馬太福音 15 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

馬太福音 15:1-39

傳統與誡命

1有幾個法利賽人和律法教師從耶路撒冷來質問耶穌: 2「為什麼你的門徒吃飯前不行洗手禮,破壞祖先的傳統呢?」

3耶穌回答說:「為什麼你們拘守傳統而違背上帝的誡命呢? 4上帝說,『要孝敬父母』,又說,『咒罵父母的,必被處死。』 5你們卻說,『人如果把供養父母的錢奉獻給上帝, 6他就不必供養父母。』你們這是用傳統來廢掉上帝的誡命。 7你們這些偽君子,以賽亞指著你們說的預言一點沒錯,

8『這些人嘴上尊崇我,

心卻遠離我,

9他們的教導無非是人的規條,

他們敬拜我也是枉然。』」

10耶穌召集了眾人,對他們說:「你們要聽,也要明白。 11入口的東西不會使人污穢,從口中出來的才會使人污穢。」

12門徒上前對祂說:「你知道嗎?法利賽人聽見你的話很反感。」

13耶穌回答說:「凡不是我天父栽種的都要被連根拔起來。 14隨便他們吧!他們是瞎眼的嚮導。瞎子給瞎子領路,二人都會掉進坑裡。」

15彼得對耶穌說:「請給我們解釋一下這個比喻。」

16耶穌說:「你們還不明白嗎? 17豈不知入口的東西都是進到肚子裡,然後排泄到廁所裡嗎? 18可是,從口中出來的乃是發自內心,會使人污穢。 19因為從心裡出來的有惡念、謀殺、通姦、淫亂、偷盜、假見證和毀謗, 20這些東西才使人污穢。不洗手吃飯並不會使人污穢。」

迦南婦人的信心

21耶穌從那裡退到泰爾西頓境內。 22那地方有個迦南的婦人前來大聲懇求耶穌:「主啊!大衛的後裔啊!可憐我吧!我的女兒被鬼附身,受盡折磨!」 23耶穌卻一言不發。門徒上前求祂說:「請讓她走吧!她老是在後面喊叫。」

24耶穌說:「我奉差遣只是來尋找以色列家迷失的羊。」

25那婦人上前跪下,說:「主啊!求你幫幫我吧!」

26耶穌答道:「把兒女的食物丟給狗吃,不合適。」

27婦人說:「主啊,沒錯,可是狗也吃主人飯桌上掉下來的碎渣呀!」

28耶穌說:「婦人,你的信心真大!我答應你的要求。」就在那一刻,她女兒就好了。

耶穌使四千人吃飽

29耶穌離開那裡,來到加利利湖邊,上了山,在那裡坐下。 30大群的人把瘸子、瞎子、殘疾的、啞巴及許多別的病人帶來,放在祂腳前,祂就治好了他們。 31大家看見啞巴說話,殘疾的復原,瘸子走路,瞎子看見,都很驚奇,就讚美以色列的上帝。

32耶穌把門徒召集過來,對他們說:「我憐憫這些人,他們跟我在一起已經三天,沒有任何吃的。我不願讓他們餓著肚子回去,以免他們在路上體力不支。」

33門徒說:「在這荒野,我們到哪裡找足夠的食物給這麼多人吃呢?」

34耶穌問:「你們有多少餅?」

門徒答道:「七個,還有幾條小魚。」

35耶穌便吩咐大家坐在地上。 36祂拿著那七個餅和幾條魚祝謝後,掰開,遞給門徒,門徒再分給大家。 37大家都吃了,並且吃飽了,剩下的零碎裝滿了七個筐子。 38當時吃飯的,除了婦女和小孩,共有四千男人。 39隨後,耶穌叫眾人散去,自己坐船去了馬加丹地區。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 15:1-39

Miyambo ya Makolo

1Pamenepo Afarisi ena ndi aphunzitsi amalamulo anabwera kwa Yesu kuchokera ku Yerusalemu ndipo anamufunsa kuti, 2“Chifukwa chiyani ophunzira anu amaphwanya mwambo wa akuluakulu? Iwo sasamba mʼmanja pakudya!”

3Yesu anayankha kuti, “Nanga chifukwa chiyani inu mumaphwanya lamulo la Mulungu chifukwa cha mwambo wa makolo anu? 4Pakuti Mulungu anati, ‘Lemekeza abambo ako ndi amayi ako’ ndipo ‘aliyense amene atemberera abambo ake kapena amayi ake ayenera kuphedwa.’ 5Koma inu mumati, ngati munthu anena kwa abambo ake kapena amayi ake kuti, ‘Thandizo lililonse mukalirandira kuchokera kwa ine ndi mphatso yoperekedwa kwa Mulungu,’ 6iye sakulemekeza nayo abambo ake ndipo ndi khalidwe lotere inu mumapeputsa nalo Mawu a Mulungu chifukwa cha mwambo wanu. 7Inu anthu achiphamaso, Yesaya ananenera za inu kuti,

8“ ‘Anthu awa amandilemekeza Ine ndi milomo yawo,

koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.

9Amandilambira Ine kwachabe

ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.’ ”

10Yesu anayitana gulu la anthu nati, “Mverani ndipo zindikirani. 11Chimene chimalowa mʼkamwa mwa munthu sichimuchititsa kukhala woyipa, koma chimene chimatuluka mʼkamwa mwake, icho ndi chimene chimamuchititsa kukhala woyipa.”

12Pamenepo ophunzira anabwera kwa Iye ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukudziwa kuti Afarisi anakhumudwa pamene anamva mawu aja?”

13Iye anayankha kuti, “Mbewu iliyonse imene Atate anga akumwamba sanadzale idzazulidwa ndi mizu yomwe. 14Alekeni, ndi atsogoleri osaona. Ngati munthu wosaona atsogolera wosaona mnzake, onse awiri adzagwera mʼdzenje.”

15Petro anati, “Timasulireni fanizoli.”

16Yesu anawafunsa kuti, “Kani ngakhale inunso simumvetsa? 17Kodi inu simudziwa kuti chilichonse cholowa mʼkamwa chimapita mʼmimba ndipo kenaka chimatuluka kunja kwa thupi? 18Koma zinthu zimene zituluka mʼkamwa zimachokera mu mtima ndipo zimenezi zimamuchititsa munthu kukhala woyipa. 19Pakuti mu mtima mumatuluka maganizo oyipa, zakupha, zachigololo, zadama, zakuba, zaumboni wonama ndi zachipongwe. 20Izi ndi zimene zimachititsa munthu kukhala woyipa; koma kudya ndi mʼmanja mosasamba sikumuchititsa munthu kukhala woyipa.”

Mayi wa ku Kanaani

21Yesu atachoka kumalo amenewo anapita kudera la ku Turo ndi ku Sidoni. 22Mayi wa Chikanaani wochokera dera la komweko anabwera kwa Iye akulira, nati, “Ambuye, Mwana wa Davide, ndichitireni chifundo! Mwana wanga wamkazi akuzunzika kwambiri ndi chiwanda.”

23Yesu sanayankhe kanthu. Ndipo ophunzira ake anabwera namupempha Iye kuti, “Muwuzeni achoke chifukwa akulira mofuwula pambuyo pathu.”

24Iye anayankha kuti, “Ine ndinatumidwa kwa nkhosa zotayika za Israeli zokha.”

25Mayiyo anabwera ndi kugwada pamaso pake, nati, “Ambuye ndithandizeni!”

26Iye anayankha kuti, “Sibwino kutenga chakudya cha ana ndi kuponyera agalu.”

27Mayiyo anati, “Inde Ambuye. Komatu ngakhale agalu amadya nyenyeswa zimene zimagwa kuchokera pa tebulo la mbuye wawo.”

28Pomwepo Yesu anayankha kuti, “Mayi iwe uli ndi chikhulupiriro chachikulu! Pempho lako lamveka.” Ndipo mwana wake wamkazi anachira nthawi yomweyo.

Yesu Adyetsa Anthu 4,000

29Yesu anachoka kumeneko napita mʼmbali mwa nyanja ya Galileya. Ndipo anakwera ku phiri nakhala pansi. 30Gulu lalikulu la anthu linabwera kwa Iye ndi anthu olumala, osaona, ofa ziwalo, osayankhula ndi ena ambiri nawagoneka pa mapazi ake ndipo Iye anawachiritsa. 31Anthu ataona osayankhula akuyankhula, ofa ziwalo akuchira, olumala miyendo akuyenda ndi osaona akuona anadabwa kwambiri. Ndipo analemekeza Mulungu wa Israeli.

32Yesu anayitana ophunzira ake nati, “Ndili ndi chifundo ndi anthu awa; akhala kale ndi Ine masiku atatu ndipo alibe chakudya. Ine sindifuna kuti apite kwawo ndi njala chifukwa angakomoke pa njira.”

33Ophunzira anayankha kuti, “Ndikuti kumene tingakapeze buledi mʼtchire muno okwanira kudyetsa gulu lotere?”

34Yesu anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati?”

Iwo anayankha kuti, “Asanu ndi awiri ndi tinsomba pangʼono.”

35Iye anawuza gululo kuti likhale pansi. 36Kenaka anatenga malofu asanu ndi awiri aja ndi tinsombato ndipo atayamika anagawa napatsa ophunzira ake ndipo iwo anagawira anthuwo. 37Onse anadya ndipo anakhuta. Pomaliza ophunzira anatolera zotsalira nadzaza madengu asanu ndi awiri. 38Chiwerengero cha anthu amene anadya chinali 4,000 kupatula amayi ndi ana. 39Yesu atatha kuwuza gululo kuti lipite kwawo, analowa mʼbwato ndipo anapita kudera la Magadala.