詩篇 94 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 94:1-23

第 94 篇

上帝是審判者

1耶和華啊,你是伸冤的上帝;

伸冤的上帝啊,

求你彰顯你的榮光。

2審判世界的主啊,

求你起來使驕傲人受到應得的報應。

3耶和華啊,

惡人洋洋得意,要到何時呢?

要到何時呢?

4他們大放厥詞,狂妄自大。

5耶和華啊,他們壓迫你的子民,

苦害你的產業。

6他們謀害寡婦、外族人和孤兒,

7並說:「耶和華看不見,

雅各的上帝不會知道。」

8愚昧的人啊,你們要思想;

無知的人啊,你們何時才能明白呢?

9難道創造耳朵的上帝聽不見嗎?

難道創造眼睛的上帝看不見嗎?

10管教列國的上帝難道不懲罰你們嗎?

賜知識的上帝難道不知道嗎?

11耶和華洞悉人的思想,

祂知道人的思想虛妄,

12耶和華啊,蒙你管教並用律法訓誨的人有福了!

13你使他們在患難中有平安,

惡人終必滅亡。

14耶和華不會丟棄祂的子民,

也不會遺棄祂的產業。

15公正的審判必重現,

心地正直的人都必擁護。

16誰肯為我奮起攻擊惡人?

誰肯為我起來抵擋作惡的人?

17耶和華若不幫助我,

我早已歸入死亡的沉寂中了。

18我說:「我要倒下了!」

耶和華啊,你便以慈愛扶助我。

19當我憂心忡忡的時候,

你的撫慰帶給我歡樂。

20藉律例製造不幸的首領,

豈能與你聯盟?

21他們結黨攻擊義人,

殘害無辜。

22但耶和華是我的堡壘,

我的上帝是保護我的磐石。

23祂必使惡人自食惡果,

因他們的罪惡而毀滅他們。

我們的上帝耶和華必毀滅他們。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 94:1-23

Salimo 94

1Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango,

Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.

2Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi;

bwezerani kwa odzikuza zowayenera.

3Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova,

mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?

4Amakhuthula mawu onyada;

onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.

5Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova;

amapondereza cholowa chanu.

6Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko;

amapha ana amasiye.

7Iwo amati, “Yehova sakuona;

Mulungu wa Yakobo salabadirako.”

8Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu;

zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?

9Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva?

Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?

10Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga?

Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?

11Yehova amadziwa maganizo a munthu;

Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.

12Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza,

munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;

13mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto,

mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.

14Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake;

Iye sadzasiya cholowa chake.

15Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo,

ndipo onse olungama mtima adzachitsata.

16Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa?

Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?

17Yehova akanapanda kundithandiza,

bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.

18Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,”

chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.

19Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga,

chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.

20Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu

umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?

21Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama

ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.

22Koma Yehova wakhala linga langa,

ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.

23Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo

ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo;

Yehova Mulungu wathu adzawawononga.