1 Mafumu 21 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 21:1-29

Munda Wamphesa wa Naboti

1Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya. 2Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”

3Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”

4Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.

5Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”

6Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’ ”

7Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”

8Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake. 9Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti:

“Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu. 10Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”

11Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera. 12Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu. 13Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha. 14Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”

15Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.” 16Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.

17Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti, 18“Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake. 19Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’ ”

20Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!”

Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova. 21Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu. 22Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’

23“Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’

24“Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”

25(Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli. 26Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).

27Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.

28Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti, 29“Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”

Священное Писание

3 Царств 21:1-29

Виноградник Навота

1Через некоторое время произошли следующие события. У Навота из Изрееля был виноградник в Изрееле, рядом с дворцом Ахава, царя Самарии. 2Ахав сказал Навоту:

– Отдай мне твой виноградник под огород, ведь он расположен вблизи моего дворца. В обмен я дам тебе виноградник ещё лучше или, если хочешь, заплачу тебе его цену.

3Но Навот ответил:

– Не приведи Вечный, чтобы я отдал наследие моих отцов.

4Ахав пошёл домой мрачный и разгневанный, потому что Навот из Изрееля сказал: «Я не отдам тебе наследия моих отцов». Он отказался есть, лёг в постель и отвернулся.

5Его жена Иезевель вошла к нему и спросила:

– Почему ты такой мрачный? Почему ты не ешь?

6Он ответил ей:

– Потому что я сказал Навоту из Изрееля: «Продай мне виноградник или, если хочешь, я дам тебе вместо него другой». А он сказал: «Я не отдам тебе виноградник».

7Его жена Иезевель сказала:

– Разве ты поступаешь как царь Исраила? Встань и поешь! Ободрись, я добуду тебе виноградник Навота из Изрееля.

8Она написала письма от лица Ахава, скрепила их его печатью и разослала старейшинам и знатным людям, жившим в городе Навота. 9В этих письмах она написала:

«Объявите день поста и усадите Навота на почётное место среди народа. 10Но напротив него посадите двух негодяев, и пусть они произнесут свидетельство, что он оскорбил и Всевышнего, и царя21:10 См. Лев. 24:16; Втор. 17:6-7.. После этого выведите его и забейте камнями до смерти».

11Старейшины со знатными людьми, которые жили в городе Навота, сделали так, как приказала им в письмах Иезевель. 12Они объявили пост и усадили Навота на почётное место среди народа. 13Затем пришли два негодяя, сели напротив него и обвинили Навота перед народом:

– Навот оскорблял и Всевышнего, и царя.

После этого его вывели за город и забили камнями. 14Потом они послали известить Иезевель:

– Навота забили камнями, и он умер.

15Как только Иезевель услышала о том, что Навота забили камнями, она сказала Ахаву:

– Вставай и бери себе виноградник Навота из Изрееля, который он отказался продать тебе. Его больше нет в живых, он мёртв.

16Когда Ахав услышал, что Навот мёртв, он встал и пошёл, чтобы взять себе виноградник Навота.

Пророчество Ильяса против Ахава и Иезевели

17И к Ильясу из Тишбы было слово Вечного:

18– Иди навстречу Ахаву, царю Исраила, который правит в Самарии. Он сейчас в винограднике Навота, куда он пришёл, чтобы завладеть им. 19Скажи ему: Так говорит Вечный: «Ты убил человека, а теперь ещё захватываешь его имущество?» Потом скажи ему: Так говорит Вечный: «Там, где псы лизали кровь Навота, псы будут лизать и твою кровь!»21:19 Об исполнении этого пророчества см. 22:29-38; 4 Цар. 9:24-26.

20И Ильяс пошёл к Ахаву. Ахав сказал Ильясу:

– Итак, ты нашёл меня, мой враг!

– Нашёл, – ответил он, – потому что ты решил творить зло в глазах Вечного. 21Поэтому так говорит Вечный: «Я наведу на тебя беду. Я истреблю твоих потомков и искореню у тебя всякого человека мужского пола – и раба, и свободного. 22Я уподоблю твой дом дому Иеровоама, сына Невата, и дому Бааши, сына Ахии, потому что ты вызвал Мой гнев и склонил Исраил к греху»21:22 См. 14:10-11; 16:3-4.. 23Также и о Иезевели Вечный говорит: «Псы сожрут Иезевель у стены Изрееля». 24Тех из людей Ахава, кто умрёт в городе, сожрут псы, а тех, кто умрёт в поле, склюют птицы21:23-24 Об исполнении этих пророчеств см. 4 Цар. 9:24-26, 30-37; 10:1-11, 17..

25(Не было ещё подобного Ахаву, который решил делать зло в глазах Вечного, подстрекаемый своей женой Иезевелью. 26Он поступал крайне омерзительно, поклоняясь идолам, подобно аморреям, которых Вечный прогнал от исраильтян.)

27Когда Ахав услышал эти слова, он разорвал на себе одежду, оделся в рубище и постился. Он спал на мешковине и ходил мрачный.

28И к Ильясу из Тишбы было слово Вечного:

29– Ты видел, как Ахав смирился передо Мной? Из-за того, что он смирился передо Мной, Я не наведу беду при его жизни, но наведу её на его дом при жизни его сына.