路加福音 24 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

路加福音 24:1-53

耶穌死裡復活

1週日黎明時分,幾位婦女帶著預備好的香料來到墳前, 2發現墓口的大石頭已經滾到旁邊, 3便進去,卻沒有看見主耶穌的遺體。 4正在猜疑之間,突然有兩個衣服發光的人站在旁邊, 5她們嚇得俯伏在地。那兩個人對她們說:「你們為什麼在死人中找活人呢? 6祂不在這裡,已經復活了!記住祂在加利利對你們說的話, 7『人子必須被交在罪人的手中,被釘在十字架上,在第三天復活。』」

8她們想起耶穌的話來, 9便離開墓地回去把事情的經過告訴十一個使徒和其他人。 10這些婦女就是抹大拉瑪麗亞約亞娜雅各的母親瑪麗亞及其他人。

11大家聽了都不相信,認為是無稽之談。 12彼得卻起身跑到墓地,屈身往墓裡張望,只見細麻布在那裡,他便離開了,對發生的事大惑不解。

耶穌的顯現

13同一天,有兩個門徒前往離耶路撒冷十一公里的以馬忤斯村, 14一路談論著最近發生的一切事。 15正談論的時候,耶穌走過來和他們同行。 16可是,他們認不出耶穌。

17耶穌問他們:「你們一路上在談論什麼?」

他們停下腳步,滿面愁容, 18其中一個叫革流巴的說:「難道在耶路撒冷作客的人中,只有你不知道近日發生的大事嗎?」

19耶穌問:「什麼事?」

他們說:「就是拿撒勒人耶穌的事。祂本來是個先知,在上帝和百姓面前言談舉止充滿力量。 20我們的祭司長和官長卻把祂押去判了死刑,釘在十字架上。

21「我們一直希望祂就是要拯救以色列的那位。還有,今天是事發後的第三天, 22我們當中有幾位婦女一早到耶穌的墳墓, 23發現耶穌的遺體不見了,回來說天使曾向她們顯現並告訴她們耶穌已經復活了。

24「後來我們有幾個人親自去墳墓察看,果然像她們所說的,耶穌的遺體不見了。」

25耶穌對他們說:「無知的人啊!為什麼遲遲不肯相信先知的話呢? 26基督豈不是要先這樣受害,然後進入祂的榮耀嗎?」

27耶穌接著從摩西和眾先知的記載開始,把有關自己的經文都向他們講解明白。

28快到以馬忤斯村時,耶穌好像還要繼續前行。 29他們極力挽留祂,說:「天快黑了,時候不早了,跟我們一同住宿吧。」耶穌就和他們一起進村住下。

30吃飯的時候,耶穌拿起餅來,祝謝後,掰開遞給他們。 31忽然他們眼睛明亮了,認出是耶穌。耶穌很快從他們眼前消失了。

32二人彼此議論說:「一路上祂和我們說話、為我們解釋聖經的時候,我們心裡不是很火熱嗎?」 33二人馬上趕回耶路撒冷,看到十一位使徒及其同伴正聚在一起談論: 34「主真的復活了,祂向西門顯現了。」

35二人也把路上發生的事以及掰餅時認出主的經過述說了一遍。

36正說的時候,耶穌出現在他們中間,說:「願你們平安!」 37他們又驚又怕,以為是看見了鬼魂。

38耶穌說:「你們為什麼憂心忡忡?為什麼心存疑惑呢? 39你們看我的手和腳,就知道真的是我。來摸摸看,鬼魂沒有骨和肉,你們看!我有。」 40說完,便伸出手和腳給他們看。

41門徒又驚又喜,半信半疑。耶穌問:「你們這裡有吃的嗎?」 42他們便給祂一片烤魚, 43祂接過魚來在他們面前吃了。

44耶穌對他們說:「我跟你們在一起的時候曾經說過,摩西的律法書、先知的書以及詩篇裡有關我的記載都要應驗。」 45於是,耶穌開啟了他們的心竅,使他們明白這些經文, 46又對他們說:「聖經上說,基督必受害,然後在第三天從死裡復活, 47人們要奉祂的名傳揚悔改、赦罪的福音,從耶路撒冷一直傳遍萬國。

48「你們是這些事的見證人, 49我要把我父所應許的賜給你們。不過,你們要留在城裡,直到你們得到天上來的能力。」

耶穌升天

50耶穌帶著門徒來到伯大尼附近,舉起雙手為他們祝福。 51正祝福的時候,祂就離開了他們,被接到天上去了。 52門徒都敬拜祂,然後歡歡喜喜地回到耶路撒冷53他們常在聖殿裡讚美上帝。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 24:1-53

Yesu Auka kwa Akufa

1Pa tsiku loyamba la Sabata, mmamawa kwambiri, amayi anatenga zonunkhira napita ku manda. 2Anaona mwala wa pa manda utagubuduzika 3ndipo atalowamo sanapeze mtembo wa Ambuye Yesu. 4Pamene iwo ankadabwa za zimenezi, mwadzidzidzi, amuna awiri ovala zovala zonyezimira kwambiri anayimirira pambali pawo. 5Ndi mantha, amayiwo anaweramitsa nkhope zawo pansi, koma amunawo anawawuza kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukufuna wamoyo pakati pa akufa? 6Iye sali muno ayi. Wauka! Kumbukirani zimene anakuwuzani pamene anali nanu ku Galileya: 7‘Mwana wa Munthu ayenera kuperekedwa mʼmanja mwa anthu ochimwa, napachikidwa ndipo tsiku lachitatu adzaukitsidwanso.’ ” 8Ndipo anakumbukira mawu ake.

9Atabwerera kuchokera ku mandako, anafotokoza zinthu zonse kwa khumi ndi mmodziwo ndi kwa ena onse. 10Amayi anali Mariya Magadalena, Yohana, Mariya amayi a Yakobo, ndi ena anali nawo amene anawuza atumwi. 11Koma iwo sanawakhulupirire amayiwa, chifukwa mawu awo amaoneka kwa iwo ngati opanda nzeru. 12Komabe Petro anayimirira ndi kuthamangira ku manda. Atasuzumira, anaona nsalu zimene anamukulungira zija zili pa zokha, ndipo iye anachoka, akudabwa ndi zimene zinachitikazo.

Zochitika pa Njira ya ku Emau

13Ndipo tsiku lomwelo, awiri a iwo ankapita ku mudzi wotchedwa Emau, pafupifupi makilomita khumi ndi imodzi kuchokera ku Yerusalemu. 14Iwo ankayankhulana za zonse zimene zinachitikazo. 15Pamenepo Yesu mwini wake anabwera ndi kuyenda nawo pamodzi; 16koma iwo sanamuzindikire.

17Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukukambirana zotani mʼnjira muno?”

Iwo anayima ndi nkhope zakugwa. 18Mmodzi wa iwo wotchedwa Kaliyopa anamufunsa kuti, “Kodi ndiwe wekha wokhala mu Yerusalemu amene sukudziwa zinthu zimene zachitika mʼmasiku awa?”

19Iye anafunsa kuti, “Zinthu zotani?”

Iwo anayankha nati, “Za Yesu wa ku Nazareti, Iye anali mneneri, wamphamvu mʼmawu ndi mu zochita pamaso pa Mulungu ndi anthu onse. 20Akulu a ansembe ndi oweruza anamupereka Iye kuti aphedwe, ndipo anamupachika Iye; 21koma ife tinkayembekezera kuti Iye ndiye amene akanawombola Israeli. Ndipo kuwonjeza apo, lero ndi tsiku lachitatu chichitikireni izi. 22Kuwonjezanso apo, ena mwa amayi athu atidabwitsa ife. Iwo anapita ku manda mmamawa 23koma sanakapeze mtembo wake. Iwo anabwera ndi kudzatiwuza ife kuti anaona masomphenya a angelo amene anati Yesu ali moyo. 24Kenaka ena mwa anzathu anapita ku manda ndipo anakapeza monga momwe amayiwo ananenera, koma Iye sanamuone.”

25Iye anawawuza kuti, “Inu ndinu anthu opusa, osafuna kukhulupirira msanga zonse zimene aneneri ananena! 26Kodi Khristu sanayenera kumva zowawa izi ndipo kenaka ndi kulowa mu ulemerero wake?” 27Ndipo kuyambira ndi Mose ndi aneneri onse Iye anawafotokozera zimene zinalembedwa mʼmalemba wonse zokhudzana ndi Iye mwini.

28Atayandikira mudzi omwe amapitako, Yesu anachita ngati akupitirira. 29Koma iwo anamupempha Iye kwambiri kuti, “Mukhale ndi ife, popeza kwatsala pangʼono kuda, ndipo dzuwa lili pafupi kulowa.” Ndipo Iye anapita kukakhala nawo.

30Iye ali pa tebulo pamodzi nawo, anatenga buledi ndipo anayamika, nanyema nayamba kuwagawira. 31Kenaka maso awo anatsekuka ndipo anamuzindikira Iye, ndipo anachoka pakati pawo. 32Iwo anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi mitima yathu sinali kutentha mʼkati mwathu pamene Iye ankayankhulana nafe pa njira ndi mmene anatitsekulira malemba?”

33Nthawi yomweyo iwo anayimirira ndi kubwerera ku Yerusalemu. Iwo anapeza khumi ndi mmodziwo ndi ena anali nawo nasonkhana pamodzi 34ndipo anati, “Ndi zoonadi! Ambuye auka ndipo anaonekera kwa Simoni.” 35Kenaka awiriwo anawawuza zimene zinachitika pa njira, ndi mmene iwo anamudziwira Yesu, Iye atanyema buledi.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira

36Akufotokoza zimenezi, Yesu mwini wake anayimirira pakati pawo ndipo anati, “Mukhale ndi mtendere.”

37Koma chifukwa choti anathedwa nzeru ndi kuchita mantha, ankaganiza kuti akuona mzukwa. 38Iye anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuvutika? Nʼchifukwa chiyani mukukayika mu mtima mwanu? 39Taonani manja anga ndi mapazi anga. Ine ndine amene! Khudzeni kuti muone. Mzukwa ulibe mnofu ndi mafupa monga mukuonera ndili nazo.”

40Iye atanena izi anawaonetsa manja ake ndi mapazi ake. 41Ndipo pamene iwo samakhulupirirabe, chifukwa cha chimwemwe ndi kudabwa, Iye anawafunsa kuti, “Kodi muli ndi chakudya chilichonse pano?” 42Iwo anamupatsa Iye kachidutswa ka nsomba yophika. 43Iye anakatenga ndi kukadya iwo akuona.

44Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene ndinakuwuzani pamene ndinali nanu: chilichonse chiyenera kukwaniritsidwa chimene chinalembedwa cha Ine mʼbuku la Malamulo a Mose, Aneneri ndi Masalimo.”

45Kenaka anawatsekula maganizo kuti azindikire Malemba. 46Iye anawawuza kuti, “Izi ndi zimene zinalembedwa: Khristu adzazunzika ndipo adzauka kwa akufa tsiku lachitatu. 47Ndipo kutembenuka mtima ndi kukhululukidwa kwa machimo zidzalalikidwa mu dzina lake kwa anthu amitundu yonse kuyambira mu Yerusalemu. 48Inu ndinu mboni za zimenezi. 49Ine ndidzakutumizirani chimene Atate anga analonjeza. Koma khalani mu mzinda muno mpaka mutavekedwa mphamvu yochokera kumwamba.”

Kupita Kumwamba

50Iye atawatengera kunja kwa mzindawo mpaka ku Betaniya, anakweza manja ake ndi kuwadalitsa. 51Iye akuwadalitsa, anawasiya ndipo anatengedwa kupita kumwamba. 52Pamenepo anamulambira Iye ndipo anabwerera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu. 53Ndipo iwo anakhalabe ku Nyumba ya Mulungu, akulemekeza Mulungu.