馬太福音 8 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

馬太福音 8:1-34

痲瘋病痊癒

1耶穌下山的時候,有許多人跟著。 2有一個患痲瘋病的人跑來跪在祂跟前,說:「主啊,如果你肯,一定能使我潔淨。」

3耶穌伸手摸他,說:「我肯,你潔淨了吧!」那人的痲瘋病就立刻潔淨了。

4耶穌對他說:「不要把這事告訴別人,要去讓祭司查看你的身體,並且照摩西的規定獻祭,向眾人證明你已經潔淨了。」

百夫長的信心

5耶穌到了迦百農,一個百夫長前來向祂求助,說: 6「主啊,我的僕人癱瘓,躺在家裡,非常痛苦。」

7耶穌說:「我這就去醫治他。」

8百夫長說:「主啊,我不配讓你親自來我家。你只要說一句話,我僕人就會痊癒。 9因為我有上司,也有部下。我命令我的部下去,他就去;要他來,他就來。我吩咐僕人做什麼事,他一定照辦。」

10耶穌聽了,感到驚奇,便對跟隨祂的人說:「我實在告訴你們,我在以色列從未見過信心這麼大的人。 11我告訴你們,將來有許多從東從西來的人會在天國與亞伯拉罕以撒雅各一同歡宴。 12但那些本應承受天國的人反會被趕出去,在黑暗裡哀哭切齒。」

13耶穌對百夫長說:「你回去吧!就照你所信的給你成就。」就在那時候,他的僕人便痊癒了。

治病趕鬼

14耶穌來到彼得家,看見彼得的岳母正在發燒,躺在床上。 15耶穌一摸她的手,燒就退了。她便起來服侍耶穌。

16當天晚上,有人帶著許多被鬼附身的人來見耶穌。耶穌一句話就把鬼趕出去了,並醫好了所有的病人。 17這是要應驗以賽亞先知的話:「祂擔當了我們的軟弱,背負了我們的疾病。」

跟從耶穌的代價

18耶穌看到人群圍著祂,就吩咐門徒渡到湖對岸。 19這時,有一位律法教師上前對耶穌說:「老師,無論你往哪裡去,我都要跟從你。」

20耶穌說:「狐狸有洞,飛鳥有窩,人子卻沒有安枕之處。」

21另一個門徒對耶穌說:「主啊,請讓我先回去安葬我的父親。」 22耶穌對他說:「跟從我,讓死人去埋葬他們的死人吧!」

平靜風浪

23耶穌上了船,門徒也跟著祂上了船。 24忽然,湖面上狂風大作,波濤洶湧,船快要被巨浪吞沒,耶穌卻在睡覺。

25門徒連忙叫醒耶穌,說:「主啊,救命!我們快淹死了!」

26耶穌答道:「你們的信心太小了,為什麼害怕呢?」於是祂起來斥責風和浪,風浪就完全平靜了。

27門徒很驚奇,說:「祂究竟是什麼人?連風浪都聽祂的!」

治好兩個被鬼附身的人

28耶穌到了對岸加大拉8·28 加大拉」即格拉森地區。人的地方,有兩個被鬼附身的人從墳地裡出來見祂。他們非常凶惡,沒有人敢從那裡經過。 29他們喊著說:「上帝的兒子啊!我們和你有什麼關係?時候還沒有到,你就來叫我們受苦嗎?」

30當時,有一大群豬在附近吃食。 31鬼就哀求耶穌:「如果你要趕我們出去,就讓我們進入豬群吧!」

32耶穌說:「去吧!」

於是,鬼從那二人身上出來,進入豬群,整群豬就一路奔下陡坡,衝進湖裡淹死了。 33放豬的人逃進城,把事情的經過以及被鬼附身者的遭遇告訴了城裡的人。 34於是,全城的人都出來見耶穌,見到後,便請求祂離開那地方。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 8:1-34

Yesu Achiritsa Wakhate

1Iye atatsika ku phiri kuja, anthu ambirimbiri anamutsata. 2Ndipo munthu wakhate anadza kwa Yesu namugwadira nati, “Ambuye, ngati mufuna, mukhoza kundiyeretsa.”

3Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” Nthawi yomweyo anachiritsidwa khate lake. 4Ndipo Yesu anati kwa iye, “Taona, usawuze wina aliyense. Koma upite kwa mkulu wa ansembe ukadzionetse wekha ndi kupereka mphatso imene Mose analamulira, kuti ukhale umboni kwa iwo.”

Chikhulupiriro cha Kenturiyo

5Yesu atalowa mʼKaperenamu, Kenturiyo anabwera kwa Iye napempha chithandizo, 6nati, “Ambuye, wantchito wanga ali chigonere ku nyumba, sakuthanso kuyenda, akumva kuwawa kwambiri.”

7Ndipo Yesu anati kwa iye, “Ine ndibwera kudzamuchiritsa.”

8Kenturiyo uja anayankha kuti, “Ambuye, ndine wosayenera kuti Inu mukalowe mʼnyumba mwanga. Koma mungonena mawu ndipo wantchito wanga adzachiritsidwa. 9Pakuti inenso ndili pansi pa ulamuliro ndipo ndili ndi asilikali amene ndiwalamulira. Ndikalamulira mmodzi kuti, ‘Pita,’ amapita; ndi kwa wina kuti, ‘Bwera,’ amabwera. Ndikawuza wantchito wanga kuti, ‘Chita ichi,’ iye amachita.”

10Yesu atamva zimenezi, anadabwa ndipo anati kwa omutsatira, “Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti sindinapeze wina aliyense mu Israeli wachikhulupiriro chachikulu chotere. 11Ndikuwuzani kuti ambiri adzabwera kuchokera kummawa ndi kumadzulo, nadzakhala nawo pa phwando pamodzi ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo mu ufumu wakumwamba. 12Koma eni ake ufumuwo adzaponyedwa ku mdima wakunja kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”

13Pamenepo Yesu anati kwa Kenturiyo, “Pita! Zichitike monga momwe wakhulupirira.” Ndipo wantchito wake anachira pa nthawi yomweyo.

Yesu Achiritsa Anthu Ambiri

14Ndipo Yesu atalowa mʼnyumba ya Petro, anaona mpongozi wake wa Petro ali gone akudwala malungo. 15Ndipo Yesu anakhudza dzanja lake ndipo pomwepo anachira nayamba kumutumikira.

16Itafika nthawi yamadzulo, anthu anabweretsa kwa Iye anthu ambiri ogwidwa ndi ziwanda ndipo anatulutsa ziwandazo ndi mawu okha, nachiritsa odwala onse. 17Uku kunali kukwaniritsa zimene ananena mneneri Yesaya kuti,

“Iye anatenga zofowoka zathu,

nanyamula nthenda zathu.”

Za Kutsatira Yesu

18Yesu ataona gulu la anthu litamuzungulira, analamula kuti awolokere kutsidya lina la nyanja. 19Ndipo mphunzitsi wa malamulo anabwera kwa Iye nati, “Aphunzitsi, ine ndidzakutsatani kulikonse kumene muzipita.”

20Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ndi mbalame zamlengalenga zili ndi zisa, koma Mwana wa Munthu alibe malo ogona ngakhale potsamira mutu wake.”

21Wophunzira wina anati kwa Iye, “Ambuye, mundilole ndiyambe ndakayika maliro a abambo anga.”

22Koma Yesu anamuwuza kuti, “Nditsate Ine ndipo uwaleke akufa ayikane akufa okhaokha.”

Yesu Aletsa Namondwe

23Iye atalowa mʼbwato, ophunzira ake anamutsatira. 24Ndipo taonani mwadzidzidzi mphepo yayikulu yamkuntho inawomba pa nyanjapo, kotero kuti bwatolo linayamba kumizidwa ndi mafunde. Koma Yesu anali mtulo. 25Ophunzira ake anapita namudzutsa nati, “Ambuye! Tipulumutseni! Tikumira!”

26Iye anawayankha kuti, “Inu achikhulupiriro chochepa, chifukwa chiyani mukuchita mantha?” Ndipo anayimirira nadzudzula mphepoyo ndi mafunde ndipo panali bata lalikulu.

27Ndipo ophunzirawo anadabwa nafunsa kuti, “Ndi munthu wotani uyu? Kuti ngakhale mphepo ndi mafunde zimvera Iye!”

Ogwidwa ndi Ziwanda a ku Gadara

28Ndipo atafika ku mbali ina ya dera la Gadara, anakumana ndi anthu awiri ogwidwa ndi ziwanda akuchokera ku manda. Iwowa anali woopsa kwambiri kotero kuti panalibe munthu akanatha kudzera njira imeneyo. 29Ndipo iwo anafuwulira kwa Yesu nati, “Mukufuna chiyani kwa ife, Inu Mwana wa Mulungu? Kodi mwabwera kuno kudzatizunza nthawi yake isanafike?”

30Ndipo patali pake panali gulu la nkhumba zimene zimadya. 31Ndipo ziwandazo zinamupempha Yesu kuti, “Ngati mutitulutsa ife mutitumize mu nkhumba izo.”

32Iye anati kwa ziwandazo, “Pitani!” Ndipo pamenepo zinatuluka ndi kukalowa mʼnkhumbazo ndipo nkhumba zonse zinathamangira mʼnyanja ndi kufera momwemo. 33Koma amene amaziweta anathawa nalowa mʼmudzi nafotokoza zonse, kuphatikizapo zimene zinachitika ndi anthu ogwidwa ndi ziwanda aja. 34Ndipo anthu onse a mʼmudziwo anatuluka kukakumana ndi Yesu. Ndipo atamuona Iye, anamupempha kuti achoke mʼdera lawo.