Genesis 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Genesis 1:1-31

Chiyambi cha Chilengedwe

1Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi. 2Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.

3Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi. 4Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima. 5Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.

6Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.” 7Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi. 8Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.

9Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi. 10Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.

11Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi. 12Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino. 13Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.

14Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka; 15zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.” 16Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi. 17Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi, 18kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino. 19Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.

20Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.” 21Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino. 22Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.” 23Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.

24Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi. 25Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.

26Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”

27Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.

Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu;

analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.

28Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”

29Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu. 30Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.

31Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

New Russian Translation

Бытие 1:1-31

Сотворение мира

1В начале сотворил Бог небо и землю1:1 Или: «Когда Бог начал творить небо и землю, земля была»; или: «В начале, когда Бог сотворил небо и землю».. 2Земля была безлика и пуста, тьма была над бездной, и Дух Божий парил над водами1:2 Или: «и дыхание Божье проносилось над водами»; или: «и мощный ветер проносился над водами»..

3Бог сказал: «Да будет свет», и появился свет. 4Бог увидел, что свет хорош, и отделил его от тьмы. 5Бог назвал свет днем, а тьму – ночью. Был вечер, и было утро – день первый.

6И сказал Бог: «Да будет свод между водами, чтобы отделить воду от воды». 7Бог создал свод и отделил воду под сводом от воды над ним, и стало так. 8Бог назвал свод небом. Был вечер, и было утро – день второй.

9И сказал Бог: «Да соберутся вместе воды под небом, и да появится суша», и стало так. 10Бог назвал сушу землей, а собранные воды назвал морями. И увидел Бог, что это хорошо.

11«Да произведет земля растительность: растения с их семенами и различные виды деревьев на земле, которые приносят плод с семенем внутри», – сказал Бог, и стало так. 12Земля произвела растительность: разные виды растений, приносящих семя, и все виды деревьев, приносящих плод с семенем внутри. И Бог увидел, что это хорошо. 13Был вечер, и было утро – день третий.

14И Бог сказал: «Да будут светила на небесном своде, чтобы отделять день от ночи, и пусть они служат знаками, чтобы различать времена, дни и годы, 15и пусть они будут светильниками на небесном своде, чтобы светить на землю». И стало так. 16Бог создал два великих светила – большое светило, чтобы управлять днем, и малое светило, чтобы управлять ночью, а также Он создал звезды. 17Бог поместил их на небесном своде, чтобы они светили на землю, 18управляли днем и ночью и отделяли свет от тьмы. Бог увидел, что это хорошо. 19Был вечер, и было утро – день четвертый.

20Бог сказал: «Да наполнится вода живностью, и да полетят над землей по небосводу птицы». 21Бог создал огромных морских чудищ, разные виды движущейся живности, кишащей в воде, и разные виды крылатых птиц. И увидел Бог, что это хорошо. 22Бог благословил их и сказал: «Плодитесь и размножайтесь, наполняйте воды в морях, и пусть птицы множатся на земле». 23Был вечер, и было утро – день пятый.

24И сказал Бог: «Да произведет земля разные виды живности: скот, пресмыкающихся и диких зверей», и стало так. 25Бог создал разные виды диких зверей и скота и все виды пресмыкающихся. И увидел Он, что это хорошо.

26Потом Бог сказал: «Создадим человека1:26 Или: «человеческий род»; евр.: «адам». – Наш образ и Наше подобие, – пусть он царствует над рыбами морскими и птицами небесными, над скотом, над всей землей1:26 В одном из древних переводов: «над всеми дикими зверями». и над всеми пресмыкающимися».

27Так Бог сотворил человека по образу Своему,

по образу Божьему Он сотворил его;

мужчиной и женщиной Он сотворил их.

28Бог благословил их и сказал: «Плодитесь и размножайтесь; наполняйте землю и владейте ею. Царствуйте над рыбами морскими, и птицами небесными, и над всеми пресмыкающимися».

29Затем Бог сказал: «Я даю вам все растения с семенами по всей земле и все деревья, дающие плод с семенем внутри; они будут вам в пропитание. 30И всем зверям земным, и всем птицам небесным, и всем пресмыкающимся – всем, в ком дышит жизнь, – Я даю в пищу всякую зелень». И стало так.

31Бог посмотрел на все, что Он создал, и все было очень хорошо. Был вечер, и было утро – день шестой.