路加福音 18 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

路加福音 18:1-43

恆心禱告

1耶穌講了一個比喻來教導門徒要常常禱告,不要灰心。

2祂說:「某城有一位既不敬畏上帝也不尊重人的審判官。 3那城裡有一位寡婦常常來哀求這位審判官,說,『求你為我伸冤,懲辦我的對頭。』 4審判官總是充耳不聞,但後來心裡想,『雖然我不怕上帝,也不在乎人, 5可是這寡婦一直來煩我,還是替她伸冤好了,免得她再來煩我!』」

6主接著說:「你們聽,這不義的審判官尚且這麼說, 7難道上帝聽到祂揀選的人晝夜呼求,不替他們伸冤嗎?難道祂會一直耽延不理嗎? 8我告訴你們,祂必很快為他們伸冤。不過當人子來的時候,在世上找得到有信心的人嗎?」

兩種禱告

9耶穌對那些自以為義、藐視別人的人講了一個比喻: 10「有兩個人到聖殿裡禱告,一個是法利賽人,一個是稅吏。 11法利賽人站在那裡自言自語地禱告說,『上帝啊!我感謝你,因為我不像別人那樣勒索、不義、通姦,也不像這稅吏。 12我每週禁食兩次,奉獻全部收入的十分之一。』

13「但那稅吏卻遠遠地站著,連頭也不敢抬起來,捶著胸說,『上帝啊,求你憐憫我這個罪人!』

14「我告訴你們,二人回家後,被上帝算為義的是稅吏而不是法利賽人,因為自高的人必遭貶抑,謙卑的人必得尊榮。」

祝福孩子

15有許多人把嬰孩帶來要讓耶穌摸一摸他們,為他們祝福,門徒看見,就責備這些人。 16耶穌卻招呼他們過來,並對門徒說:「讓小孩子到我這裡來,不要阻止他們,因為上帝的國屬於這樣的人。 17我實在告訴你們,人若不像小孩子一樣接受上帝的國,絕不能進去。」

富豪求問永生

18一位官長問耶穌:「良善的老師,我該做什麼才能承受永生?」

19耶穌說:「你為什麼稱呼我『良善的老師』呢?只有上帝是良善的。 20你知道『不可通姦,不可殺人,不可偷盜,不可作偽證,要孝敬父母』這些誡命」。

21那人說:「我從小就遵行這些誡命。」

22耶穌聽了就對他說:「你還有一件事沒有做,就是變賣你所有的產業,分給窮人,你必有財寶存在天上,然後你還要來跟從我。」 23那人聽了,極其憂愁,因為他非常富有。

24耶穌見狀,就說;「有錢人進上帝的國真難啊! 25駱駝穿過針眼比有錢人進上帝的國還容易呢!」

26聽見的人就問:「這樣,誰能得救呢?」

27耶穌回答說:「對人而言,這不可能,但對上帝而言,凡事都可能。」

28彼得說:「你看!我們已經撇下一切來跟從你了。」

29耶穌說:「我實在告訴你們,任何人為了上帝的國而撇下房屋、妻子、弟兄、父母或兒女, 30今世必得百倍的獎賞,來世必得永生。」

再次預言受害和復活

31耶穌把十二使徒帶到一邊,對他們說:「你們要留意,我們現在前往耶路撒冷,先知書上有關人子的記載都要應驗, 32人子將被交在外族人的手裡,被他們嘲弄、虐待、吐唾沫、 33鞭打和殺害,但第三天祂必復活。」 34使徒卻一點也不明白,因為這番話的含意是隱藏的,他們聽不明白。

治癒耶利哥的瞎子

35耶穌快到耶利哥城的時候,有一個瞎子坐在路旁討飯。 36他聽見許多人經過,就詢問是怎麼回事。 37有人告訴他是拿撒勒人耶穌經過此地, 38他就高聲呼喊:「大衛的後裔耶穌啊,可憐我吧!」

39走在前面的人責備他,讓他安靜,但他反而叫得更大聲:「大衛的後裔啊,可憐我吧!」

40耶穌停下腳步,命人把他帶過來,然後問他: 41「你要我為你做什麼?」

他說:「主啊!我想能夠看見。」

42耶穌對他說:「你看見吧!你的信心救了你。」 43他立刻得見光明,並跟隨耶穌,一路讚美上帝。目睹這事的人也都讚美上帝。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Luka 18:1-43

Fanizo la Mayi Wakhama pa Kupempha

1Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke. 2Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu. 3Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’

4“Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu, 5koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’ ”

6Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena. 7Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira? 8Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”

Fanizo la Mfarisi ndi Wolandira Msonkho

9Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse. 10“Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho. 11Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu. 12Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’

13“Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’

14“Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”

Yesu Adalitsa Ana Aangʼono

15Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula. 16Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere. 17Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”

Munthu Wachuma ndi Ufumu wa Mulungu

18Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?”

19Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha. 20Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’ ”

21Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”

22Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”

23Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri. 24Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu! 25Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”

26Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”

27Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”

28Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”

29Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu 30adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.”

Yesu Aneneratu za Imfa Yake Kachitatu

31Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa. 32Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira, 33adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”

34Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.

Yesu Achiritsa Wosaona

35Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha, 36anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika. 37Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”

38Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”

39Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”

40Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti, 41“Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?”

Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”

42Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.” 43Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.