詩篇 147 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 147:1-20

第 147 篇

讚美上帝復興耶路撒冷

1你們要讚美耶和華!

歌頌我們的上帝,真是美好!

讚美祂,真是快樂合宜!

2耶和華重建耶路撒冷

召集被擄去的以色列人。

3祂醫治心靈破碎的人,

包紮他們的創傷。

4祂決定眾星的數目,

給它們一一命名。

5我們的主偉大無比,充滿力量,

祂的智慧沒有窮盡。

6耶和華扶持謙卑人,

毀滅邪惡人。

7你們要以感恩的心歌頌耶和華,

彈琴讚美我們的上帝。

8祂以雲霞遮蔽天空,

降雨水滋潤大地,

使山上長出綠草。

9祂賜食物給走獸,

餵養嗷嗷待哺的小烏鴉。

10耶和華所喜悅的不是強健的馬匹,

也不是矯捷的戰士,

11而是敬畏祂、仰望祂慈愛的人。

12耶路撒冷啊,要頌讚耶和華;

錫安啊,要讚美你的上帝。

13因為祂使你的城門堅固,

賜福給你的兒女。

14祂使你四境平安,

飽享上好的麥子。

15祂向大地發出命令,

祂的話迅速傳開。

16祂降下羊毛般的白雪,

撒下爐灰般的寒霜。

17祂拋下碎石般的冰雹,

誰能經得住祂降下的嚴寒呢?

18祂一聲令下,冰雪便溶化,

微風便吹拂,河川便奔流。

19祂將自己的話傳於雅各

將自己的律例和法令指示以色列

20祂未曾這樣對待其他國家,

他們不知道祂的律法。

你們要讚美耶和華!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 147:1-20

Salimo 147

1Tamandani Yehova.

Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu,

nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!

2Yehova akumanga Yerusalemu;

Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.

3Akutsogolera anthu osweka mtima

ndi kumanga mabala awo.

4Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi,

ndipo iliyonse amayitchula dzina.

5Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri;

nzeru zake zilibe malire.

6Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa,

koma amagwetsa pansi anthu oyipa.

7Imbirani Yehova ndi mayamiko;

imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.

8Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo;

amapereka mvula ku dziko lapansi

ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.

9Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe

ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.

10Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo,

kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.

11Yehova amakondwera ndi amene amamuopa,

amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.

12Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu;

tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,

13pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako

ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.

14Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako

ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.

15Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi;

mawu ake amayenda mwaliwiro.

16Amagwetsa chisanu ngati ubweya

ndi kumwaza chipale ngati phulusa.

17Amagwetsa matalala ngati miyala.

Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?

18Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka;

amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.

19Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo,

malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.

20Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu;

anthu enawo sadziwa malamulo ake.

Tamandani Yehova.