詩篇 96 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 96:1-13

第 96 篇

上帝是至高的君王

(平行經文:歷代志上16·23-33

1你們要向耶和華唱新歌,

普世都要向耶和華歌唱。

2要向耶和華歌唱,稱頌祂的名,

天天傳揚祂的拯救之恩。

3要在列國述說祂的榮耀,

在萬民中述說祂的奇妙作為。

4因為耶和華無比偉大,

當受至高的頌揚;

祂超越一切神明,當受敬畏。

5列邦的神明都是假的,

唯獨耶和華創造了諸天。

6祂尊貴威嚴,

祂的聖所充滿能力和榮美。

7萬族萬民啊,

要把榮耀和能力歸給耶和華,

歸給耶和華!

8要把耶和華當得的榮耀歸給祂,

要帶著祭物到祂的院宇敬拜祂。

9你們當在聖潔的耶和華面前俯伏敬拜,

大地要在祂面前戰抖。

10要告訴列國:

「耶和華掌權,

祂使大地堅立不搖,

祂必公正地審判萬民。」

11願天歡喜,願地快樂,

願海和其中的一切都歡呼澎湃。

12願田野和其中的萬物都喜氣洋洋,

願林中的樹木都歡然讚美耶和華。

13因為祂要來審判大地,

祂要按公義審判世界,

憑祂的信實審判萬民。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 96:1-13

Salimo 96

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;

Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.

2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,

ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.

5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,

koma Yehova analenga mayiko akumwamba.

6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,

mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;

bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.

9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;

njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”

Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;

Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.

11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;

nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.

Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;

13idzayimba pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lonse mwachilungamo

ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.