1 Mafumu 11 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 11:1-43

Akazi a Solomoni

1Komatu Mfumu Solomoni anakonda akazi ambiri achilendo ndipo kuwonjezera pa mwana wamkazi wa Farao, analinso ndi akazi a mitundu iyi: Amowabu, Aamoni, Aedomu, Asidoni, ndi Ahiti. 2Akazi amenewa anali ochokera ku mitundu ija imene Yehova anawuza Aisraeli kuti, “Simuyenera kudzakwatirana nawo amenewa, chifukwa ndithu, amenewa adzatembenuza mitima yanu kuti mutsatire milungu yawo.” Komabe Solomoni anawakonda kwambiri akazi amenewa. 3Iye anali ndi akazi 700 ochokera ku mabanja achifumu ndi azikazi 300 ndipo akaziwo anamusocheretsa. 4Solomoni atakalamba, akazi akewo anakopa mtima wake kuti atsatire milungu ina, ndipo sanatsatire Yehova Mulungu wake ndi mtima wodzipereka, monga unalili mtima wa Davide abambo ake. 5Pakuti iye ankapembedza Asitoreti, mulungu wamkazi wa Asidoni, ndiponso Moleki mulungu wonyansa wa Aamoni. 6Kotero Solomoni anachita zoyipa pamaso pa Yehova. Sanatsatire Yehova kwathunthu monga anachitira Davide abambo ake.

7Pa phiri la kummawa kwa Yerusalemu, anamanga malo opembedzerapo Kemosi, mulungu wonyansa wa Mowabu, ndiponso malo a Moleki, mulungu wonyansa wa Aamoni. 8Iye anamangiranso malo oterewa akazi ake onse achilendo, amene amafukiza lubani ndi kumapereka nsembe kwa milungu yawo.

9Choncho Yehova anakwiyira Solomoni chifukwa mtima wake unatembenuka kuchoka kwa Yehova Mulungu wa Israeli, amene anamuonekera kawiri konse. 10Ngakhale kuti Yehova anamuletsa Solomoni kutsatira milungu ina, iyeyo sanamvere lamulo la Yehova. 11Pamenepo Yehova anati kwa Solomoni, “Popeza mtima wako ndi wotere ndipo sunasunge pangano langa ndi malamulo anga amene ndinakuwuza, ndithudi, Ine ndidzawugawa ufumuwu kuwuchotsa kwa iwe ndi kuwupereka kwa mmodzi mwa atumiki ako. 12Koma chifukwa cha Davide abambo ako, sindidzachita zimenezi iwe uli moyo. Ndidzawugawa mʼdzanja la mwana wako. 13Komabe sindidzamulanda ufumu wonse, koma ndidzamusiyira fuko limodzi chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso chifukwa cha Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha.”

Adani a Solomoni

14Ndipo Yehova anamuutsira Solomoni mdani, Hadadi Mwedomu, wochokera ku banja laufumu ku Edomu. 15Kale pamene Davide ankachita nkhondo ndi Aedomu, Yowabu mkulu wa ankhondo, amene anapita kukakwirira Aisraeli akufa, anakantha amuna onse ku Edomu. 16Yowabu ndi Aisraeli onse anakhala kumeneko miyezi isanu ndi umodzi mpaka anawononga amuna onse a ku Edomu. 17Koma Hadadi akanali mwana anathawira ku Igupto pamodzi ndi akuluakulu ena a ku Edomu amene ankatumikira abambo ake. 18Iwo ananyamuka ku Midiya ndi kupita ku Parani. Ndipo anatenga amuna ena ku Paraniko, napita nawo ku Igupto, kwa Farao mfumu ya Igupto, amene anamupatsa nyumba, malo ndiponso chakudya.

19Farao anamukomera mtima Hadadi ndipo anamupatsa mkazi amene anali mngʼono wake wa Mfumukazi Tahipenesi. 20Mngʼono wake wa Tahipenesi anabereka mwana wamwamuna ndipo anamutcha Genubati, amene analeredwa mʼnyumba yaufumu ndi Tahipenesi. Genubatiyo ankakhala limodzi ndi ana a Farao.

21Ali ku Iguptoko, Hadadi anamva kuti Davide ndi Yowabu anamwalira. Pamenepo Hadadi anati kwa Farao, “Loleni ndichoke kuti ndibwerere ku dziko la kwathu.”

22Farao anafunsa kuti, “Kodi ukusowa chiyani kuno kuti ufune kubwerera ku dziko la kwanu?”

Hadadi anayankha kuti, “Palibe chimene ndikusowa, koma loleni kuti ndichoke!”

23Ndipo Mulungu anawutsira Solomoni mdani wina, Rezoni mwana wa Eliada, amene anali atathawa mbuye wake, Hadadezeri mfumu ya ku Zoba. 24Iye anasonkhanitsa anthu ndipo anali mtsogoleri wa anthu owukira pamene Davide anapha ankhondo a ku Zoba. Anthu owukirawa anapita ku Damasiko, nakakhala kumeneko ndi kuyamba kulamulira. 25Rezoni anali mdani wa Israeli pa masiku onse a Solomoni, kuwonjezera pa mavuto amene ankabweretsa Hadadi. Kotero Rezoni ankalamulira ku Aramu ndipo ankadana ndi Israeli.

Yeroboamu Awukira Solomoni

26Yeroboamu, mwana wa Nebati anawukiranso mfumu. Iye anali mmodzi mwa akuluakulu a Solomoni wa fuko la Efereimu, wa ku Zeredi, ndipo amayi ake anali Zeruya, mkazi wamasiye.

27Nkhani ya kuwukira kwa Yeroboamu inali yotere: Solomoni anamanga malo a chitetezo a Milo ndipo anakonza khoma logumuka la mzinda wa Davide, abambo ake. 28Tsono Yeroboamu anali munthu wamphamvu kwambiri ndipo Solomoni ataona kuti mnyamatayo amadziwa kugwira ntchito bwino, anamuyika kukhala woyangʼanira anthu a ntchito onse a nyumba ya Yosefe.

29Tsiku lina Yeroboamu ali pa ulendo kuchokera ku Yerusalemu, anakumana ndi mneneri Ahiya pa msewu, ndipo Ahiyayo anali atavala mwinjiro watsopano. Awiriwo anali okha kuthengoko, 30ndipo Ahiya anagwira mwinjiro watsopano umene anavala ndi kuwungʼamba zidutswa 12. 31Tsono iye anati kwa Yeroboamu, “Tenga zidutswa khumi, pakuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Taona, Ine ndidzachotsa ufumu mʼdzanja la Solomoni ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi. 32Koma chifukwa cha mtumiki wanga Davide ndiponso mzinda wa Yerusalemu, umene ndinawusankha pakati pa mafuko a Israeli, iye adzakhala ndi fuko limodzi lokha. 33Ndidzachita zimenezi chifukwa wandisiya Ine ndi kupembedza Asitoreti mulungu wamkazi wa Asidoni, Kemosi mulungu wa Amowabu ndiponso Moleki mulungu wa Aamoni, ndipo sanayende mʼnjira yanga, kapena kusunga mawu anga ndi malamulo anga monga anachitira Davide abambo ake.

34“ ‘Koma sindidzalanda ufumu wonse mʼdzanja la Solomoni. Ine ndamuyika kukhala wolamulira masiku onse a moyo wake chifukwa cha mtumiki wanga Davide, amene ndinamusankha ndiponso amene anamvera malamulo anga ndi mawu anga. 35Ndidzalanda ufumu mʼdzanja la mwana wake ndipo ndidzakupatsa iwe mafuko khumi. 36Ndidzapereka fuko limodzi kwa mwana wake ndi cholinga choti Davide mtumiki wanga adzakhale nyale nthawi zonse pamaso panga mu Yerusalemu, mzinda umene ndinawusankha kuyikamo Dzina langa. 37Koma kunena za iwe, ndidzakutenga ndipo udzalamulira chilichonse chimene mtima wako ukukhumba; udzakhala mfumu ya Israeli. 38Ngati udzamvera zonse zimene ndidzakulamula ndi kuyenda mʼnjira yanga ndi kuchita zabwino pamaso panga, posunga malamulo anga ndi mawu anga monga anachitira Davide mtumiki wanga, Ine ndidzakhala nawe. Ndidzakupatsa ufumu umene udzakhala wokhazikika monga ndinamupatsira Davide, ndipo Ine ndidzakupatsa Israeli. 39Ine ndidzalanga zidzukulu za Davide chifukwa cha zimenezi, koma osati kwamuyaya.’ ”

40Solomoni anafunitsitsa kupha Yeroboamu, koma Yeroboamu anathawira ku Igupto, kwa Sisaki mfumu ya Igupto ndipo anakhala kumeneko mpaka Solomoni atamwalira.

Kumwalira kwa Solomoni

41Ntchito zina za Solomoni, zonse zomwe anachita komanso za nzeru zake, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya Solomoni? 42Solomoni analamulira Aisraeli onse mu Yerusalemu kwa zaka makumi anayi. 43Ndipo anagona ndi makolo ake nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide abambo ake. Ndipo Rehobowamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo ake.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

3 Царств 11:1-43

Сулаймон отворачивается от Вечного

1Но, кроме дочери фараона, царь Сулаймон полюбил ещё много других чужеземных женщин – моавитянок, аммонитянок, эдомитянок, сидонянок и хеттеянок. 2Они были из тех народов, о которых Вечный сказал исроильтянам: «Не роднитесь с ними браком, потому что они непременно обратят ваше сердце к своим богам». А Сулаймона тянуло к ним. 3У него было семьсот жён царского рода и триста наложниц, и жёны сбили его с истинного пути. 4Когда Сулаймон состарился, жёны обратили его сердце к чужим богам, и оно перестало быть полностью преданным Вечному, его Богу, каким было сердце Довуда, его отца. 5Он пошёл за Астартой11:5 Астарта – богиня любви и плодородия, богиня-воительница., богиней сидонян, и Молохом11:5 Молох – аммонитский бог, в жертву которому приносились дети. По Закону за поклонение Молоху исроильтянам грозила смертная казнь (см. Лев. 18:21; 20:2-5)., омерзительным богом аммонитян.

6Сулаймон делал зло в глазах Вечного, он не следовал за Вечным полностью, как Довуд, его отец. 7На холме, к востоку от Иерусалима, Сулаймон построил капище Хемошу11:7 Хемош – божество, в жертвы которому приносились люди., омерзительному богу Моава, и Молоху, омерзительному богу аммонитян. 8То же самое он сделал для всех чужеземных жён, которые возжигали благовония и приносили жертвы своим богам.

9Вечный разгневался на Сулаймона, потому что его сердце отвернулось от Вечного, Бога Исроила, который дважды являлся ему. 10Несмотря на то что Он запретил Сулаймону идти за чужими богами, Сулаймон не выполнил повеления Вечного. 11И Вечный сказал Сулаймону:

– Раз ты не сохранил Моего священного соглашения и Моих установлений, которые Я повелел тебе соблюдать, Я непременно отниму у тебя царство и отдам его одному из твоих подданных. 12Но ради Довуда, твоего отца, Я не сделаю этого при твоей жизни. Я вырву его из рук твоего сына. 13Но Я отниму у него не всё царство. Я оставлю ему один род ради Довуда, Моего раба, и ради Иерусалима, который Я избрал.

Враги Сулаймона

14И Вечный воздвиг Сулаймону врага – эдомитянина Хадада из царской семьи Эдома. 15Прежде, когда Довуд был в Эдоме, начальник войска Иоав пришёл хоронить погибших и перебил в Эдоме всех мужчин. 16Иоав и все исроильтяне оставались там шесть месяцев, пока не истребили в Эдоме всех мужчин. 17Но Хадад, тогда ещё лишь ребёнок, бежал в Египет с некоторыми эдомскими вельможами, служившими его отцу. 18Они отправились в путь из Мадиана и пришли в пустыню Паран. Взяв с собой людей из Парана, они пришли в Египет, к фараону, царю Египта, который дал Хададу дом, пропитание и землю.

19Хадад был так угоден фараону, что тот дал ему в жёны сестру своей жены, царицы Тахпенесы. 20Сестра Тахпенесы родила ему сына Генувата, которого Тахпенеса вырастила в царском дворце. Генуват жил там вместе с детьми фараона.

21Будучи в Египте, Хадад услышал о том, что Довуд упокоился со своими предками и что начальник войска Иоав умер. Тогда Хадад сказал фараону:

– Отпусти меня в мою страну.

22– Чего тебе недостаёт у меня, что ты так хочешь вернуться в свою страну? – спросил фараон.

– Всего вдоволь, – ответил Хадад, – но всё-таки отпусти меня!

23Всевышний воздвиг Сулаймону и другого врага – Резона, сына Элиады, который убежал от своего господина Ададезера, царя Цовы. 24После того как Довуд разбил войска Цовы, Резон собрал вокруг себя бунтовщиков и возглавил их. Они пришли в Дамаск, поселились там и сделали его царём Дамаска. 25Резон был врагом Исроила всё время, пока был жив Сулаймон, умножая зло, чинимое Хададом. Он правил Сирией и презирал Исроил.

Пророчество Ахии о разделении царства

26Иеровоам, сын Невата, поднял мятеж против царя. Он был одним из приближённых Сулаймона, ефраимит из города Цереды, а матерью его была вдова по имени Церуа.

27Вот история о том, как он поднял мятеж против царя: Сулаймон построил Милло и заделал брешь в стене Города Довуда, своего отца. 28А Иеровоам был очень способным, и когда Сулаймон заметил, как хорошо этот молодой человек исполняет свою работу, он поставил его над всеми подневольными людьми из дома Юсуфа.

29В то время Иеровоаму случилось выйти из Иерусалима, и на пути его встретил пророк Ахия из города Шило, одетый в новую одежду. Они были в том поле лишь вдвоём, 30и Ахия, взявшись за новую одежду, что была на нём, разорвал её на двенадцать кусков.

31Затем он сказал Иеровоаму:

– Возьми десять кусков себе, потому что так говорит Вечный, Бог Исроила: «Вот Я вырываю царство из рук Сулаймона и отдаю тебе десять родов. 32Но ради Моего раба Довуда и города Иерусалима, который Я избрал среди всех родов Исроила, у него будет один род. 33Я сделаю это, потому что он оставил Меня и поклонялся Астарте, богине сидонян, Хемошу, богу моавитян, и Молоху, богу аммонитян, и не следовал Моими путями, не делал того, что праведно в Моих глазах, и не соблюдал Мои установления и законы, как делал Довуд, его отец.

34Но Я заберу из рук Сулаймона не всё царство. Я сделал его правителем во все дни его жизни ради Довуда, Моего раба, которого Я избрал и который исполнял Мои повеления и установления. 35Я возьму царство из рук его сына и отдам тебе десять родов. 36Я дам один род его сыну, чтобы у Довуда, Моего раба, всегда был потомок на троне11:36 Букв.: «светильник предо Мной». в Иерусалиме, в городе, который Я избрал, чтобы пребывать там. 37А тебя Я избираю, и ты будешь править всем, чем пожелает править твоё сердце, – ты будешь царём Исроила. 38Если ты будешь исполнять всё, что Я тебе велю, ходить Моими путями и делать то, что праведно в Моих глазах, исполняя Мои установления и повеления, как делал Мой раб Довуд, то Я буду с тобой. Я создам тебе такой же крепкий дом, как тот, что Я создал Довуду, и отдам тебе Исроил. 39Я накажу потомков Довуда, но не навеки».

40Сулаймон пытался убить Иеровоама, но Иеровоам бежал в Египет к царю Сусакиму и оставался там до смерти Сулаймона.

Смерть Сулаймона

(2 Лет. 9:29-31)

41Прочие события царствования Сулаймона, всё, что он сделал, и его мудрость записаны в «Книге дел Сулаймона». 42Сулаймон правил в Иерусалиме всем Исроилом сорок лет. 43Потом он упокоился со своими предками и был похоронен в Городе Довуда, своего отца. И царём вместо него стал его сын Реховоам.