1 Atesalonika 5 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Atesalonika 5:1-28

Tsiku la Ambuye

1Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni, 2chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku. 3Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.

4Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala. 5Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima. 6Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga. 7Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku. 8Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa. 9Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 10Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi. 11Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.

Malangizo Otsiriza

12Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani. 13Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake. 14Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense. 15Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.

16Kondwerani nthawi zonse. 17Pempherani kosalekeza. 18Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

19Musazimitse moto wa Mzimu Woyera. 20Musanyoze mawu a uneneri. 21Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino. 22Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.

23Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu. 24Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.

25Abale, mutipempherere. 26Perekani moni wachikondi kwa onse. 27Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.

28Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.

Slovo na cestu

1. Tesalonickým 5:1-28

Buď připraven: nikdo neví, kdy se Pán vrátí

1Kdy se to má stát? O tom skutečně nemusím nic říkat, milí bratři, 2vždyť sami dobře víte, že to nikdo neví. Ta chvíle přijde nečekaně jako zloděj v noci. 3Až si lidé budou říkat „všechno je v pořádku, žádné nebezpečí nehrozí“, tehdy zčista jasna dopadne na ně zkáza, jako porodní bolesti přepadají rodičku. Nikdo neunikne, nikdo se neschová. 4Ale vy, bratři, netápejte ve tmách. Vás Kristův příchod nepřekvapí jako zloděj. 5Vy jste děti světla a dne, ne děti noci a temnoty. 6Buďte tedy bdělí a nespěte jako ostatní, čekejte a buďte střízliví. 7Noc je čas spáčů a opilců. 8Ale my, kdo žijeme ve světle, zůstaňme střízliví, chráněni pancířem víry a lásky a přilbou radostné naděje záchrany.

9Nás přece Bůh neurčil k tomu, abychom propadli jeho soudu, ale abychom byli zachráněni zásluhou našeho Pána, Ježíše Krista: 10on za nás zemřel, abychom s ním mohli žít věčně, ať už se jeho příchodu dožijeme či nikoliv. 11Tak se vzájemně povzbuzujte a pomáhejte si, jak jste to dělali doposud.

Základní tóny křesťanského života

12Milí bratři, važte si svých představených v církvi, kteří se pro vás namáhají a napomínají vás. 13Mějte je ve zvláštní úctě a lásce, vždyť vám slouží. A mezi sebou se nehádejte. 14Neukázněné a líné napomínejte, malomyslné povzbuzujte, ujímejte se slabých a se všemi mějte trpělivost. 15Křivdy neoplácejte, prokazujte dobro sobě navzájem i ostatním. 16Buďte radostnými lidmi. 17Neochabujte v modlitbách. 18Za všech okolností děkujte Bohu, neboť to očekává ode všech, kdo patří Ježíši Kristu.

19Nepřekážejte působení Božího Ducha 20a nezlehčujte jeho poselství. 21-22Bedlivě však posuzujte vše, co se za Boží slovo vydává, a přijímejte jen to, co odpovídá Písmu. Co mu odporuje, není dobré a s tím nic nemějte.

23Prosíme Boha, který nám dává svůj pokoj, aby vás přivedl k dokonalosti a celou vaši bytost – ducha, duši i tělo – zachoval bez úhony až do dne, kdy přijde Pán Ježíš Kristus. 24Bůh, který vás přijal za své děti, to pro vás jistě učiní, jak sám slíbil.

25Bratři, i vy se za nás modlete. 26Obejměte za nás všechny spoluvěřící. 27A všem dejte tento dopis přečíst, je to mé přání a vaše povinnost před Pánem.

28Nechť vám Ježíš Kristus všem bohatě žehná.

Váš Pavel