1 Mafumu 8 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 8:1-66

Abwera ndi Bokosi la Chipangano ku Nyumba ya Yehova

1Pamenepo Mfumu Solomoni inasonkhanitsa akuluakulu a Israeli, atsogoleri onse a mafuko ndi akuluakulu a mabanja a Aisraeli mu Yerusalemu, kuti akatenge Bokosi la Chipangano la Yehova ku Ziyoni, Mzinda wa Davide. 2Aisraeli onse anasonkhana pamaso pa Mfumu Solomoni nthawi ya chikondwerero cha mwezi wa Etanimu, mwezi wachisanu ndi chiwiri.

3Akuluakulu onse a Israeli atafika, ansembe ananyamula Bokosi la Chipangano, 4ndipo anabwera nalo Bokosi la Yehova pamodzi ndi tenti ya msonkhano ndi ziwiya zonse zopatulika zimene zinali mʼmenemo. Ansembe ndi Alevi ndiye anazinyamula, 5ndipo Mfumu Solomoni ndi gulu lonse la Aisraeli amene anasonkhana naye anali patsogolo pa Bokosi la Chipangano, akupereka nsembe nkhosa zambiri ndi ngʼombe zambiri zosawerengeka.

6Ansembe anafika nalo Bokosi la Chipangano la Yehova mʼchipinda chamʼkati mwenimweni, Malo Opatulika Kwambiri, ndipo analiyika pansi pa mapiko a akerubi. 7Akerubiwo anatambalitsa mapiko awo pamwamba pa Bokosi la Chipangano ndipo anaphimba bokosilo pamodzi ndi mitengo yonyamulira. 8Mitengoyi inali yayitali kwambiri ndipo inkaonekera kunja kwa chipinda chamʼkati cha Malo Opatulika koma osati kunja kwa Malo Opatulikawo; ndipo mitengoyi ilipo mpaka lero lino. 9Mʼbokosimo munalibe kanthu kena kalikonse kupatula miyala iwiri imene Mose anayikamo ku Horebu, kumene Yehova anachita pangano ndi Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto.

10Ansembe atatuluka mʼMalo Opatulikawo, mtambo unadzaza Nyumba ya Yehova. 11Ndipo ansembewo sanathe kugwira ntchito yawo chifukwa cha mtambowo, pakuti ulemerero wa Yehova unadzaza mʼNyumba ya Yehova.

12Pamenepo Solomoni anati, “Yehova anati adzakhala mʼmitambo yakuda; 13taonani ndithu, ine ndakumangirani Nyumba yokongola kwambiri, malo woti muzikhalamo mpaka muyaya.”

14Aisraeli onse ali chiyimire pomwepo, mfumu inatembenuka ndi kuwadalitsa. 15Ndipo inati:

“Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wachita ndi dzanja lake zimene analonjeza ndi pakamwa pake kwa Davide abambo anga. Pakuti Iye anati, 16‘Kuyambira tsiku limene ndinatulutsa anthu anga Aisraeli ku Igupto, sindinasankhe mzinda wina uliwonse pa fuko lina lililonse la Aisraeli kuti kumeneko andimangire Nyumba, koma ndasankha Davide kuti alamulire anthu anga Aisraeli.’

17“Abambo anga Davide anali ndi maganizo mu mtima mwawo oti amangire nyumba Yehova, Mulungu wa Israeli. 18Koma Yehova ananena kwa abambo anga, Davide, kuti, ‘Popeza zinali mu mtima mwako kumangira nyumba Dzina langa, unachita bwino kukhala ndi maganizo amenewa mu mtima mwakomo. 19Komatu, si iwe amene udzamanga Nyumba ya Mulungu, koma mwana wako, mwana amene iwe udzabereke. Iyeyo ndiye adzandimangire Nyumba.’

20“Yehova wasunga zimene analonjeza: ine ndalowa mʼmalo mwa abambo anga Davide ndipo tsopano ndili pa mpando waufumu wa Israeli, monga momwe Yehova analonjezera, ndipo ndamangira nyumba Dzina la Yehova, Mulungu wa Israeli. 21Ndalikonzera malo Bokosi la Chipangano mmene muli pangano la Yehova limene anapangana ndi makolo athu pamene anawatulutsa mʼdziko la Igupto.”

Pemphero Lodzipereka la Solomoni

22Pamenepo Solomoni anayimirira patsogolo pa guwa lansembe la Yehova pamaso pa gulu lonse la Aisraeli ndipo anakweza manja ake kumwamba, 23nati:

“Inu Yehova, Mulungu wa Israeli, palibe Mulungu wofanana nanu kumwamba kapena pansi pa dziko, inu amene mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa atumiki anu amene amayenda pamaso panu ndi mtima wawo wonse. 24Inu mwasunga lonjezo lanu kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu. Inde zimene munalonjeza ndi pakamwa panu, mwazikwaniritsa ndi manja anu, monga mmene tikuonera lero lino.

25“Ndipo tsopano, Inu Yehova Mulungu wa Israeli, sungani zimene munalonjeza kwa abambo anga Davide, mtumiki wanu, pamene munati, ‘Sudzasowa munthu wokhala pamaso panga pa mpando waufumu wa Israeli, ngati ana ako adzasamalira mayendedwe awo mokhulupirika monga iwe wachitira.’ 26Ndipo tsopano, Inu Mulungu wa Israeli, lolani kuti mawu anu akwaniritsidwe amene munalonjeza mtumiki wanu Davide abambo anga.

27“Kodi Mulungu angakhaledi pa dziko lapansi? Mlengalenga ngakhale kumwamba kwenikweni, sikungakukwaneni. Nanga kuli bwanji ndi Nyumba iyi imene ndamanga! 28Koma Inu Yehova Mulungu wanga, imvani pemphero ndi pembedzero la mtumiki wanu. Imvani kulira ndi pemphero la mtumiki wanu limene ndikupempha pamaso panu lero lino. 29Maso anu azikhala otsekuka kuyangʼana Nyumba ino usiku ndi usana, malo ano amene Inu munanena kuti, ‘Dzina langa lidzakhala mʼmenemo,’ choncho imvani pemphero limene mtumiki wanu akupemphera akuyangʼana malo ano. 30Imvani pembedzero la mtumiki wanu ndi la anthu anu Aisraeli pamene akupemphera akuyangʼana malo ano. Imvani kumwambako, malo anu amene mumakhala; ndipo mukamva muzitikhululukira.

31“Munthu akalakwira mnzake, nawuzidwa kuti alumbire, akabwera kudzalumbira patsogolo pa guwa lansembe la Nyumba ino, 32imvani kumwambako ndi kuchitapo kanthu. Weruzani atumiki anuwo, wochimwa mugamule kuti ndi wolakwa ndipo alangidwe chifukwa cha zimene wachita. Wosachimwa mugamule kuti ndi wosalakwa, ndipo muonetse kusalakwa kwakeko.

33“Anthu anu Aisraeli akagonja kwa adani awo chifukwa akuchimwirani, ndipo akatembenukira kwa Inu ndi kuvomereza Dzina lanu, kupemphera ndi kupembedzera kwa Inu mʼNyumba ino, 34pamenepo imvani kumwambako ndi kukhululukira tchimo la anthu anu Aisraeli ndi kuwabweretsa ku dziko limene munawapatsa makolo awo.

35“Pamene kumwamba kwatsekeka ndipo mvula sikugwa chifukwa anthu anu akuchimwirani, ndipo pamene apemphera akuyangʼana malo ano ndi kuvomereza Dzina lanu, ndi kutembenuka kuchoka ku machimo awo chifukwa inu mwawalanga, 36pamenepo imvani kumwambako ndipo muwakhululukire atumiki anu, anthu anu Aisraeli. Aphunzitseni makhalidwe oyenera ndipo gwetsani mvula mʼdziko limene munapereka kwa anthu anu monga cholowa chawo.

37“Pamene mʼdziko mwagwa njala kapena mliri, chinoni kapena chiwawu, dzombe kapena kapuchi, kapena pamene mdani wazungulira mzinda wawo wina uliwonse, kaya mavuto kapena matenda abwera, 38ndipo wina aliyense mwa Aisraeli akapemphera kapena kukudandaulirani, aliyense wa iwo akadziwa masautso a mu mtima mwake ndi kukweza manja awo kuloza Nyumba ino, 39pamenepo imvani kumwambako, malo anu wokhalamo. Khululukani ndipo chitanipo kanthu. Muchitire aliyense molingana ndi zonse zimene anachita, popeza inu mumadziwa mtima wake (pakuti ndinu nokha amene mumadziwa mitima ya anthu onse), 40motero iwo adzakuopani masiku onse amene adzakhale mʼdziko limene munalipereka kwa makolo athu.

41“Ndipo kunena za mlendo amene si mmodzi wa anthu anu Aisraeli, koma wabwera kuchokera ku dziko lakutali chifukwa cha dzina lanu, 42pakuti anthu adzamva za dzina lanu lotchukali ndiponso za dzanja lanu lamphamvu ndi lochita zazikulu, kudzapemphera akuyangʼana Nyumba ino, 43pamenepo imvani kumwambako, malo anu okhalamo, ndipo muchite zonse zimene mlendoyo akukupemphani, kotero kuti anthu onse a dziko lapansi adziwe dzina lanu ndi kukuopani monga amachitira anthu anu Aisraeli, ndipo adziwe kuti Nyumba ino imene ndakumangirani imadziwika ndi Dzina lanu.

44“Pamene anthu anu apita ku nkhondo kukamenyana ndi adani awo, kulikonse kumene mungawatume, ndipo pamene apemphera kwa Yehova moyangʼana mzinda umene mwausankha ndi Nyumba imene ine ndamangira Dzina lanu, 45imvani kumwambako pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo apambanitseni.

46“Pamene akuchimwirani, popeza palibe munthu amene sachimwa, ndipo Inu nʼkuwakwiyira ndi kuwapereka kwa mdani, amene adzawatenga ukapolo kupita ku dziko lake, kutali kapena pafupi; 47ndipo ngati asintha maganizo ali ku dziko la ukapololo ndi kulapa ndi kukudandaulirani mʼdziko la owagonjetsa ndi kunena kuti, ‘Ife tachimwa, tachita zolakwa, tachita zinthu zoyipa,’ 48ndipo ngati abwerera kwa Inu ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse mʼdziko la adani awo amene anawatenga ukapolo, ndi kupemphera kwa Inu moyangʼana dziko limene munapereka kwa makolo awo, moyangʼana mzinda umene munawusankha ndiponso Nyumba imene ine ndamangira Dzina lanu, 49imvani kumwambako, malo anu wokhalamo, imvani pemphero lawo ndi kudandaula kwawo, ndipo muwachitire zabwino. 50Ndipo khululukirani anthu anu amene akuchimwirani. Khululukirani zolakwa zonse akuchitirani ndipo mufewetse mitima ya amene anawagonjetsawo kuti awachitire chifundo; 51popeza ndi anthu anu ndiponso cholowa chanu, anthu omwe munawatulutsa ku Igupto, kuwachotsa mʼngʼanjo yamoto yosungunula zitsulo.

52“Maso anu atsekuke kuti aone dandawulo la mtumiki wanu ndiponso madandawulo a anthu anu Aisraeli, ndipo mutchere khutu nthawi iliyonse pamene akulirirani. 53Pakuti Inu munawasiyanitsa ndi anthu a mitundu ina yonse ya dziko lonse kuti akhale cholowa chanu, monga momwe munanenera kudzera mwa mtumiki wanu Mose pamene Inu, Ambuye Yehova, munatulutsa makolo athu ku Igupto.”

54Solomoni atamaliza mapemphero ndi mapembedzero onsewa kwa Yehova, anayimirira pa guwa lansembe la Yehova, nagwada atakweza manja ake kumwamba. 55Anayimirira ndi kudalitsa gulu lonse la Aisraeli ndi mawu okweza, nati:

56“Atamandike Yehova, amene wapereka mpumulo kwa anthu ake Aisraeli monga momwe analonjezera. Palibe mawu ndi amodzi omwe amene anapita pachabe pa malonjezo ake onse abwino amene anawapereka kudzera mwa mtumiki wake Mose. 57Yehova Mulungu wathu akhale nafe monga momwe anakhalira ndi makolo athu; asatisiye kapena kutitaya. 58Atembenuzire mitima yathu kwa Iye, kuti tiyende mʼnjira zake zonse ndi kusunga mawu ake, malamulo ake ndi malangizo ake amene anapereka kwa makolo athu. 59Ndipo mawu angawa, amene ndapemphera pamaso pa Yehova, asayiwalike pamaso pa Yehova Mulungu wathu usana ndi usiku, ndipo Iye alimbikitse mtumiki wake ndiponso athandize Aisraeli, anthu ake powapatsa zosowa zawo za tsiku ndi tsiku, 60kotero kuti anthu a mitundu yonse pa dziko lapansi adziwe kuti Yehova ndi Mulungu ndipo kuti palibenso wina. 61Koma mitima yanu ikhale yodzipereka kwathunthu kwa Yehova Mulungu wanu, kutsatira malamulo ake ndi kumvera malangizo ake, monga lero lino.”

Mwambo Wopereka Nyumba ya Mulungu

62Ndipo mfumu pamodzi ndi Aisraeli onse anapereka nsembe pamaso pa Yehova. 63Solomoni anapereka nsembe zachiyanjano kwa Yehova: ngʼombe 22,000, nkhosa ndi mbuzi 120,000. Motero mfumu pamodzi ndi Aisraeli onse anapatula Nyumba ya Yehova.

64Tsiku lomwelo mfumu inapatulanso malo a pakati pa bwalo limene linali kutsogolo kwa Nyumba ya Yehova ndiponso nthuli za mafuta za nsembe yachiyanjano, chifukwa guwa lansembe la mkuwa limene linali pamaso pa Yehova linali lochepa kwambiri ndipo nsembe zonse zopsereza, nsembe zachakudya, ndi nthuli za mafuta a nsembe zachiyanjano sizikanakwanirapo.

65Choncho nthawi imeneyi, Solomoni anachita chikondwerero pamodzi ndi Aisraeli onse. Unali msonkhano waukulu, kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Chigwa cha ku Igupto. Anachita chikondwerero chimenechi pamaso pa Yehova Mulungu wathu kwa masiku asanu ndi awiri, anawonjezerapo masiku ena asanu ndi awiri, onse pamodzi ngati masiku 14. 66Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Solomoni anawuza anthu kuti apite kwawo. Anthuwo anathokoza mfumu ndipo kenaka anapita kwawo mokondwa ndi mosangalala mʼmitima mwawo chifukwa cha zinthu zabwino zimene Yehova anachitira mtumiki wake Davide ndi anthu ake Aisraeli.

New International Reader’s Version

1 Kings 8:1-66

The Ark Is Brought to the Temple

1Then King Solomon sent for the elders of Israel. He told them to come to him in Jerusalem. They included all the leaders of the tribes. They also included the chiefs of the families of Israel. Solomon wanted them to bring up the ark of the Lord’s covenant from Zion. Zion was the City of David. 2All the Israelites came together to where King Solomon was. It was at the time of the Feast of Booths. The feast was held in the month of Ethanim. That’s the seventh month.

3All the elders of Israel arrived. Then the priests picked up the ark and carried it. 4They brought up the ark of the Lord. They also brought up the tent of meeting and all the sacred things in the tent. The priests and Levites carried everything up. 5The entire community of Israel had gathered around King Solomon. All of them were in front of the ark. They sacrificed huge numbers of sheep and cattle. There were so many animals that they couldn’t be recorded. In fact, they couldn’t even be counted.

6The priests brought the ark of the Lord’s covenant law to its place in the Most Holy Room of the temple. They put it under the wings of the cherubim. 7Their wings were spread out over the place where the ark was. They covered the ark. They also covered the poles used to carry it. 8The poles were very long. Their ends could be seen from the Holy Room in front of the Most Holy Room. But they couldn’t be seen from outside the Holy Room. They are still there to this day. 9There wasn’t anything in the ark except the two stone tablets. Moses had placed them in it at Mount Horeb. That’s where the Lord had made a covenant with the Israelites. He made it after they came out of Egypt.

10The priests left the Holy Room. Then the cloud filled the temple of the Lord. 11The priests couldn’t do their work because of it. That’s because the glory of the Lord filled his temple.

12Then Solomon said, “Lord, you have said you would live in a dark cloud. 13As you can see, I’ve built a beautiful temple for you. You can live in it forever.”

14The whole community of Israel was standing there. The king turned around and gave them his blessing. 15Then he said,

“I praise the Lord. He is the God of Israel. With his own mouth he made a promise to my father David. With his own powerful hand he made it come true. He said, 16‘I brought my people Israel out of Egypt. Ever since, I haven’t chosen a city in any tribe of Israel where a temple could be built for my Name. But I have chosen David to rule over my people Israel.’

17“With all his heart my father David wanted to build a temple. He wanted to do it so the Lord could put his Name there. The Lord is the God of Israel. 18But the Lord spoke to my father David. He said, ‘With all your heart you wanted to build a temple for my Name. It is good that you wanted to do that. 19But you will not build the temple. Instead, your son will build the temple for my Name. He is your own flesh and blood.’

20“The Lord has kept the promise he made. I’ve become the next king after my father David. Now I’m sitting on the throne of Israel. That’s exactly what the Lord promised would happen. I’ve built the temple where the Lord will put his Name. He is the God of Israel. 21I’ve provided a place for the ark there. The tablets of the Lord’s covenant law are inside it. He made that covenant with our people of long ago. He made it when he brought them out of Egypt.”

Solomon Prays to Set the Temple Apart to the Lord

22Then Solomon stood in front of the Lord’s altar. He stood in front of the whole community of Israel. He spread out his hands toward heaven. 23He said,

Lord, you are the God of Israel. There is no God like you in heaven above or on earth below. You keep the covenant you made with us. You show us your love. You do that when we follow you with all our hearts. 24You have kept your promise to my father David. He was your servant. With your mouth you made a promise. With your powerful hand you have made it come true. And today we can see it.

25Lord, you are the God of Israel. Keep the promises you made to my father David. Do it for him. He was your servant. Here is what you said to him. ‘A son from your family line will sit before me on the throne of Israel. This will always be true if your children after you are careful in everything they do. They must live in my sight faithfully the way you have lived.’ 26God of Israel, let your promise to my father David come true.

27“But will you really live on earth? After all, the heavens can’t hold you. In fact, even the highest heavens can’t hold you. So this temple I’ve built certainly can’t hold you! 28But please pay attention to my prayer. Lord my God, be ready to help me as I make my appeal to you. Listen to my cry for help. Hear the prayer I’m praying to you today. 29Let your eyes look toward this temple night and day. You said, ‘I will put my Name there.’ So please listen to the prayer I’m praying toward this place. 30Hear me when I ask you to help us. Listen to your people Israel when they pray toward this place. Listen to us from heaven. It’s the place where you live. When you hear us, forgive us.

31“Suppose someone does something wrong to their neighbor. And the person who has done something wrong is required to give their word. They must tell the truth about what they have done. They must come and do it in front of your altar in this temple. 32When they do, listen to them from heaven. Take action. Judge between the person and their neighbor. Punish the guilty one. Do to that person what they have done to their neighbor. Deal with the one who isn’t guilty in a way that shows they are free from blame. That will prove they aren’t guilty.

33“Suppose your people Israel have lost the battle against their enemies. And suppose they’ve sinned against you. But they turn back to you and praise your name. They pray to you in this temple. And they ask you to help them. 34Then listen to them from heaven. Forgive the sin of your people Israel. Bring them back to the land you gave to their people who lived long ago.

35“Suppose your people have sinned against you. And because of that, the sky is closed up and there isn’t any rain. But your people pray toward this place. They praise you by admitting they’ve sinned. And they turn away from their sin because you have made them suffer. 36Then listen to them from heaven. Forgive the sin of your people Israel. Teach them the right way to live. Send rain on the land you gave them as their share.

37“Suppose there isn’t enough food in the land. And a plague strikes the land. The hot winds completely dry up our crops. Or locusts or grasshoppers come and eat them up. Or an enemy surrounds one of our cities and gets ready to attack it. Or trouble or sickness comes. 38But suppose one of your people prays to you. They ask you to help them. They are aware of how much their own heart is suffering. And they spread out their hands toward this temple to pray. 39Then listen to them from heaven. It’s the place where you live. Forgive them. Take action. Deal with everyone in keeping with everything they do. You know their hearts. In fact, you are the only one who knows every human heart. 40Your people will have respect for you. They will respect you as long as they are in the land you gave our people long ago.

41“Suppose there are outsiders who don’t belong to your people Israel. And they have come from a land far away. They’ve come because they’ve heard about your name. 42When they get here, they will find out even more about your great name. They’ll hear about how you reached out your mighty hand and powerful arm. So they’ll come and pray toward this temple. 43Then listen to them from heaven. It’s the place where you live. Do what those outsiders ask you to do. Then all the nations on earth will know you. They will have respect for you. They’ll respect you just as your own people Israel do. They’ll know that your Name is in this house I’ve built.

44“Suppose your people go to war against their enemies. It doesn’t matter where you send them. And suppose they pray to you toward the city you have chosen. They pray toward the temple I’ve built for your Name. 45Then listen to them from heaven. Listen to their prayer for your help. Stand up for them.

46“Suppose your people sin against you. After all, there isn’t anyone who doesn’t sin. And suppose you get angry with them. You hand them over to their enemies. They take them as prisoners to their own lands. It doesn’t matter whether those lands are near or far away. 47But suppose your people change their ways in the land where they are held as prisoners. They turn away from their sins. They beg you to help them in the land of those who won the battle over them. They say, ‘We have sinned. We’ve done what is wrong. We’ve done what is evil.’ 48And they turn back to you with all their heart and soul. Suppose it happens in the land of their enemies who took them away as prisoners. There they pray to you toward the land you gave their people long ago. They pray toward the city you have chosen. And they pray toward the temple I’ve built for your Name. 49Then listen to them from heaven. It’s the place where you live. Listen to their prayer. Listen to them when they ask you to help them. Stand up for them. 50Your people have sinned against you. Please forgive them. Forgive them for all the wrong things they’ve done against you. And make those who won the battle over them show mercy to them. 51After all, they are your people. They belong to you. You brought them out of Egypt. You brought them out of that furnace that melts iron down and makes it pure.

52“Let your eyes be open to me when I ask you to help us. Let them be open to your people Israel when they ask you to help them. Pay attention to them every time they cry out to you. 53After all, you chose them out of all the nations in the world. You made them your very own people. You did it just as you had announced through your servant Moses. That’s when you brought out of Egypt our people of long ago. You are our Lord and King.”

54Solomon finished praying. He finished asking the Lord to help his people. Then he got up from in front of the Lord’s altar. He had been down on his knees with his hands spread out toward heaven. 55He stood in front of the whole community of Israel. He blessed them with a loud voice. He said,

56“I praise the Lord. He has given peace and rest to his people Israel. That’s exactly what he promised to do. He gave his people good promises through his servant Moses. Every single word of those promises has come true. 57May the Lord our God be with us, just as he was with our people who lived long ago. May he never leave us. May he never desert us. 58May he turn our hearts to him. Then we will live the way he wants us to. We’ll obey the commands, rules and directions he gave our people of long ago. 59I’ve prayed these words to the Lord our God. May he keep them close to him day and night. May he stand up for me. May he also stand up for his people Israel. May he give us what we need every day. 60Then all the nations on earth will know that the Lord is God. They’ll know that there isn’t any other god. 61And may you commit your lives completely to the Lord our God. May you live by his rules. May you obey his commands. May you always do as you are doing now.”

The Temple Is Set Apart to the Lord

62Then the king and the whole community of Israel offered sacrifices to the Lord. 63Solomon sacrificed friendship offerings to the Lord. He sacrificed 22,000 oxen. He also sacrificed 120,000 sheep and goats. So the king and the whole community set the temple of the Lord apart to him.

64On that same day the king set the middle area of the courtyard apart to the Lord. It was in front of the Lord’s temple. There Solomon sacrificed burnt offerings and grain offerings. He also sacrificed the fat of the friendship offerings there. He did it there because the bronze altar that stood in front of the Lord was too small. It wasn’t big enough to hold all the burnt offerings, the grain offerings and the fat of the friendship offerings.

65At that time Solomon celebrated the Feast of Booths. The whole community of Israel was with him. It was a huge crowd. People came from as far away as Lebo Hamath and the Wadi of Egypt. For seven days they celebrated in front of the Lord our God. The feast continued for seven more days. That made a total of 14 days. 66On the following day Solomon sent the people away. They asked the Lord to bless the king. Then they went home. The people were glad. Their hearts were full of joy. That’s because the Lord had done so many good things for his servant David and his people Israel.