1 Mafumu 8 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 8:1-66

Abwera ndi Bokosi la Chipangano ku Nyumba ya Yehova

1Pamenepo Mfumu Solomoni inasonkhanitsa akuluakulu a Israeli, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli mu Yerusalemu, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, Mzinda wa Davide. 2Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Mfumu Solomoni nthawi ya chikondwerero cha mwezi wa Etanimu, mwezi wachisanu ndi chiwiri.

3Akuluakulu onse a Israeli atafika, ansembe ananyamula Bokosi la Chipangano, 4ndipo anabwera nalo Bokosi la Yehova pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula, 5ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.

6Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a akerubi. 7Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira. 8Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino. 9Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.

10Ansembe atatuluka mʼMalo Opatulikawo, mtambo unadzaza Nyumba ya Yehova. 11Ndipo ansembewo sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza mʼNyumba ya Yehova.

12Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda; 13taonani ndithu, ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”

14Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa. 15Ndipo inati:

“Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati, 16‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga Aisraeli ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba, koma ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’

17“Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli. 18Koma Yehova ananena kwa abambo anga, Davide, kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira nyumba Dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo. 19Komatu, si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu, koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye adzandimangire Nyumba.’

20“Yehova wasunga zimene analonjeza: ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli. 21Ndalikonzera malo Bokosi la Chipangano mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi makolo athu pamene anawatulutsa mʼdziko la Igupto.”

Pemphero Lodzipereka la Solomoni

22Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba, 23nati:

“Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pansi pa dziko, inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse. 24Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu, monga mmene tikuonera lero lino.

25“Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu, pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo mokhulupirika monga iwe wachitira.’ 26Ndipo tsopano, Inu Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide abambo anga.

27“Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni, sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga! 28Koma Inu Yehova Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu lero lino. 29Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usiku ndi usana, malo ano amene Inu munanena kuti, ‘Dzina langa lidzakhala mʼmenemo,’ choncho imvani pemphero limene mtumiki wanu akupemphera akuyangʼana malo ano. 30Imvani pembedzero la mtumiki wanu ndi la anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.

31“Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino, 32imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti ndi wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.

33“Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani, ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera kwa Inu mʼNyumba ino, 34pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa makolo awo.

35“Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu, ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga, 36pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.

37“Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene mdani wazungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera, 38ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso a mu mtima mwake ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino, 39pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo chitanipo kanthu. Muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita, popeza inu mumadziwa mtima wake (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu onse), 40motero iwo adzakuopani masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.

41“Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu, 42pakuti anthu adzamva za dzina lanu lotchukali ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino, 43pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti Nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi Dzina lanu.

44“Pamene anthu anu apita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo pamene apemphera kwa Yehova moyangʼana mzinda umene mwausankha ndi Nyumba imene ine ndamangira Dzina lanu, 45imvani kumwambako pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo apambanitseni.

46“Pamene akuchimwirani, popeza palibe munthu amene sachimwa, ndipo Inu nʼkuwakwiyira ndi kuwapereka kwa mdani, amene adzawatenga ukapolo kupita ku dziko lake, kutali kapena pafupi; 47ndipo ngati asintha maganizo ali ku dziko la ukapololo ndi kulapa ndi kukudandaulirani mʼdziko la owagonjetsa ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa, tachita zinthu zoyipa,’ 48ndipo ngati abwerera kwa Inu ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse mʼdziko la adani awo amene anawatenga ukapolo, ndi kupemphera kwa Inu moyangʼana dziko limene munapereka kwa makolo awo, moyangʼana mzinda umene munawusankha ndiponso Nyumba imene ine ndamangira Dzina lanu, 49imvani kumwambako, malo anu wokhalamo, imvani pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwachitire zabwino. 50Ndipo khululukirani anthu anu amene akuchimwirani. Khululukirani zolakwa zonse akuchitirani ndipo mufewetse mitima ya amene anawagonjetsawo kuti awachitire chifundo; 51popeza ndi anthu anu ndiponso cholowa chanu, anthu omwe munawatulutsa ku Igupto, kuwachotsa mʼngʼanjo yamoto yosungunula zitsulo.

52“Maso anu atsekuke kuti aone dandawulo la mtumiki wanu ndiponso madandawulo a anthu anu Aisraeli, ndipo mutchere khutu nthawi iliyonse pamene akulirirani. 53Pakuti Inu munawasiyanitsa ndi anthu a mitundu ina yonse ya dziko lonse kuti akhale cholowa chanu, monga momwe munanenera kudzera mwa mtumiki wanu Mose pamene Inu, Ambuye Yehova, munatulutsa makolo athu ku Igupto.”

54Solomoni atamaliza mapemphero ndi mapembedzero onsewa kwa Yehova, anayimirira pa guwa lansembe la Yehova, nagwada atakweza manja ake kumwamba. 55Anayimirira ndi kudalitsa gulu lonse la Aisraeli ndi mawu okweza, nati:

56“Atamandike Yehova, amene wapereka mpumulo kwa anthu ake Aisraeli monga momwe analonjezera. Palibe mawu ndi amodzi omwe amene anapita pachabe pa malonjezo ake onse abwino amene anawapereka kudzera mwa mtumiki wake Mose. 57Yehova Mulungu wathu akhale nafe monga momwe anakhalira ndi makolo athu; asatisiye kapena kutitaya. 58Atembenuzire mitima yathu kwa Iye, kuti tiyende mʼnjira zake zonse ndi kusunga mawu ake, malamulo ake ndi malangizo ake amene anapereka kwa makolo athu. 59Ndipo mawu angawa, amene ndapemphera pamaso pa Yehova, asayiwalike pamaso pa Yehova Mulungu wathu usana ndi usiku, ndipo Iye alimbikitse mtumiki wake ndiponso athandize Aisraeli, anthu ake powapatsa zosowa zawo za tsiku ndi tsiku, 60kotero kuti anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi adziwe kuti Yehova ndi Mulungu ndipo kuti palibenso wina. 61Koma mitima yanu ikhale yodzipereka kwathunthu kwa Yehova Mulungu wanu, kutsatira malamulo ake ndi kumvera malangizo ake, monga lero lino.”

Mwambo Wopereka Nyumba ya Mulungu

62Ndipo mfumu pamodzi ndi Aisraeli onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova. 63Solomoni anapereka nsembe zachiyanjano kwa Yehova: ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Motero mfumu pamodzi ndi Aisraeli onse anapatula Nyumba ya Yehova.

64Tsiku lomwelo mfumu inapatulanso malo a pakati pa bwalo limene linali kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndiponso nthuli za mafuta za nsembe yachiyanjano, chifukwa guwa lansembe la mkuwa limene linali pamaso pa Yehova linali lochepa kwambiri ndipo nsembe zonse zopsereza, nsembe zachakudya, ndi nthuli za mafuta a nsembe zachiyanjano sizikanakwanirapo.

65Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha ku Igupto. Anachita chikondwerero chimenechi pamaso pa Yehova Mulungu wathu kwa masiku asanu ndi awiri, anawonjezerapo masiku ena asanu ndi awiri, onse pamodzi ngati masiku 14. 66Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Solomoni anawuza anthu kuti apite kwawo. Anthuwo anathokoza mfumu ndipo kenaka anapita kwawo mokondwa ndi mosangalala mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira mtumiki wake Davide ndi anthu ake Aisraeli.

New Serbian Translation

1. Књига о царевима 8:1-66

Освећење Дома

1Тада је Соломон окупио у Јерусалиму израиљске старешине, све племенске кнезове и вође израиљских породица, да пренесу Ковчег савеза Господњег из Давидовог града, са Сиона. 2Сви Израиљци су се окупили код цара Соломона на празник у месецу Етаниму, што је седми месец.

3Кад су дошле све израиљске старешине, свештеници су понели Ковчег. 4Понели су и Ковчег Господњи и Шатор од састанка и све свето посуђе, које је било у Шатору; носили су их свештеници и Левити. 5А цар Соломон и сва заједница Израиљаца, који су се окупили код њега пред Ковчегом, приносили су на жртву толико ситне и крупне стоке да их се није могло избројити ни прорачунати.

6Затим су свештеници донели Ковчег савеза Господњег на његово место, у унутрашње Светилиште Дома, у Светињу над светињама, под крила херувима. 7Наиме, херувими су имали раширена крила над Ковчегом, тако да су од горе заклањали Ковчег и његове дршке. 8Дршке су биле толико дугачке да су се њихови крајеви видели из Светилишта испред Светиње над светињама. Ипак, нису се виделе споља. Тамо су до дана данашњег. 9У Ковчегу није било ничег осим две камене плоче, које је тамо положио Мојсије на Хориву, кад је Господ склопио савез са Израиљцима, након што су изашли из Египта.

10Кад су свештеници изашли из Светилишта, облак је испунио Дом Господњи. 11Свештеници нису могли да стоје и обављају службу због облака, јер је слава Господња испунила Дом Господњи.

12Тада Соломон рече: „Господ је рекао да ће пребивати у густој тами. 13Ја сам ти саградио величанствени Дом, стан где ћеш пребивати довека.“

Соломонов говор

14Затим се цар окренуо и благословио сав збор Израиљев, док је сав збор Израиљев стајао.

15Тада рече:

„Нека је благословен Господ, Бог Израиљев, који је својом руком извршио оно што је својим устима обећао моме оцу Давиду, рекавши: 16’Од дана кад сам извео свој народ Израиљ из Египта, нисам изабрао град међу свим племенима Израиљевим да се сагради Дом где би пребивало моје име; али сам изабрао Давида да влада над мојим народом Израиљем.’

17Мој отац Давид је наумио да сазида Дом имену Господа, Бога Израиљевог. 18Но, Господ рече моме оцу Давиду: ’Добро си учинио што си у свом срцу наумио да сазидаш Дом моме имену. 19Ипак, нећеш ти саградити Дом, него ће твој син, који је потекао из твојих бедара, саградити Дом моме имену.’

20Господ је одржао обећање, те сам ја наследио свога оца Давида на Израиљевом престолу, како је Господ обећао, и изградио Дом имену Господа, Бога Израиљевог. 21Поставио сам и место за Ковчег, где је савез Господњи, који је он склопио са нашим прецима кад их је извео из Египта.“

Соломонова молитва

22Соломон је стао пред жртвеник Господњи, испред свег збора Израиљевог, испружио руке према небу 23и рекао:

„О, Господе, Боже Израиљев, нема Бога као што си ти, горе на небесима, ни доле на земљи, који чуваш савез и милост својим слугама који ходају пред тобом свим својим срцем. 24Ти си испунио што си рекао своме слузи, моме оцу Давиду; што си рекао својим устима, то си извршио својом руком, као што је то данас.

25А сад, Господе, Боже Израиљев, одржи што си обећао своме слузи, моме оцу Давиду, кад си рекао: ’Неће ти нестати потомка преда мном који ће седети на Израиљевом престолу, само ако твоји синови буду пазили на свој пут и ходили преда мном, као што си ти ходио преда мном.’ 26А сад, Боже Израиљев, нека се обистини твоја реч, коју си рекао своме слузи, моме оцу Давиду.

27Али зар ће Бог заиста боравити на земљи? Ни највиша те небеса не могу обухватити, а камоли овај Дом што сам саградио. 28Обазри се на молитву слуге свога и на његову молбу, Господе Боже; послушај вапај и молитву, коју слуга твој упућује данас пред тобом. 29Нека твоје очи мотре на овај Дом и ноћу и дању, према месту за које си рекао: ’Моје ће име бити тамо’, како би чуо молитву коју ти слуга твој упућује на овом месту. 30Почуј преклињање свога слуге и свога народа Израиља којим се моле на овом месту. Послушај на небу, на месту где пребиваш – послушај и опрости.

31Кад неко згреши против свог ближњега, те се од њега тражи да се закуне, и он дође и закуне се пред твојим жртвеником у овом Дому, 32ти чуј с небеса и делуј, те осуди онога који је учинио безакоње сваљујући на његову главу према ономе што је учинио. А праведника награди према његовој праведности.

33Ако твој народ Израиљ буде поражен од непријатеља зато што су згрешили против тебе, али се покају пред тобом и дају славу твоме имену, па се помоле и преклињу за милост у овом Дому, 34ти чуј на небесима и опрости грех свога народа Израиља, и врати их у земљу коју си дао њиховим прецима.

35Ако се небо затвори и не даје кишу, јер су згрешили против тебе, па се помоле на овом месту, те одају славу твоме имену и покају се за своје грехе, пошто их понизиш, 36ти чуј на небесима и опрости грех својих слугу, свога народа Израиља. И кад их научиш добром путу да по њему ходе, пошаљи кишу својој земљи, коју си дао своме народу у наследство.

37Ако земљу задеси глад, или помор, суша, кукољ, скакавци, гусенице, или кад их непријатељ опколи у којем од њихових градова; каква год да је пошаст или болест, 38па било ко од свег твог народа Израиља осети тегобу у свом срцу и упути молитву или молбу ширећи руке према овом Дому, 39услиши на небесима, на твом Пребивалишту. Опрости и делуј: дај свакоме по свим његовим делима, јер ти знаш његово срце – само ти знаш срце свих људи – 40да би те се бојали у све дане док живе у земљи коју си дао њиховим оцима.

41Ако и странац, који није од твог народа Израиља, дође из далеке земље ради твог имена, 42јер ће се чути за твоје велико име и за твоју моћну руку и испружену мишицу – ако дође и помоли се у овом Дому – 43услиши га на небесима, на твом Пребивалишту, и учини све за шта ти овај странац завапи, да би народи на земљи упознали твоје име и да би те се бојали, као твој народ Израиљ, и да би знали да се твоје име призива над овим Домом који сам саградио.

44Ако твој народ изађе у бој против свога непријатеља путем којим га ти пошаљеш, и они се помоле Господу према граду који си изабрао, и према Дому који сам саградио твоме имену, 45чуј на небесима њихову молитву и њихову молбу, те им додели правду.

46Ако згреше против тебе – јер нема човека који не чини грех – и ти се разгневиш на њих и изручиш их њиховим непријатељима, који их одведу као заробљенике у непријатељску земљу, било далеко или близу, 47ако тада дођу к себи у земљи у којој су заробљени и покају се, те се почну молити теби у земљи својих поробљивача, говорећи: ’Згрешили смо, учинили смо неправду, скривили смо’, 48па се врате к теби свим срцем и свом душом у земљи својих непријатеља који су их поробили, и помоле се теби према својој земљи коју си дао њиховим оцима и према граду који си изабрао и према Дому који сам саградио за твоје име, 49ти чуј на небесима, на твом Пребивалишту, њихову молитву и молбу, и учини им по правди. 50Тада опрости своме народу, који је згрешио против тебе и за све преступе који су учинили против тебе, и смилуј им се пред њиховим поробљивачима да би се они смиловали на њих. 51Јер они су твој народ и твоје наследство, кога си извео из Египта, из топионице гвожђа.

52Нека твоје очи бдију над молбом твога слуге и над молбом твога народа Израиља, и услиши их кад год те призову. 53Јер ти си их, Господе Боже, издвојио себи за наследство од свих народа на земљи, као што си рекао преко свога слуге Мојсија, кад си извео наше очеве из Египта.“

Соломон благосиља народ

54Кад је Соломон завршио сву ову молитву и молбу коју је упутио Господу, устао је испред жртвеника Господњег где је клечао на својим коленима с раширеним рукама према небу. 55Затим се усправио, па је громким гласом благословио сав збор Израиљев, рекавши:

56„Нека је благословен Господ који је дао починак своме народу Израиљу, као што је обећао; ниједна реч није остала неиспуњена од свих добрих обећања које је дао преко свога слуге Мојсија. 57Нека Господ, Бог наш, буде с нама као што је био с нашим оцима; нека нас не напусти и не остави. 58Нека приклони наша срца к себи, да следимо све његове путеве, и да држимо његове заповеди, прописе и одредбе, које је заповедио нашим оцима. 59Нека ове речи што сам измолио пред Господом, буду близу Господа, Бога нашега, дању и ноћу, да би дан за даном чинио правду своме слузи и своме народу Израиљу, 60те да би сви народи на земљи знали да Господ јесте Бог и да нема другог. 61Стога, нека ваше срце буде потпуно предано Господу, Богу нашем, следећи његове прописе и држећи његове заповеди, као овога дана.“

Посвећење Дома

62Затим су цар и сав израиљски народ с њим принели жртве пред Господом. 63Соломон је принео Господу као жртву мира двадесет две хиљаде говеда и стотину двадесет хиљада оваца. Тако су цар и сви Израиљци посветили Дом Господњи.

64Тог дана је цар посветио средиште дворишта, које је испред Дома Господњег. Наиме, тамо је принео жртву свеспалницу, житну жртву, и сало жртава мира, пошто је бронзани жртвеник који је био пред Господом био премален да би на њега стале жртве свеспалнице, житне жртве и сало жртава мира.

65У то време је Соломон, са свим Израиљем, приредио свечаност – велики сабор пред Господом, Богом нашим, с народом од Лево-Амата до Египатског потока, седам дана и још седам дана, укупно четрнаест дана. 66Осмог дана је отпремио народ, а они су благословили цара и отишли својим кућама, веселећи се и радујући се у срцу због свег добра што је Господ учинио своме слузи Давиду и своме народу Израиљу.