1 Atesalonika 5 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Atesalonika 5:1-28

Tsiku la Ambuye

1Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni, 2chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku. 3Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.

4Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala. 5Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima. 6Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga. 7Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku. 8Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa. 9Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 10Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi. 11Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.

Malangizo Otsiriza

12Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani. 13Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake. 14Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense. 15Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.

16Kondwerani nthawi zonse. 17Pempherani kosalekeza. 18Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

19Musazimitse moto wa Mzimu Woyera. 20Musanyoze mawu a uneneri. 21Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino. 22Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.

23Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu. 24Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.

25Abale, mutipempherere. 26Perekani moni wachikondi kwa onse. 27Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.

28Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.

Nova Versão Internacional

1 Tessalonicenses 5:1-28

1Irmãos, quanto aos tempos e épocas, não precisamos escrever 2pois vocês mesmos sabem perfeitamente que o dia do Senhor virá como ladrão à noite. 3Quando disserem: “Paz e segurança”, a destruição virá sobre eles de repente, como as dores de parto à mulher grávida; e de modo nenhum escaparão.

4Mas vocês, irmãos, não estão nas trevas, para que esse dia os surpreenda como ladrão. 5Vocês todos são filhos da luz, filhos do dia. Não somos da noite nem das trevas. 6Portanto, não durmamos como os demais, mas estejamos atentos e sejamos sóbrios; 7pois os que dormem, dormem de noite, e os que se embriagam, embriagam-se de noite. 8Nós, porém, que somos do dia, sejamos sóbrios, vestindo a couraça da fé e do amor e o capacete da esperança da salvação. 9Porque Deus não nos destinou para a ira, mas para recebermos a salvação por meio de nosso Senhor Jesus Cristo. 10Ele morreu por nós para que, quer estejamos acordados quer dormindo, vivamos unidos a ele. 11Por isso, exortem-se e edifiquem-se uns aos outros, como de fato vocês estão fazendo.

Instruções Finais

12Agora pedimos a vocês, irmãos, que tenham consideração para com os que se esforçam no trabalho entre vocês, que os lideram no Senhor e os aconselham. 13Tenham-nos na mais alta estima, com amor, por causa do trabalho deles. Vivam em paz uns com os outros. 14Exortamos vocês, irmãos, a que advirtam os ociosos5.14 Ou insubordinados, confortem os desanimados, auxiliem os fracos, sejam pacientes para com todos. 15Tenham cuidado para que ninguém retribua o mal com o mal, mas sejam sempre bondosos uns para com os outros e para com todos.

16Alegrem-se sempre. 17Orem continuamente. 18Deem graças em todas as circunstâncias, pois esta é a vontade de Deus para vocês em Cristo Jesus.

19Não apaguem o Espírito. 20Não tratem com desprezo as profecias, 21mas ponham à prova todas as coisas e fiquem com o que é bom. 22Afastem-se de toda forma de mal.

23Que o próprio Deus da paz os santifique inteiramente. Que todo o espírito, a alma e o corpo de vocês sejam preservados irrepreensíveis na vinda de nosso Senhor Jesus Cristo. 24Aquele que os chama é fiel e fará isso.

25Irmãos, orem por nós.

26Saúdem todos os irmãos com beijo santo.

27Diante do Senhor, encarrego vocês de lerem esta carta a todos os irmãos.

28A graça de nosso Senhor Jesus Cristo seja com vocês.