1 Mbiri 17 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 17:1-27

Lonjezo la Mulungu kwa Davide

1Davide atakhazikika mʼnyumba yake yaufumu, anawuza mneneri Natani kuti, “Ine pano ndikukhala mʼnyumba yaufumu yomanga ndi mitengo ya mkungudza, pomwe Bokosi la Chipangano la Yehova lili mu tenti.”

2Natani anayankha Davide kuti, “Chitani chilichonse chimene chili mu mtima mwanu, chifukwa Mulungu ali nanu.”

3Usiku umenewo mawu a Mulungu anafika kwa Natani, ndipo anati,

4“Pita kamuwuze mtumiki wanga Davide kuti, ‘Yehova akunena kuti, sudzandimangira ndiwe nyumba yokhalamo.’ 5Ine sindinakhalepo mʼnyumba kuyambira tsiku limene ndinatulutsa Israeli mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ndakhala ndikuyenda kuchoka mʼtenti ina kupita mʼtenti ina, kuchoka malo ena kupita malo ena. 6Konse ndakhala ndikuyenda ndi Aisraeli onse, kodi ndinanenapo kwa wina aliyense wa atsogoleri awo amene ndinamulamula kuweta anthu anga kuti, ‘Kodi nʼchifukwa chiyani simunandimangire nyumba ya mitengo ya mkungudza?’ ”

7Ndipo tsopano umuwuze mtumiki wanga Davide kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndinakutenga ku busa ukuweta nkhosa, kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga, Aisraeli. 8Ineyo ndinali nawe kulikonse kumene unkapita, ndipo ndachotsa adani ako onse pamaso pako. Tsopano ndidzakuza dzina lako kuti likhale mʼgulu la mayina a anthu otchuka kwambiri pa dziko lapansi. 9Ndipo ndidzawapatsa malo anthu anga, Aisraeli ndipo ndidzawadzala pamalo awoawo kuti asadzavutitsidwenso. Anthu oyipa sadzawazunzanso monga ankachitira poyamba paja; 10monga akhala akuchitira kuchokera nthawi imene ndinasankha atsogoleri a anthu anga Aisraeli. Ine ndidzagonjetsanso adani anu onse.

“ ‘Ine ndikulengeza kwa iwe kuti Yehova adzakhazikitsa banja lako. 11Masiku ako akadzatha ndipo ukadzatsatira makolo ako, Ine ndidzawutsa mphukira yako imene idzalowa mʼmalo mwako, mmodzi mwa ana ako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake. 12Iye ndiye amene adzandimangira nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wake kwamuyaya. 13Ine ndidzakhala abambo ake, ndipo iye adzakhala mwana wanga. Ine sindidzasiya kumukonda monga ndinachitira ndi amene unalowa mʼmalo mwawo. 14Ndidzamuyika kukhala wolamulira nyumba yanga ndi ufumu wanga kwamuyaya. Mpando wake waufumu udzakhazikika kwamuyaya.’ ”

15Natani anafotokozera Davide mawu onse avumbulutso limene analandira.

Pemphero la Davide

16Choncho Mfumu Davide analowa mu tenti nakhala pamaso pa Yehova, ndipo anati,

“Ine ndine yani, Inu Yehova Mulungu, ndipo banja langa nʼchiyani kuti mundifikitse pamene ndafikapa? 17Inu Mulungu, kukhala ngati izi ndi zosakwanira pamaso panu, Inuyo mwayankhula zatsogolo la banja la mtumiki wanu. Mwandiyangʼana ndipo mwandiyesa ngati munthu wolemekezeka kwambiri pakati pa anthu, Inu Yehova Mulungu.”

18“Kodi Davide anenenso chiyani kwa Inu, pakuti mwachitira ulemu wotere mtumiki wanu? Pakuti Inu mukumudziwa mtumiki wanu. 19Inu Yehova, chifukwa cha mtumiki wanu komanso mwa chifuniro chanu, mwachita chinthu chachikulu ichi ndipo mwawulula malonjezo anu aakulu onse.

20“Palibe wina wofanana nanu, Inu Yehova, ndipo palibe Mulungu wina koma Inu nokha monga tamvera ndi makutu athu. 21Ndipo ndi ndani wofanana ndi anthu anu Aisraeli, mtundu wokhawo pa dziko lapansi umene Mulungu wake anapita kukawuwombola, monga anthu akeake ndi kukadzitchukitsa yekha pochita zinthu zodabwitsa zazikulu, pothamangitsa mitundu ina pamaso pa anthu ake, amene Inu munawawombola ku Igupto? 22Inu munawapanga anthu anu Aisraeli kukhala anuanu kwamuyaya, ndipo Inu, Inu Yehova ndinu Mulungu wawo.

23“Ndipo tsopano Yehova, sungani kwamuyaya lonjezo limene mwachita ndi mtumiki wanu ndi banja lake, likhazikitseni kwamuyaya. Chitani monga mwalonjezera, 24kotero dzina lanu likhazikike ndi kukhala lotchuka mpaka muyaya. Ndipo anthu adzanena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa woyangʼanira Israeli, ndi Mulungu wa Israeli!’ Ndipo banja la mtumiki wanu Davide lidzakhazikika pamaso panu.

25“Inu Mulungu wanga, mwaululira mtumiki wanu kuti mudzamumangira nyumba. Nʼchifukwa chake ine mtumiki wanu ndalimba mtima kupemphera motere. 26Inu Yehova, ndinu Mulungu! Mwalonjeza zinthu zabwinozi kwa mtumiki wanu. 27Ndipo chakukomerani kudalitsa banja la mtumiki wanu kuti likhale pamaso panu mpaka muyaya. Pakuti Inu Yehova mwalidalitsa, lidzakhala lodalitsika mpaka muyaya.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

1 Летопись 17:1-27

Обещание Всевышнего Довуду

(2 Цар. 7:1-17)

1После того как Довуд поселился в своём дворце, он сказал пророку Нафану:

– Смотри, я живу во дворце из кедра, а сундук соглашения с Вечным стоит в шатре.

2Нафан ответил Довуду:

– Иди и делай то, что у тебя на сердце, потому что Всевышний с тобой.

3В ту ночь к Нафану было слово Всевышнего:

4– Пойди и скажи Моему рабу Довуду: Так говорит Вечный: «Не ты построишь Мне дом для обитания. 5Я не жил в доме с того дня, как вывел Исроил из Египта, и до сегодняшнего дня, но обитал в шатре и переходил с места на место. 6Где бы Я ни ходил со всеми исроильтянами, разве Я когда-либо говорил кому-нибудь из их судей17:6 В период после завоевания Ханона и до восшествия на престол царей Всевышний ставил вождей, называемых судьями, которые защищали и управляли исроильским народом. Об этом можно прочитать в книге Судей., которым Я повелел пасти Мой народ: „Почему вы не построили Мне дом из кедра?“»

7Итак, скажи Моему рабу Довуду: Так говорит Вечный, Повелитель Сил: «Я взял тебя, когда ты смотрел и ухаживал на пастбище за овцами, чтобы ты стал правителем Моего народа Исроила. 8Я был с тобой, куда бы ты ни ходил, и сокрушил перед тобой всех твоих врагов. Я сделаю твоё имя великим, подобным именам великих людей земли. 9Я устрою место для Своего народа Исроила и укореню его, чтобы у него был свой дом и чтобы никто его больше не тревожил. Нечестивые люди не будут больше притеснять его, как прежде, 10с того времени, как Я поставил судей над Своим народом Исроилом. Я смирю всех твоих врагов.

Я объявляю тебе, что Сам устрою твой дом. 11Когда твои дни завершатся, и ты отойдёшь к своим предкам, Я возведу на престол твоего потомка, одного из твоих сыновей, и упрочу его царство. 12Он построит Мне дом, а Я упрочу его престол навеки. 13Я буду назван его Отцом, а он Мне сыном наречётся. Я не отниму от него Своей любви, как отнял её от твоего предшественника. 14Я поставлю его над Своим домом и Своим царством навечно, и его престол будет установлен навеки»17:13-14 Эти слова также являются пророчеством об Исо Масехе (см. Лк. 1:32; Рим. 1:3-4; Евр. 1:5)..

15Нафан передал Довуду все слова этого откровения.

Молитва Довуда

(2 Цар. 7:18-29)

16Тогда царь Довуд вошёл, сел перед Вечным и сказал:

– Кто я, о Вечный Бог, и что такое моя семья, что Ты так возвеличил меня? 17И словно этого не было достаточно в Твоих глазах, Всевышний, Ты ещё рассказал о будущем дома Твоего раба. Ты открыл мне то, что человек желает знать, о Вечный Бог. 18Что ещё может сказать Тебе Довуд за прославление Твоего раба? Ведь Ты знаешь Своего раба, 19о Вечный! Ради Своего раба и по Своей воле Ты совершил это великое дело и дал все эти великие обещания.

20Нет подобного Тебе, Вечный, и нет Бога, кроме Тебя, как слышали мы своими ушами. 21И кто подобен Исроилу, единственному народу на земле, который Всевышний выкупил Себе, чтобы сделать Своим народом? Чтобы все узнали имя Твоё, Ты совершил великие и ужасные дела, выкупив Свой народ из Египта и изгнав перед ним другие народы. 22Ты сделал Исроил Своим собственным народом навеки, и Ты, о Вечный, стал его Богом.

23И теперь, Вечный, пусть обещание, которое Ты дал о Своём рабе и его доме, утвердится навеки, и сделай, как Ты обещал. 24Пусть пребудет и возвеличится Твоё имя вовеки, чтобы люди говорили: «Вечный, Повелитель Сил, Бог Исроила, есть Бог над Исроилом!» И дом Твоего раба Довуда утвердится перед Тобой.

25Так как Ты, мой Бог, открыл Своему рабу, что устроишь его дом, то раб Твой нашёл в себе смелость молиться перед Тобой. 26Вечный, Ты – Бог! Ты обещал Своему рабу это благо. 27Пусть же станет Тебе угодно благословлять дом Твоего раба, чтобы он был перед Тобой вечно. Ведь Ты, Вечный, благословил его, и он будет благословен навеки!