1 Mafumu 6 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 6:1-38

Solomoni Amanga Nyumba ya Mulungu

1Patapita zaka 480 Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto, chaka chachinayi cha ulamuliro wa Solomoni mu Israeli, mwezi wa Zivi, umene ndi mwezi wachiwiri, Solomoni anayamba kumanga Nyumba ya Yehova.

2Nyumba imene Solomoni anamangira Yehova mulitali mwake inali mamita 27, mulifupi mwake inali mamita asanu ndi anayi, ndipo msinkhu wake unali mamita 13 ndi theka. 3Chipinda chakubwalo mʼmbali mwake chinali mamita asanu ndi anayi kulingana ndi mulifupi mwa Nyumbayo ndipo kutalika kwake kunali kwa mamita anayi ndi theka. 4Anapanga mazenera amene maferemu ake anali olowa mʼkati mwa makoma a Nyumbayo. 5Mʼmbali mwa makoma a Nyumba yayikulu ndi chipinda chopatulika chamʼkati, anamanga zipinda zosanjikizana, mozungulira. 6Chipinda chapansi, mulifupi mwake chinali mamita awiri, chipinda chapakati mulifupi mwake chinali mamita awiri ndi theka ndipo chipinda chapamwamba penipeni mulifupi mwake chinali mamita atatu. Iye anapanga zinthu zosongoka kunja kwa khoma la kunja kuzungulira Nyumbayo kuti asamapise kanthu pa makoma a Nyumba ya Mulungu.

7Poyimanga Nyumbayo, anagwiritsa ntchito miyala yosemeratu, ndipo pogwira ntchitoyo sipanamveke nyundo, nkhwangwa kapena chida china chilichonse.

8Chipata cholowera ku chipinda chapansi chinali mbali ya kummwera kwa Nyumbayo. Panali makwerero okwerera ku chipinda chapakati ndiponso chipinda cha pamwamba. 9Choncho anamanga Nyumbayo mpaka kuyimaliza ndipo denga lake linali la mitanda ndi matabwa a mkungudza. 10Msinkhu wa chipinda chilichonse unali mamita awiri, ndipo anazilumukiza ku Nyumbayo ndi mitanda yamkungudza.

11Yehova anayankhula ndi Solomoni kuti, 12“Kunena za Nyumba imene ukumangayi, ngati iwe udzamvera malangizo anga ndi kutsatira mawu anga, ngati udzasunga malamulo anga ndi kuwachita, Ine ndidzakwaniritsa zonse zomwe ndinalonjeza Davide abambo ako. 13Ndipo Ine ndidzakhazikika pakati pa ana a Israeli ndipo sindidzawasiya anthu anga Aisraeli.”

14Kotero Solomoni anamanga Nyumba ya Mulungu nayimaliza. 15Anakuta khoma la mʼkati mwake ndi matabwa a mkungudza, kuyambira pansi pa Nyumbayo mpaka ku denga ndipo pansi pa Nyumbayo anayalapo matabwa a payini. 16Kumbuyo kwa Nyumbayo anadula chipinda chachitali mamita asanu ndi anayi. Chipindachi anachimanga ndi matabwa a mkungudza kuyambira pansi mpaka ku denga kuti chikhale chipinda chopatulika chamʼkati mwa Nyumba ya Mulungu ngati Malo Wopatulika Kwambiri. 17Chipinda chachikulu chimene chinali kutsogolo kwa Malo Wopatulika Kwambiriwa, chinali mamita 18 mulitali mwake. 18Mʼkati mwa Nyumbayi munali matabwa a mkungudza, pamene anajambulapo zithunzi za zikho ndi maluwa. Paliponse panali mkungudza wokhawokha. Panalibe mwala uliwonse umene unkaonekera.

19Anakonza malo wopatulika mʼkati mwa Nyumbayi kuti ayikemo Bokosi la Chipangano cha Yehova. 20Malo wopatulika a mʼkatiwo anali a mamita asanu ndi anayi mulitali mwake, mulifupi mwake, ndi msinkhu wake. Anakuta mʼkati mwake ndi golide weniweni ndiponso anapanga guwa lansembe la matabwa a mkungudza. 21Solomoni anakutira golide weniweni mʼkati mwake mwa Nyumbayi, ndipo anayalika maunyolo a golide mopingasa kutsogolo kwa malo wopatulika amene anakutidwa ndi golide. 22Motero anakuta mʼkati monse ndi golide. Anakutanso ndi golide guwa lansembe la mʼkati mwa chipinda chopatulika.

23Mʼchipinda chopatulika cha mʼkati anapangamo akerubi awiri a mtengo wa olivi. Msinkhu wa kerubi aliyense unali mamita anayi ndi theka. 24Phiko limodzi la kerubi kutalika kwake kunali mamita awiri ndi theka, phiko linanso linali mamita awiri ndi theka, kutambasula mapiko awiriwo, kuchokera msonga ina mpaka msonga ina kutalika kwake kunali mamita anayi ndi theka. 25Kerubi wachiwiriyo msinkhu wake unalinso mamita anayi ndi theka, pakuti akerubi awiriwo anali a misinkhu yofanana ndi a mapangidwe ofanana. 26Msinkhu wa kerubi aliyense unali mamita anayi ndi theka. 27Solomoni anayika akerubiwo mʼchipinda cha mʼkati mwenimweni mwa Nyumba ya Mulungu, atatambasula mapiko awo. Phiko la kerubi wina limakhudza khoma lina, pamene phiko la winayo limakhudza khoma linanso ndipo mapiko awo amakhudzana pakati pa chipindacho. 28Akerubiwo anawakuta ndi golide.

29Pa makoma onse kuzungulira Nyumbayo, mʼzipinda za mʼkati ndi za kunja zomwe, anajambulapo akerubi, mitengo ya mgwalangwa ndi maluwa. 30Anayala golide pansi mu Nyumbamo mʼzipinda zamʼkati ndi zakunja zomwe.

31Ndipo pa khomo lolowera ku malo wopatulika amʼkati anapanga zitseko za mtengo wa olivi ndipo khonde lake linali ndi mbali zisanu. 32Ndipo pa zitseko ziwiri zija za mtengo wa olivi anajambulapo kerubi, mitengo ya mgwalangwa ndi maluwa ndipo anapaka golide akerubiwo ndi mitengo ya mgwalangwayo. 33Anapanganso chimodzimodzi mphuthu za mbali zinayi za mtengo wa olivi za pa khomo la Nyumbayo. 34Solomoni anapanganso zitseko ziwiri za payini. Chitseko chilichonse chinali ndi mbali ziwiri zotha kuzipinda. 35Pa zitsekozo anagobapo akerubi, mitengo ya mgwalangwa ndi maluwa wotambasuka ndipo zojambulazo anazikuta ndi golide wopyapyala.

36Ndipo anamanga bwalo la mʼkati lokhala ndi khoma lokhala ndi mizere itatu ya miyala yosema ndiponso mzere umodzi wa matabwa osemedwa a mkungudza.

37Maziko a Nyumba ya Yehova anamangidwa pa chaka chachinayi, mwezi wa Zivi. 38Pa chaka cha 11 mwezi wa Buli, mwezi wachisanu ndi chitatu, madera onse a Nyumba anatha kumangidwa monga momwe kunkafunikira. Anamanga Nyumbayo kwa zaka zisanu ndi ziwiri.

New Russian Translation

3 Царств 6:1-38

Соломон строит храм

(2 Пар. 3:1-4)

1В четыреста восьмидесятом году после выхода израильтян из Египта, в четвертый год своего правления Израилем, в месяце зив, во втором месяце6:1 В середине весны 966 г. до н. э., Соломон начал строить дом Господу.

2Дом, который Соломон построил Господу, был шестьдесят локтей в длину, двадцать в ширину и тридцать в высоту6:2 Около 30 м в длину, 10 м в ширину и 15 м в высоту.. 3Притвор перед главным помещением дома был двадцать локтей6:3 Около 10 м. в ширину, соответственно ширине дома, и отходил от дома на десять локтей6:3 Около 5 м.. 4В доме он сделал окна, расширяющиеся внутрь. 5Он сделал пристройку вокруг стен дома и внутреннего святилища. В пристройке он сделал комнаты. 6Первый этаж был пять локтей6:6 Около 2,5 м; также в стихах 10 и 24. в ширину, второй – шесть локтей6:6 Около 3 м., и третий – семь локтей6:6 Около 3,5 м.. Вокруг дома снаружи он сделал на стене выступы, чтобы поддерживающие брусья не входили в стены дома.

7В строительстве дома использовали только те камни, что были обтесаны в каменоломне, и ни молотка, ни тесла, ни какого другого железного орудия не было слышно на месте строительства дома.

8Вход на первый этаж находился на южной стороне дома. Лестница вела на второй этаж, а оттуда – на третий. 9Так он построил дом и завершил его, покрыв его брусьями и кедровыми досками. 10Вдоль всего дома он построил боковые комнаты. Высотой каждая из них была в пять локтей; они присоединялись к дому кедровыми брусьями.

11И вот, к Соломону было слово Господа:

12– Что до этого дома, который ты строишь, то если ты будешь следовать Моим установлениям, соблюдать Мои правила и хранить все Мои повеления и выполнять их, Я исполню через тебя обещание, которое Я дал твоему отцу Давиду. 13Я буду жить среди израильтян и не покину Мой народ, Израиль.

14Соломон построил дом и завершил его.

Внутренняя отделка дома Господня

(2 Пар. 3:5-14)

15Соломон обшил стены с внутренней стороны кедровыми досками, забрав их от пола дома до стропил6:15 Так в одном из древних переводов; в нормативном еврейском тексте: «стен» потолка, и покрыл пол дома кипарисовыми досками. 16В глубине дома он отгородил кедровыми досками от пола до стропил двадцать локтей6:16 Около 10 м., чтобы сделать в доме внутреннее святилище, Святое Святых. 17Комната перед Святым Святых была длиной в сорок локтей6:17 Около 20 м.. 18Внутри дом был обшит кедровым деревом, на котором были вырезаны подобия тыкв и распустившиеся цветы. Все было сделано из кедра; камня нигде не было видно.

19Он приготовил внутреннее святилище в доме, чтобы поместить там ковчег Господнего завета. 20Внутреннее святилище было двадцать локтей в длину, двадцать в ширину и двадцать в высоту6:20 Около 10 м в длину, ширину и высоту.. Он покрыл внутренние поверхности чистым золотом и обшил жертвенник, находящийся перед Святым Святых, кедром. 21Соломон покрыл внутренние поверхности дома чистым золотом и перетянул золотыми цепями вход во внутреннее святилище, которое было покрыто золотом. 22Также покрыл золотом всю внутреннюю часть дома, всю до конца. Еще он покрыл золотом жертвенник, который принадлежал к внутреннему святилищу.

23Во внутреннем святилище он сделал двух херувимов из оливкового дерева, каждого в десять локтей6:23 Около 5 м. высотой. 24Крыло первого херувима было пять локтей в длину, и другое крыло пять локтей в длину – десять локтей от конца одного крыла до конца другого. 25Второй херувим также был десяти локтей, так как оба херувима были одного размера и вида. 26Высота каждого херувима была десять локтей. 27Он поставил херувимов с распростертыми крыльями во внутреннюю часть дома. Крыло одного херувима касалось одной стены, крыло второго – противоположной стены, а другие крылья херувимов соприкасались друг с другом посередине комнаты. 28Соломон покрыл херувимов золотом.

29На стенах вокруг всего дома, и внутри, и снаружи, он вырезал херувимов, пальмы и распустившиеся цветы. 30Еще он покрыл пол, и внутри, и снаружи дома, золотом.

31Для входа во внутреннее святилище он сделал двери из оливкового дерева с пятиугольными косяками. 32А на двух дверях из оливкового дерева он вырезал херувимов, пальмы и распустившиеся цветы и покрыл херувимов и пальмы золотом. 33Точно так же он сделал из оливкового дерева четырехугольные косяки для входа в главное помещение. 34Еще он сделал две двери из кипарисового дерева, каждую с двумя подвижными створками. 35Он вырезал на них херувимов, пальмы и распустившиеся цветы и покрыл их золотом, ровно наложенным на резьбу.

36Он построил внутренний двор из трех рядов обтесанного камня и ряда кедровых балок.

37Основание дома Господа было заложено на четвертом году, в месяце зив. 38На одиннадцатом году правления Соломона, в месяце буле, – а это восьмой месяц, – дом был завершен в соответствии со всеми замыслами о нем. Соломон строил его семь лет.