1 Mafumu 2 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 2:1-46

Davide Alangiza Solomoni

1Davide ali pafupi kumwalira, analangiza mwana wake Solomoni kuti:

2“Ndatsala pangʼono kupita kumene munthu wina aliyense amayenera kupitako. Tsono khala wamphamvu, uvale zilimbe, 3ndipo uzichita zimene Yehova Mulungu wako amafuna, uziyenda mʼnjira zake, uzisunga malangizo ndi malamulo ake monga momwe zinalembedwera mʼMalamulo a Mose, kuti zonse zimene udzachite zidzakuyendere bwino kulikonse kumene udzapite. 4Ndipo Yehova akwaniritse zimene anandilonjeza kuti, ‘Ngati zidzukulu zako zidzakhala mosamala, niziyenda mokhulupirika pamaso panga ndi mtima wawo wonse ndi moyo wawo wonse, sudzasowa munthu wokhala pa mpando waufumu wa Israeli.’

5“Tsono iwe ukudziwanso zoyipa zimene Yowabu mwana wa Zeruya anandichitira pakupha atsogoleri awiri a ankhondo a Israeli, Abineri mwana wa Neri ndi Amasa mwana wa Yeteri. Iye anawapha ndi kukhetsa magazi nthawi ya mtendere ngati nthawi ya nkhondo, ndipo anapaka magazi amenewo pa lamba wa mʼchiwuno mwake ndi pa nsapato za ku mapazi ake. 6Iwe uchite kwa iye molingana ndi nzeru zako, koma usalole kuti afe ndi ukalamba ndi kupita ku manda mwamtendere.

7“Koma ana a Barizilai wa ku Giliyadi uwakomere mtima ndipo uwalole kuti akhale mʼgulu la anthu amene azidya pamodzi nawe. Pakuti anandisamalira pamene ndinkathawa mʼbale wako Abisalomu.

8“Ndipo kumbukira kuti uli ndi Simei mwana wa Gera, wa fuko la Benjamini wochokera ku Bahurimu, amene ananditemberera koopsa tsiku limene ndimapita ku Mahanaimu. Atabwera kudzakumana nane ku Yorodani, ine ndinalumbira mʼdzina la Yehova kuti, ‘Sindidzakupha iwe ndi lupanga.’ 9Koma tsopano usamuyese ngati munthu wosalakwa. Iwe ndiwe munthu wanzeru. Udzadziwa choti uchite naye. Ngakhale ndi wokalamba, aphedwe ndithu.”

10Tsono Davide anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide. 11Iyeyo nʼkuti atalamulira Israeli kwa zaka makumi anayi. Ku Hebroni analamulira zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ku Yerusalemu analamulira zaka 33. 12Choncho Solomoni anakhala pa mpando waufumu wa abambo ake Davide, ndipo ufumu wake unakhazikika kwambiri.

Kukhazikika kwa Ufumu wa Solomoni

13Tsono Adoniya, mwana wa Hagiti, anapita kwa Batiseba, amayi ake a Solomoni. Batiseba anamufunsa kuti, “Kodi wabwera mwamtendere?”

Iye anayakha kuti, “Eya, ndi zamtendere.” 14Ndipo iye anawonjezera kunena kuti, “Ndili ndi mawu oti ndiyankhule nanu.”

Batiseba anayankha kuti, “Yankhula.”

15Tsono Adoniya anati, “Monga inu mukudziwa, ufumu unali wanga. Aisraeli onse ankayembekezera kuti ine ndidzakhala mfumu yawo. Koma zinthu zinasintha ndipo ufumu wapita kwa mʼbale wanga; pakuti wapatsa iye ufumuwu ndi Yehova. 16Tsono ndili ndi pempho limodzi kwa inu. Musandikanize ayi.”

Batiseba anati, “Nena.”

17Adoniya anapitiriza kunena kuti, “Chonde, inu mupemphe mfumu Solomoni kuti andipatse Abisagi wa ku Sunemu kuti akhale mkazi wanga pakuti mukapempha inu sadzakukanizani.”

18Batiseba anayankha kuti, “Chabwino. Ndidzakuyankhulira kwa mfumu.”

19Batiseba atapita kwa Mfumu Solomoni kukayankhula naye mʼmalo mwa Adoniya, mfumu inanyamuka kukumana naye, ndipo inaweramira amayi akewo, kenaka inakhala pa mpando wake waufumu. Iye anayitanitsa mpando wina kuti amayi ake akhalepo ndipo anakhala pansi ku dzanja lake lamanja.

20Amayi akewo anati, “Ndikufuna ndikupempheni kanthu kakangʼono. Chonde musandikanize.”

Mfumu inayankha kuti, “Pemphani amayi, ine sindikukanizani.”

21Ndipo amayiwo anati, “Mulole kuti Abisagi wa ku Sunemu akhale mkazi wa mʼbale wanu Adoniya.”

22Koma Mfumu Solomoni inayankha amayi ake aja kuti, “Chifukwa chiyani mukupemphera Adoniya Abisagi wa ku Sunemu? Mungathenso kumupemphera ufumu pakuti iyeyu ndi mkulu wanga ndipo mupemphereninso wansembe Abiatara ndi Yowabu mwana wa Zeruya!”

23Pamenepo Mfumu Solomoni inalumbira mʼdzina la Yehova kuti, “Mulungu andilange ine koopsa ngati Adoniya saphedwa chifukwa cha pempho lakeli! 24Tsono pali Yehova wamoyo, amene anandikhazikitsa ine pa mpando waufumu wa abambo anga Davide ndi kundipatsa ufumu monga analonjezera, Adoniya aphedwa lero lomwe lino!” 25Choncho Mfumu Solomoni inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo anakantha Adoniyayo, nafa.

26Ndipo mfumu inati kwa Abiatara wansembe, “Pita ku Anatoti ku minda yako chifukwa ndiwe woyenera kufa, koma sindikupha tsopano, chifukwa unkanyamula Bokosi la Chipangano la Ambuye Yehova pamaso pa abambo anga Davide ndipo unazunzika limodzi ndi abambo angawo.” 27Kotero Solomoni anachotsa Abiatara pa udindo wokhala wansembe wa Yehova, kukwaniritsa mawu a Yehova amene anayankhula za nyumba ya Eli ku Silo.

28Yowabu atamva zimenezi anathawira ku tenti ya Yehova ndipo anakagwira msonga za guwa lansembe, popeza Yowabu ndiye anathandiza Adoniya kuwukira koma sanathandize Abisalomu. 29Mfumu Solomoni inawuzidwa kuti Yowabu wathawira ku tenti ya Yehova ndipo ali pambali pa guwa lansembe. Tsono Solomoni analamula Benaya mwana wa Yehoyada kuti, “Pita, kamukanthe!”

30Choncho Benaya analowa mʼtenti ya Yehova ndipo anati kwa Yowabu, “Mfumu ikuti ‘Tuluka!’ ”

Koma iye anayankha kuti, “Ayi, ine ndifera muno.”

Benaya anakafotokozera mfumu kuti, “Umu ndi mmene Yowabu wandiyankhira.”

31Pamenepo mfumu inalamula Benaya kuti, “Kachite monga iye wanenera. Ukamukanthe ndi kumuyika mʼmanda. Ukatero udzandichotsera ine pamodzi ndi nyumba ya abambo anga mlandu wa anthu osalakwa amene Yowabu anawapha. 32Yehova adzamubwezera zomwe anachita pokhetsa magazi, chifukwa iye anakantha ndi lupanga anthu awiri abwino ndi olungama kuposa iye, nawapha, abambo anga Davide osadziwa. Anthu awiriwo ndi Abineri mwana wa Neri, wolamulira gulu lankhondo la Israeli ndi Amasa mwana wa Yeteri, wolamulira gulu lankhondo la Yuda. 33Magazi amene Yowabu anakhetsa akhale pamutu pake ndi pa zidzukulu zake kwamuyaya. Koma pa Davide ndi zidzukulu zake, nyumba yake ndi mpando wake waufumu pakhale mtendere wochokera kwa Yehova kwamuyaya.”

34Choncho Benaya mwana wa Yehoyada anapita kukakantha Yowabu nʼkumupha ndipo anayikidwa mʼmanda mʼnyumba yakeyake ya ku chipululu. 35Mfumu inayika Benaya mwana wa Yehoyada kuti akhale woyangʼanira gulu lankhondo mʼmalo mwa Yowabu ndipo inayika Zadoki kuti akhale wansembe mʼmalo mwa Abiatara.

36Kenaka mfumu inatuma anthu kukayitana Simei ndipo inamuwuza kuti, “Udzimangire nyumba mu Yerusalemu ndipo uzikhala kumeneko, koma usatuluke mu mzinda kupita kwina kulikonse. 37Tsiku lomwe udzatulukemo ndi kuwoloka Chigwa cha Kidroni, udziwiretu kuti udzafa ndipo magazi ako adzakhala pamutu pako.”

38Simei anayankha mfumu kuti, “Zimene mwanenazi nʼzabwino. Kapolo wanu adzachita monga mbuye wanga mfumu mwanenera.” Choncho Simei anakhala mu Yerusalemu nthawi yayitali.

39Koma patatha zaka zitatu, akapolo awiri a Simei anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka, mfumu ya ku Gati, ndipo Simei anawuzidwa kuti, “Akapolo anu ali ku Gati.” 40Atamva zimenezi, anakwera bulu wake ndipo anapita kwa Akisi ku Gati kukafunafuna akapolo ake. Choncho Simei anapita ndi kukatenga akapolo ake ku Gati ndipo anabwera nawo.

41Solomoni atawuzidwa kuti Simei anatuluka mu Yerusalemu ndi kupita ku Gati ndipo kuti wabwerako, 42mfumu inamuyitanitsa Simei ndipo inamufunsa kuti, “Kodi sindinakulumbiritse mʼdzina la Yehova ndi kukuchenjeza kuti, ‘Tsiku limene udzatuluka kupita kwina kulikonse, udziwe kuti udzafa’? Nthawi imeneyo iwe unandiwuza kuti, ‘Zimene mwanena nʼzabwino. Ine ndidzamvera.’ 43Chifukwa chiyani tsono sunasunge lumbiro lako kwa Yehova? Bwanji nanga sunamvere lamulo limene ndinakuwuza?”

44Mfumuyo inawuzanso Simei kuti, “Ukudziwa mu mtima mwakomo zoyipa zonse zimene unachitira abambo anga Davide. Tsopano Yehova akubwezera zoyipa zakozo. 45Koma Mfumu Solomoni idzadalitsidwa ndipo mpando waufumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova kwamuyaya.”

46Pamenepo mfumu inalamula Benaya mwana wa Yehoyada ndipo iye anapita kukakantha Simei ndi kumupha.

Tsono ufumu unakhazikika mʼdzanja la Solomoni.

Священное Писание

3 Царств 2:1-46

Последние наставления Давуда Сулейману

1Когда приблизился смертный час Давуда, он дал своему сыну Сулейману наставление.

2– Я ухожу путём всей земли, – сказал он. – Будь твёрд, мужествен 3и исполняй то, чего требует Вечный, твой Бог. Ходи Его путями и исполняй Его установления и повеления, Его законы и заповеди, как написано в Законе Мусы, чтобы тебе преуспеть во всём, что бы ты ни делал и куда бы ни шёл, 4и чтобы Вечный исполнил Своё слово, которое Он сказал обо мне: «Если твои потомки будут внимательны к путям своим и будут ходить передо Мной в истине от всего сердца и от всей души, то ты никогда не лишишься преемника на престоле Исраила».

5Далее, ты сам знаешь о том, что сделал мне Иоав, сын Церуи, что сделал он с двумя военачальниками Исраила – Авнером, сыном Нера, и Амасой, сыном Иетера. Он убил их, мстя во время мира за кровь, что была пролита на войне, и запятнал кровью войны пояс на бёдрах и сандалии на ногах2:5 См. 2 Цар. 3:17-30; 20:4-13.. 6Действуй по своей мудрости, но не дай его седой голове сойти в могилу2:6 Букв.: «в Шеол». Шеол – место, где пребывают души умерших. То же в ст. 9. с миром.

7А сыновьям Барзиллая из Галаада яви милость, и пусть они будут в числе тех, кто ест за твоим столом. Они пришли ко мне, когда я бежал от твоего брата Авессалома2:7 См. 2 Цар. 17:27-29; 19:31-39..

8Ещё у тебя есть Шимей, сын Геры, вениамитянин из Бахурима. Он осыпал меня страшными проклятиями в день, когда я шёл в Маханаим. Когда он вышел встречать меня к Иордану, я поклялся ему Вечным: «Я не предам тебя мечу». 9Но теперь не считай его невиновным. Ты мудрый человек, ты поймёшь, что с ним сделать. Сведи его седую голову в могилу в крови2:8-9 См. 2 Цар. 16:5-13; 19:15-23..

Смерть Давуда

(1 Лет. 29:26-28)

10И Давуд упокоился со своими предками и был похоронен в Городе Давуда. 11Он правил Исраилом сорок лет – семь лет в Хевроне и тридцать три года в Иерусалиме. 12А на престол своего отца Давуда сел Сулейман, и царство его упрочилось.

Казнь Адонии

13Адония, сын Хаггиты, пришёл к матери Сулеймана Вирсавии. Вирсавия спросила его:

– С миром ли ты пришёл?

– С миром, – ответил он.

14Затем он спросил:

– Могу ли я с тобой поговорить?

– Говори, – ответила она.

15– Ты знаешь, – сказал он, – что царство было моим, и на меня смотрел весь Исраил как на будущего царя. Но всё изменилось, и царство перешло к моему брату, ведь оно было суждено ему от Вечного. 16И вот я прошу тебя об одном. Не откажи мне.

– Говори, – сказала она.

17Он сказал:

– Прошу тебя, поговори с царём Сулейманом – тебе он не откажет, – чтобы он отдал мне в жёны шунемитянку Авишаг.

18– Хорошо, – ответила Вирсавия. – Я поговорю о тебе с царём.

19Когда Вирсавия пришла к царю Сулейману поговорить с ним об Адонии, царь встал, чтобы встретить её, поклонился ей и сел на свой престол. Он велел принести престол для царской матери, и она села по правую руку от него.

20– У меня к тебе маленькая просьба, – сказала она. – Не откажи мне.

Царь ответил:

– Проси, моя мать, я не откажу тебе.

21И она сказала:

– Пусть шунемитянку Авишаг отдадут в жёны твоему брату Адонии.

22Царь Сулейман ответил матери:

– И зачем ты просишь для Адонии шунемитянку Авишаг? Проси уж для него и царство – он ведь мой старший брат! Да, для него, для священнослужителя Авиатара и для Иоава, сына Церуи!

23И царь Сулейман поклялся Вечным:

– Пусть Всевышний сурово накажет меня, если Адония не заплатит за эту просьбу жизнью! 24Верно, как и то, что жив Вечный, Который утвердил меня и посадил меня на престол моего отца Давуда и укрепил мой дом, как и обещал, – Адония сегодня же будет предан смерти!

25Царь Сулейман отдал приказ Бенаи, сыну Иодая, и тот убил Адонию.

Наказание Авиатара и смерть Иоава

26А священнослужителю Авиатару царь сказал:

– Ступай в Анатот, к своим полям. Ты заслуживаешь казни, но сегодня я не предам тебя смерти, потому что ты носил сундук2:26 Сундук – см. пояснительный словарь, а также Исх. 25:10-22. Владыки Вечного перед моим отцом Давудом и делил все тяготы жизни с моим отцом.

27И Сулейман отстранил Авиатара от служения Вечному, исполняя этим слово, которое Вечный сказал в Шило о доме Илия2:27 См. 1 Цар. 2:27-36.. 28Когда новости дошли до Иоава, а Иоав поддержал Адонию, хотя и не поддержал Авессалома, он вбежал в священный шатёр Вечного и схватился за рога жертвенника2:28 См. сноску на 1:50.. 29Царю Сулейману доложили, что Иоав убежал в священный шатёр Вечного и находится у жертвенника. И Сулейман приказал Бенаи, сыну Иодая:

– Иди, убей его!

30Беная вошёл в священный шатёр Вечного и сказал Иоаву:

– Так говорит царь: «Выходи!»

Но тот ответил:

– Нет, я умру здесь.

Беная доложил царю:

– Вот так ответил мне Иоав.

31Тогда царь приказал Бенае:

– Сделай, как он говорит. Срази его и похорони, и тем очисть меня и дом моего отца от вины за невинную кровь, что пролил Иоав. 32Вечный воздаст ему за кровь, которую он пролил, потому что он без ведома моего отца Давуда напал на двух человек и убил их мечом. Оба они – Авнер, сын Нера, военачальник Исраила, и Амаса, сын Иетера, военачальник Иудеи, – были праведнее и лучше его. 33Пусть вина за их кровь падёт на голову Иоава и его потомков навеки. Но на Давуде и его потомках, его доме и престоле пусть навеки будет мир Вечного.

34Беная, сын Иодая, пошёл и убил Иоава, и его похоронили на его участке в пустыне. 35Царь поставил Бенаю, сына Иодая, над войском вместо Иоава и заменил Авиатара священнослужителем Цадоком.

Смерть Шимея

36После этого царь послал за Шимеем и сказал ему:

– Построй себе дом в Иерусалиме и живи там, больше никуда не ходи. 37Знай, в тот день, когда ты уйдёшь и пересечёшь реку Кедрон, ты умрёшь и сам будешь виновен в своей гибели.

38Шимей ответил царю:

– Хорошо. Твой раб сделает так, как сказал господин мой царь.

И Шимей оставался в Иерусалиме долгое время. 39Но три года спустя двое из рабов Шимея убежали к царю города Гата Ахишу, сыну Маахи, и Шимею донесли:

– Твои рабы в Гате.

40Тогда он оседлал осла и отправился к Ахишу в Гат искать рабов. Так Шимей ушёл и привёл рабов из Гата. 41Когда Сулейману доложили, что Шимей уходил из Иерусалима в Гат и вернулся, 42царь призвал Шимея и сказал ему:

– Разве я не взял с тебя клятву Вечным и не предупредил тебя: «Знай, в тот день, когда ты пойдёшь, куда бы то ни было, ты умрёшь»? Ты тогда сказал мне: «Хорошо. Я буду послушен». 43Почему же ты не сдержал клятву Вечному и не послушался моего повеления?

44Ещё царь сказал Шимею:

– В своём сердце ты хранишь память обо всём том зле, которое ты сделал моему отцу Давуду. Теперь Вечный воздаст тебе за твоё злодеяние. 45А царь Сулейман будет благословен, и престол Давуда останется непоколебимым перед Вечным вовеки.

46И царь отдал приказ Бенаи, сыну Иодая, и тот вышел и убил Шимея. Так царство надёжно упрочилось во власти Сулеймана.