1 Atesalonika 5 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Atesalonika 5:1-28

Tsiku la Ambuye

1Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni, 2chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku. 3Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.

4Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala. 5Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima. 6Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga. 7Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku. 8Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa. 9Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 10Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi. 11Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.

Malangizo Otsiriza

12Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani. 13Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake. 14Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense. 15Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.

16Kondwerani nthawi zonse. 17Pempherani kosalekeza. 18Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

19Musazimitse moto wa Mzimu Woyera. 20Musanyoze mawu a uneneri. 21Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino. 22Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.

23Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu. 24Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.

25Abale, mutipempherere. 26Perekani moni wachikondi kwa onse. 27Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.

28Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.

New International Version – UK

1 Thessalonians 5:1-28

The day of the Lord

1Now, brothers and sisters, about times and dates we do not need to write to you, 2for you know very well that the day of the Lord will come like a thief in the night. 3While people are saying, ‘Peace and safety’, destruction will come on them suddenly, as labour pains on a pregnant woman, and they will not escape.

4But you, brothers and sisters, are not in darkness so that this day should surprise you like a thief. 5You are all children of the light and children of the day. We do not belong to the night or to the darkness. 6So then, let us not be like others, who are asleep, but let us be awake and sober. 7For those who sleep, sleep at night, and those who get drunk, get drunk at night. 8But since we belong to the day, let us be sober, putting on faith and love as a breastplate, and the hope of salvation as a helmet. 9For God did not appoint us to suffer wrath but to receive salvation through our Lord Jesus Christ. 10He died for us so that, whether we are awake or asleep, we may live together with him. 11Therefore encourage one another and build each other up, just as in fact you are doing.

Final instructions

12Now we ask you, brothers and sisters, to acknowledge those who work hard among you, who care for you in the Lord and who admonish you. 13Hold them in the highest regard in love because of their work. Live in peace with each other. 14And we urge you, brothers and sisters, warn those who are idle and disruptive, encourage the disheartened, help the weak, be patient with everyone. 15Make sure that nobody pays back wrong for wrong, but always strive to do what is good for each other and for everyone else.

16Rejoice always, 17pray continually, 18give thanks in all circumstances; for this is God’s will for you in Christ Jesus.

19Do not quench the Spirit. 20Do not treat prophecies with contempt 21but test them all; hold on to what is good, 22reject every kind of evil.

23May God himself, the God of peace, sanctify you through and through. May your whole spirit, soul and body be kept blameless at the coming of our Lord Jesus Christ. 24The one who calls you is faithful, and he will do it.

25Brothers and sisters, pray for us.

26Greet all God’s people with a holy kiss.

27I charge you before the Lord to have this letter read to all the brothers and sisters.

28The grace of our Lord Jesus Christ be with you.