1 Mafumu 14 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 14:1-31

Ahiya Anenera za Kugwa kwa Yeroboamu

1Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala, 2ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa. 3Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.” 4Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo.

Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba. 5Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”

6Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa. 7Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli. 8Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga. 9Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.

10“ ‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu. 11Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’

12“Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira. 13Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.

14“Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino. 15Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera. 16Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”

17Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira. 18Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.

19Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli. 20Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Rehobowamu Mfumu ya Yuda

21Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.

22Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira. 23Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri. 24Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.

25Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu. 26Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga. 27Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu. 28Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.

29Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda? 30Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu. 31Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

3 Царств 14:1-31

Пророчество Ахии против дома Иеровоама

1В то время Авия, сын Иеровоама, заболел, 2и Иеровоам сказал жене:

– Пойди переоденься, чтобы в тебе нельзя было узнать жену Иеровоама. Потом иди в Шило. Там есть пророк Ахия – тот, кто сказал, что я стану царём этого народа. 3Возьми с собой десять хлебов, несколько лепёшек, кувшин мёда и иди к нему. Он скажет тебе, что будет с мальчиком.

4Жена Иеровоама сделала так, как он говорил, и пошла к дому Ахии в Шило. А Ахия уже не видел, его глаза ослепли от старости. 5Но Вечный сказал Ахии:

– Жена Иеровоама идёт, чтобы спросить тебя о сыне, потому что он заболел. Ответь ей так-то и так-то. Придя, она будет притворяться другой женщиной.

6Когда Ахия услышал у двери звук её шагов, он сказал:

– Входи, жена Иеровоама. Зачем ты притворяешься? У меня для тебя плохие вести. 7Иди, скажи Иеровоаму, что так говорит Вечный, Бог Исраила: «Я возвысил тебя над народом и сделал тебя вождём Моего народа Исраила. 8Я отнял царство у дома Давуда и отдал его тебе, но ты не был подобен Моему рабу Давуду, который исполнял Мои повеления и следовал за Мной от всего сердца, делая лишь то, что правильно в Моих глазах. 9Ты сделал больше зла, чем все, кто жил до тебя. Ты сделал себе других богов, истуканы из металла, вызвав Мой гнев, а ко Мне повернулся спиной. 10Из-за этого Я навожу на твой дом беду. Я истреблю у Иеровоама всякого мужчину – и раба, и свободного. Я буду жечь твой дом, как жгут навоз, пока он не сгорит дотла. 11Тех, кто умрёт у тебя в городе, сожрут псы, а тех, кто умрёт в поле, склюют небесные птицы». Так сказал Вечный!14:10-11 Об исполнении этого пророчества см. 15:29-30.

12А ты возвращайся домой. Когда твоя нога ступит в город, мальчик умрёт. 13Весь Исраил оплачет и похоронит его. Он единственный в доме Иеровоама, кто удостоится погребения потому что он один в его доме, в ком Вечный, Бог Исраила, нашёл что-то доброе.

14Вечный воздвигнет Себе над Исраилом царя, который истребит дом Иеровоама, и это начнётся уже сегодня, и даже сейчас. 15Вечный поразит Исраил, и тот будет как тростник, колеблемый стремительным потоком. Он искоренит Исраил из этой доброй земли, которую Он дал их предкам, и рассеет их за рекой Евфрат, потому что они разгневали Вечного, делая столбы Ашеры14:15 Столбы Ашеры – культовые символы вавилонско-ханаанской богини Ашеры. Ашера считалась матерью богов и людей, владычицей моря и всего сущего.. 16Он отдаст Исраил в руки его врагов из-за грехов, которые Иеровоам совершил и к которым он склонил исраильтян.

17Жена Иеровоама встала и пошла в Тирцу. Как только она переступила порог дома, мальчик умер. 18Его похоронили, и весь Исраил оплакивал его, как Вечный и сказал через Своего раба, пророка Ахию.

Смерть Иеровоама

19Прочие события царствования Иеровоама, его войны и то, как он правил, записаны в «Книге летописей царей Исраила». 20Он правил двадцать два года и упокоился со своими предками. И царём вместо него стал его сын Надав.

Реховоам – царь Иудеи

(2 Лет. 12:9-16)

21Реховоам, сын Сулеймана, стал царём в Иудее. Ему был сорок один год, когда он стал царём, и правил он семнадцать лет в Иерусалиме, городе, который Вечный избрал из всех родов Исраила, чтобы пребывать там. Его мать звали Наама, она была аммонитянкой.

22Люди Иудеи делали зло в глазах Вечного. Своими грехами они возбудили Его ревнивый гнев сильнее, чем их отцы. 23Они тоже устроили у себя капища на возвышенностях, священные камни и столбы Ашеры на каждом высоком холме и под каждым тенистым деревом. 24В стране были даже храмовые блудники14:24 Храмовые блудники – имеются в виду мужчины, занимавшиеся культовой проституцией, которая была неотъемлемой частью весьма распространённых в те дни языческих культов плодородия., ведь народ перенял все отвратительные обычаи тех народов, которых Вечный прогнал от исраильтян.

25На пятом году правления царя Реховоама царь Египта Сусаким14:25 Сусаким – фараон Шешонк I, основатель XXII (ливийской) династии, правил с 950 по 929 гг. до н. э. напал на Иерусалим. 26Он унёс сокровища храма Вечного и сокровища царского дворца. Он забрал всё, включая и все золотые щиты, которые сделал Сулейман. 27Царь Реховоам сделал вместо них щиты из бронзы и вверил их начальникам стражи, что охраняла вход в царский дворец. 28Всякий раз, когда царь шёл в храм Вечного, стража несла щиты, а после возвращала их в комнату стражи.

29Прочие события царствования Реховоама и всё, что он сделал, записано в «Книге летописей царей Иудеи». 30Между Реховоамом и Иеровоамом всё время шла война. 31Реховоам упокоился со своими предками и был похоронен с ними в Городе Давуда. Его мать звали Наама, она была аммонитянкой. И царём вместо него стал его сын Авия.