雅歌 2 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

雅歌 2:1-17

女子:

1我是沙崙平原的玫瑰花,

是谷中的百合花。

男子:

2我的愛人在眾少女中,

就像荊棘中的一朵百合花。

女子:

3我的良人在眾男子中,

好像林中的一棵蘋果樹。

我歡歡喜喜地坐在他的樹蔭下,

輕嚐他香甜無比的果子。

4他帶我走進宴席大廳,

眾人都看見他對我充滿柔情愛意。

5請用葡萄乾來補充我的力氣,

用蘋果來提振我的精神,

因為我思愛成病。

6他的左手扶著我的頭,

他的右手緊抱著我。

7耶路撒冷的少女啊!

我指著羚羊和田野的母鹿2·7 羚羊和田野的母鹿」在希伯來文中與「萬軍之全能上帝」發音相似。吩咐你們,

不要叫醒或驚動愛情,

等它自發吧。

8聽啊!是我良人的聲音,

他攀過高崗,躍過山丘,

終於來了!

9我的良人好像羚羊和幼鹿。

看啊,他就在牆外,

正從窗戶往裡觀看,

從窗櫺間往裡窺視。

10他對我說:

「我的愛人,起來吧!

我的佳偶,跟我來!

11你看!冬天過去了,

雨水止住了。

12大地百花盛開,

百鳥爭鳴的季節已經來臨,

田野也傳來斑鳩的叫聲。

13無花果快成熟了,

葡萄樹也開滿了花,

散發著陣陣芬芳。

我的愛人,起來吧;

我的佳偶,跟我來。」

男子:

14我的鴿子啊,

你在岩石縫中,

在懸崖的隱秘處。

讓我看看你的臉,

聽聽你的聲音吧,

因為你的聲音溫柔,

你的臉龐秀麗。

15為我們抓住那些狐狸,

抓住那些破壞葡萄園的小狐狸吧,

因為我們的葡萄樹正在開花。

女子:

16我的良人屬於我,我也屬於他。

他在百合花間牧放羊群。

17我的良人啊,

涼風吹起、日影飛逝的時候,

但願你像比特山的羚羊和小鹿一樣快快回來。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 2:1-17

Mkazi

1Ine ndine duwa la ku Saroni,

duwa lokongola la ku zigwa.

Mwamuna

2Monga duwa lokongola pakati pa minga

ndi momwe alili wokondedwa wanga pakati pa atsikana.

Mkazi

3Monga mtengo wa apulosi pakati pa mitengo ya mʼnkhalango

ndi momwe alili bwenzi langa pakati pa anyamata.

Ndimakondwera kukhala pansi pa mthunzi wako,

ndipo chipatso chake ndi chokoma mʼkamwa mwanga.

4Iye wanditengera ku nyumba yaphwando,

ndipo mbendera yake yozika pa ine ndi chikondi.

5Undidyetse keke ya mphesa zowuma,

unditsitsimutse ndi ma apulosi,

pakuti chikondi chandifowoketsa.

6Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere,

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

7Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

8Tamverani bwenzi langa!

Taonani! Uyu akubwera apayu,

akulumphalumpha pa mapiri,

akujowajowa pa zitunda.

9Bwenzi langa ali ngati gwape kapena mwana wa mbawala.

Taonani! Uyo wayima kuseri kwa khoma lathulo,

akusuzumira mʼmazenera,

akuyangʼana pa mpata wa zenera.

10Bwenzi langa anayankha ndipo anati kwa ine,

“Dzuka bwenzi langa,

wokongola wanga, ndipo tiye tizipita.

11Ona, nyengo yozizira yatha;

mvula yatha ndipo yapitiratu.

12Maluwa ayamba kuoneka pa dziko lapansi;

nthawi yoyimba yafika,

kulira kwa njiwa kukumveka

mʼdziko lathu.

13Mtengo wankhuyu ukubereka zipatso zake zoyambirira;

mitengo ya mpesa ya maluwa ikutulutsa fungo lake.

Dzuka bwenzi langa, wokongola wanga

tiye tizipita.”

Mwamuna

14Nkhunda yanga yokhala mʼmingʼalu ya thanthwe,

mʼmalo obisala a mʼmbali mwa phiri,

onetsa nkhope yako,

nʼtamvako liwu lako;

pakuti liwu lako ndi lokoma,

ndipo nkhope yako ndi yokongola.

15Mutigwirire nkhandwe,

nkhandwe zingʼonozingʼono

zimene zikuwononga minda ya mpesa,

minda yathu ya mpesa imene yayamba maluwa.

Mkazi

16Bwenzi langa ndi wangadi ndipo ine ndine wake;

amadyetsa gulu lake la ziweto pakati pa maluwa okongola.

17Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira

ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,

unyamuke bwenzi langa,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena ngati mwana wa mbawala

pakati pa mapiri azigwembezigwembe.