1 Akorinto 11 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 11:1-34

1Tsatirani chitsanzo changa, monga inenso nditsatira chitsanzo cha Khristu.

Makhalidwe Oyenera pa Mapemphero

2Ndikukuyamikani chifukwa chondikumbukira pa zonse ndiponso posunga ziphunzitso monga ndinakuphunzitsirani. 3Tsopano ndikufuna muzindikire kuti Khristu ndiye mutu wa munthu aliyense, ndipo mwamuna ndiye mutu wamkazi, ndipo mutu wa Khristu ndi Mulungu. 4Mwamuna aliyense wopemphera kapena kunenera ataphimba mutu wake akunyoza mutu wakewo. 5Ndipo mkazi aliyense wopemphera kapena kunenera asanaphimbe mutu wake sakulemekeza mutu wakewo. Kuli chimodzimodzi kumeta mutu wake. 6Ngati mkazi saphimba kumutu kwake, ndiye kuti amete tsitsi lake. Ngati nʼchamanyazi kwa mkazi kungoyepula kapena kumeta mpala, ndiye kuti aphimbe kumutu kwake.

7Mwamuna sayenera kuphimba kumutu popeza ndi chifaniziro ndi ulemerero wa Mulungu; pamene mkazi ndi ulemerero wa mwamuna. 8Pakuti mwamuna sachokera kwa mkazi, koma mkazi kwa mwamuna. 9Ndipo mwamuna sanalengedwe chifukwa cha mkazi, koma mkazi analengedwera mwamuna. 10Pa chifukwa ichi, ndiponso pa chifukwa cha angelo, mkazi akuyenera kukhala ndi chizindikiro cha ulamuliro wake. 11Komabe mwa Ambuye, mkazi amadalira mwamuna ndipo mwamuna amadalira mkazi. 12Pakuti monga mkazi anachokera kwa mwamuna, momwemonso mwamuna anabadwa mwa mkazi. Koma zonse zichokera kwa Mulungu.

13Dziweruzeni. Kodi nʼchabwino kuti mkazi apemphere kwa Mulungu wopanda chophimba kumutu? 14Kodi chikhalidwe chathu sichitiphunzitsa kuti nʼchamanyazi kuti mwamuna akhale ndi tsitsi lalitali, 15koma mkazi akakhala ndi tsitsi lalitali ndi ulemerero wake? Pakuti mkazi anapatsidwa tsitsi lalitali monga chophimba kumutu. 16Ngati wina akufuna kutsutsapo pa zimenezi, ife ndiponso mipingo ya Mulungu tilibe machitidwe ena apadera koma ndi omwewa.

Mgonero wa Ambuye

17Koma popereka malangizo awa sindikufuna kukuyamikirani popeza mʼmisonkhano yanu mumachita zoyipa kuposa zabwino. 18Choyamba, ndikumva kuti mukasonkhana mu mpingo mumasankhana ndipo ndikukhulupirira kuti zimenezi kwinaku nʼzoona. 19Nʼzosakayikitsa kuti pali kugawikana pakati panu kuti adziwike amene ndi ovomerezeka ndi Mulungu. 20Tsono, mukasonkhana pamodzi, chimene mumadya si Mgonero wa Ambuye. 21Pakuti mukamadya, aliyense amangodzidyera zomwe anakonza. Wina amakhala ndi njala pamene wina amaledzera. 22Kodi mulibe nyumba zanu kumene mungamadyere ndi kumwa? Kapena mumapeputsa mpingo wa Mulungu ndi kuchititsa manyazi amene alibe kalikonse? Ndikunena chiyani kwa inu? Moti ndikuyamikireni pa zimenezi? Ayi, pa zinthu izi sindingakuyamikireni.

23Pakuti zimene ndinalandira kwa Ambuye ndi zomwe ndinakupatsani. Ambuye Yesu, usiku umene anaperekedwa uja, anatenga buledi. 24Atayamika ndi kumunyema ananena kuti, “Ili ndi thupi langa lomwe laperekedwa kwa inu; muzichita zimenezi pokumbukira Ine.” 25Chimodzimodzi, atatha kudya, anatenga chikho, nati, “Chikho ichi ndi pangano latsopano la magazi anga; imwani nthawi zonse pokumbukira Ine.” 26Pakuti nthawi zonse pamene mudya bulediyu ndikumwa chikhochi, mukulalikira imfa ya Ambuye mpaka Iye adzabweranso.

27Chifukwa chake, aliyense amene adya buledi kapena kumwa chikho cha Ambuye mʼnjira yosayenera adzachimwira thupi ndi magazi a Ambuye. 28Munthu adzisanthule yekha asanadye buledi kapena kumwa chikhochi. 29Popeza aliyense amene adya kapena kumwa mosazindikira thupi la Ambuye, amadya ndi kumwa chiweruzo chake chomwe. 30Nʼchifukwa chake pakati panu ambiri mwa inu ndi ofowoka ndi odwala, ndipo ambirinso agona tulo. 31Koma tikanadziyesa tokha sitikaweruzidwanso. 32Pamene tiweruzidwa ndi Ambuye, ndiye kuti akukonza khalidwe lathu kupewa kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi anthu osakhulupirira.

33Ndiye tsono abale anga, pamene musonkhana pa chakudya, mudikirirane. 34Ngati wina ali ndi njala, adye ku nyumba kwake kuti pamene musonkhana pamodzi zisafike poti muweruzidwe nazo.

Ndipo ndikabwera ndidzakupatsani malangizo ena owonjezera.

Słowo Życia

1 Koryntian 11:1-34

1Naśladujcie więc mnie, tak jak ja naśladuję Chrystusa.

Nakrywanie głowy przez kobiety

2Tak się cieszę, przyjaciele, że pamiętacie wszystko, czego was nauczyłem, i przestrzegacie tego. 3Wiedzcie jednak, że głową męża jest Chrystus, głową żony—mąż, a głową Chrystusa—Bóg. 4Dlatego jeśli mężczyzna modli się albo prorokuje z nakrytą głową, przynosi wstyd swojej głowie. 5Jeśli zaś kobieta publicznie modli się albo prorokuje z odkrytą głową, również przynosi wstyd swojej głowie, wygląda bowiem tak, jakby nie miała włosów. 6Jeśli nie chce nakrywać głowy, niech zetnie włosy. A skoro wstydzi się to zrobić, niech postępuje zgodnie ze zwyczajem i nakrywa głowę. 7Mąż natomiast nie powinien nakrywać głowy. Jest bowiem obrazem Boga, przynoszącym Mu chwałę, żona zaś jest obrazem męża. 8To nie mężczyzna powstał z kobiety, ale ona z niego. 9I nie mąż został stworzony dla żony, ale żona dla męża. 10Dlatego żona powinna nosić nakrycie głowy—ze względu na aniołów.

11Przed Panem jednak ani żona, ani mąż nie są niezależni od siebie, 12bo chociaż pierwsza kobieta pochodzi od mężczyzny, to jednak każdy mężczyzna rodzi się z kobiety—a wszyscy pochodzą od Boga. 13Sami zresztą oceńcie: Czy wypada kobiecie publicznie modlić się do Boga z odkrytą głową? 14Długie włosy u mężczyzny są czymś sprzecznym z naturą i przynoszą mu wstyd. 15Kobiecie zaś—wręcz przeciwnie, dodają urody, bo zostały jej dane jako nakrycie głowy. 16Takie zasady panują we wszystkich kościołach, nie ma więc sensu sprzeczać się o te rzeczy.

Wieczerza Pańska

17Przekazując te zalecenia, chciałbym poruszyć jeszcze jedną sprawę. Nie mogę was pochwalić za to, że wasze wspólne spotkania zamiast przynosić pożytek, wyrządzają szkodę. 18Usłyszałem bowiem—i po części temu wierzę—że gdy zbieracie się jako kościół, dochodzi wśród was do podziałów. 19Zresztą musi dojść do podziałów, bo stanowią one próbę wiary.

20Wasze spotkania nie mają nic wspólnego z prawdziwą Wieczerzą Pańską. 21Każdy spożywa bowiem własny posiłek. Niektórzy są jednak głodni, a inni—pijani. 22Czy nie możecie się najeść i napić w domu? Czemu lekceważycie kościół Boga i upokarzacie biednych, których nie stać na to, aby przynieść coś do jedzenia? Co ja mam z wami zrobić? Pochwalić? Za to na pewno was nie pochwalę!

23To, co przekazałem wam na temat Wieczerzy, otrzymałem od samego Pana. On, tej nocy, której został zdradzony, wziął chleb, 24podziękował za niego Bogu, połamał na kawałki i powiedział do uczniów: „Jedzcie! To jest moje ciało, które oddaję za was. Czyńcie to pamiętając o Mnie”. 25Po posiłku podał im kielich z winem i rzekł: „Ten kielich jest nowym przymierzem, które przypieczętuję przelewając własną krew. Pijcie z niego pamiętając o Mnie”. 26Zawsze więc, gdy spożywacie ten chleb i pijecie z tego kielicha, ogłaszacie śmierć Pana! Tak będzie aż do czasu Jego powrotu.

27Jeśli więc ktoś niegodnie spożywa chleb i niegodnie pije z kielicha Pana, grzeszy przeciwko Jego ciału i krwi. 28Dlatego każdy, kto sięga po ten chleb i kielich, niech osądzi swoje serce. 29Ten bowiem, kto uczestnicząc w Wieczerzy lekceważy ciało Chrystusa, ściąga na siebie Boży sąd. 30Z tego właśnie powodu jest wśród was wielu słabych i chorych, a niektórzy nawet umarli. 31Jeśli jednak będziecie osądzać swoje serca, ominie was ta kara. 32A gdy Pan nas osądza i karze, czyni to po to, abyśmy nie zostali potępieni wraz z całym światem. 33Zatem, moi przyjaciele, przychodząc na Wieczerzę Pańską, czekajcie na siebie nawzajem. 34Jeśli ktoś jest bardzo głodny, niech się naje w domu. Nie pozwólcie, aby z powodu waszych spotkań dotknęła was Boża kara. O pozostałych sprawach powiem wam, gdy do was przybędę.