1 Atesalonika 3 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Atesalonika 3:1-13

1Nʼchifukwa chake pamene sitinathenso kupirira, tinaganiza kuti kunali bwino kuti atisiye tokha ku Atene. 2Tinatuma Timoteyo, mʼbale wathu ndi mnzathu wogwira naye ntchito ya Mulungu yofalitsa Uthenga Wabwino wa Khristu, kuti adzakulimbitseni mitima ndi kukukhazikitsani mʼchikhulupiriro chanu, 3ndi cholinga chakuti wina asasunthike ndi mavutowa. Inu mukudziwa bwino lomwe kuti ndife oyenera kukumana ndi zimenezi. 4Kunena zoona, pamene tinali nanu, tinkakuwuzani kuti tidzayenera kuzunzidwa. Ndipo monga mukudziwa bwino, zimenezi zinachitikadi. 5Nʼchifukwa chake, pamene sindikanathanso kupirira, ndinatuma Timoteyo kuti adzaone mmene chikhulupiriro chanu chilili. Ndinkaopa kuti mwina wonyengayo, wakunyengani mʼnjira ina yake ndi kuti ntchito zathu zasanduka zosapindula.

Nkhani Yolimbikitsa Kuchokera kwa Timoteyo

6Koma tsopano Timoteyo wabwera kuchokera kwanuko ndipo watibweretsera nkhani yabwino ya chikhulupiriro chanu ndi chikondi chanu. Iye watiwuzanso kuti masiku onse mumatikumbukira mokondwa, ndipo kuti mumafunitsitsa kutionanso, monga momwe ifenso timalakalakira kukuonani inuyo. 7Motero abale, mʼmasautso ndi mʼmazunzo athu onse, chikhulupiriro chanu chatilimbikitsa. 8Ife tsopano tili moyodi, pakuti mukuyima molimbika mwa Ambuye. 9Tingathe bwanji kuyamika Mulungu mokwanira poona chimwemwe chonse chimene tili nacho pamaso pa Mulungu wathu chifukwa cha inu? 10Usana ndi usiku timapemphera ndi mtima wonse kuti tionanenso nanu, ndi kukwaniritsa zimene zikusowa pa chikhulupiriro chanu.

11Tikupempha kuti Mulungu ndi Atate athu mwini, ndi Ambuye athu Yesu, atikonzere njira yabwino kuti tidzafike kwanuko. 12Ambuye achulukitse chikondi chanu ndi kuti chisefukire kwa wina ndi mnzake ndiponso kwa wina aliyense, monga momwe chikondi chathu chichitira kwa inu. 13Iye alimbikitse mitima yanu kuti mukhale opanda cholakwa ndi oyera mtima pamaso pa Mulungu ndi Atate athu pamene Ambuye athu Yesu akubwera ndi oyera ake onse.

Slovo na cestu

1. Tesalonickým 3:1-13

Dobré zprávy vždy potěší a povzbudí

1-2Když se mi po vás v Aténách stýskalo, rozhodl jsem se poslat Timotea, toho milého bratra a Božího spoluslužebníka. Měl vás navštívit a povzbudit vaši víru, 3abyste v pronásledování nezakolísali. 4Trpět patří ke křesťanskému údělu; to jsme vám přece říkali už od začátku, a tak nebuďte překvapeni, když k tomu opravdu dochází.

5Proto jsem tehdy poslal Timotea k vám, abych se tu nemusel trápit úzkostí, jestli vás protivník přece jen nedostal na svou návnadu a nepřivedl všechnu naši práci vniveč. 6Teď se však právě Timoteus vrátil s dobrými zprávami, že jste ve víře ani v lásce nepolevili, že na nás stále myslíte a toužíte po novém setkání stejně jako my. 7-8A tak nás při všech těch trampotách tady potěšily zprávy o vaší věrnosti Pánu. Vydržíme všechno, jen když víme, že s vaší vírou je vše v pořádku. 9Jak se Bohu odvděčit za všechnu tu radost, jakou z vás máme? 10Dnem i nocí vroucně prosíme, abychom vás mohli znovu spatřit a podle potřeby upevnit vaši víru. 11Přejeme si, aby nám Bůh, náš Otec, a Ježíš, náš Pán, připravili cestu k vám! 12Ať dá bohatě růst vaší lásce navzájem i navenek, stejně jako naší lásce k vám. 13Ať vás vnitřně posílí, abyste se mohli bezúhonní a dokonalí postavit před Boha, našeho Otce, až se náš Pán, Ježíš Kristus, vrátí se všemi svými.