1 Mafumu 17 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 17:1-24

Makwangwala Adyetsa Eliya

1Ndipo mneneri Eliya wa ku Tisibe ku Giliyadi, anati kwa Ahabu, “Pali Yehova wamoyo, Mulungu wa Israeli, amene ndimamutumikira, sipadzakhala mame kapena mvula zaka zikubwerazi, pokhapokha ine nditanena.”

2Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya kuti, 3“Choka kuno, upite kummawa, ukabisale mʼmbali mwa mtsinje wa Keriti, pafupi ndi Yorodani. 4Uzikamwa mu mtsinjemo, ndipo ndalamula makwangwala kuti azikakudyetsa kumeneko.”

5Choncho Eliya anachita zomwe Yehova anamuwuza. Anapita ku mtsinje wa Keriti, pafupi ndi Yorodani, nakakhala kumeneko. 6Makwangwala ankabweretsera buledi ndi nyama mmawa ndi madzulo, ndipo ankamwa mu mtsinjemo.

Mayi Wamasiye wa ku Zarefati

7Patapita masiku, mtsinjewo unaphwa chifukwa mvula sinagwe mʼdzikomo. 8Yehova anayankhula naye kuti, 9“Nyamuka tsopano, pita ku Zarefati ku Sidoni ndipo ukakhale kumeneko. Ndalamula mkazi wamasiye wa kumeneko kuti azikakudyetsa.” 10Choncho iye ananyamuka napita ku Zarefati. Atafika pa chipata cha mzindawo, taonani mkazi wamasiye amatola nkhuni. Anamuyitana ndi kumuwuza kuti, “Patseni madzi pangʼono mʼchikho kuti ndimwe.” 11Mayi wamasiye uja ankapita kukatunga madzi, Eliya anamuyitananso namuwuza kuti, “Chonde munditengerekonso buledi.”

12Iye anayankha kuti “Pali Yehova Mulungu wanu wamoyo, ine ndilibe chakudya china chilichonse, koma kaufa pangʼono mʼmbiya ndi mafuta pangʼono mʼbotolo. Ine ndikutola tinkhuni tochepa kuti ndipite nato ku nyumba ndi kukaphika chakudya changa ndi cha mwana wanga, kuti tikadye kenaka tife.”

13Eliya anati kwa iye, “Musachite mantha. Pitani mukachite monga mwaneneramo. Koma poyamba mundipangire kachakudya pangʼono kuchokera pa ufa umene muli nawo ndi kubwera nako kwa ine, ndipo kenaka mukaphike choti mudye inuyo ndi mwana wanuyo. 14Pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ufa umene uli mʼmbiyamo sudzatha ndipo mafuta amene ali mʼbotolomo sadzathanso mpaka tsiku limene Yehova adzagwetse mvula pa dziko lapansi.’ ”

15Mayi wamasiyeyo anapita nakachita zimene Eliya anamuwuza. Choncho panali chakudya cha Eliya, mayiyo pamodzi ndi banja lake lonse chimene anadya masiku ambiri. 16Pakuti ufa umene unali mʼmbiya sunathe ndiponso mafuta amene anali mʼbotolo sanathe, monga momwe ananenera Yehova kudzera mwa Eliya.

17Tsiku lina mwana wake wa mkazi wamasiye uja, mwini nyumbayo, anadwala. Matenda ananka nakulirakulirabe, ndipo kenaka analeka kupuma. 18Mayiyo anati kwa Eliya, “Kodi ndakulakwirani chiyani, inu munthu wa Mulungu? Kodi munabwera kuno kudzandikumbutsa tchimo langa ndi kudzandiphera mwana wanga?”

19Eliya anayankha kuti, “Patseni mwana wanuyo.” Iye anatenga mwanayo mʼmanja mwa mayiyo napita naye mʼchipinda chapamwamba, kumene Eliyayo amagona, namugoneka pa bedi lake. 20Kenaka Eliya anafuwula kwa Yehova nati, “Inu Yehova Mulungu wanga, kodi mwabweretsanso choyipa chotere pa mkazi wamasiye amene ine ndikukhala naye, pakuchititsa kuti mwana wake afe?” 21Pamenepo Eliya anakumbatira mwanayo katatu ndi kufuwula kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Mulungu wanga, mubwezereni mwanayu moyo wake!”

22Yehova anamva kufuwula kwa Eliya, ndipo moyo wa mwanayo unabwerera mwa iye ndipo anatsitsimuka. 23Eliya ananyamula mwanayo natsika naye kuchoka mʼchipinda chapamwamba chija nalowa naye mʼnyumba. Anamupereka kwa amayi ake ndipo anati, “Taonani, mwana wanu ali ndi moyo!”

24Pamenepo mayiyo anati kwa Eliya, “Tsopano ndadziwa kuti ndinu munthu wa Mulungu ndipo mawu a Yehova amene mumayankhula ndi owona.”

Bibelen på hverdagsdansk

1. Kongebog 17:1-24

Elias profeterer hungersnød over Israel

1Der var på det tidspunkt en profet ved navn Elias, som boede i Tishbe i Gilead. Han kom til kong Ahab i Samaria med et budskab fra Herren: „Så sandt Herren lever—Israels Gud, som jeg tilbeder og tjener—så skal der i de kommende år hverken falde regn eller dug uden på min udtrykkelige befaling!”

2Derefter sagde Herren til Elias: 3„Tag væk herfra og hold dig skjult i Kerit-kløften øst for Jordanfloden. 4Du kan drikke vand fra bækken der, og jeg har befalet ravnene at bringe dig mad.”

5Elias gjorde, som Herren sagde, og holdt sig skjult i kløften, 6hvor ravnene bragte ham frisk brød og kødstykker hver morgen og aften, og han drak vand af bækken.

Elias og enken i Zarepta

7Men nogen tid efter tørrede bækken ud, for der faldt ingen regn i landet. 8Da sagde Herren til Elias:

9„Tag af sted til landsbyen Zarepta oppe ved Sidon og slå dig ned der! Dér bor en enke, som jeg har befalet at sørge for dig.” 10Så tog Elias til Zarepta. Uden for byens port så han en enke, der gik og samlede brænde. Han kaldte på hende og bad om lidt vand at drikke. 11Da hun gik for at hente vandet, tilføjede han: „Tag også lidt brød med til mig!”

12„Jeg sværger ved Herren, din Gud, at jeg ikke har brød i huset!” svarede enken. „I melkrukken er der kun en håndfuld tilbage, og olivenolien er næsten brugt op. Jeg var netop i færd med at samle brænde for at bage et brød til mig og min søn af det sidste mel. Når vi har spist det, må vi lægge os til at dø.”

13„Du skal ikke være bange,” sagde Elias. „Gå bare hjem og gør, som du har sagt. Bag brødet, men kom så tilbage og giv det til mig! Bagefter kan du bage noget til dig selv og din søn, 14for Herren, Israels Gud, siger: Melet i krukken vil ikke slippe op, og kanden med olie vil ikke blive tom, før Herren sender regn igen.”

15Så gjorde enken som Elias sagde. Elias og enken og hendes søn havde derefter nok at spise, 16for som Herren havde sagt gennem Elias, sådan blev det: Melet i krukken slap ikke op, og kanden med olie blev ikke tom.

17Men en dag blev kvindens søn syg. Det gik hurtigt ned ad bakke med ham og han døde.

18„Åh, du profet!” græd hun, „Hvad galt har jeg gjort imod dig? Kom du hertil for at minde Gud om mine synder, så han kunne straffe mig ved at slå min dreng ihjel?”

19„Giv drengen til mig!” svarede Elias. Så tog han drengen i sine arme, bar ham ovenpå til gæsteværelset, hvor han boede, og lagde ham på sengen. 20Derpå råbte han til Herren: „Min Gud, hvorfor har du bragt ulykke over denne enke, som har vist mig så stor en gæstfrihed?” 21Derefter bøjede han sig hen over drengen tre gange, mens han fortsat råbte til Herren: „Herre, min Gud, gør dog drengen levende igen!”

22Herren hørte Elias’ bøn, og drengen blev levende igen. 23Så fulgte Elias ham nedenunder til hans mor. „Se, her er din søn!” sagde han. „Han lever!”

24Da udbrød enken: „Nu ved jeg, at du er en profet, og at det, du siger, er sandt, for det er jo Herrens ord!”