1 Atesalonika 4 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Atesalonika 4:1-18

Moyo Wokondweretsa Mulungu

1Potsiriza, abale, tinakulangizani kale momwe mukuyenera kukhalira kuti mukondweretse Mulungu, monga momwe mukukhaliramo. Tsopano tikukupemphani ndi kukulimbikitsani mwa Ambuye Yesu kuti muchite zimenezi koposa kale. 2Inu mukudziwa malangizo amene tinakupatsani mwa ulamuliro wa Ambuye Yesu.

3Ndi chifuniro cha Mulungu kuti muyeretsedwe: kuti mupewe dama; 4aliyense wa inu aphunzire kulamulira thupi lake mʼnjira yoyera ndi yaulemu, 5osati yotsata chilakolako chonyansa monga amachitira akunja, amene sadziwa Mulungu. 6Pa zimenezi munthu asachimwire mʼbale wake kapena kumuonerera. Ambuye adzalanga anthu onse amene amachita machimo amenewa, monga tinakuwuzani kale ndi kukuchenjezani. 7Pakuti Mulungu sanatiyitane kuti tizichita zonyansa, koma kuti tikhale oyera mtima. 8Choncho, aliyense amene akukana malangizo awa sakukana munthu koma Mulungu, Mulungu weniweniyo amene amakupatsani Mzimu Woyera.

9Tsono kunena za kukondana wina ndi mnzake, nʼkosafunikira kuti tikulembereni, popeza ndi Mulungu amene anakuphunzitsani za kukondana wina ndi mnzake. 10Ndipo kunena zoona, mumakonda abale onse a mʼbanja la Mulungu a ku Makedoniya. Komabe, abale tikukulimbikitsani kuti muzichita zimenezi koposa kale.

11Yesetsani kuti mukhale moyo wofatsa. Aliyense asamale ntchito yakeyake ndi kugwira ntchito ndi manja ake. 12Mukatero akunja adzalemekeza makhalidwe anu a tsiku ndi tsiku, ndi kuti inuyo mukhale osadalira wina aliyense.

Kubweranso kwa Ambuye

13Abale, ife sitikufuna mukhale osadziwa za amene akugona, kapena kumva chisoni ngati anthu ena opanda chiyembekezo. 14Ife timakhulupirira kuti Yesu anamwalira naukanso. Moteronso timakhulupirira kuti amene anamwalira ali mwa Yesu, Mulungu adzawaukitsa nʼkubwera nawo pamodzi ndi Yesuyo. 15Molingana ndi mawu a Ambuye mwini, tikukuwuzani kuti, ife amene tikanali ndi moyo, otsala mpaka kubwera kwa Ambuye, sitidzawasiya kumbuyo amene anagona kale. 16Pakuti Ambuye mwini adzatsika kuchokera kumwamba, ndi mfuwu waulamuliro, ndi liwu la mngelo wamkulu, ndi kulira kwa lipenga la Mulungu, ndipo akufa amene ali mwa Yesu adzauka poyamba. 17Kenaka, ife amene tili ndi moyo, otsalafe, tidzakwatulidwa pamodzi ndi iwo mʼmitambo kukakumana ndi Ambuye mlengalenga. Tsono ife tidzakhala ndi Ambuye mpaka muyaya. 18Nʼchifukwa chake tsono muzilimbikitsana ndi mawu amenewa.

Knijga O Kristu

1 Solunjanima 4:1-18

Život ugodan Bogu

1Na koncu, draga braćo i sestre, zaklinjemo vas u imenu Gospodina Isusa da živite životom ugodnim Bogu kao što smo vas poučili. Vi već tako i živite. Napredujte i dalje. 2Znate zapovijedi koje smo vam dali u ime Gospodina Isusa. 3Bog želi da budete sveti i čisti, da se uzdržavate od grijeha bluda. 4Tako će svatko od nas znati nadzirati svoje tijelo4:4 U grčkome: znati kako posjedovati svoju posudu. u svetosti i časti, 5a ne živjeti u strasti i pohoti poput pogana koji ne poznaju Boga.

6Nikada u tomu ni u čemu drugome ne varajte svojega brata kršćanina jer Gospodin se za to osvećuje, kao što sam vas već upozorio. 7Jer nas Bog nije pozvao da živimo pokvarenim, već čistim životom. 8Tko odbacuje ove zapovijedi, ne odbacuje čovjeka, nego Boga koji vam daje svojega Svetog Duha.

9O bratskoj ljubavi koja mora vladati među Božjim narodom ne moram vam ni pisati jer vas je sam Bog poučio da volite jedni druge. 10Vi zaista iskazujete veliku ljubav braći u cijeloj Makedoniji. Molimo vas ipak, draga braćo, da u tome još više napredujete. 11Trudite se mirno živjeti, baviti se svojim poslom i raditi vlastitim rukama, kako smo vam zapovjedili. 12Tako ćete časno živjeti pred nevjernicima i nitko vam neće trebati novčano pomagati.

Nada uskrsnuća

13Želim, braćo i sestre, da znate što će se dogoditi s umrlim kršćanima, da ne tugujete kao drugi koji nemaju nade. 14Vjerujemo da je Isus umro i uskrsnuo te da će Bog, kad Isus opet dođe, s Isusom dovesti i kršćane koji su usnuli u Isusu.

15Govorim vam ovo poučen izravno od Gospodina: oni od nas koji još budu živi kad se Gospodin vrati, neće preteći umrle. 16Sam će Gospodin sići s neba na zapovijed, na glas arhanđela, na zov Božje trublje. Najprije će uskrsnuti umrli u Kristu. 17Zatim će oni od nas koji još budu živi biti uzneseni u vis, na oblake, u susret Gospodinu, da s njime zauvijek ostanu. 18Tješite se međusobno tim riječima.