1 Mafumu 22 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 22:1-53

Mikaya Anenera Motsutsa Ahabu

1Kwa zaka zitatu panalibe nkhondo pakati pa Aramu ndi Israeli. 2Koma pa chaka chachitatu, Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita kukacheza ndi mfumu ya ku Israeli. 3Mfumu ya ku Israeli nʼkuti itawuza atumiki ake kuti, “Kodi inu simukudziwa kuti Ramoti Giliyadi ndi dera lathu ndipo ife palibe chimene tikuchita kuti tilitenge deralo mʼmanja mwa mfumu ya Aramu?”

4Tsono iye anafunsa Yehosafati kuti, “Kodi udzapita nane ku nkhondo ku Ramoti Giliyadi?”

Yehosafati anayankha mfumu ya ku Israeli kuti, “Ine ndili monga inu, anthu anga monga anthu anu, akavalo anga monga akavalo anu.” 5Koma Yehosafati anawuzanso mfumu ya ku Israeli kuti, “Poyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”

6Choncho mfumu ya Israeli inasonkhanitsa pamodzi aneneri okwanira 400, ndipo inawafunsa kuti, “Kodi ndipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena ndileke?”

Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Ambuye waupereka mzindawo mʼmanja mwa mfumu.”

7Koma Yehosafati anafunsa kuti, “Kodi kuno kulibenso mneneri wina wa Yehova kumene ife tingakafunsireko nzeru?”

8Mfumu ya ku Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife tingakafunsire kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa iyeyo samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa nthawi zonse. Dzina lake ndi Mikaya mwana wa Imula.”

Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu musatero.”

9Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa atumiki ake ndipo inati, “Kayitane Mikaya mwana wa Imula msangamsanga.”

10Atavala mikanjo yawo yaufumu, mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopondera tirigu pafupi ndi chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo. 11Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana nʼkuti atapanga nyanga zachitsulo ndipo iye ananenera kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi, inu mudzagunda nazo Aaramu mpaka iwo atawonongeka.’ ”

12Aneneri ena onse ananenera zomwezonso. Iwo anati, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”

13Wamthenga amene anapita kukayitana Mikaya anamuwuza kuti, “Taonani, aneneri onse monga munthu mmodzi akunenera za kupambana kwa mfumu. Mawu anunso akhale ogwirizana ndi mawu awo, ndipo mukayankhule zabwino.”

14Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndikawawuza zokhazo zimene Yehova akandiwuze.”

15Atafika, Ahabu anamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite kukathira nkhondo Ramoti Giliyadi, kapena tileke?”

Iye anayankha kuti, “Pitani ndipo mukapambana, pakuti Yehova adzawupereka mzindawo mʼdzanja la mfumu.”

16Ahabu anati kwa iye, “Kodi ndikulumbiritse kangati kuti undiwuze zoona zokhazokha mʼdzina la Yehova?”

17Pamenepo Mikaya anayankha kuti, “Ndinaona Aisraeli onse atamwazikana pa mapiri ngati nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mwamtendere.’ ”

18Mfumu ya ku Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti ameneyu samanenera kanthu kalikonse kabwino ka ine, koma zoyipa zokhazokha?”

19Mikaya anapitiriza kuyankhula nati, “Tsono imvani mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu, gulu lonse la kumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi ku dzanja lake lamanzere. 20Ndipo Yehova anati, ‘Kodi ndani amene akamukope Ahabu kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi, nʼkukafera komweko?’ ”

“Wina anapereka maganizo ena ndipo winanso maganizo ena. 21Potsirizira, mzimu wina unabwera ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, ‘Ine ndidzamukopa.’ ”

22Yehova anafunsa kuti, “Ukamukopa bwanji?”

Mzimuwo unati, “Ndidzapita ndi kukakhala mzimu wabodza pakamwa pa aneneri ake onse.”

Yehova anati, “ ‘Iwe udzamukopadi. Pita kachite zomwezo.’

23“Ndipo tsopano taonani, Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anu onsewa. Yehova waneneratu kuti mukaona mavuto.”

24Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi namenya Mikaya patsaya. Iye anafunsa Mikaya kuti, “Kodi mzimu wa Yehova unadzera njira iti pamene umatuluka mwa ine kuti uziyankhula ndi iwe?”

25Mikaya anayankha kuti, “Udzaona pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”

26Pamenepo mfumu ya ku Israeli inalamula kuti, “Mugwireni Mikaya ndipo mubwerere naye kwa Amoni mkulu wa mzinda, ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu 27ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyikeni mʼndende munthu uyu ndipo musamupatse chakudya china koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwerera mwamtendere.’ ”

28Mikaya ananena kuti, “Ngati mudzabwerera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo iye anapitiriza kunena kuti, “Gwiritsitsani mawu angawa, anthu inu nonse!”

Ahabu Aphedwa ku Ramoti Giliyadi

29Choncho mfumu ya ku Israeli ndi Yehosafati mfumu ya ku Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi. 30Mfumu ya ku Israeli inawuza Yehosafati kuti, “Ine ndidzalowa mu nkhondoyi modzibisa, koma inu muvale zovala zanu zaufumu.” Choncho mfumu ya ku Israeli inadzibisa ndi kupita ku nkhondo.

31Tsono mfumu ya ku Aramu nʼkuti italamulira anthu ake 32 olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu, koma mfumu ya ku Israeli.” 32Olamulira magaleta ataona Yehosafati, ankaganiza kuti, “Ndithu iyi ndiye mfumu ya ku Israeli.” Choncho anabwerera kukamenyana naye, koma Yehosafati atafuwula, 33olamulira akavalo anaona kuti sanali mfumu ya ku Israeli ndipo analeka kumuthamangitsa.

34Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndi kulasa mfumu ya ku Israeli polumikizira malaya ake odzitetezera. Mfumu inawuza woyendetsa galeta lake kuti, “Tembenuka ndipo undichotse pa nkhondo pano pakuti ndalasidwa.” 35Nkhondo inakula kwambiri tsiku limenelo, ndipo mfumu inakhala tsonga mʼgaleta lake moyangʼanana ndi Aaramu. Magazi ake ankayenderera pansi kuchokera mʼgaleta, ndipo pa nthawi ya madzulo inamwalira. 36Pamene dzuwa linkalowa, kunamveka mfuwu wa nkhondo kuti, “Munthu aliyense apite ku mzinda wa kwawo, aliyense apite ku dziko la kwawo!”

37Ndipo mfumu ija inafa, nabwera nayo ku Samariya, ndipo anayika mʼmanda kumeneko. 38Anatsuka galeta lija pa dziwe la ku Samariya (pamene ankasamba akazi achiwerewere) ndipo agalu ananyambita magazi a mfumuyo, monga momwe Yehova ananenera.

39Tsono ntchito zina za Ahabu, kuphatikiza zonse anazichita, nyumba yaufumu imene anamanga yokutidwa ndi minyanga ya njovu, mizinda yotetezedwa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli? 40Ahabu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Ahaziya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Yehosafati Mfumu ya ku Yuda

41Yehosafati, mwana wa Asa anakhala mfumu ya ku Yuda chaka chachinayi cha Ahabu mfumu ya ku Israeli. 42Yehosafati anali wa zaka 35 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira ku Yerusalemu zaka 25. Amayi ake anali Azuba mwana wa Silihi. 43Pa zinthu zonse, Yehosafati anayenda mʼnjira za Asa abambo ake ndipo sanachite zotsutsana ndi machitidwe a abambo ake. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova. Komabe, malo azipembedzo sanawawononge, ndipo anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko. 44Yehosafati anakhala mwamtendere ndi mfumu ya ku Israeli.

45Ntchito zake zina za Yehosafati, zinthu zimene anachita ndi zamphamvu zimene anaonetsa, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Yuda? 46Iye anachotsa mʼdzikomo amuna onse ochita zachiwerewere mwa chipembedzo amene anatsalira pa nthawi ya ulamuliro wa Asa, abambo ake. 47Nthawi imeneyo kunalibe mfumu ku Edomu, amene ankalamulira anali munthu woyikidwa ndi mfumu ya ku Yuda.

48Yehosafati anapanga sitima zapamadzi zopita ku Ofiri kukatenga golide, koma sitimazo sizinayende chifukwa zinawonongeka ku Ezioni Geberi. 49Nthawi imeneyo Ahaziya mwana wa Ahabu anawuza Yehosafati kuti, “Anthu anga ayende pa madzi pamodzi ndi anthu anu,” koma Yehosafati anakana.

50Ndipo Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Ahaziya Mfumu ya ku Israeli

51Ahaziya mwana wa Ahabu anakhala mfumu ya ku Israeli ku Samariya mʼchaka cha 17 cha Yehosafati mfumu ya ku Yuda, ndipo analamulira Israeli zaka ziwiri. 52Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, chifukwa anayenda mʼnjira za abambo ndi amayi ake komanso mʼnjira za Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa Israeli. 53Potumikira ndi kupembedza Baala, iye anakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli, monga momwe anachitira abambo ake.

Bibelen på hverdagsdansk

1. Kongebog 22:1-54

Profeten Mika advarer Ahab

1Fredsaftalen mellem Aram og Israel holdt i to år.

2Men i det tredje år—på et tidspunkt, hvor kong Joshafat af Juda var på besøg hos kong Ahab i Israel— 3lod Ahab i sine embedsmænds påhør en bemærkning falde om, at aramæerne stadig holdt byen Ramot-Gilead besat. „Ærligt talt,” tilføjede han, „det er for galt, at vi endnu ikke har gjort noget for at befri byen.” 4Derefter vendte han sig mod Joshafat og spurgte ham ligeud: „Vil du hjælpe mig med at befri Ramot-Gilead?” „Selvfølgelig!” svarede Joshafat. „Vi er jo forbundsfæller, du og jeg. Mine folk vil kæmpe sammen med dine, og mine heste står til din rådighed.” 5Men så tilføjede han: „Vi bør dog først spørge Herren til råds.”

6Derpå tilkaldte kong Ahab sine 400 profeter og spurgte dem: „Skal jeg gå til angreb på Ramot-Gilead eller ej?” „Du skal gå til angreb,” svarede de. „Herren vil give dig sejr!”

7Men kong Joshafat var ikke tilfreds. „Er der ikke en af Herrens profeter, vi kan spørge til råds?” spurgte han. 8„Jo, en enkelt,” svarede Ahab, „men jeg bryder mig ikke om ham, for han profeterer altid ulykke for mig, aldrig noget godt. Manden hedder Mika, søn af Jimla.” „Sådan bør du ikke tale!” indvendte Joshafat. 9Kong Ahab gav derefter ordre til, at Mika straks skulle hentes.

10I mellemtiden fortsatte Ahabs profeter med at profetere for de to konger, der sad klædt i deres kongekåber på hver sin trone på tærskepladsen nær ved byporten. 11En af profeterne ved navn Zidkija, søn af Kena’ana, lavede nogle horn af jern og erklærede: „Herren siger: Du skal stange den aramæiske hær sønder og sammen med disse horn og udrydde den totalt!”

12De andre profeter sagde det samme: „Gå kun til angreb på Ramot-Gilead, for Herren vil give dig sejr!”

13Kongens tjener, som var blevet sendt for at hente Mika, fortalte ham, hvad de andre profeter havde sagt, og opfordrede ham til at sige det samme. 14Men Mika svarede: „Så sandt Herren lever: Jeg kan ikke sige andet, end det Herren fortæller mig!”

15Da Mika ankom, spurgte kong Ahab: „Mika, skal vi angribe Ramot-Gilead eller ej?” „Ja, tag endelig af sted!” svarede Mika. „Lykken er med dig. Herren vil give dig sejr!” 16„Hør nu her,” sagde Ahab. „Hvor mange gange skal jeg få dig til at sværge på, at du kun siger sandheden, når du taler i Herrens navn?”

17Så sagde Mika: „Jeg så Israels folk spredt ud over bjergene som får, der ingen hyrde har. Og Herren sagde: Kongen er død! Send folket hjem!” 18Kongen vendte sig beklagende til Joshafat. „Sagde jeg det ikke nok! Aldrig profeterer han noget godt. Evigt og altid kun dårlige budskaber.”

19„Så hør dog Herrens ord!” afbrød Mika. „Jeg så Herren sidde på sin trone, og en hær af engle var samlet omkring ham. 20Så sagde Herren: ‚Hvem vil lokke Ahab i fælden, så han dør i Ramot-Gilead?’ Og efter at adskillige planer var blevet foreslået, 21trådte en af ånderne frem og sagde: ‚Det vil jeg gøre!’ 22‚Men hvordan?’ spurgte Herren.

Ånden svarede: ‚Jeg vil være en løgneånd i alle hans profeters mund!’ ‚Du kan klare opgaven,’ sagde Herren. ‚Gå bare i gang!’ ”

23Mika fortsatte: „Kong Ahab, kan du ikke gennemskue dine profeter? Herren har jo fyldt dem alle med en løgnens ånd, og i virkeligheden har han planer om at få ram på dig.”

24Ved de ord gik profeten Zidkija hen til Mika og gav ham en lussing. „Vil du måske påstå, at Herrens Ånd kun taler gennem dig og ikke gennem mig?” snerrede han. 25Mika svarede: „Svaret på det spørgsmål får du, den dag du rædselsslagen prøver at gemme dig i et baglokale i et hus.”

26Efter det ordskifte gav kong Ahab ordre til at arrestere Mika. „Før ham til Amon, byens borgmester, og til min søn Joash,” sagde han. 27„Giv dem besked om at kaste ham i fængsel og sætte ham på vand og brød, til jeg kommer uskadt tilbage fra slaget.” 28„Hvis du kommer tilbage, har Herren ikke talt gennem mig!” sagde Mika. „Har I hørt det alle sammen?”

Kong Ahabs død

29Derefter førte kong Ahab af Israel og kong Joshafat af Juda deres hære mod Ramot-Gilead, 30men Ahab sagde til Joshafat: „Før jeg kaster mig ud i kampen, vil jeg forklæde mig som en menig soldat. Men behold du bare din kongelige rustning på.” Så forklædte kong Ahab sig og slaget begyndte.

31Den aramæiske konge havde imidlertid givet sine 32 vognstyrere ordre til at være på udkig efter kong Ahab og koncentrere sig om at fælde ham. 32-33Da de fik øje på kong Joshafat, tænkte de: „Dér er han!” og vendte om for at få fat i ham. Men da Joshafat råbte22,32-33 Teksten her siger blot, at han råbte, men 2.Krøn. 18,31 antyder, at han råbte til Herren om hjælp. om hjælp, forstod de, at han ikke var Israels konge, og trak sig tilbage. 34Men en af bueskytterne skød en tilfældig pil af sted, og pilen borede sig ind mellem remmene i kong Ahabs brynje.

„Lad os komme væk fra fronten!” stønnede Ahab til sin vognstyrer. „Jeg er alvorligt såret.”

35Kampen trak i langdrag, og blev mere og mere intens. Kong Ahab holdt øje med kampen på afstand, men kunne dårligt holde sig oprejst i vognen. Blodet flød fra hans sår og ned i vognens bund, og hen under aften døde han. 36-37Ved solnedgang gik det som en løbeild gennem kolonnerne: „Det er forbi—kongen er død! Lad os vende hjem!”

Ahabs lig blev ført til Samaria, hvor begravelsen foregik. 38Da man vaskede hans vogn ren ved Samarias dam, løb blodet ud i vandet, som hundene drak af, og de prostituerede vaskede sig med. Således gik det ord i opfyldelse, som Herren havde talt.

39Alt, hvad Ahab ellers foretog sig, for eksempel at han byggede sig et palads udsmykket med elfenben og befæstede en række byer, er nedskrevet i Israels kongers krønikebog. 40Da Ahab var død, blev hans søn Ahazja konge i Israel.

Kong Joshafat af Juda

41Joshafat, søn af Asa, blev konge over Judas land i kong Ahabs fjerde regeringsår. 42Han var 35 år, da han kom til magten, og han regerede i Jerusalem i 25 år. Hans mor hed Azuba og var datter af Shilhi. 43Han fulgte sin fars eksempel og adlød Herren i alle forhold, 44men det lykkedes ham ikke at udrydde offerstederne på højene rundt omkring i landet, og derfor blev folket ved med at bringe deres ofre på disse altre i stedet for i Jerusalem. 45Han indgik forbund med kong Ahab af Israel, så der var fred mellem de to lande. 46Hvad der ellers er at fortælle om kong Joshafat, hans heltebedrifter og krige, er nedskrevet i Judas kongers krønikebog.

47Selv om hans far, Asa, havde landsforvist de mandlige og kvindelige prostituerede, som holdt til ved offerhøjene, var der stadig enkelte tilbage. Dem fik Joshafat fjernet. 48På den tid var der ingen konge i Edom, så han tog også magten der.

49Joshafat byggede nogle store Tarshish-skibe,22,49 Se noten til 10,22. der skulle fragte guld fra Ofir, men de forliste straks efter afrejsen fra Etzjon-Geber. 50Ahazja, kong Ahabs søn og efterfølger, tilbød at lade sine sømænd overtage ledelsen, men det afslog Joshafat.

51Da kong Joshafat døde, blev han begravet i familiegravstedet i Davidsbyen, og hans søn Joram efterfulgte ham som konge.

Kong Ahazja af Israel

52Ahazja, Ahabs søn, blev konge i Israel i kong Joshafat af Judas 17. regeringsår, og han regerede i to år med residens i Samaria. 53Ahazja gjorde, hvad der var ondt i Herrens øjne, for han fulgte sin fars og mors eksempel. De fulgte alle i Jeroboams fodspor, den mand, som lokkede Israels folk til synd ved at indføre afgudsdyrkelsen. 54Ahazja tilbad også Ba’al, som hans far havde gjort, og det vakte Herrens, Israels Guds, vrede.