詩篇 34 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 34:1-22

第 34 篇

上帝的美善

大衛在亞比米勒面前裝瘋,被趕出去後,作了此詩。

1我要常常稱頌耶和華,

時刻讚美祂。

2我要誇耀祂的作為,

困苦人聽見必歡欣。

3讓我們一同頌讚祂的偉大,

尊崇祂的名!

4我向祂禱告,祂便應允我,

救我脫離一切恐懼。

5凡仰望祂的必有榮光,

不致蒙羞。

6我這可憐的人向祂呼求,

祂就垂聽,

救我脫離一切困境。

7祂的天使必四面保護敬畏祂的人,拯救他們。

8你們要親身體驗,

就知道耶和華的美善;

投靠祂的人有福了!

9耶和華的聖民啊,

你們要敬畏祂,

因為敬畏祂的人一無所缺。

10壯獅也會忍饑挨餓,

但尋求耶和華的人什麼福分都不缺。

11孩子們啊,聽我說,

我要教導你們敬畏耶和華。

12若有人熱愛生命,

渴望長壽和幸福,

13就要舌頭不出惡言,

嘴唇不說詭詐的話。

14要棄惡行善,

竭力追求和睦。

15耶和華的眼睛看顧義人,

祂的耳朵垂聽他們的呼求。

16耶和華嚴懲作惡之人,

從世上剷除他們。

17義人向耶和華呼救,祂就垂聽,

拯救他們脫離一切患難。

18祂安慰悲痛欲絕的人,

拯救心靈破碎的人。

19義人也會遭遇許多患難,

但耶和華必拯救他,

20保全他一身的骨頭,

連一根也不折斷。

21惡人必遭惡報,

與義人為敵的必被定罪。

22耶和華必救贖祂的僕人,

投靠祂的人必不被定罪。

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 34:1-22

Salimo 34

Salimo la Davide. Pamene iye ananyengezera misala pamaso pa Abimeleki, amene anamupirikitsa, iyeyo nʼkuchoka.

1Ndidzayamika Yehova nthawi zonse;

matamando ake adzakhala pa milomo yanga nthawi zonse.

2Moyo wanga udzanyadira Yehova;

anthu osautsidwa amve ndi kukondwera.

3Lemekezani Yehova pamodzi ndi ine;

tiyeni pamodzi tikuze dzina lake.

4Ine ndinafunafuna Yehova ndipo Iye anandiyankha;

anandilanditsa ku mantha anga onse.

5Iwo amene amayangʼana kwa Iye, nkhope zawo zimanyezimira;

nkhope zawo sizikhala zophimbidwa ndi manyazi.

6Munthu wosauka uno anayitana, ndipo Yehova anamumva;

Yehova anamupulumutsa ku mavuto ake onse.

7Mngelo wa Yehova amatchinjiriza amene amakonda Iye

ndi kuwalanditsa.

8Lawani ndipo onani kuti Yehova ndi wabwino;

wodala munthu amene amathawira kwa Iye.

9Wopani Yehova inu oyera mtima ake,

pakuti iwo amene amaopa Iye sasowa kanthu.

10Mikango itha kulefuka ndi kumva njala

koma iwo amene amafunafuna Yehova sasowa kanthu kalikonse kabwino.

11Bwerani ana anga, mundimvere;

ndidzakuphunzitsani kuopa Yehova.

12Aliyense wa inu amene amakonda moyo wake

ndi kukhumba kuti aone masiku abwino ambiri,

13asunge lilime lake ku zoyipa

ndi milomo yake kuti isayankhule zonama.

14Tembenuka kuchoka ku zoyipa ndipo chita zabwino;

funafuna mtendere ndi kuwulondola.

15Maso a Yehova ali pa olungama

ndipo makutu ake ali tcheru kumva kulira kwawo;

16nkhope ya Yehova ikutsutsana ndi amene amachita zoyipa,

kuwachotsa kuti asawakumbukirenso pa dziko lapansi.

17Olungama amafuwula, ndipo Yehova amawamva;

Iye amawalanditsa ku mavuto awo onse.

18Yehova ali pafupi kwa osweka mtima

ndipo amapulumutsa iwo amene asweka mu mzimu.

19Munthu wolungama atha kukhala ndi mavuto ambiri,

Koma Yehova amamulanditsa ku mavuto onsewo,

20Iye amateteza mafupa ake onse,

palibe limodzi la mafupawo limene lidzathyoledwa.

21Choyipa chidzapha anthu oyipa;

adani a olungama adzapezeka olakwa.

22Yehova amawombola atumiki ake;

aliyense amene amathawira kwa Iye sadzapezeka wolakwa.