1 Mbiri 21 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 21:1-30

Davide Awerenga Ankhondo Ake

1Satana anafuna kuvutitsa Aisraeli choncho anawutsa mtima wa Davide kuti awerenge Aisraeli. 2Choncho Davide anati kwa Yowabu pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo, “Pitani mukawerenge Aisraeli kuyambira ku Beeriseba mpaka ku Dani. Ndipo mudzandiwuze kuti ndidziwe chiwerengero chawo.”

3Yowabu anayankha kuti, “Yehova achulukitse ankhondo ake kukhala miyandamiyanda. Mbuye wanga mfumu, kodi anthu onsewa sali pansi panu? Nʼchifukwa chiyani mbuye wanga mukufuna kuchita zimenezi? Nʼchifukwa chiyani mukufuna kuchimwitsa Israeli?”

4Komabe mawu a mfumu anapambana mawu a Yowabu, kotero Yowabu anapita mu Israeli monse ndipo kenaka anabwera ku Yerusalemu. 5Yowabu anapereka chiwerengero cha anthu ankhondo kwa Davide: Mu Israeli monse munali anthu ankhondo 1,100,000 amene amadziwa kugwiritsa ntchito lupanga, kuphatikizapo anthu 470,000 a fuko la Yuda.

6Koma Yowabu sanaphatikizepo fuko la Levi ndi fuko la Benjamini pa chiwerengerochi, pakuti lamulo la mfumu linamuyipira. 7Lamulo limeneli silinakomerenso Mulungu. Kotero Iye analanga Israeli.

8Choncho Davide anati kwa Mulungu, “Ine ndachimwa kwambiri pa zimene ndachita. Tsono ndikupempha kuti mukhululuke kulakwa kwa mtumiki wanu. Ine ndachita zopusa kwambiri.”

9Yehova anati kwa Gadi, mlosi wa Davide, 10“Pita ukamuwuze Davide kuti, ‘Yehova akuti, Ine ndikukupatsa zinthu zitatu izi. Usankhepo chimodzi pa zimenezi choti ndikuchitire.’ ”

11Choncho Gadi anapita kwa Davide ndipo anati kwa Iye, “Yehova akuti, ‘Musankhepo chimene mungakonde kuti chichitike: 12mʼdziko mukhale njala zaka zitatu, mukhale mukuthawa adani anu kwa miyezi itatu, akukukanthani ndi lupanga la Yehova, kapena mʼdziko mukhale mliri kwa masiku atatu, mngelo wa Yehova akuwononga Israeli yense.’ Ndipo tsono ganizirani bwino chomwe ndikamuyankhe amene wandituma.”

13Davide anati kwa Gadi, “Ine ndavutika kwambiri mu mtima mwanga. Ine andilange ndi Yehova, pakuti chifundo chake ndi chachikulu kwambiri; koma ndisalangidwe ndi anthu.”

14Choncho Yehova anabweretsa mliri pa Aisraeli, ndipo unapha Aisraeli 70,000. 15Ndipo Mulungu anatumiza mngelo kuti awononge Yerusalemu. Koma pamene mngeloyo amachita zimenezi, Yehova anaona ndipo anavutika mu mtima chifukwa cha zowawazo ndipo anati kwa mngelo amene ankawononga anthu uja, “Basi kwakwanira! Leka kuwononga.” Nthawi imeneyo mngelo wa Yehova anali atayima pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi.

16Davide anakweza maso ake ndipo anaona mngelo wa Yehova atayima pakati pa dziko lapansi ndi kumwamba, mʼdzanja lake muli lupanga lotambalitsa kuloza ku Yerusalemu. Ndipo Davide ndi akuluakulu, atavala ziguduli, anadzigwetsa pansi chafufumimba.

17Davide anati kwa Mulungu, “Kodi si ine amene ndinalamula kuti ankhondo awerengedwe? Ine mʼbusa ndi amene ndachimwa, ndiye ndachita zoyipa. Anthuwa ali ngati nkhosa zosalakwa. Kodi iwowa achita chiyani? Inu Yehova Mulungu wanga, langani ineyo pamodzi ndi banja langa, koma musalole kuti mliriwu ukhale pa anthu anuwa.”

18Pamenepo mngelo wa Yehova analamula Gadi kuti awuze Davide kuti akamange guwa lansembe la Yehova pamalo opunthira tirigu a Arauna Myebusi. 19Ndipo Davide anapita pomvera mawu amene Gadi ananena mʼdzina la Yehova.

20Pamene Arauna ankapuntha tirigu, anatembenuka ndipo anaona mngelo ndipo ana ake anayi aamuna amene anali naye anabisala. 21Davide anayandikira, ndipo Arauna atayangʼana ndi kumuona, anachoka popunthira tirigupo ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi pamaso pa Davide.

22Davide anati kwa Arauna, “Undipatse malo ako opunthira tirigu kuti ndimangire Yehova guwa lansembe, kuti mliri uli pa anthuwa usiye. Undigulitse ine pa mtengo woyenera ndithu.”

23Arauna anati kwa Davide, “Tengani! Mbuye wanga mfumu achite chomukomera. Taonani ine ndidzapereka ngʼombe zazimuna za nsembe yopsereza, zopunthira tirigu zidzakhala nkhuni ndipo tiriguyu adzakhala chopereka chachakudya. Ndidzapereka zonsezi.”

24Koma mfumu Davide inayankha Arauna kuti, “Ayi, ine ndikuti ndipereka mtengo wathunthu. Sindingatenge chinthu chako ndi kuchipereka kwa Yehova, kapena kupereka nsembe imene sindinayigule.”

25Choncho Davide analipira Arauna masekeli agolide 600 chifukwa cha malowo. 26Davide anamangira Yehova guwa lansembe pamenepo ndipo anaperekapo nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano. Iye anapemphera kwa Yehova, ndipo Yehova anayankha potumiza moto pa guwa lansembe zopsereza kuchokera kumwamba.

27Tsono Yehova anayankhula kwa mngelo, ndipo analowetsa lupanga lake mʼchimake. 28Pa nthawi imeneyo, Davide ataona kuti Yehova wamuyankha pa malo opunthira tirigu a Arauna Myebusi, anapereka nsembe pamenepo. 29Tenti ya Yehova imene Mose anapanga mʼchipululu, ndi guwa lansembe zopsereza pa nthawi imeneyi zinali pa phiri ku Gibiyoni. 30Koma Davide sanathe kupita kumeneko kuti akapemphere pamaso pa Yehova, chifukwa amaopa lupanga la mngelo wa Yehova.

Священное Писание

1 Летопись 21:1-30

Вечный наказывает Давуда за перепись

(2 Цар. 24:1-17)

1Сатана21:1 Сатана – это имя переводится как «противник», «обвинитель». восстал на Исраил и побудил Давуда устроить перепись населения Исраила. 2Давуд сказал Иоаву и начальникам войска:

– Пойдите, произведите перепись исраильтян от Беэр-Шевы на юге до Дана на севере и доложите мне, чтобы я знал, сколько их.

3Но Иоав ответил:

– Пусть Вечный умножит количество Своего народа стократно. Разве не все они, господин мой царь, твои рабы? Зачем мой господин хочет это сделать? Зачем ему наводить грех на Исраил?

4Но царское слово оказалось сильнее слова Иоава, и Иоав ушёл, прошёл по всему Исраилу и вернулся в Иерусалим. 5Иоав представил Давуду результаты переписи. Во всём Исраиле было один миллион сто тысяч мужчин, способных владеть мечом, включая четыреста семьдесят тысяч в Иудее. 6Но Иоав не включил в общее число роды Леви и Вениамина, потому что приказ царя ему не понравился. 7Этот приказ был неугоден и Всевышнему, и Он наказал Исраил.

8Тогда Давуд сказал Всевышнему:

– Сделав это, я совершил великий грех. Теперь я молю Тебя, сними вину с Твоего раба! Я поступил крайне безрассудно.

9Вечный сказал Гаду, провидцу Давуда:

10– Иди и скажи Давуду: Так говорит Вечный: «Я предлагаю тебе три наказания. Выбери, каким из них Мне наказать тебя».

11Гад пришёл к Давуду и сказал ему:

– Так говорит Вечный: «Выбирай: 12или три года голода, или три месяца опустошения врагами, когда их меч будет неотступно преследовать тебя, или три дня меча Вечного – это дни мора в стране, когда Ангел Вечного21:12 Ангел Вечного – этот особенный ангел отождествляется с Самим Вечным. Многие толкователи видят в Нём явления Исы Масиха до Его воплощения. станет губить людей по всей земле Исраила». Итак, обдумай это и реши, что мне ответить Пославшему меня.

13И Давуд сказал Гаду:

– Мне очень тяжело. Пусть лучше я попаду в руки Вечного, ведь Его милость очень велика, но не дай мне попасть в человеческие руки!

14И Вечный послал на Исраил мор, и погибло семьдесят тысяч исраильтян. 15И Всевышний послал Ангела, чтобы Тот погубил Иерусалим. Но когда Ангел стал истреблять город, Вечный увидел это и пожалел о бедствии и сказал Ангелу-губителю:

– Довольно! Опусти Свою руку!

Ангел Вечного стоял тогда над гумном иевусея Арауны21:15 Букв.: «Орнан»; во 2 Цар. 24:16 он назван Арауной. Также в ст. 18-28.. 16Давуд поднял взгляд и увидел Ангела Вечного, Который стоял между землёй и небом с обнажённым мечом в руке, протянутым в сторону Иерусалима. И Давуд со старейшинами, одетые в знак раскаяния в рубище, пали лицом на землю. 17Давуд сказал Всевышнему:

– Разве не я велел пересчитать народ? Я согрешил и сделал зло, а эти овцы – что они сделали? Вечный, мой Бог, пусть же Твоя рука обратится на меня и на мою семью, но не дай Твоему народу погибнуть от мора.

Давуд сооружает жертвенник

(2 Цар. 24:18-25)

18Тогда Ангел Вечного повелел Гаду сказать Давуду, чтобы тот пошёл и построил жертвенник Вечному на гумне иевусея Арауны. 19И Давуд пошёл, как повелел через Гада Вечный.

20Когда Арауна молотил пшеницу, он обернулся и увидел Ангела. Четверо сыновей Арауна, которые были с ним, попрятались. 21Давуд пришёл к Арауне, и когда Арауна посмотрел и увидел Давуда, он вышел из гумна и поклонился Давуду лицом до земли. 22Давуд сказал ему:

– Отдай мне своё гумно, я построю на его месте жертвенник Вечному, чтобы прекратился мор среди народа. Продай его мне за полную цену.

23Арауна сказал Давуду:

– Бери его! Пусть господин мой царь делает то, что ему угодно. Вот я отдаю волов для всесожжения, молотильную доску на дрова и пшеницу для хлебного приношения. Я отдаю всё это.

24Но царь Давуд ответил Арауне:

– Нет, я заплачу тебе полную цену. Я не возьму для Вечного того, что принадлежит тебе, и не стану приносить жертву, которая мне ничего не стоила.

25И Давуд заплатил Арауне более семи килограммов21:25 Букв.: «шестьсот шекелей». золота за это место. 26Давуд построил там жертвенник Вечному и принёс всесожжения и жертвы примирения. Он призвал Вечного, и Вечный ответил ему, послав огонь с небес на жертвенник для всесожжений. 27После этого Вечный сказал Ангелу, и тот вложил Свой меч в ножны.

28В то время Давуд, увидев, что Вечный ответил ему на гумне иевусея Арауны, стал приносить Ему там жертвы. 29Священный шатёр Вечного, который сделал в пустыне Муса, и жертвенник для всесожжений находились в то время в Гаваоне. 30Но Давуд не мог пойти туда, чтобы говорить с Вечным, потому что боялся меча Ангела Вечного.