詩篇 36 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 36:1-12

第 36 篇

人的邪惡與上帝的美善

耶和華的僕人大衛的詩,交給樂長。

1罪惡在惡人內心深處說話,

他們眼中毫無對上帝的畏懼。

2他們自以為是,渾然不知自己的罪,

也不憎惡自己的罪。

3他們滿口惡言謊話,

毫無智慧和善行。

4他們躺在床上盤算作惡,

執意走罪惡的道路,

無惡不作。

5耶和華啊,你的慈愛廣及諸天,

你的信實高達穹蒼。

6你的公義穩如高山,

你的判斷深不可測。

耶和華啊,你保護人類,

也保護牲畜。

7上帝啊,

你的慈愛無比寶貴!

世人都在你的翅膀下尋求蔭庇。

8你讓他們飽享你殿裡的美食,

暢飲你樂河中的水。

9因為你是生命的泉源,

在你的光中我們得見光明。

10求你常施慈愛給認識你的人,

以公義恩待心地正直的人。

11別讓驕傲人的腳踐踏我,

別讓兇惡人的手驅趕我。

12看啊!惡人已經摔倒在地,

再也爬不起來。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 36:1-12

Salimo 36

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova.

1Uthenga uli mu mtima mwanga

wonena za kuchimwa kwa munthu woyipa:

Mu mtima mwake

mulibe kuopa Mulungu.

2Pakuti iye mʼkuona kwake amadzinyenga yekha kwambiri,

sazindikira kapena kudana ndi tchimo lake.

3Mawu a pakamwa pake ndi oyipa ndi achinyengo;

iyeyo waleka kukhala wanzeru ndi kuchita zabwino.

4Ngakhale ali pa bedi pake amakonzekera zoyipa;

iye amadzipereka yekha ku njira ya uchimo

ndipo sakana cholakwa chilichonse.

5Chikondi chanu Yehova, chimafika ku mayiko a kumwamba,

kukhulupirika kwanu mpaka ku mitambo.

6Chilungamo chanu Mulungu chili ngati mapiri aakulu,

chiweruzo chanu chili ngati kuzama kwakukulu.

Yehova mumasunga munthu pamodzi ndi chinyama.

7Chikondi chanu chosatha ndi chamtengowapatali!

Otchuka pamodzi ndi anthu wamba pakati pa anthu

amapeza pothawirapo mu mthunzi wa mapiko anu.

8Iwo amadyerera zinthu zambiri za mʼnyumba yanu;

Inu mumawapatsa chakumwa kuchokera mu mtsinje wanu wachikondwerero.

9Pakuti kwa Inu kuli kasupe wamoyo;

mʼkuwala kwanu ifenso timaona kuwala.

10Pitirizani chikondi chanu pa iwo amene amakudziwani,

chilungamo chanu kwa olungama mtima.

11Musalole kuti phazi la wodzikuza libwere kulimbana nane,

kapena dzanja la oyipa kundithamangitsa.

12Onani momwe ochita zoyipa agonera atagwa,

aponyeni pansi, kuti asathe kudzukanso!