詩篇 41 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 41:1-13

第 41 篇

病中的禱告

大衛的詩,交給樂長。

1善待窮人的有福了!

耶和華必救他們脫離困境。

2耶和華必保護他們,

救他們的性命,

使他們在地上享福,

不讓仇敵惡謀得逞。

3他們生病在床,

耶和華必看顧,

使他們康復。

4我禱告說:「耶和華啊,

求你憐憫我,醫治我,

因為我得罪了你。」

5我的仇敵惡狠狠地說:

「他何時才會死,

並且被人遺忘呢?」

6他們來看我時,

心懷惡意,滿口謊言,

出去後散佈流言。

7所有恨我的人都交頭接耳,

設計害我。

8他們說:「他患了惡病,

再也起不來了!」

9連我所信賴、吃我飯的摯友也用腳踢我。

10耶和華啊,

求你憐憫我,叫我痊癒,

我好報復他們。

11我知道你喜悅我,

因為你沒有讓仇敵勝過我。

12你因我正直而扶持我,

讓我永遠侍立在你面前。

13從亙古到永遠,

以色列的上帝耶和華當受稱頌。

阿們!阿們!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 41:1-13

Salimo 41

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Wodala ndi munthu amene amaganizira anthu osauka;

Yehova amamuwombola pa nthawi yamsautso.

2Yehova adzamuteteza ndi kusunga moyo wake;

Yehova adzamudalitsa iye mʼdziko

ndipo sadzamupereka ku zofuna za adani ake.

3Yehova adzamuthandiza pamene akudwala

ndipo adzamuchiritsa pa bedi lake la matenda.

4Ndinati, “Inu Yehova, mundichitire chifundo;

chiritseni pakuti ndakuchimwirani.”

5Adani anga mwankhwidzi amanena za ine kuti,

“Kodi munthu ameneyu adzafa liti kuti ayiwalike?”

6Pamene wina abwera kudzandiona,

amayankhula mwachinyengo, pomwe mtima wake ukusonkhanitsa zachipongwe;

kenaka iye amatuluka ndi kukalengeza kunja.

7Adani anga onse amanongʼonezana pamodzi kulimbana nane,

iwo amalingalira zoyipa kwambiri za ine, ponena kuti,

8“Matenda owopsa amugwira;

sadzaukapo pamalo pamene wagona.”

9Ngakhale bwenzi langa la pamtima amene ndinamudalira,

iye amene amadya pamodzi ndi ine

watukula chidendene chake kulimbana nane.

10Koma Yehova mundichititre chifundo,

dzutseni kuti ndiwabwezere.

11Ine ndikudziwa kuti mukukondwera nane,

pakuti mdani wanga sandigonjetsa.

12Mu ungwiro wanga Inu mumandisunga

ndi kundiyimika pamaso panu kwamuyaya.

13Atamandike Yehova Mulungu wa Israeli

kuchokera muyaya mpaka muyaya.

Ameni ndi Ameni.