詩篇 43 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 43:1-5

第 43 篇

流亡異鄉者的禱告

1上帝啊,

求你為我伸張正義,

在不虔敬的人面前為我辯護,

救我脫離詭詐邪惡的人。

2你是保護我的上帝,

你為何丟棄我?

為何讓我受仇敵的攻擊,

使我哀傷不已呢?

3求你以光明和真理引導我,

領我到你的聖山,到你的居所。

4我要到上帝的祭壇前,

到賜我喜樂的上帝面前。

上帝啊,我的上帝,

我要彈琴讚美你。

5我的心啊!

你為何沮喪?為何煩躁?

要仰望上帝,

因為我還要讚美祂——我的救主,我的上帝。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 43:1-5

Salimo 43

1Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;

ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;

mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.

2Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.

Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?

Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,

woponderezedwa ndi mdani?

3Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu

kuti zinditsogolere;

mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,

kumalo kumene inu mumakhala.

4Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,

kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.

Ndidzakutamandani ndi zeze,

Inu Mulungu wanga.

5Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?

Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?

Khulupirira Mulungu,

pakuti ndidzamutamandabe Iye,

Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.