1 Mafumu 9 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 9:1-28

Yehova Aonekera Solomoni

1Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene ankafuna, 2Yehova anamuonekera kachiwiri, monga momwe anamuonekera ku Gibiyoni. 3Yehova ananena kwa iye kuti:

“Ndamva pemphero ndi pembedzero lako pa zimene wapempha pamaso panga. Ndayipatula Nyumba iyi, imene wamanga, poyikamo Dzina langa mpaka muyaya. Maso anga ndi mtima wanga zidzakhala pamenepo nthawi zonse.

4“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika, mwangwiro ndi moona mtima monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga, 5Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu pa Israeli mpaka muyaya, monga ndinalonjezera abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu pa mpando waufumu wa Israeli.’

6“Koma ngati iwe kapena ana ako mudzapatuka ndi kuleka kusunga malamulo ndi mawu anga amene ndakupatsani ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, 7pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko limene ndinawapatsa ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndayipatula chifukwa cha Dzina langa. Pamenepo Aisraeli adzasanduka mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse. 8Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzatsonya ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’ 9Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova Mulungu wawo amene anatulutsa makolo awo mʼdziko la Igupto, ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’ ”

Zina zimene Solomoni Anachita

10Patatha zaka makumi awiri, ndiye nthawi imene Solomoni anamanga nyumba ziwirizi: Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, 11Mfumu Solomoni anapereka mizinda makumi awiri ya ku Galileya kwa Hiramu mfumu ya ku Turo chifukwa Hiramu nʼkuti atapereka mitengo yonse ya mkungudza ndi ya payini ndiponso golide yense zimene Solomoni ankazifuna. 12Koma Hiramu atabwera kuchokera ku Turo kudzaona mizinda imene Solomoni anamupatsa, sanasangalatsidwe nayo mizindayo. 13Iye anafunsa kuti, “Mʼbale wanga, kodi iyi nʼkukhala mizinda yondipatsa?” Ndipo iye anayitcha mizindayo Dziko la Kabuli, dzina lomwe amatchedwa mpaka lero lino. 14Koma Hiramu anali atatumiza kwa mfumu golide oposa makilogalamu 4,000.

15Izi ndi zimene anachita Mfumu Solomoni: Analamula anthu kuti agwire ntchito yathangata pomanga Nyumba ya Yehova, nyumba yake, malo achitetezo a Milo, mpanda wa Yerusalemu, Hazori, Megido ndi Gezeri. 16(Farao mfumu ya ku Igupto inali itathira nkhondo ndi kulanda Gezeri. Iye anatentha mzindawo. Anapha Akanaani amene ankakhala mʼmenemo ndipo kenaka anawupereka ngati mphatso yaukwati kwa mwana wake wamkazi amene anakwatiwa ndi Solomoni. 17Ndipo Solomoni anamanganso Gezeri.) Iye anamanga Beti-Horoni Wakumunsi, 18Baalati ndi Tadimori ku chipululu, mʼdziko lake lomwelo, 19pamodzinso ndi mizinda yake yosungira chuma ndiponso mizinda yosungiramo magaleta ndi akavalo ake. Anamanganso chilichonse chimene anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.

20Panali anthu amene anatsala pakati pa mitundu ya Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi (anthu awa sanali Aisraeli). 21Zimenezi ndiye zinali zidzukulu zawo zotsalira mʼdzikoli, anthu amene Aisraeli sanathe kuwawononga kotheratu. Solomoni anawatenga ndi kukhala akapolo ake ogwira ntchito yathangata, monga zilili mpaka lero lino. 22Koma Solomoni sanagwiritse ntchito ya ukapolo Mwisraeli aliyense; iwo anali anthu ake ankhondo, nduna zake, atsogoleri a ankhondo, akapitawo ake, olamulira magaleta ndi oyendetsa magaleta ake. 23Amenewa ndiwo anali akuluakulu oyangʼanira ntchito za Solomoni. Anthu okwana 550 ndiwo ankayangʼanira anthu amene ankagwira ntchitowo.

24Mwana wamkazi wa Farao atachoka mu Mzinda wa Davide, kupita ku nyumba ya mfumu imene Solomoni anamumangira, Solomoni anamanga malo achitetezo a Milo.

25Katatu pa chaka Solomoni ankapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe limene anamangira Yehova ndiponso ankafukiza lubani pamaso pa Yehova. Potero ankakwaniritsa zoyenera kuchitika mu Nyumba ya Yehova.

26Mfumu Solomoni anapanganso sitima zapamadzi ku Ezioni Geberi, malo amene ali pafupi ndi Eloti ku Edomu, mʼmbali mwa Nyanja Yofiira. 27Ndipo Hiramu anatumiza anthu ake oyendetsa sitima zapamadzi amene ankadziwa za pa nyanja kuti aziyendetsa pamodzi ndi anthu a Solomoni. 28Iwo anapita ku Ofiri ndipo anakatenga golide okwana makilogalamu 14,000, amene anamupereka kwa Mfumu Solomoni.

New Russian Translation

3 Царств 9:1-28

Господь является Соломону

(2 Пар. 7:11-22)

1Когда Соломон закончил строить Господень дом, царский дворец и все, что желал построить, 2Господь явился ему во второй раз, как являлся ему в Гаваоне. 3Господь сказал ему:

– Я услышал молитву и мольбу, которую ты вознес Мне. Я освятил Себе дом, который ты построил, поместив там навеки Свое имя. Мои глаза и сердце будут там всегда. 4А ты, если будешь ходить предо Мной в непорочности сердца и в правоте, как ходил твой отец Давид, исполнять все, что Я повелю, и соблюдать Мои установления и законы, 5то Я упрочу твой царский престол над Израилем навеки, как Я обещал Давиду, твоему отцу, когда сказал: «Ты не лишишься преемника на престоле Израиля».

6Но если вы или ваши сыновья отвернетесь от Меня, не будете соблюдать повеления и установления, которые Я дал вам, и пойдете служить другим богам и поклоняться им, 7то Я искореню Израиль из земли, которую Я дал им, и отвергну этот дом, который Я освятил для Своего имени. Израиль станет у всех народов притчей и посмешищем. 8И хотя этот дом сейчас превознесен, всякий, кто пройдет мимо, поразится и присвистнет, говоря: «Почему Господь обошелся так с этой страной и с этим домом?» 9А отвечать будут: «Потому что они оставили Господа, своего Бога, Который вывел их предков из Египта, приняли других богов, поклонялись и служили им – вот за что Господь навел на них все эти беды».

Другие дела Соломона

(2 Пар. 8:1-18)

10По истечении двадцати лет, в которые Соломон строил два этих здания – дом Господа и царский дворец, – 11он отдал двадцать городов Галилеи царю Тира Хираму, потому что Хирам поставлял ему столько кедрового и кипарисового дерева и золота, сколько тот хотел. 12Но когда Хирам прибыл из Тира, чтобы осмотреть города, которые дал ему Соломон, он остался недоволен.

13– Что же это за города ты мне дал, брат мой? – спросил он.

И он назвал их землею Кавул9:13 Землею Кавул – возможное значение этого названия – «негодная земля». – название, которое осталось за ними до сегодняшнего дня.

14(Хирам же послал царю сто двадцать талантов9:14 Около 4 тонн. золота.)

15Вот сведения о подневольных людях, чей труд царь Соломон использовал для строительства дома Господа, своего дворца, укрепления Милло9:15 Милло – искусственная земляная платформа, удерживаемая стеной или стенами, на которой находились здания., иерусалимской стены, а еще Хацора, Мегиддо и Гезера. 16Фараон, царь Египта, напал на Гезер и захватил его. Он предал его огню, перебил его ханаанских обитателей и отдал его в приданое своей дочери, жене Соломона. 17Соломон отстроил Гезер, Нижний Бет-Хорон, 18Баалаф и Тадмор9:18 Другое чтение топонима в данном месте еврейского текста: «Фамарь». в пустыне, в своей земле, 19а также все города для хранения запасов и города для своих колесниц и коней9:19 Или: «колесничих»; или: «всадников».. Соломон построил все, что ему хотелось построить в Иерусалиме, на Ливане и во всех землях, которыми он правил.

20Весь народ, оставшийся от аморреев, хеттов, ферезеев, хиввеев и иевусеев (все они не были израильтянами), 21то есть их потомков, оставшихся в стране, которых израильтяне не смогли искоренить9:21 На языке оригинала стоит слово, которое говорит о полном посвящении предметов или людей Господу, часто осуществлявшемся через их уничтожение., Соломон использовал подневольными рабочими, как это есть и до сегодняшнего дня. 22Но израильтян Соломон не обращал в рабов, они были его воинами, военачальниками и начальниками его колесниц и колесничих. 23Еще они были главными распорядителями его строительных работ – пятьсот пятьдесят надсмотрщиков над работавшими людьми.

24После того как дочь фараона перебралась из Города Давида во дворец, который построил для нее Соломон, он построил Милло.

25Три раза в год Соломон возносил всесожжения и жертвы примирения на жертвеннике, что построил для Господа, возжигая благовония перед Господом вместе с ними. Итак, он завершил строительство дома.

26Еще царь Соломон строил корабли в Эцион-Гевере, что рядом с Элатом в земле Эдома, на побережье Красного моря. 27Хирам послал с кораблями своих людей – моряков, знавших море, вместе с людьми Соломона. 28Они отплыли в Офир и привезли оттуда четыреста двадцать талантов9:28 Около 14,5 тонн. золота, которое и доставили царю Соломону.