1 Atesalonika 5 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Atesalonika 5:1-28

Tsiku la Ambuye

1Tsono abale, za nthawi ndi nyengo yake nʼkosafunikira kuti tikulembereni, 2chifukwa mukudziwa bwino lomwe kuti tsiku la Ambuye lidzafika ngati mbala usiku. 3Pamene anthu akunena kuti, “Mtendere ndi chitetezo,” chiwonongeko chidzafika pa iwo mwadzidzidzi, monga zowawa za amayi pobereka, ndipo sadzathawa.

4Koma inu abale, simuli mu mdima kuti tsiku limeneli lidzakudzidzimutseni ngati mbala. 5Nonse ndinu ana a kuwunika ndi ana a usana. Sindife anthu a usiku kapena mdima. 6Chomwecho tsono, tisafanane ndi ena amene akugona koma tikhale maso ndi odzisunga. 7Pakuti amene akugona, amagona usiku, ndi amene amaledzera, amaledzera usiku. 8Koma popeza ndife a usana, tikhale odzisunga, titavala chikhulupiriro ndi chikondi ngati chovala pachifuwa, ndi chiyembekezo cha chipulumutso ngati chipewa. 9Pakuti Mulungu sanatisankhe kuti tikavutike ndi mkwiyo koma kuti tilandire chipulumutso kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 10Iye anatifera ndi cholinga chakuti, kaya tili ndi moyo kapena tagona, tikhale naye pamodzi. 11Choncho limbikitsanani wina ndi mnzake ndi kuthandizana kukula mu mzimu, monga momwe mukuchitira.

Malangizo Otsiriza

12Tsopano tikukupemphani abale kuti muziwalemekeza amene akugwira ntchito pakati panu, amene amakuyangʼanirani mwa Ambuye ndi amene amakulimbikitsani. 13Muziwachitira ulemu kwambiri mwachikondi chifukwa cha ntchito yawo. Mukhale pa mtendere wina ndi mnzake. 14Ndipo tikukupemphani abale, muwachenjeze amene akungokhala osagwira ntchito, alimbikitseni amanyazi, thandizani ofowoka ndipo muzilezera mtima aliyense. 15Onetsetsani kuti wina asabwezere choyipa kwa omuchitira choyipa koma nthawi zonse yesetsani kukhala okoma mtima kwa wina ndi mnzake; ndiponso ndi kwa anthu ena onse.

16Kondwerani nthawi zonse. 17Pempherani kosalekeza. 18Yamikani mu zonse, pakuti ichi ndi chifuniro cha Mulungu kwa inu mwa Khristu Yesu.

19Musazimitse moto wa Mzimu Woyera. 20Musanyoze mawu a uneneri. 21Yesani zinthu zonse. Gwiritsitsani chimene ndi chabwino. 22Mupewe choyipa cha mtundu wina uliwonse.

23Mulungu mwini, Mulungu wamtendere, akuyeretseni kotheratu. Mzimu wanu wonse, moyo ndi thupi zisungidwe zopanda cholakwa mpaka kubwera kwa Ambuye athu Yesu Khristu. 24Amene anakuyitanani ndi wokhulupirika ndipo Iye adzachita zimenezi.

25Abale, mutipempherere. 26Perekani moni wachikondi kwa onse. 27Pamaso pa Ambuye ndikulamula kuti kalatayi iwerengedwe kwa abale onse.

28Chisomo cha Ambuye athu Yesu Khristu chikhale nanu.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרת פולוס הראשונה אל-התסלוניקים 5:1-28

1אחים יקרים, איני צריך לכתוב לכם מתי כל זה יתרחש, 2כי הלא יודעים אתם שאיש אינו יודע את המועד. יום ה׳ יבוא במפתיע – כגנב בלילה.

3כאשר בני־האדם יחיו בשלווה ויחשבו שלא יקרה דבר, יירד עליהם האסון במפתיע, כיולדת שאינה יודעת מתי יתקפוה צירי הלידה, ואיש לא יוכל לברוח.

4אבל אתם, אחים יקרים, אינכם שרויים בחשכה בכל הנוגע לדברים אלה, ולכן יום ה׳ לא יפתיע אתכם כגנב. 5כולכם בני־האור ובני־היום; אינכם בני־הלילה ואינכם שייכים לחושך. 6משום כך עמדו על המשמר! אל תירדמו כמו האחרים, אלא צפו לבואו בשקידה ובערנות, 7כי אלה שנרדמים נרדמים בלילה והשיכורים משתכרים בלילה. 8אולם אנחנו בני אור־היום, ועל כן נישאר ערים ומפוכחים, מוגנים על־ידי אמונתנו ואהבתנו וחוסים בתקווה הנפלאה של ישועתנו.

9אלוהים לא בחר בנו כדי לשפוך את זעמו עלינו, אלא כדי להושיענו על־ידי אדוננו ישוע המשיח, 10אשר מת בעדנו למען נחיה איתו לנצח, בין אם נהיה חיים או מתים בשובו. 11לכן המשיכו לעודד ולבנות איש את אחיו כפי שעשיתם עד כה.

12אחים יקרים, אנו מבקשים מכם לכבד את האחראים עליכם מטעם הקהילה, כי אלוהים מינה אותם להשגיח עליכם ולהוכיח אתכם בעת הצורך. 13עליכם להעריך את העבודה שהם עושים למענכם ולאהוב אותם, שכן הם משתדלים לעזור לכם. זכרו, חיו בשלום זה עם זה.

14אחים יקרים, הזהירו את העצלנים שביניכם, עודדו את הפוחדים, חזקו את החלשים והיו סבלנים עם כולם. 15אל תניחו לאיש לשלם רעה תחת רעה, אלא עזרו תמיד איש לאחיו ולכל אדם. 16שמחו תמיד באמונתכם. 17התמידו בתפילה. 18הודו לאלוהים על כל דבר, כי זהו רצון אלוהים מכל המאמינים במשיח.

19אל תבלמו ואל תכלאו את רוח הקודש. 20לעולם אל תזלזלו במה שנאמר בשם ה׳. 21בחנו כל דבר והאמינו רק במה שטוב, ישר ואמיתי. 22התרחקו מכל מעשה רע. 23ואלוהי השלום יטהר ויקדש אתכם לעצמו, וישמור את רוחכם, נפשכם וגופכם בריאים וללא־חטא, עד יום שובו של אדוננו ישוע המשיח. 24אתם יכולים לסמוך על האלוהים אשר בחר בכם שימלא את כל הבטחותיו.

25אחים יקרים, התפללו בעדנו. 26דרשו בשלום כל האחים בנשיקה הקדושה. 27בשם ישוע המשיח אדוננו אני משביע אתכם שתקראו מכתב זה באוזני כל המאמינים.

28חסד אדוננו ישוע המשיח עם כל אחד ואחד מכם. – אמן.