詩篇 71 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 71:1-24

第 71 篇

一個老年人的祈禱

1耶和華啊,我投靠了你,

求你使我永不蒙羞。

2求你憑公義搭救我,

側耳聽我的懇求,拯救我。

3求你成為保護我的磐石,

讓我可以隨時投靠你。

求你下令救我,

因為你是我的磐石和堡壘。

4我的上帝啊,

求你從惡人手中拯救我,

從邪惡、殘暴之徒掌下拯救我。

5主耶和華啊,你是我的盼望,

我從小就信靠你。

6你使我出了母胎,

我從出生就依靠你,

我要永遠讚美你。

7我的遭遇使許多人感到驚駭,

但你是我堅固的避難所。

8我口中充滿對你的讚美,

終日述說你的榮耀。

9我年老時,求你不要丟棄我;

我體力衰微時,求你不要離棄我。

10我的仇敵議論我,

那些想殺害我的一起策劃陰謀,說:

11「上帝已經丟棄了他。

去追趕、捉拿他吧,

因為無人會救他。」

12上帝啊,不要遠離我;

我的上帝啊,求你快來幫助我!

13願我的仇敵在羞辱中滅亡,

願那些害我的人抱愧蒙羞。

14我必常常心懷盼望,

向你獻上更多的讚美。

15雖然我無法測度你的公義和拯救之恩,

但我要終日傳揚你的作為。

16主耶和華啊,

我要傳揚你大能的作為,

單單述說你的公義。

17上帝啊,

我從小就受你的教導,

直到今日我仍傳揚你奇妙的作為。

18上帝啊,

就是我年老髮白的時候,

求你也不要丟棄我,

好讓我把你的大能告訴下一代,世代相傳。

19上帝啊,你的公義高達穹蒼,

你成就了奇妙大事。

上帝啊,有誰能像你?

20你使我經歷了許多患難,

最終必使我重獲新生,

救我脫離死亡的深淵。

21你必賜我更大的尊榮,

你必再次安慰我。

22我的上帝啊,

我要彈琴讚美你的信實;

以色列的聖者啊,

我要伴隨著琴聲讚美你。

23你救贖了我的靈魂,

我的口和靈魂都要歡呼歌頌你。

24我要終日向人述說你的公義,

因為那些想害我的人已經蒙羞受辱。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 71:1-24

Salimo 71

1Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;

musalole kuti ndichititsidwe manyazi.

2Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,

mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.

3Mukhale thanthwe langa lothawirapo,

kumene ine nditha kupita nthawi zonse;

lamulani kuti ndipulumuke,

pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.

4Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,

kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.

5Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,

chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.

6Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;

Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga,

ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.

7Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri

koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.

8Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu,

kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.

9Musanditaye pamene ndakalamba;

musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.

10Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane;

iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.

11Iwo amati, “Mulungu wamusiya;

mutsatireni ndi kumugwira,

pakuti palibe amene adzamupulumutse.”

12Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu,

bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.

13Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi,

iwo amene akufuna kundipweteka

avale chitonzo ndi manyazi.

14Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse,

ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.

15Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu,

za chipulumutso chanu tsiku lonse,

ngakhale sindikudziwa muyeso wake.

16Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse.

Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.

17Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa,

ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa

18Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu

musanditaye Inu Mulungu,

mpaka nditalengeza mphamvu zanu

kwa mibado yonse yakutsogolo.

19Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba.

Ndani wofanana nanu Inu Mulungu,

amene mwachita zazikulu?

20Ngakhale mwandionetsa mavuto

ambiri owawa,

mudzabwezeretsanso moyo wanga;

kuchokera kunsi kwa dziko lapansi,

mudzandiukitsanso.

21Inu mudzachulukitsa ulemu wanga

ndi kunditonthozanso.

22Ndidzakutamandani ndi zeze

chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu,

ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe,

Inu Woyera wa Israeli.

23Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe

pamene ndidzayimba matamando kwa Inu

amene mwandiwombola.

24Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo

tsiku lonse,

pakuti iwo amene amafuna kundipweteka

achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.