雅各書 3 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

雅各書 3:1-18

邪惡的舌頭

1我的弟兄姊妹,不要個個當教師,因為你們知道,我們為人師表的將受到更嚴格的評判, 2因為我們在許多方面難免有過失。如果誰在言語上沒有過失,他就是純全的人,也能在各方面保持自制。 3我們如果把嚼環放在馬嘴裡,便可以使牠順服,駕馭牠。 4一艘大船在遭遇暴風吹襲時,船身雖然龐大,但舵手只要操縱一個小小的舵,就能隨意駕駛它。

5同樣,人的舌頭雖然很小,卻能說誇大的話。

看啊,小火星能點燃大森林。 6舌頭就是火,是我們身體上的一個充滿邪惡的世界,能玷污人的全身,足以毀掉人的一生,它是從地獄點燃的火。 7自然界中的各類走獸、飛禽、爬蟲、水族都可以被馴服,也已經被人類馴服了, 8但無人能馴服自己的舌頭,因為舌頭是個無法控制的邪惡之物,充滿了致命的毒氣。 9我們用舌頭來讚美主和天父,也用舌頭來咒詛照著上帝的形像被造的人。 10讚美和咒詛竟然從同一張嘴裡發出來。我的弟兄姊妹,這是不應該的! 11同一個泉源能湧出甜苦兩樣水嗎? 12我的弟兄姊妹,無花果樹能結出橄欖嗎?葡萄樹能結出無花果嗎?一個鹹水泉必流不出甜水來。

天上的智慧

13你們當中誰是有智慧、有見識的呢?請他帶著來自智慧的謙和,在善行上表現出來。 14但如果你們心懷苦毒的嫉妒和自私的野心,就不要自誇說有智慧,也不要違背真理去撒謊。 15這種智慧並非來自天上,而是從世俗、私慾和魔鬼來的。 16哪裡有嫉妒和自私的野心,哪裡就會有混亂和各樣的惡事。

17但從天上來的智慧首先是純潔,然後是愛好和平、溫良柔順、充滿憐憫、多結善果、不存偏見、沒有虛偽。 18使人和睦的人撒下和平的種子,必收穫仁義的果實。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yakobo 3:1-18

Za Lilime

1Abale anga, ambiri musakhale aphunzitsi chifukwa mumadziwa kuti aphunzitsife tidzaweruzidwa mowuma kuposa anthu ena onse. 2Tonsefe timapunthwa mʼnjira zambiri. Ngati wina salakwa poyankhula, ameneyo ndi munthu wangwiro, wodziwa kuyangʼanira bwino thupi lake lonse.

3Tikayika tizitsulo mʼkamwa mwa akavalo kuti atimvere, timatha kuwongolera thupi lake lonse. 4Taonani sitima zapamadzi. Ngakhale ndi zazikulu kwambiri ndipo zimakankhidwa ndi mphepo yamphamvu, zimawongoleredwa ndi tsigiro lalingʼono kulikonse kumene woyendetsayo akufuna kupita. 5Momwemonso, lilime ndi kachiwalo kakangʼono ka thupi koma limadzitama kuti nʼkuchita zikuluzikulu. Tangoganizirani za nkhalango yayikulu imene ingapse ndi kalawi kamoto koyamba mochepa. 6Lilime nalonso ndi moto, dziko la zoyipa pakati pa ziwalo za thupi. Limawononga munthu yense wathunthu. Limayika zonse za moyo wake pa moto, ndipo moto wake ndi wochokera ku gehena.

7Mitundu yonse ya nyama, ya mbalame, ya zokwawa ndi ya zolengedwa za mʼnyanja, zikuwetedwa ndipo munthu wakhala akuziweta, 8koma palibe munthu amene angaweta lilime. Lilime ndipo silitha kupuma, ndi lodzaza ndi ululu wakupha.

9Ndi lilime lomwelo timatamanda Ambuye ndi Atate athu, komanso ndi lilime lomwelo timalalatira anthu, amene anapangidwa mʼchifanizo cha Mulungu. 10Mʼkamwa momwemo mutuluka matamando ndi kulalata. Abale anga, zisamatero ayi. 11Kodi madzi abwino ndi a mchere angatuluke pa kasupe mmodzi? 12Abale anga, kodi mtengo wa mkuyu nʼkubala mphesa, kapena mtengo wampesa nʼkubala nkhuyu? Kasupe wa madzi a mchere sangatulutsenso madzi abwino.

Mitundu Iwiri ya Nzeru

13Ndani mwa inu amene ndi wanzeru ndi womvetsa zinthu? Mulekeni aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru ndiye zikutsogolera kudzichepetsa kwake ndi zochita zake 14Koma ngati muli ndi mtima wakaduka ndi odzikonda, musadzitamandire kapena kukana choonadi. 15“Nzeru” zotere sizochokera kumwamba koma ndi za mʼdziko lapansi, si zauzimu koma ndi za ziwanda. 16Pakuti pamene pali kaduka ndi kudzikonda pomweponso pamakhala chisokonezo ndi zochitika zoyipa zonse.

17Koma nzeru imene imachoka kumwamba, poyamba ndi yangwiro, ndi yokonda mtendere, yoganizira za ena, yogonjera, yodzaza ndi chifundo ndi chipatso chabwino, yosakondera ndi yoona mtima. 18Anthu amtendere amene amadzala mtendere amakolola chilungamo.