23.17 the chief: or, the first23.17 very many: Heb. highly multiplied 18Of the sons of Izhar; Shelomith the chief.23.18 Shelomith: also called, Shelomoth 19Of the sons of Hebron; Jeriah the first, Amariah the second, Jahaziel the third, and Jekameam the fourth. 20Of the sons of Uzziel; Michah the first, and Jesiah the second.

21¶ The sons of Merari; Mahli, and Mushi. The sons of Mahli; Eleazar, and Kish. 22And Eleazar died, and had no sons, but daughters: and their brethren the sons of Kish took them.23.22 brethren: or, kinsmen 23The sons of Mushi; Mahli, and Eder, and Jeremoth, three.

24¶ These were the sons of Levi after the house of their fathers; even the chief of the fathers, as they were counted by number of names by their polls, that did the work for the service of the house of the LORD, from the age of twenty years and upward. 25For David said, The LORD God of Israel hath given rest unto his people, that they may dwell in Jerusalem for ever:23.25 that…: or, and he dwelleth in Jerusalem, etc 26And also unto the Levites; they shall no more carry the tabernacle, nor any vessels of it for the service thereof. 27For by the last words of David the Levites were numbered from twenty years old and above:23.27 numbered: Heb. number 28Because their office was to wait on the sons of Aaron for the service of the house of the LORD, in the courts, and in the chambers, and in the purifying of all holy things, and the work of the service of the house of God;23.28 their…: Heb. their station was at the hand of the sons of Aaron 29Both for the shewbread, and for the fine flour for meat offering, and for the unleavened cakes, and for that which is baked in the pan, and for that which is fried, and for all manner of measure and size;23.29 pan: or, flat plate 30And to stand every morning to thank and praise the LORD, and likewise at even; 31And to offer all burnt sacrifices unto the LORD in the sabbaths, in the new moons, and on the set feasts, by number, according to the order commanded unto them, continually before the LORD: 32And that they should keep the charge of the tabernacle of the congregation, and the charge of the holy place, and the charge of the sons of Aaron their brethren, in the service of the house of the LORD.