1 Mafumu 1 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Mafumu 1:1-53

Adoniya Adziyika Kukhala Mfumu

1Mfumu Davide atakalamba sankamva kufunda ngakhale akamufunditsa mabulangeti. 2Choncho nduna zake zinamuwuza kuti, “Tiloleni tifune namwali woti azikhala nanu ndi kumakusamalirani. Namwaliyo azigona pafupi nanu kuti mbuye wathu mfumu muzimva kufundira.”

3Kotero anafunafuna mʼdziko lonse la Israeli mtsikana wokongola ndipo anapeza Abisagi wa ku Sunemu, nabwera naye kwa mfumu. 4Mtsikanayo anali wokongola kwambiri ndipo ankasamalira mfumu ndi kumayitumikira, koma mfumuyo sinakhale naye malo amodzi.

5Nthawi imeneyi Adoniya, mwana wa Hagiti, anayamba kudzitukumula ndipo anati, “Ndidzakhala mfumu ndine.” Choncho anadzikonzera galeta ndi akavalo, pamodzi ndi anthu 50 woti azithamanga patsogolo pake. 6(Abambo ake sanalowererepo nʼkamodzi komwe ndipo sanafunsepo kuti, “Nʼchifukwa chiyani ukuchita zimenezi?” Adoniyayo anali wokongola kwambiri ndipo anali wopondana ndi Abisalomu).

7Adoniya anagwirizana ndi Yowabu mwana wa Zeruya ndiponso Abiatara wansembe, ndipo iwowa anamuthandiza. 8Koma Zadoki wansembe, Benaya mwana wa Yehoyada, mneneri Natani, Simei ndi Rei ndiponso asilikali amphamvu a Davide sanamutsate Adoniya uja.

9Kenaka Adoniya anapereka nsembe za nkhosa ndi ngʼombe ndiponso ana angʼombe onenepa ku Mwala wa Zohereti kufupi ndi Eni Rogeli. Iye anayitana abale ake onse, ana aamuna a mfumu ndiponso akuluakulu onse a ku Yuda, 10koma sanayitane mneneri Natani kapena Benaya kapenanso asilikali amphamvu a Davide ngakhalenso mʼbale wake Solomoni.

11Pamenepo Natani anafunsa Batiseba, amayi ake a Solomoni, kuti, “Kodi simunamve kuti Adoniya, mwana wa Hagiti, walowa ufumu popanda Davide mbuye wathu kudziwa? 12Tsopano ine ndikulangizeni inu mmene mungapulumutsire moyo wanu ndi moyo wa mwana wanu Solomoni. 13Pitani msanga kwa Mfumu Davide ndipo mukanene kuti, ‘Mbuye wanga mfumu, kodi simunalumbire kwa ine mdzakazi wanu kuti, ‘Ndithu mwana wako Solomoni ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwanga, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu?’ Nanga nʼchifukwa chiyani Adoniya walowa ufumu?’ 14Pamene inu muzikayankhula ndi mfumu, ine ndidzalowa ndi kuchitira umboni mawu anuwo.”

15Choncho Batiseba anapita nakalowa ku chipinda kukaonana ndi mfumu imene inali itakalamba kwambiri, kumene Abisagi wa ku Sunemu uja ankayisamalira. 16Batiseba anagwada nalambira mfumu.

Mfumu inamufunsa kuti, “Kodi nʼchiyani chimene ukufuna?”

17Iye anayankha kuti, “Mbuye wanga, inu mwini munalumbira kwa ine mdzakazi wanu mʼdzina la Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Solomoni mwana wako ndiye adzakhale mfumu mʼmalo mwa ine, ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.’ 18Koma tsopano Adoniya ndiye walowa ufumu, ndipo inu mbuye wanga mfumu, simukuzidziwa zimenezi. 19Ndipo wapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndi nkhosa ndi mbuzi ndipo wayitana ana anu onse, wansembe Abiatara ndiponso Yowabu mkulu wa ankhondo, koma sanayitane kapolo wanu Solomoni. 20Mbuye wanga mfumu, maso a Aisraeli onse ali pa inu, kuti adziwe kuchokera kwa inu amene adzakhala pa mpando waufumu wa mbuye wanga mʼmalo mwanu. 21Mukapanda kutero, mbuye wanga, mukadzangotisiya nʼkulondola kumene kunapita makolo anu, ine pamodzi ndi mwana wangayu Solomoni adzatiyesa owukira.”

22Pamene Batiseba amayankhula ndi mfumu, mneneri Natani analowa. 23Ndipo anthu anawuza mfumu kuti, “Kwabwera mneneri Natani.” Kotero iye anafika pamaso pa mfumu ndipo anawerama nagunditsa nkhope yake pansi.

24Natani anafunsa kuti, “Mbuye wanga mfumu, kodi mwalengeza kuti Adoniya adzakhala mfumu mʼmalo mwanu, ndi kuti adzakhala pa mpando wanu waufumu? 25Lero lomwe lino wakapereka nsembe ngʼombe zambiri, ana angʼombe onenepa ndiponso nkhosa ndi mbuzi. Iye wayitana ana anu onse, atsogoleri a nkhondo, ndiponso wansembe Abiatara. Panopa onsewa akudya ndi kumwa naye ndipo akunena kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Adoniya!’ 26Koma ine kapolo wanu, wansembe Zadoki ndi Benaya mwana wa Yehoyada, ndiponso kapolo wanu Solomoni sanatiyitane. 27Kodi zimenezi mbuye wanga mfumu mwazichita ndinu, osawawuza atumiki anu kuti adziwe amene adzakhale pa mpando waufumu mʼmalo mwanu?”

Davide Alonga Ufumu Solomoni

28Pamenepo mfumu Davide anati, “Muyitaneni Batiseba.” Kotero Batiseba analowa ndipo anayimirira pamaso pa mfumu.

29Tsono mfumu inalumbira kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene anandipulumutsa ine ku mavuto onse, 30ndithu ine lero ndichita zonse zimene ndinalumbira kwa Yehova Mulungu wa Israeli kuti, mwana wako Solomoni adzakhala mfumu mʼmalo mwanga ndipo adzakhala pa mpando wanga waufumu.”

31Pamenepo Batiseba anawerama, nagunditsa mutu wake pansi nalambira mfumu, ndipo anati, “Mbuye wanga Mfumu Davide mukhale ndi moyo wautali!”

32Mfumu Davide anati, “Ndiyitanireni wansembe Zadoki, mneneri Natani ndi Benaya mwana wa Yehoyada.” Atafika pamaso pa mfumu, 33mfumuyo inati kwa iwo, “Tengani atumiki anga ndipo mukweze mwana wanga Solomoni pa bulu wanga ndipo mupite naye ku Gihoni. Mukalize lipenga ndi kufuwula kuti, ‘Akhale ndi moyo wautali mfumu Solomoni!’ 34Kumeneko Zadoki wansembe ndi mneneri Natani akamudzoze kuti akhale mfumu ya Israeli. Kenaka mukalize lipenga ndi kumanena kuti ‘Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni.’ 35Ndipo pobwera muzikamutsata pambuyo. Iyeyo akabwere kuno ndi kudzakhala pa mpando wanga waufumu ndi kudzalamulira mʼmalo mwanga. Ndamusankha kukhala wolamulira Israeli ndi Yuda.”

36Benaya mwana wa Yehoyada anayankha mfumu kuti, “Ameni! Yehova Mulungu wa mbuye wanga mfumu akhazikitse kuti zichitike motero. 37Monga momwe Yehova wakhalira ndi inu mbuye wanga mfumu, momwemonso akhale ndi Solomoni ndi kukhazikitsa ufumu wake kuti ukhale waukulu kuposa ufumu wa mbuye wanga Mfumu Davide!”

38Kotero Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndiponso Apeleti, anthu oteteza mfumu, anapita kukamukweza Solomoni pa bulu wa Mfumu Davide ndi kupita naye ku Gihoni. 39Wansembe Zadoki anatenga nyanga ya mafuta yochokera ku malo opatulika ndi kumudzoza Solomoni. Kenaka analiza lipenga ndipo anthu onse anafuwula kuti, “Akhale ndi moyo wautali Mfumu Solomoni!” 40Ndipo anthu onsewo anapita namutsatira pambuyo akuyimba zitoliro ndi kukondwerera kwambiri, kotero nthaka inagwedezeka chifukwa cha phokoso lawo.

41Adoniya pamodzi ndi anthu onse oyitanidwa amene anali naye anamva zimenezi pamene ankamaliza madyerero awo. Atamva kulira kwa malipenga, Yowabu anafunsa kuti, “Kodi phokoso lonselo mu mzindamo likutanthauza chiyani?”

42Iye akuyankhula, Yonatani mwana wa wansembe Abiatara anafika. Adoniya anati, “Lowa. Munthu wabwino ngati iwe ayenera kubweretsa nkhani yabwino.”

43Yonatani anayankha Adoniya kuti, “Ayi ndithu, zinthu sizili bwino! Mbuye wathu Mfumu Davide walonga Solomoni ufumu. 44Mfumu yatuma Zadoki wansembe, mneneri Natani, Benaya mwana wa Yehoyada, Akereti ndi Apeleti ku Gihoni ndipo iwo amukweza pa bulu wa mfumu, 45ndipo Zadoki wansembe ndi mneneri Natani adzoza Solomoni ku Gihoni kuti akhale mfumu. Ndipo kuchokera kumeneko akhala akululutira, kotero kuti mu mzinda monse muli phokoso lokhalokha. Ndiyetu phokoso limene mukulimvalo. 46Ndipo Solomoni wakhala kale pa mpando wake waufumu. 47Kuwonjezera pamenepo, nduna za mfumu zabwera kale kudzayamika mbuye wathu Mfumu Davide, pomanena kuti, ‘Mulungu wanu atchukitse dzina la Solomoni kuposa dzina lanu ndipo ufumu wake ukule kupambana ufumu wanu!’ Ndipo mfumu inawerama niyamba kupembedza pa bedi lake, 48inati, ‘Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, amene wasankha wolowa mʼmalo mwanga ine ndikanali ndi moyo lero lino.’ ”

49Anthu onse amene Adoniya anawayitana ananjenjemera ndi mantha, ndipo anayimirira, kenaka anamwazikana. 50Koma Adoniya, poopa Solomoni, anapita ku Nyumba ya Mulungu nakagwira msonga za guwa lansembe. 51Tsono Solomoni anawuzidwa kuti, “Adoniya akukuopani inu Mfumu Solomoni ndipo wagwira msonga za guwa lansembe. Iye akuti, ‘Mfumu Solomoni alumbire kuti sadzapha kapolo wake ndi lupanga.’ ”

52Solomoni anayankha kuti, “Ngati iyeyo aonetse kuti ndi munthu wakhalidwe labwino, ngakhale tsitsi la mʼmutu mwake silidzathothoka ndi kugwera pansi, koma akapezeka kuti ali ndi khalidwe loyipa, adzafa ndithu.” 53Pamenepo Mfumu Solomoni inatuma anthu ndipo anakamutenga paguwa paja. Adoniya anabwera ndi kudzalambira Mfumu Solomoni, ndipo Solomoni anati, “Pita ku nyumba yako.”

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

3 Царств 1:1-53

Довуд в старости

1Царь Довуд состарился и достиг преклонных лет. Его покрывали одеждами, но он всё равно не мог согреться. 2Тогда слуги сказали ему:

– Пусть господину нашему царю подыщут молодую девушку, чтобы она прислуживала царю и заботилась о нём. Она будет ложиться рядом с тобой, и господину нашему царю будет тепло.

3Они стали искать красивую девушку по всему Исроилу, нашли шунемитянку Авишаг и привели её к царю. 4Девушка была очень красива, она заботилась о царе и ухаживала за ним, но царь не имел с ней близости.

Адония претендует на престол

5Адония, сын Довуда от Хаггиты, кичливо говорил:

– Я буду царём.

Он завёл у себя колесницы и коней1:5 Или: «колесничих»; или: «всадников»., и пятьдесят слуг, которые бежали перед ним. 6(А его отец никогда не задавал ему вопроса: «Почему ты так поступаешь?» Адония родился после Авессалома и был очень красив.)

7Адония сговорился с Иоавом, сыном Церуи, и со священнослужителем Авиатаром, и они поддержали его. 8Но священнослужитель Цадок, Беная, сын Иодая, пророк Нафан, Шимей, Рей и личная стража Довуда не встали на сторону Адонии.

9Адония принёс в жертву овец, волов и откормленных телят у камня Зохелет, что рядом с Ен-Рогелом, и пригласил всех своих братьев, сыновей царя, и всех царских приближённых из Иудеи, 10но не пригласил ни пророка Нафана, ни Бенаю, ни личную стражу Довуда, ни своего брата Сулаймона.

Довуд передаёт престол Сулаймону

11Тогда пророк Нафан спросил у Вирсавии, матери Сулаймона:

– Разве ты не слышала, что Адония, сын Хаггиты, стал царём, а наш господин Довуд о том и не знает? 12Так вот, позволь мне посоветовать тебе, как спасти свою жизнь и жизнь твоего сына Сулаймона. 13Сейчас же пойди к царю Довуду и скажи ему: «Господин мой царь, разве ты не клялся мне, твоей рабыне, говоря: „Твой сын Сулаймон непременно будет царём после меня и сядет на моём престоле“? Так почему же царём стал Адония?» 14Когда ты ещё будешь говорить с царём, я войду вслед за тобой и подтвержу твои слова.

15И Вирсавия пошла к престарелому царю в его комнату, где ему прислуживала шунемитянка Авишаг. 16Вирсавия склонилась и поклонилась царю.

– Чего ты хочешь? – спросил царь.

17Она сказала ему:

– Мой господин, ты сам клялся мне, твоей рабыне, Вечным1:17 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусо и народу Исроила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь., твоим Богом: «Сулаймон, твой сын, будет царём после меня и сядет на моём престоле». 18Но вот царём стал Адония, а ты, господин мой царь, и не знаешь об этом. 19Он принёс в жертву множество волов, откормленных телят и овец, пригласил всех царских сыновей, священнослужителя Авиатара и военачальника Иоава, но не пригласил твоего раба Сулаймона. 20Господин мой царь, взоры всего Исроила устремлены на тебя, чтобы ты объявил им, кто сядет на престоле господина моего царя после тебя. 21Ведь иначе, как только господин мой царь упокоится со своими предками, меня и моего сына Сулаймона сочтут изменниками.

22Когда она ещё говорила с царём, вошёл пророк Нафан. 23Царю доложили:

– Пришёл пророк Нафан.

Тогда Нафан предстал перед царём и поклонился ему лицом до земли.

24Он сказал:

– Говорил ли ты, господин мой царь, что Адония будет царём после тебя и сядет на твоём престоле? 25Сегодня он пошёл и принёс в жертву множество волов, откормленных телят и овец. Он пригласил всех царских сыновей, военачальников и священнослужителя Авиатара. Сейчас они едят и пьют с ним и говорят: «Да здравствует царь Адония!» 26Но меня, твоего раба, священнослужителя Цадока, Бенаю, сына Иодая, и твоего раба Сулаймона он не пригласил. 27Было ли это сделано по воле господина моего царя, который не известил своих рабов о том, кто сядет на престоле моего господина царя после него?

28Тогда царь Довуд сказал:

– Позовите ко мне Вирсавию.

Она вошла к царю и предстала перед ним.

29И царь поклялся:

– Верно, как и то, что жив Вечный, Который избавил меня от всякой беды, – 30я непременно исполню сегодня то, о чём я клялся тебе Вечным, Богом Исроила: Сулаймон, твой сын, станет царём после меня и сядет на моём престоле вместо меня.

31Вирсавия склонилась лицом до земли, поклонилась царю и сказала:

– Пусть господин мой царь Довуд живёт вечно!

32Довуд сказал:

– Позовите ко мне священнослужителя Цадока, пророка Нафана и Бенаю, сына Иодая.

Когда они вошли к царю, 33он сказал им:

– Возьмите с собой моих слуг, посадите моего сына Сулаймона на моего мула и доставьте его к источнику Гихон. 34Там пусть священнослужитель Цадок и пророк Нафан помажут1:34 Посредством обряда помазания человек посвящался на определённое служение. Такого помазания удостаивались пророки, цари и священнослужители. его в цари над Исроилом. Трубите в рог и восклицайте: «Да здравствует царь Сулаймон!» 35Потом проводите его назад, и пусть он сядет на мой престол и правит вместо меня. Я поставил его правителем над Исроилом и Иудеей.

36Беная, сын Иодая, ответил царю:

– Аминь!1:36 Аминь – еврейское слово, которое переводится как «да, верно, воистину так» или «да будет так». Да скажет так Вечный, Бог господина моего царя! 37Как Вечный был с господином моим царём, так пусть он будет и с Сулаймоном, чтобы возвеличить его престол больше, чем престол господина моего царя Довуда!

38И священнослужитель Цадок, пророк Нафан, Беная, сын Иодая, керетиты и пелетиты1:38 Керетиты и пелетиты – чужеземные наёмники, которые, возможно, были царскими телохранителями. пошли, усадили Сулаймона на мула царя Довуда и сопроводили его в Гихон. 39Священнослужитель Цадок взял из священного шатра рог с маслом и помазал Сулаймона. После этого затрубили в рога, и весь народ закричал:

– Да здравствует царь Сулаймон!

40И весь народ пошёл вслед за ним, играя на свирелях и радуясь, да так, что земля сотрясалась от шума.

Сулаймон щадит Адонию

41Адония и все гости, которые были с ним, услышали это в конце пира. Услышав звук рога, Иоав спросил:

– Что это за шум в городе?

42Он ещё не договорил, как пришёл Ионафан, сын священнослужителя Авиатара. Адония сказал:

– Подойди. Ты достойный человек и, конечно, несёшь добрые вести.

43– Нет, – ответил Ионафан Адонии. – Наш господин, царь Довуд, сделал царём Сулаймона. 44Царь отправил его со священнослужителем Цадоком, пророком Нафаном, Бенаей, сыном Иодая, и керетитами и пелетитами, и они усадили его на царского мула, 45а священнослужитель Цадок и пророк Нафан помазали его в цари в Гихоне. Они ушли оттуда в радости, и город пришёл в движение. Этот-то шум ты и слышишь. 46Больше того, Сулаймон сел на царский престол, 47а царские приближённые пришли поздравлять господина нашего царя Довуда, говоря: «Пусть твой Бог прославит имя Сулаймона ещё больше, чем твоё, и возвеличит его престол больше твоего престола!» А царь поклонился на постели 48и сказал так: «Хвала Вечному, Богу Исроила, Который дал мне сегодня увидеть на престоле моего преемника!»

49Тут все гости Адонии, задрожав от страха, поднялись и разбежались. 50А Адония, боясь Сулаймона, пошёл и схватился за рога жертвенника в священном шатре1:50 Человек, которому грозит смерть, мог просить о пощаде, взявшись за рога жертвенника, которые возвышались с каждого из его четырёх углов (см. 3 Цар. 1:50-53).. 51Сулаймону доложили:

– Адония боится царя Сулаймона и не отпускает рогов жертвенника. Он говорит: «Пусть царь Сулаймон даст мне сегодня клятву, что он не предаст своего раба мечу».

52Сулаймон ответил:

– Если он покажет себя достойным человеком, то ни один волос с его головы не упадёт на землю, но если в нём обнаружится зло, он умрёт.

53Царь Сулаймон послал людей за Адонией, и они привели его от жертвенника. Адония вошёл и поклонился царю Сулаймону, и Сулаймон сказал:

– Ступай домой.