1 Akorinto 10 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

1 Akorinto 10:1-33

Chenjezo Kuchokera Mʼmbiri ya Israeli

1Pakuti sindikufuna kuti inu mukhale osadziwa zenizeni, abale, kuti makolo athu anatsogozedwa ndi mtambo ndikuti onse anawoloka nyanja. 2Ndipo onse anabatizidwa mwa Mose mu mtambo ndi mʼnyanja. 3Onse anadya chakudya chimodzi chauzimu 4ndipo anamwa chakumwa chimodzi chauzimu; popeza anamwa kuchokera mʼthanthwe lomwe anayenda nalo, ndipo thanthwe limeneli linali Khristu. 5Ngakhale zinali choncho, Mulungu sanakondwere ndi ambiri a iwo, motero ambiri mwa iwo anafera mʼchipululu.

6Tsono zinthu izi zinachitika kuti zikhale chitsanzo, kuti ife tisayike mitima yathu pa zinthu zoyipa monga anachitira makolo athuwo. 7Musakhale anthu opembedza mafano, monga analili ena mwa iwo. Pakuti zalembedwa kuti, “Anthuwo anakhala pansi nayamba kudya ndi kumwa. Kenaka anayimirira nayamba kuvina mwachilendo.” 8Tisachite chigololo monga ena mwa iwo anachitira ndipo tsiku limodzi anafapo anthu 23,000. 9Tisamuyese Khristu, monga ena mwa iwo anachitira ndipo anaphedwa ndi njoka. 10Ndipo osamawiringula, monga ena mwa iwo anachitira naphedwa ndi mngelo wowononga.

11Zinthu izi zinawachitikira kuti zikhale chitsanzo ndipo zinalembedwa kuti zikhale chenjezo kwa ife, amene tiyandikira nthawi ya kutha kwa zonse. 12Choncho, ngati mukuganiza kuti mwayima mwamphamvu, samalani mungagwe! 13Palibe mayesero amene mwakumana nawo oposa amene anthu ena onse anakumana nawo. Mulungu ngokhulupirika; sadzalola kuti inu muyesedwe koposa muyeso umene mutha kupirira. Koma pamene mwayesedwa, Iyenso adzakupatsani njira yopambanira mayeserowo.

Maphwando a Mafano ndi Mgonero wa Ambuye

14Choncho abwenzi anga okondedwa, lekani kupembedza mafano. 15Ndikuyankhula kwa a anthu anzeru zawo, nokha muweruze pa zimene ndikunenazi. 16Pamene tidalitsa chikho cha Mgonero wa Ambuye, mothokoza Mulungu, kodi sitikugawana magazi a Khristu? Nanga buledi amene timanyemayo, kodi sitikugawana thupi la Khristu? 17Pakuti buledi ndi mmodzi yekha, ifenso ngakhale tili ambiri, ndife thupi limodzi, popeza tonse timagawana buledi mmodzi yemweyo.

18Taganizirani zimene amachita Aisraeli. Kodi onse amene amadya zoperekedwa nsembe, samachita nawo miyambo ya pa guwapo? 19Kodi ndikutanthauza kuti nsembe zoperekedwa kwa mafano ndi kanthu konse, kapena kuti mafano ndi kanthu konse? 20Ayi. Nsembe za osakhulupirira zimaperekedwa kwa ziwanda, osati kwa Mulungu, ndipo sindikufuna kuti muziyanjana ndi ziwandazo. 21Simungamwe chikho cha Ambuye, ndi kukamweranso chikho cha ziwanda. Simungadyere pa tebulo la Ambuye ndiponso la ziwanda. 22Kodi tikufuna kuwutsa mkwiyo wa Ambuye? Kodi ndife amphamvu kuposa Iye?

Ufulu wa Munthu Wokhulupirira

23Mutha kunena kuti, “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zili za phindu. “Zinthu zonse nʼzololedwa,” komatu si zonse zimathandiza. 24Munthu aliyense asafunefune zokomera iye yekha, koma zokomeranso ena.

25Idyani nyama iliyonse imene amagulitsa pa msika, osafunsa mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu. 26Popeza kuti, “Dziko lapansi ndi la Ambuye ndi zonse za mʼmenemo ndi zake.”

27Ngati wosakhulupirira akuyitanani kuti mukadye naye, inuyo ndi kuvomera kupitako, mukadye chilichonse chimene akakupatseni ndipo musakafunse mafunso okhudzana ndi chikumbumtima chanu. 28Koma ngati wina akuwuzani kuti, “Izi zaperekedwa nsembe,” musadye zimenezo, pofuna kuthandiza amene wakuwuzaniyo komanso chifukwa cha chikumbumtima. 29Ndikunena za chikumbumtima cha winayo osati chanu. Tsono mungafunse kuti, nʼchifukwa chiyani ufulu wanga ukuphwanyidwa chifukwa cha chikumbumtima cha munthu wina? 30Ngati ndikuyamika Mulungu chifukwa cha chakudya, nanga munthu angandinyoze bwanji pa zinthu zomwe ndayamikira nazo Mulungu?

31Nʼchifukwa chake chilichonse mungadye kapena kumwa, kapena chimene mungachite, chitani zonse ku ulemerero wa Mulungu. 32Musakhumudwitse aliyense, kaya ndi Myuda, Mgriki, kapena mpingo wa Mulungu. 33Mu zonse ndikuyesetsa kukondweretsa aliyense mʼnjira iliyonse. Popeza sindikufunafuna zokondweretsa ine ndekha koma zokomera ambiri kuti apulumutsidwe.

Słowo Życia

1 Koryntian 10:1-33

Ostrzeżenia płynące z historii Izraela

1Przyjaciele, przypomnijcie sobie pewne fakty: Kiedyś na pustyni nasi przodkowie byli prowadzeni przez obłok i wszyscy przeszli przez Morze Czerwone. 2Wszyscy, wraz z Mojżeszem, zostali zanurzeni w obłoku i w morzu. 3Wszyscy spożywali ten sam duchowy pokarm 4i pili ten sam duchowy napój. Czerpali bowiem wodę z towarzyszącej im duchowej skały, którą był sam Chrystus. 5Mimo to większość z nich nie znalazła uznania w oczach Boga i zginęła na pustyni.

6Powinno to być dla nas przestrogą, abyśmy, tak jak oni, nie dążyli do zła. 7Nie oddawajcie czci bożkom—jak tamci. Pismo przecież mówi, że oddając cześć złotemu cielcowi „zasiedli do jedzenia i picia, a potem wstali, aby tańczyć”. 8Nie ulegajmy rozwiązłości seksualnej—jak tamci, gdy jednego dnia zginęło dwadzieścia trzy tysiące osób. 9Nie róbmy testów na wiarygodność Chrystusa—jak oni robili i poginęli z powodu jadowitych węży. 10I nie narzekajcie na Boga—jak oni narzekali i zginęli, porażeni przez anioła śmierci. 11Wszystko, co ich spotkało, stanowi ostrzeżenie i zostało zapisane dla nas, żyjących u progu końca czasów. Jest to przestroga dla nas. 12Dlatego ten, kto sądzi, że stoi, niech uważa, żeby nie upadł. 13Pokusy, których doświadczacie, są normalną i ludzką rzeczą. Ale Bóg jest wierny i nie pozwoli, abyście byli kuszeni ponad wasze siły. Dopuszczając pokusę, pokaże wam również drogę wyjścia, abyście mogli wyjść z niej cało.

Kult bożków a Wieczerza Pańska

14Kochani, unikajcie wszystkiego, co ma jakikolwiek związek z kultem bożków. 15Wiem, że jesteście mądrzy, więc sami oceńcie moje słowa: 16Czy kielich z winem, za który dziękujemy podczas Wieczerzy Pańskiej, nie wyraża naszego udziału we krwi Chrystusa? A wspólnie łamany chleb? Czy nie wyraża naszej jedności jako Jego ciała? 17Wszyscy dzielimy się przecież jednym chlebem, bo choć jest nas wielu, stanowimy jedno ciało. 18Zwróćcie uwagę na przykład Izraela: Ci, którzy spożywają pokarm ofiarowany na ołtarzu świątyni, jednoczą się w ten sposób ze świątynią Boga.

19Czy chcę przez to powiedzieć, że pogańskie bóstwa lub ofiary składane im mają jakieś znaczenie? Absolutnie nie! 20Chcę tylko pokazać wam, że ofiary te w rzeczywistości składane są demonom, a nie Bogu. Ja zaś nie chciałbym, abyście mieli z nimi cokolwiek wspólnego. 21Nie możecie jednocześnie pić z kielicha Pana i z kielicha demonów! Nie możecie również zasiadać za stołem Pana i za stołem demonów! 22Czy mamy pobudzać Pana do zazdrości o nas? Czy jesteśmy od Niego mocniejsi?

Wolność wierzącego

23Wszystko jest dozwolone, ale nie wszystko przynosi korzyść. Wszystko nam wolno, ale nie wszystko wzmacnia naszą wiarę. 24Nie bądźcie egoistami—dbajcie o dobro innych!

25Kupujcie takie mięso, jakie jest w sprzedaży. Dla spokoju sumienia nie pytajcie, czy było ono ofiarowane bożkom. 26„Do Pana należy bowiem ziemia i wszystko, co na niej żyje”.

27Jeśli zostaniecie zaproszeni przez kogoś, kto nie wierzy Jezusowi, i chcecie skorzystać z jego gościny, jedzcie wszystko, czym was poczęstuje, dla spokoju sumienia nie pytając o pochodzenie pokarmu. 28Ale gdyby ktoś was ostrzegł, mówiąc: „Te pokarmy były przecież ofiarowane bożkom!”, nie jedzcie—ze względu na tego człowieka i sumienie. 29Mówię oczywiście o jego sumieniu, nie waszym. Dlaczego bowiem czyjeś sumienie miałoby ograniczać moją wolność? 30Jeśli dzięki łasce Boga mogę coś zjeść i dziękuję Mu za ten pokarm, to dlaczego ktoś miałby mnie potępiać?

31Tak więc, jeśli jecie, pijecie lub czynicie cokolwiek innego, zawsze róbcie to tak, aby oddawać chwałę Bogu. 32Nie doprowadzajcie do upadku ani Żydów, ani pogan, ani kogokolwiek, kto należy do kościoła Boga. 33Postępujcie tak, jak ja, który zabiegam o dobro innych ludzi i nie szukam własnej korzyści. Staram się bowiem, aby inni mogli dostąpić zbawienia.