1 Mafumu 4 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 4:1-34

Nduna za Solomoni ndi Abwanamkubwa

1Ndipo Mfumu Solomoni inakhala mfumu ya Aisraeli onse. 2Nduna zake zikuluzikulu zinali izi:

Azariya mwana wa Zadoki anali wansembe;

3Elihorefe ndi Ahiya, ana a Sisa, anali alembi;

Yehosafati mwana wa Ahiludi, anali mlembi wa zochitika;

4Benaya mwana wa Yehoyada, anali mtsogoleri wa ankhondo;

Zadoki ndi Abiatara, anali ansembe;

5Azariya mwana wa Natani, anali woyangʼanira nduna za mʼzigawo;

Zabudi mwana wa Natani, anali wansembe ndi bwenzi la mfumu;

6Ahisara, anali mkulu woyangʼanira nyumba ya mfumu;

Adoniramu mwana wa Abida, anali mkulu woyangʼanira ntchito za thangata.

7Solomoni analinso ndi abwanamkubwa khumi ndi awiri amene ankayangʼanira zigawo zonse za dziko la Israeli. Iwo ankapereka chakudya kwa mfumu ndiponso ku banja laufumu. Bwanamkubwa aliyense ankapereka chakudya mwezi umodzi pa chaka. 8Mayina awo ndi awa:

Beni-Huri, wa ku dziko la mapiri la Efereimu;

9Beni-Dekeri, woyangʼanira mizinda ya Makazi, Saalibimu, Beti-Semesi ndi Eloni Beti-Hanani;

10Beni-Hesedi, woyangʼanira mizinda ya Aruboti (Soko ndi dziko lonse la Heferi);

11Beni-Abinadabu, woyangʼanira Nafoti Dori (iye anakwatira Tafati mwana wa Solomoni);

12Baana mwana wa Ahiludi, anali woyangʼanira Taanaki ndi Megido, ndi ku Beti Sani konse, kufupi ndi ku Zaretani kumunsi kwa Yezireeli, kuyambira ku Beti-Seani mpaka ku Abeli-Mehola kukafika mpaka ku Yokineamu;

13Beni-Geberi, anali woyangʼanira Ramoti Giliyadi (midzi ya Yairi inali ya mwana wa Manase ku Giliyadi, pamodzinso ndi chigawo cha Arigobu ku Basani ndiponso mizinda yake yayikulu makumi asanu ndi umodzi yokhala ndi malinga ndi mipiringidzo yamkuwa).

14Ahinadabu mwana wa Ido, anali woyangʼanira Mahanaimu;

15Ahimaazi anali woyangʼanira Nafutali (iyeyu anakwatira Basemati mwana wa Solomoni);

16Baana mwana wa Husai, anali woyangʼanira Aseri ndi Bealoti;

17Yehosafati mwana wa Paruwa, anali woyangʼanira Isakara;

18Simei mwana wa Ela, anali woyangʼanira Benjamini;

19Geberi mwana wa Uri, anali woyangʼanira Giliyadi (dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi mfumu ya Basani). Iye ankayangʼanira chigawo chonsechi yekha.

Chakudya cha Tsiku ndi Tsiku cha Solomoni

20Anthu a ku Yuda ndi ku Israeli anali ochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Ankadya ndi kumwa ndipo ankasangalala. 21Ndipo Solomoni analamulira mayiko onse kuyambira ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku dziko la Afilisti, kukafika mpaka ku malire a dziko la Igupto. Mayikowa ankabweretsa mphatso ndipo anali pansi pa ulamuliro wa Solomoni moyo wake wonse.

22Chakudya cha tsiku ndi tsiku cha Solomoni chinali madengu 150 a ufa wosalala ndi madengu 300 a mgayiwa, 23ngʼombe khumi zonenepa zodyetsera mʼkhola, ngʼombe za ku busa makumi awiri, ndiponso nkhosa ndi mbuzi 100, pamodzinso ndi mbawala, agwape, mphoyo ndi mbalame zoweta zonona. 24Pakuti ankalamulira dziko lonse la kumadzulo kwa mtsinje wa Yufurate kuyambira ku Tifisa mpaka ku Gaza, mafumu onse a kumadzulo kwa Mtsinje, ndipo anali pa mtendere ndi mayiko onse ozungulira. 25Pa nthawi ya Solomoni, Yuda ndi Israeli anali pa mtendere, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba. Munthu aliyense ankangodzikhalira pansi pa mpesa wake ndi mtengo wake wa mkuyu.

26Solomoni anali ndi zipinda 4,000 zodyeramo akavalo okoka magaleta ake ndi anthu 12,000 oyendetsa magaleta.

27Abwanamkubwa a zigawo aja, aliyense pa mwezi wake, ankapereka chakudya cha Mfumu Solomoni ndi cha anthu onse amene ankadya naye. Iwo ankaonetsetsa kuti pasasowe kalikonse. 28Ankabweretsanso ku malo ake ofunikira muyeso wawo wa barele ndi udzu wa akavalo okoka magaleta ndiponso akavalo ena.

Nzeru za Solomoni

29Mulungu anamupatsa Solomoni nzeru ndi luntha losaneneka ndipo nzeru zake zinali zochuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. 30Nzeru za Solomoni zinali zoposa nzeru za anthu onse a Kummawa ndiponso nzeru zonse za ku Igupto. 31Iye anali wanzeru kuposa munthu wina aliyense, kuposa ngakhale Etani wa banja la Ezara, Hemani, Kalikoli ndi Darida, ana a Maholi. Ndipo mbiri yake inamveka kwa mitundu yonse ya anthu ozungulira. 32Solomoni anapeka miyambi 3,000 ndi kulemba nyimbo 1,005. 33Iye ankaphunzitsa za mitengo, kuyambira mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni mpaka kachitsamba ka hisope khomera pa khoma. Iye ankaphunzitsanso za nyama ndi mbalame, zinthu zokwawa pansi ndiponso za nsomba. 34Anthu a mitundu yonse ankabwera kudzamva nzeru za Solomoni. Anthu amenewa ankatumizidwa ndi mafumu onse a dziko lapansi amene anamvapo za nzeru zakezo.

King James Version

1 Kings 4:1-34

1So king Solomon was king over all Israel. 2And these were the princes which he had; Azariah the son of Zadok the priest,4.2 priest: or, chief officer 3Elihoreph and Ahiah, the sons of Shisha, scribes; Jehoshaphat the son of Ahilud, the recorder.4.3 scribes: or, secretaries4.3 recorder: or, remembrancer 4And Benaiah the son of Jehoiada was over the host: and Zadok and Abiathar were the priests: 5And Azariah the son of Nathan was over the officers: and Zabud the son of Nathan was principal officer, and the king’s friend: 6And Ahishar was over the household: and Adoniram the son of Abda was over the tribute.4.6 tribute: or, levy

7¶ And Solomon had twelve officers over all Israel, which provided victuals for the king and his household: each man his month in a year made provision. 8And these are their names: The son of Hur, in mount Ephraim:4.8 The son…: or, Ben-hur 9The son of Dekar, in Makaz, and in Shaalbim, and Beth-shemesh, and Elon-beth-hanan:4.9 The son…: or, Ben-dekar 10The son of Hesed, in Aruboth; to him pertained Sochoh, and all the land of Hepher:4.10 The son…: or, Ben-hesed 11The son of Abinadab, in all the region of Dor; which had Taphath the daughter of Solomon to wife:4.11 The son…: or, Ben-abinadab 12Baana the son of Ahilud; to him pertained Taanach and Megiddo, and all Beth-shean, which is by Zartanah beneath Jezreel, from Beth-shean to Abel-meholah, even unto the place that is beyond Jokneam: 13The son of Geber, in Ramoth-gilead; to him pertained the towns of Jair the son of Manasseh, which are in Gilead; to him also pertained the region of Argob, which is in Bashan, threescore great cities with walls and brasen bars:4.13 The son…: or, Ben-geber 14Ahinadab the son of Iddo had Mahanaim:4.14 Mahanaim: or, to Mahanaim 15Ahimaaz was in Naphtali; he also took Basmath the daughter of Solomon to wife: 16Baanah the son of Hushai was in Asher and in Aloth: 17Jehoshaphat the son of Paruah, in Issachar: 18Shimei the son of Elah, in Benjamin: 19Geber the son of Uri was in the country of Gilead, in the country of Sihon king of the Amorites, and of Og king of Bashan; and he was the only officer which was in the land.

20¶ Judah and Israel were many, as the sand which is by the sea in multitude, eating and drinking, and making merry. 21And Solomon reigned over all kingdoms from the river unto the land of the Philistines, and unto the border of Egypt: they brought presents, and served Solomon all the days of his life.

22¶ And Solomon’s provision for one day was thirty measures of fine flour, and threescore measures of meal,4.22 provision: Heb. bread4.22 measures: Heb. cors 23Ten fat oxen, and twenty oxen out of the pastures, and an hundred sheep, beside harts, and roebucks, and fallowdeer, and fatted fowl. 24For he had dominion over all the region on this side the river, from Tiphsah even to Azzah, over all the kings on this side the river: and he had peace on all sides round about him. 25And Judah and Israel dwelt safely, every man under his vine and under his fig tree, from Dan even to Beer-sheba, all the days of Solomon.4.25 safely: Heb. confidently

26¶ And Solomon had forty thousand stalls of horses for his chariots, and twelve thousand horsemen. 27And those officers provided victual for king Solomon, and for all that came unto king Solomon’s table, every man in his month: they lacked nothing. 28Barley also and straw for the horses and dromedaries brought they unto the place where the officers were, every man according to his charge.4.28 dromedaries: or, mules, or, swift beasts

29¶ And God gave Solomon wisdom and understanding exceeding much, and largeness of heart, even as the sand that is on the sea shore. 30And Solomon’s wisdom excelled the wisdom of all the children of the east country, and all the wisdom of Egypt. 31For he was wiser than all men; than Ethan the Ezrahite, and Heman, and Chalcol, and Darda, the sons of Mahol: and his fame was in all nations round about. 32And he spake three thousand proverbs: and his songs were a thousand and five. 33And he spake of trees, from the cedar tree that is in Lebanon even unto the hyssop that springeth out of the wall: he spake also of beasts, and of fowl, and of creeping things, and of fishes. 34And there came of all people to hear the wisdom of Solomon, from all kings of the earth, which had heard of his wisdom.