詩篇 137 – CCBT & CCL

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 137:1-9

第 137 篇

被擄者的哀歌

1我們坐在巴比倫河畔,

想起錫安禁不住淒然淚下。

2我們把琴掛在柳樹上。

3俘虜我們的人要我們唱歌,

擄掠我們的人要我們歌唱,說:

「給我們唱一首錫安的歌。」

4我們流落異邦,

怎能唱頌讚耶和華的歌呢?

5耶路撒冷啊,倘若我忘了你,

情願我的右手無法再撥弄琴弦;

6倘若我忘了你,

不以你為我的至愛,

情願我的舌頭不能再歌唱。

7耶和華啊,

求你記住耶路撒冷淪陷時以東人的行徑。

他們喊道:

「拆毀這城,把它夷為平地!」

8巴比倫城啊,

你快要滅亡了,

那向你以牙還牙為我們復仇的人有福了!

9那抓住你的嬰孩摔在石頭上的人有福了!

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 137:1-9

Salimo 137

1Mʼmbali mwa mitsinje ya ku Babuloni tinakhala pansi ndi kulira

pamene tinakumbukira Ziyoni.

2Kumeneko, pa mitengo ya misondozi

tinapachika apangwe athu,

3pakuti anthu otigwira ukapolo anatipempha kuti tiyimbe nyimbo.

Otizunza athu anafuna nyimbo zachisangalalo;

iwo anati, “Tiyimbireni imodzi mwa nyimbo za ku Ziyoni!”

4Tingayimbe bwanji nyimbo za Yehova

mʼdziko lachilendo?

5Ndikakuyiwala iwe Yerusalemu,

dzanja langa lamanja liyiwale luso lake.

6Lilime langa limamatire ku nkhama za mʼkamwa mwanga

ndikapanda kukukumbukira iwe Yerusalemu,

ngati sindiyesa iwe

chimwemwe changa chachikulu.

7Kumbukirani, Inu Yehova, zimene Aedomu anachita

pa tsiku limene Yerusalemu anagonja.

Iwowo anafuwula kuti, “Mugwetseni pansi, mugwetseni pansi

mpaka pa maziko ake!”

8Iwe mwana wa mkazi wa Babuloni, woyenera kuwonongedwa,

wodalitsika ndi yemwe adzakubwezera

pa zimene watichitira.

9Amene adzagwira makanda ako

ndi kuwakankhanthitsa pa miyala.