雅各書 5 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

雅各書 5:1-20

警告為富不仁者

1你們這些富有的人啊!為那將要臨到你們身上的災難痛哭哀號吧! 2你們的財物朽壞了,衣服也被蟲蛀了。 3你們的金銀生了鏽,那鏽必要指控你們,像火一樣吞噬你們的身體。在末世的日子裡,你們只知道積攢財寶。 4工人替你們收割莊稼,你們卻剋扣他們的工錢。那工錢發出不平的呼喊,工人的冤聲已經傳到萬軍之主的耳中了。 5你們在世上奢侈享樂,在被宰殺的日子裡,把自己養得肥肥胖胖。 6你們冤枉好人、殘害無辜,他們也沒有反抗。

要忍耐到底

7弟兄姊妹,你們要一直忍耐到主來。你們看農夫怎樣耐心等候地裡寶貴的出產,等候秋雨和春雨的降臨。 8同樣,你們也要忍耐,心志堅定,因為主快來了。 9弟兄姊妹,不要互相埋怨,免得受審判。你們看,審判的主已經站在門外了。 10弟兄姊妹,你們要效法從前奉主的名說話的先知,以他們的受苦和忍耐為榜樣。 11我們認為那些忍耐到底的人是有福的。你們都知道約伯的忍耐,也知道主最終怎樣待他,因為主充滿憐憫和慈悲。

12我的弟兄姊妹,最重要的是不可起誓,不可指著天起誓,也不可指著地起誓,不可指著任何東西起誓。你們說話,是就說是,不是就說不是,免得你們受審判。

禱告的力量

13你們中間正在受苦的人應該禱告,喜樂的人應該唱歌讚美, 14生病的人應該請教會的長老來,奉主的名用油抹他的身體並為他禱告。 15出於信心的禱告必能使病人痊癒,主必使他康復。倘若他犯了罪,也必得到赦免。 16所以你們要彼此認罪,互相代禱,好得到醫治。義人的禱告有極大的力量和功效。 17以利亞先知和我們一樣同是血肉之軀,他懇切地祈求不要下雨,結果三年半沒有下雨。 18後來他再禱告求雨,天就降雨,地也長出了莊稼。

19我的弟兄姊妹,如果有人領一個偏離真道的人歸回正路, 20他該知道:使一個迷途中的罪人歸回正路就是救一個靈魂脫離死亡,並且會遮蓋許多罪。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 5:1-20

Chenjezo kwa Achuma Opondereza Anzawo

1Tsono tamverani, inu anthu achuma, lirani ndi kufuwula chifukwa cha zovuta zimene zidzakugwereni. 2Chuma chanu chawola ndipo njenjete zadya zovala zanu. 3Golide ndi siliva wanu zachita dzimbiri. Dzimbirilo lidzakhala umboni wokutsutsani ndi kuwononga mnofu wanu ngati moto. Mwadziwunjikira chuma pa masiku ano otsiriza. 4Taonani, ndalama za malipiro zimene munakanika kulipira aganyu aja ankasenga mʼmunda mwanu zikulira mokutsutsani. Kulira kwa okololawo kwamveka mʼmakutu mwa Ambuye Wamphamvuzonse. 5Mwakhala pa dziko lapansi pano moyo ofewa ndipo mwalidyera dziko lapansi. Mwadzinenepetsa pa tsiku lokaphedwa. 6Mwaweruza kuti ndi wolakwa ndipo mwapha munthu wosalakwa, amene sakutsutsana nanu.

Kupirira Mʼmasautso

7Tsono abale, pirirani mpaka kubwera kwa Ambuye. Onani mmene amachitira mlimi. Amadikirira kuti zipatso zabwino zioneke mʼmunda mwake. Amayembekezera mokhazikika mtima kuyambira nthawi ya mvula yoyamba mpaka yotsiriza. 8Inunso mukhale owugwira mtima ndi osasinthika chifukwa Ambuye ali pafupi kubwera. 9Abale, musamanenezane zoyipa kuopa kuti mungadzaweruzidwe. Woweruza ali pa khomo!

10Abale, tengerani chitsanzo cha aneneri amene anayankhula mʼdzina la Ambuye. Iwowo anakumana ndi zovuta koma anapirira. 11Monga mukudziwa, tinawatenga ngati odalitsika anthu amene anapirira. Munamva za kupirira kwa Yobu ndipo mwaona zimene Ambuye anamuchitira potsiriza pake. Ambuye ndi wodzaza ndi chisoni ndi chifundo.

12Koposa zonse, abale anga, musamalumbire. Polumbira osamatchula kumwamba kapena dziko lapansi, kapena china chilichonse. “Inde” wanu azikhala “Inde,” ndipo “Ayi” wanu azikhala “Ayi,” kuopa kuti mungadzapezeke olakwa.

Pemphero la Chikhulupiriro

13Kodi alipo wina mwa inu amene ali pa mavuto? Apemphere. Kodi wina wakondwa? Ayimbe nyimbo zolemekeza. 14Kodi alipo wina mwa inu akudwala? Ayitane akulu ampingo kuti adzamupempherere ndi kumudzoza mafuta mʼdzina la Ambuye. 15Ndipo pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa munthu wodwalayo ndipo Ambuye adzamuutsa. Ngati wachimwa adzakhululukidwa. 16Choncho, ululiranani machimo anu ndi kupemphererana wina ndi mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama ndi lamphamvu ndipo limagwira ntchito.

17Eliya anali munthu ngati ife. Iye anapemphera mwamphamvu kuti mvula isagwe ndipo sinagwedi kwa zaka zitatu ndi theka. 18Kenaka anapempheranso, ndipo kumwamba kunagwetsa mvula, ndipo dziko lapansi linatulutsa zomera zake. 19Abale anga, ngati mmodzi wa inu apatuka pa choonadi ndipo wina wake ndi kumubweza, 20kumbukirani izi: Aliyense wobweza wochimwa kuchoka ku cholakwa chake, adzamupulumutsa ku imfa ndi kukwirira machimo ambiri.