1 Akorinto 16 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 16:1-24

Ndalama Zothandizira Akhristu a ku Yerusalemu

1Tsopano za zopereka zothandiza anthu a Ambuye a ku Yerusalemu. Muchite zomwe ndinawuza mipingo ya ku Galatiya kuti ichite. 2Pa tsiku loyamba la sabata lililonse, aliyense wa inu azipatula ndalama molingana ndi zomwe wapezera. Asunge, kuti ndikabwera pasadzakhalenso msonkhamsonkha. 3Pamenepo, ndikadzafika, ndidzawapatsa makalata a umboni anthu amene mudzawasankhe ndi kuwatuma kuti akapereka mphatso zanu ku Yerusalemu. 4Ngati kutaoneka kuti nʼkoyenera kuti ndipite nawo, adzapita nane limodzi.

Paulo Afotokoza za Maulendo ake ndi Zina

5Ndidzafika kwanuko nditadutsa ku Makedoniya pakuti ndikuyembekezera kudzera ku Makedoniyako. 6Mwina ndidzakhala nanu kanthawi kochepa kapenanso nyengo yonse yozizira, kuti mudzandithandize kupitiriza ulendo wanga kulikonse kumene ndingapite. 7Sindikufuna kuti ndikuoneni tsopano mongodutsa chabe, koma ndikuyembekezera kudzakhala nanu kwa kanthawi, ngati Ambuye alola. 8Koma ndikhala ndili ku Efeso mpaka nthawi ya Pentekosite, 9pakuti mwayi waukulu wapezeka woti nʼkugwira ntchito yaphindu, koma pali ambiri amene akutsutsana nane.

10Ngati Timoteyo afike kwanuko, onetsetsani kuti pasakhale zina zomuchititsa mantha pamene ali pakati panu, pakuti iye akugwira ntchito ya Ambuye monga ine. 11Wina aliyense asamunyoze. Muthandizeni kupitiriza ulendo wake mwamtendere kubwereranso kuli ine. Ndikumuyembekeza pamodzi ndi abale ena.

12Tsono kunena za mʼbale wathu, Apolo, ndinamuwumiriza kwambiri kuti abwere kwa inu abale, ndipo iye sanafune kupita tsopano. Koma akadzapeza mpata wabwino adzabwera.

13Khalani tcheru; khazikikani mʼchikhulupiriro chanu; limbani mtima; khalani amphamvu. 14Chitani zonse mwachikondi.

15Mukudziwa kuti a mʼbanja la Stefano ndiye anali oyamba kutembenuka mtima ku Akaya, ndipo akhala akudzipereka kutumikira oyera mtima. Choncho ndikukudandaulirani, inu abale, 16kuti muziwamvera anthu oterewa, ndiponso aliyense wogwira nawo ntchitoyi modzipereka. 17Ndikondwera kuti Stefano, Fortunato ndi Akayiko afika, chifukwa akhala akundithandiza pakuti inu simuli nane. 18Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu womwe. Anthu a mtundu oterewa ngofunika kuwalemekeza.

Mawu Otsiriza

19Mpingo wa mʼchigawo cha ku Asiya ukupereka moni. Akula ndi Prisila akuperekanso moni wachisangalalo, mwa Ambuye, ndiponso mpingo umene umakumana mʼnyumba mwawo ukupereka moni. 20Abale onse kuno akupereka moni wawo. Patsanani moni wachikondi chenicheni.

21Ineyo Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa mawu awa akuti moni.

22Ngati wina sakonda Ambuye akhale wotembereredwa. Maranatha! (Ambuye athu bwerani)!

23Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi inu.

24Chikondi changa chikhale ndi nonsenu mwa Khristu Yesu.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

哥林多前書 16:1-24

捐助聖徒

1至於捐款幫助聖徒這件事,你們可以照我吩咐加拉太各教會的方法辦理。 2每逢週日,各人應按照自己的收入抽出一部分留起來,免得我到的時候才現湊。 3我到了以後,會差遣你們委託的人帶著推薦信把你們的捐款送到耶路撒冷4如果我也需要去的話,他們可以跟我一起去。

保羅的計劃

5我正打算從馬其頓經過,過了馬其頓,我就去探望你們。 6我也許會和你們住一段時期,甚至在你們那裡過冬。之後,我無論去什麼地方,你們都可以給我送行。 7我不想只是現在順道探望你們,主若許可,我盼望能夠和你們同住一段時期。 8我會在以弗所停留到五旬節, 9因為大門為我敞開了,工作很有成效,不過反對我的人也很多。

10提摩太到了以後,你們要好好接待他,讓他在你們那裡安心,因為他和我一樣,都是在為主做工。 11所以誰也不許輕視他。你們要幫助他平安地回到我這裡,我正在等候他和弟兄們同來。 12至於亞波羅弟兄,我雖然再三勸他和弟兄們去你們那裡,但他目前還不願啟行。不過他有機會就會去。

勸勉與問候

13你們要警醒,在信仰上堅定不移,做勇敢剛強的人。 14無論做什麼事,都要有愛心。

15弟兄姊妹,你們都知道司提法納一家在亞該亞是最早信主的16·15 最早信主的」希臘文是「最早的果子」。,也知道他們怎樣盡心竭力地服侍聖徒。 16你們要順服這樣的人,也要順服所有同心努力服侍的人。 17我很高興司提法納福徒拿都亞該古來我這裡,因為你們幫不到我的地方,他們都補足了。 18他們使我和你們心裡都感到十分欣慰,你們要敬重這樣的人。

19亞細亞的各教會問候你們。亞居拉百基拉夫婦和常在他們家裡聚會的信徒,奉主的名衷心地向你們問安。 20全體弟兄姊妹都問候你們。你們要以聖潔的吻彼此問候。

21保羅親筆問候你們。

22如果有人不愛主,這人可咒可詛!主啊,我願你來!

23願主耶穌基督的恩典與你們同在! 24我在基督耶穌裡愛你們所有的人。阿們!