1 Mafumu 9 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 9:1-28

Yehova Aonekera Solomoni

1Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene ankafuna, 2Yehova anamuonekera kachiwiri, monga momwe anamuonekera ku Gibiyoni. 3Yehova ananena kwa iye kuti:

“Ndamva pemphero ndi pembedzero lako pa zimene wapempha pamaso panga. Ndayipatula Nyumba iyi, imene wamanga, poyikamo Dzina langa mpaka muyaya. Maso anga ndi mtima wanga zidzakhala pamenepo nthawi zonse.

4“Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika, mwangwiro ndi moona mtima monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga, 5Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu pa Israeli mpaka muyaya, monga ndinalonjezera abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu pa mpando waufumu wa Israeli.’

6“Koma ngati iwe kapena ana ako mudzapatuka ndi kuleka kusunga malamulo ndi mawu anga amene ndakupatsani ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, 7pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko limene ndinawapatsa ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndayipatula chifukwa cha Dzina langa. Pamenepo Aisraeli adzasanduka mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse. 8Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzatsonya ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’ 9Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova Mulungu wawo amene anatulutsa makolo awo mʼdziko la Igupto, ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’ ”

Zina zimene Solomoni Anachita

10Patatha zaka makumi awiri, ndiye nthawi imene Solomoni anamanga nyumba ziwirizi: Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, 11Mfumu Solomoni anapereka mizinda makumi awiri ya ku Galileya kwa Hiramu mfumu ya ku Turo chifukwa Hiramu nʼkuti atapereka mitengo yonse ya mkungudza ndi ya payini ndiponso golide yense zimene Solomoni ankazifuna. 12Koma Hiramu atabwera kuchokera ku Turo kudzaona mizinda imene Solomoni anamupatsa, sanasangalatsidwe nayo mizindayo. 13Iye anafunsa kuti, “Mʼbale wanga, kodi iyi nʼkukhala mizinda yondipatsa?” Ndipo iye anayitcha mizindayo Dziko la Kabuli, dzina lomwe amatchedwa mpaka lero lino. 14Koma Hiramu anali atatumiza kwa mfumu golide oposa makilogalamu 4,000.

15Izi ndi zimene anachita Mfumu Solomoni: Analamula anthu kuti agwire ntchito yathangata pomanga Nyumba ya Yehova, nyumba yake, malo achitetezo a Milo, mpanda wa Yerusalemu, Hazori, Megido ndi Gezeri. 16(Farao mfumu ya ku Igupto inali itathira nkhondo ndi kulanda Gezeri. Iye anatentha mzindawo. Anapha Akanaani amene ankakhala mʼmenemo ndipo kenaka anawupereka ngati mphatso yaukwati kwa mwana wake wamkazi amene anakwatiwa ndi Solomoni. 17Ndipo Solomoni anamanganso Gezeri.) Iye anamanga Beti-Horoni Wakumunsi, 18Baalati ndi Tadimori ku chipululu, mʼdziko lake lomwelo, 19pamodzinso ndi mizinda yake yosungira chuma ndiponso mizinda yosungiramo magaleta ndi akavalo ake. Anamanganso chilichonse chimene anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.

20Panali anthu amene anatsala pakati pa mitundu ya Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi (anthu awa sanali Aisraeli). 21Zimenezi ndiye zinali zidzukulu zawo zotsalira mʼdzikoli, anthu amene Aisraeli sanathe kuwawononga kotheratu. Solomoni anawatenga ndi kukhala akapolo ake ogwira ntchito yathangata, monga zilili mpaka lero lino. 22Koma Solomoni sanagwiritse ntchito ya ukapolo Mwisraeli aliyense; iwo anali anthu ake ankhondo, nduna zake, atsogoleri a ankhondo, akapitawo ake, olamulira magaleta ndi oyendetsa magaleta ake. 23Amenewa ndiwo anali akuluakulu oyangʼanira ntchito za Solomoni. Anthu okwana 550 ndiwo ankayangʼanira anthu amene ankagwira ntchitowo.

24Mwana wamkazi wa Farao atachoka mu Mzinda wa Davide, kupita ku nyumba ya mfumu imene Solomoni anamumangira, Solomoni anamanga malo achitetezo a Milo.

25Katatu pa chaka Solomoni ankapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe limene anamangira Yehova ndiponso ankafukiza lubani pamaso pa Yehova. Potero ankakwaniritsa zoyenera kuchitika mu Nyumba ya Yehova.

26Mfumu Solomoni anapanganso sitima zapamadzi ku Ezioni Geberi, malo amene ali pafupi ndi Eloti ku Edomu, mʼmbali mwa Nyanja Yofiira. 27Ndipo Hiramu anatumiza anthu ake oyendetsa sitima zapamadzi amene ankadziwa za pa nyanja kuti aziyendetsa pamodzi ndi anthu a Solomoni. 28Iwo anapita ku Ofiri ndipo anakatenga golide okwana makilogalamu 14,000, amene anamupereka kwa Mfumu Solomoni.

New International Version – UK

1 Kings 9:1-28

The Lord appears to Solomon

1When Solomon had finished building the temple of the Lord and the royal palace, and had achieved all he had desired to do, 2the Lord appeared to him a second time, as he had appeared to him at Gibeon. 3The Lord said to him:

‘I have heard the prayer and plea you have made before me; I have consecrated this temple, which you have built, by putting my Name there for ever. My eyes and my heart will always be there.

4‘As for you, if you walk before me faithfully with integrity of heart and uprightness, as David your father did, and do all I command and observe my decrees and laws, 5I will establish your royal throne over Israel for ever, as I promised David your father when I said, “You shall never fail to have a successor on the throne of Israel.”

6‘But if you9:6 The Hebrew is plural. or your descendants turn away from me and do not observe the commands and decrees I have given you9:6 The Hebrew is plural. and go off to serve other gods and worship them, 7then I will cut off Israel from the land I have given them and will reject this temple I have consecrated for my Name. Israel will then become a byword and an object of ridicule among all peoples. 8This temple will become a heap of rubble. All9:8 See some Septuagint manuscripts, Old Latin, Syriac, Arabic and Targum; Hebrew And though this temple is now imposing, all who pass by will be appalled and will scoff and say, “Why has the Lord done such a thing to this land and to this temple?” 9People will answer, “Because they have forsaken the Lord their God, who brought their ancestors out of Egypt, and have embraced other gods, worshipping and serving them – that is why the Lord brought all this disaster on them.” ’

Solomon’s other activities

10At the end of twenty years, during which Solomon built these two buildings – the temple of the Lord and the royal palace – 11King Solomon gave twenty towns in Galilee to Hiram king of Tyre, because Hiram had supplied him with all the cedar and juniper and gold he wanted. 12But when Hiram went from Tyre to see the towns that Solomon had given him, he was not pleased with them. 13‘What kind of towns are these you have given me, my brother?’ he asked. And he called them the Land of Kabul,9:13 Kabul sounds like the Hebrew for good-for-nothing. a name they have to this day. 14Now Hiram had sent to the king 120 talents9:14 That is, about 4 metric tons of gold.

15Here is the account of the forced labour King Solomon conscripted to build the Lord’s temple, his own palace, the terraces,9:15 Or the Millo; also in verse 24 the wall of Jerusalem, and Hazor, Megiddo and Gezer. 16(Pharaoh king of Egypt had attacked and captured Gezer. He had set it on fire. He killed its Canaanite inhabitants and then gave it as a wedding gift to his daughter, Solomon’s wife. 17And Solomon rebuilt Gezer.) He built up Lower Beth Horon, 18Baalath, and Tadmor9:18 The Hebrew may also be read Tamar. in the desert, within his land, 19as well as all his store cities and the towns for his chariots and for his horses9:19 Or charioteers – whatever he desired to build in Jerusalem, in Lebanon and throughout all the territory he ruled.

20There were still people left from the Amorites, Hittites, Perizzites, Hivites and Jebusites (these peoples were not Israelites). 21Solomon conscripted the descendants of all these peoples remaining in the land – whom the Israelites could not exterminate9:21 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or people to the Lord, often by totally destroying them. – to serve as slave labour, as it is to this day. 22But Solomon did not make slaves of any of the Israelites; they were his fighting men, his government officials, his officers, his captains, and the commanders of his chariots and charioteers. 23They were also the chief officials in charge of Solomon’s projects – 550 officials supervising those who did the work.

24After Pharaoh’s daughter had come up from the City of David to the palace Solomon had built for her, he constructed the terraces.

25Three times a year Solomon sacrificed burnt offerings and fellowship offerings on the altar he had built for the Lord, burning incense before the Lord along with them, and so fulfilled the temple obligations.

26King Solomon also built ships at Ezion Geber, which is near Elath in Edom, on the shore of the Red Sea.9:26 Or the Sea of Reeds 27And Hiram sent his men – sailors who knew the sea – to serve in the fleet with Solomon’s men. 28They sailed to Ophir and brought back 420 talents9:28 That is, about 14 metric tons of gold, which they delivered to King Solomon.