1 Mbiri 16 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mbiri 16:1-43

1Iwo anabwera nalo Bokosi la Mulungu ndipo analiyika pamalo pake mʼkati mwa tenti imene Davide anayimika ndipo iwo anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Mulungu. 2Davide atatsiriza kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano, iye anadalitsa anthu mʼdzina la Yehova. 3Kenaka anagawira Mwisraeli aliyense, wamwamuna ndi wamkazi, aliyense buledi mmodzi, nthuli yanyama ndiponso keke yamphesa zowuma.

4Iye anasankha Alevi ena kuti azitumikira pamene panali Bokosi la Yehova, kuti azipemphera, azithokoza ndi kulemekeza Yehova Mulungu wa Israeli. 5Mtsogoleri wawo anali Asafu, wachiwiri anali Zekariya, kenaka Yeiyeli, Semiramoti, Yehieli, Matitiya, Eliabu, Benaya, Obedi-Edomu ndi Yeiyeli. Iwo amayimba azeze ndi apangwe, Asafu amayimba ziwaya za malipenga, 6ndipo ansembe Benaya ndi Yahazieli amawomba malipenga nthawi zonse pamaso pa Bokosi la Chipangano la Mulungu.

Nyimbo Yotamanda ya Davide

7Tsiku limeneli Davide anayamba nʼkusankha Asafu ndi anzake kuti ndiwo apereke nyimbo iyi ya matamando kwa Yehova:

8Yamikani Yehova, itanani dzina lake;

lalikani za ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu.

9Imbirani Iye, muyimbireni nyimbo zamatamando;

nenani za ntchito zake zonse zodabwitsa.

10Nyadirani dzina lake loyera;

ikondwere mitima ya iwo akufunafuna Yehova.

11Dalirani Yehova ndi mphamvu zake;

funafunani nkhope yake nthawi zonse.

12Kumbukirani ntchito zodabwitsa wazichita,

zozizwitsa zake, ndi kuweruza kwa mʼkamwa mwake,

13inu zidzukulu za Israeli mtumiki wake,

inu ana a Yakobo, osankhidwa ake.

14Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;

chiweruzo chake chili pa dziko lonse lapansi.

15Iye amakumbukira pangano lake nthawi zonse,

mawu amene Iye analamula, kwa mibado miyandamiyanda,

16pangano limene anachita ndi Abrahamu,

lonjezo limene analumbira kwa Isake.

17Iye analitsimikiza kwa Yakobo monga lamulo,

kwa Israeli monga pangano lamuyaya.

18“Kwa iwe, ine ndidzapereka dziko la Kanaani

monga cholowa chimene udzachilandira.”

19Ali anthu owerengeka,

ochepa ndithu, komanso alendo mʼdzikomo,

20iwo anayendayenda kuchoka ku mtundu wina kupita ku mtundu wina,

ku ufumu wina kupita ku ufumu wina.

21Iye sanalole munthu aliyense kuti awapondereze;

chifukwa cha iwo, Iye anadzudzula mafumu:

22“Musakhudze odzozedwa anga;

musawachitire choyipa aneneri anga.”

23Imbirani Yehova, dziko lonse lapansi;

lalikani za chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

24Lengezani za ulemerero wake kwa mitundu yonse,

ntchito zake zonse zodabwitsa kwa anthu onse.

25Pakuti Yehova ndi wamkulu ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

Iyeyo ayenera kuopedwa kuposa milungu yonse.

26Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano wopanda pake,

koma Yehova analenga kumwamba.

27Ulemerero ndi ufumu zili pamaso pake;

mphamvu ndi chimwemwe zili pa malo pokhala Iye.

28Perekani kwa Yehova, Inu mabanja a anthu a mitundu ina,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu,

29perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake.

Bweretsani chopereka ndipo mufike pamaso pake;

pembedzani Yehova mu ulemerero wachiyero chake.

30Njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi!

Dziko linakhazikika kolimba; silingasunthidwe.

31Zakumwamba zisangalale, dziko lapansi likondwere;

anene anthu a mitundu ina, “Yehova ndi mfumu!”

32Nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

minda ikondwere, ndi zonse zili mʼmenemo!

33Ndipo mitengo ya mʼnkhalango idzayimba,

idzayimba chifukwa cha chimwemwe pamaso pa Yehova,

pakuti akubwera kudzaweruza dziko lapansi.

34Yamikani Yehova, pakuti Iye ndi wabwino;

chikondi chake chikhala mpaka muyaya.

35Fuwulani kuti, “Tipulumutseni, Inu Mulungu wa chipulumutso chathu,

mutisonkhanitse ndipo mutipulumutse kwa anthu a mitundu ina,

kuti tiyamike dzina lanu loyera,

kuti tikutamandeni.”

36Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli,

kuyambira muyaya mpaka muyaya.

Ndipo anthu onse anati, “Ameni” ndipo “Tikutamandani Yehova.”

37Ndipo Davide anasiya Asafu pamodzi ndi anzake kumene kunali Bokosi la Chipangano la Yehova kuti azitumikira kumeneko nthawi zonse, monga mwa zoyenera kuchita pa tsiku lililonse. 38Iye anasiyanso Obedi-Edomu pamodzi ndi anzake 68 kuti azitumikira nawo pamodzi. Obedi-Edomu mwana wa Yedutuni ndi Hosa anali alonda a pa chipata.

39Davide anasiya wansembe Zadoki ndi ansembe anzake ku chihema cha Yehova ku malo achipembedzo ku Gibiyoni 40kuti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova pa guwa lansembe nthawi zonse mmawa ndi madzulo, potsata zonse zimene zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Yehova, amene anawapereka kwa Aisraeli. 41Anthuwo anali pamodzi ndi Hemani ndi Yedutuni ndi onse amene anawasankha mowatchula dzina kuti apereke mayamiko kwa Yehova, “pakuti chikondi chake ndi chosatha.” 42Hemani ndi Yedutuni anali oyangʼanira malipenga ndi ziwaya ndiponso zipangizo zina zoyimbira nyimbo zachipembedzo. Ana a Yedutuni anawayika kuti aziyangʼanira pa chipata.

43Kenaka anthu onse anachoka, aliyense kupita kwawo. Ndipo Davide anabwerera ku nyumba kwake kukadalitsa banja lake.

Священное Писание

1 Летопись 16:1-43

1Сундук Всевышнего принесли и поставили в шатре, который разбил для него Давуд, и принесли Всевышнему жертвы всесожжения и жертвы примирения. 2Закончив приносить жертвы всесожжения и жертвы примирения, Давуд благословил народ во имя Вечного. 3Затем он раздал каждому исраильтянину – и мужчинам, и женщинам – по одной лепёшке, по куску жареного мяса16:3 Или: «немного инжира». и по связке изюма. 4Он поставил некоторых из левитов служить перед сундуком Вечного, чтобы они взывали, благодарили и прославляли Вечного, Бога Исраила: 5Асаф был руководителем, Закария – вторым после него, затем Иеил, Шемирамот, Иехиил, Маттафия, Элиав, Беная и Овид-Эдом с Иеилом. Они должны были играть на лирах и арфах, Асаф на тарелках, 6а священнослужители Беная и Иахазиил постоянно трубить в трубы перед сундуком соглашения со Всевышним.

Хвалебная песнь Давуда

(Заб. 104:1-15; 95:1-13; 105:1, 47-48)

7В тот день Давуд впервые дал Асафу и его сородичам песню для прославления Вечного:

8Славьте Вечного, призывайте Его имя,

возвещайте народам о Его делах.

9Воспойте Ему, пойте Ему хвалу,

рассказывайте о всех Его чудесах.

10Хвалитесь Его святым именем,

пусть веселятся сердца ищущих Вечного.

11Ищите Вечного и силу Его,

всегда ищите Его лица.

12Помните чудеса, которые Он сотворил,

знамения Его и суды, что Он произнёс,

13о потомки Исраила, раба Его,

о сыны Якуба, избранные Его!

14Он – Вечный, наш Бог,

суды Его по всей земле.

15Вечно помните Его соглашение –

слово, данное Им для тысяч поколений, –

16соглашение, заключённое с Ибрахимом,

и клятву, данную Исхаку.

17Он поставил его Якубу законом,

Исраилу – вечным соглашением,

18сказав: «Я отдам тебе Ханаанскую землю

в удел твоего наследия»16:15-18 См. Нач. 15:18-21; 26:3-4; 28:13-14..

19Когда они были малочисленны и незначительны

и были чужеземцами на этой земле,

20то скитались от народа к народу

и из царства в царство.

21Он никому не давал их притеснять

и укорял за них даже царей,

22говоря: «Не трогайте помазанников Моих,

и пророкам Моим не делайте зла»16:19-22 См. Нач. 12:10-20; 20..

23Пойте Вечному, все жители земли,

говорите о Его спасении каждый день.

24Возвещайте славу Его среди народов,

чудеса Его – среди всех людей,

25потому что велик Вечный и достоин всякой хвалы;

Он внушает трепет более всех богов.

26Все боги народов – лишь идолы,

а Вечный небеса сотворил.

27Слава и величие перед Ним,

сила и радость под кровом Его.

28Воздайте Вечному, все народы,

воздайте Ему славу и силу,

29воздайте славу имени Вечного.

Принесите дары и предстаньте пред Ним;

прославьте Вечного в великолепии Его святости16:29 Или: «в святом облачении прославьте Вечного»; или: «прославьте Вечного в Его великолепном святилище»..

30Трепещи перед Ним, вся земля!

Прочно мир утверждён – не поколеблется.

31Да возвеселятся небеса и возликует земля,

и да скажут народам: «Вечный правит!»

32Да восшумит море и всё, что в нём,

да возрадуется поле и всё, что на нём,

33и да возликуют деревья лесные,

возликуют перед Вечным,

ведь Он идёт судить землю.

34Славьте Вечного, потому что Он благ

и милость Его – навеки!

35Взывайте: «Спаси нас, Всевышний, Спаситель наш,

собери нас, защити нас от народов,

чтобы славить нам Твоё святое имя

и Твоей славою хвалиться».

36Хвала Вечному, Богу Исраила,

от века и до века!

И весь народ сказал: «Аминь!»16:36 Аминь – еврейское слово, которое переводится как «да, верно, воистину так» или «да будет так». и «Хвала Вечному!»

Служение Вечному в Иерусалиме и Гаваоне

37Давуд оставил Асафа и его сородичей перед сундуком соглашения с Вечным, чтобы они служили там постоянно, в соответствии с нуждами каждого дня. 38Ещё он оставил Овид-Эдома и шестьдесят восемь его сородичей, чтобы они служили вместе с ними. Овид-Эдом, сын Иедутуна, и Хоса были привратниками.

39Давуд оставил священнослужителя Цадока и его собратьев-священнослужителей перед священным шатром Вечного в Гаваоне, 40чтобы они постоянно приносили Вечному всесожжения на жертвеннике для всесожжений утром и вечером, так, как написано в Законе Вечного, который Он дал Исраилу16:40 Хотя сундук соглашения находился в Иерусалиме, Исраил продолжал совершать жертвоприношения в шатре, который находился в Гиве, до построения храма Сулейманом. См. 1:13 и 5:5.. 41С ними были Еман и Иедутун с прочими избранными, которые были назначены поимённо, чтобы славить Вечного, ведь «милость Его – навеки». 42Еман и Иедутун отвечали за игру на трубах и тарелках, а также на прочих музыкальных инструментах, когда пелись песни Всевышнему. Сыновья Иедутуна были поставлены у ворот.

43Когда весь народ разошёлся по домам, вернулся к себе и Давуд, чтобы благословить своих домашних.